< U-Eksodusi 30 >
1 Uzakwenza lelathi lokutshisela impepha, ulenze ngesihlahla sesinga.
Upange guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani.
2 Ubude balo bube yingalo, lobubanzi balo ingalo, lilingane inhlangothi zozine; lokuphakama kwalo kube zingalo ezimbili; impondo zalo zizavela kulo.
Likhale lofanana mbali zonse. Mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91. Nyanga zake zipangidwe kumodzi ndi guwalo.
3 Njalo ulihuqe ngegolide elicwengekileyo, ingaphezulu yalo, lenhlangothi zalo ezilizingelezeleyo, lempondo zalo; wenze kulo umqolo wegolide olizingelezeleyo.
Ukute guwa lonse ndi golide wabwino kwambiri, pamwamba pake, mbali zonse zinayi, pamodzi ndi nyanga zake. Ndipo upange mkombero wagolide kuzungulira guwalo.
4 Wenze njalo amasongo amabili egolide, ngaphansi komqolo walo, enhlangothini ezimbili zalo; wenze enhlangothini zalo zombili; azakuba zindawo zemijabo ezokulithwala ngayo.
Upange mphete ziwiri zagolide ndipo uzilumikize ku guwa mʼmunsi mwa mkombero, mphete ziwiri ku mbali zonse ziwiri zoyangʼanana. Mphetozo zizigwira nsichi zonyamulira guwalo.
5 Njalo wenze imijabo ngesihlahla sesinga, uyihuqe ngegolide.
Upange mizati yamtengo wa mkesha ndipo uyikute ndi golide.
6 Uzalibeka phambi kweveyili elingasemtshokotshweni wobufakazi, phambi kwesihlalo somusa esiphezu kobufakazi, lapho engizahlangana khona lawe.
Uyike guwalo patsogolo pa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano. Apa ndi pamene ndizidzakumana nawe.
7 Njalo uAroni atshisele kulo impepha elephunga elimnandi ukusa ngokusa, eselungise izibane uzayitshisa;
“Aaroni ayenera kumafukiza lubani wonunkhira pa guwalo mmawa uliwonse. Pamene akukonza nyale zija afukizenso lubani.
8 lapho uAroni elumathisa izibane kusihlwa, ayitshise; yimpepha eqhubekayo phambi kweNkosi ezizukulwaneni zenu.
Aaroni ayenera kufukizanso lubani pamene ayatsa nyale madzulo kuti lubani akhale akuyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova kwa mibado imene ikubwera.
9 Linganikeleli kulo impepha engejwayelekanga kumbe umnikelo wokutshiswa kumbe umnikelo wokudla; njalo lingatheli kulo umnikelo wokunathwayo.
Pa guwapo usafukize lubani wachilendo kapena kuperekapo nsembe yopsereza kapena nsembe yaufa. Usathire pa guwapo ngakhale nsembe yachakumwa.
10 UAroni uzakwenza inhlawulo yokuthula empondweni zalo kanye ngomnyaka, ngegazi lomnikelo wesono wezinhlawulo zokuthula; kanye ngomnyaka uzakwenza inhlawulo yokuthula kulo ezizukulwaneni zenu; liyingcwelengcwele eNkosini.
Aaroni azidzapereka nsembe yopepesera machimo pa nyanga za guwalo kamodzi pa chaka. Mwambowu uzidzachitika pogwiritsa ntchito magazi a nsembe yopepesera machimo, ndipo zizidzachitika mʼmibado yanu yonse. Choncho guwa lansembelo lidzakhala loyera ndi loperekedwa kwa Yehova.”
11 INkosi yasikhuluma kuMozisi yathi:
Ndipo Yehova anati kwa Mose,
12 Lapho uthatha inani lonke labantwana bakoIsrayeli, njengokubalwa kwabo, bazanika ngulowo lalowo ihlawulo ngomphefumulo wakhe eNkosini, nxa ubabala; ukuze kungabi lenhlupheko phakathi kwabo, nxa ubabala.
“Pamene ukuchita kalembera wa Aisraeli, munthu aliyense ayenera kupereka kwa Yehova chowombolera moyo wake pamene akuwerengedwa. Motero mliri sudzabwera pa iwo pamene ukuwawerenga.
13 Bazanika lokhu, wonke odlulela kwababaliweyo, ingxenye yeshekeli, njengokweshekeli lendlu engcwele - ishekeli lingamagera angamatshumi amabili - ingxenye yeshekeli ngumnikelo eNkosini.
Izi ndi zimene aliyense wolembedwa mu kawundula ayenera kupereka: theka la sekeli, kutanthauza ndalama zolemera magalamu asanu ndi limodzi malingana ndi kawerengedwe ka ndalama za ku Nyumba ya Mulungu. Paja sekeli imodzi ikulingana ndi magera makumi awiri. Theka la sekeli chidzakhala chopereka cha kwa Yehova.
14 Wonke odlulela kwababaliweyo, kusukela koleminyaka engamatshumi amabili langaphezulu, anikele umnikelo weNkosi.
Aliyense wolembedwa mu kawundula amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira ayenera kupereka chopereka kwa Yehova.
15 Abanothileyo bangadlulisi, labayanga banganciphisi ingxenye yeshekeli, lapho linikela umnikelo weNkosi, ukwenzela imiphefumulo yenu inhlawulo yokuthula.
Anthu olemera asapereke koposa theka la sekeli ndipo osauka asapereke kuchepera theka la sekeli pamene mukupereka nsembe kwa Yehova yowombolera miyoyo yanu.
16 Uzathatha imali yenhlawulo zokuthula ebantwaneni bakoIsrayeli, uyinikele inkonzo yethente lenhlangano, ukuthi ibe yisikhumbuzo sabantwana bakoIsrayeli phambi kweNkosi, ukwenzela imiphefumulo yenu inhlawulo yokuthula.
Ulandire ndalama zopepeserazo kuchokera kwa Aisraeli ndipo zigwiritsidwe ntchito ya ku tenti ya msonkhano. Zoperekazi zidzakhala chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova, ndiponso zowombolera miyoyo yanu.”
17 INkosi yasikhuluma kuMozisi yathi:
Ndipo Yehova anati kwa Mose,
18 Uzakwenza lenditshi yethusi yokugezela elonyawo lwayo lwethusi, ukugezela kuyo; uyibeke phakathi laphakathi kwethente lenhlangano lelathi, uthele kuyo amanzi,
“Upange beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso. Uliyike pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo uthiremo madzi.
19 njalo uAroni lamadodana akhe bagezele kuyo izandla zabo lenyawo zabo.
Aaroni ndi ana ake azisamba mʼmanja ndi kutsuka mapazi awo ndi madzi amenewo.
20 Nxa bengena ethenteni lenhlangano bazageza ngamanzi, ukuze bangafi, loba besondela elathini ukukhonza, ukutshisa umnikelo owenzelwe iNkosi ngomlilo.
Pamene akulowa mu tenti ya msonkhano, iwo asambe madziwa kuti asafe. Ndiponso pamene akupita kukatumikira ku guwa lansembe ndi kupereka nsembe yopsereza kwa Yehova,
21 Ngakho bazageza izandla zabo lenyawo zabo ukuze bangafi; njalo kuzakuba kubo yisimiso esilaphakade, kuye lakunzalo yakhe ezizukulwaneni zabo.
azisamba mʼmanja mwawo ndi kutsuka mapazi kuti asadzafe. Limeneli ndi lamulo limene Aaroni, pamodzi ndi ana ndi zidzukulu zake mʼtsogolomo ayenera kumadzalitsatira mpaka muyaya.”
22 INkosi yakhuluma futhi kuMozisi yathi:
Ndipo Yehova anati kwa Mose,
23 Wena-ke, zithathele amakha aqakathekileyo, imure elizigelezelayo elingamashekeli angamakhulu amahlanu, lekinamoni elilephunga elimnandi ingxenye yalokho, elingamashekeli angamakhulu amabili lamatshumi amahlanu, lekalamu elilephunga elimnandi elingamashekeli angamakhulu amabili lamatshumi amahlanu,
“Utenge zonunkhira bwino kwambiri izi: makilogalamu asanu ndi limodzi a mure wamadzi, makilogalamu atatu a zonunkhira bwino za mtundu wa sinamoni, makilogalamu atatu a nzimbe yonunkhira bwino kwambiri,
24 lekhasiya elingamashekeli angamakhulu amahlanu ngokweshekeli lendlu engcwele, lamafutha omhlwathi alihini;
makilogalamu asanu ndi limodzi a mkesha. Zonsezi zikhale malingana ndi muyeso wa ku Nyumba ya Mulungu. Pakhalenso malita anayi a mafuta a olivi.
25 wenze lokhu kube ngamafutha angcwele okugcoba, amakha axutshanisiweyo njengokwenza komenzi wamakha; azakuba ngamafutha angcwele okugcoba.
Ugwiritse ntchito zinthu zimenezi kupanga mafuta opatulika odzozera, mafuta onunkhira, apangidwe ndi mʼmisiri waluso lopanga zonunkhiritsa. Awa adzakhala mafuta opatulika odzozera.
26 Uzagcoba ngawo ithente lenhlangano lomtshokotsho wobufakazi,
Tsono uwagwiritse ntchito podzoza tenti ya msonkhano, Bokosi la Chipangano,
27 letafula lezitsha zalo zonke, loluthi lwesibane lezitsha zalo, lelathi lempepha,
tebulo, ndi ziwiya zake zonse, choyikapo nyale ndi zipangizo zake, guwa lofukizirapo lubani,
28 lelathi lomnikelo wokutshiswa lezitsha zalo zonke, lenditshi yokugezela lonyawo lwayo;
guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso beseni pamodzi ndi nsichi yake.
29 ukungcwelise ukuze kube yingcwelengcwele; loba yini okukuthintayo kuzakuba ngcwele.
Zonsezi uzipatule kuti zidzakhale zopatulika, ndipo chilichonse chimene chidzakhudza zimenezi chidzakhala chopatulika.
30 Ugcobe laye uAroni lamadodana akhe, ubangcwelise ukuze bangisebenzele njengabapristi.
“Udzoze Aaroni ndi ana ake aamuna ndi kuwapatula kuti akhale ansembe onditumikira.
31 Ukhulume kubantwana bakoIsrayeli uthi: Lokhu kuzakuba kimi ngamafutha angcwele okugcoba ezizukulwaneni zenu;
Tsono awuze a Israeli kuti, mafuta wodzozera awa adzakhala wopatulika mpaka muyaya.
32 angabothelwa emzimbeni womuntu; njalo lingawenzi anjengawo ngokwenziwa kwawo; angcwele, azakuba ngcwele kini.
Musadzadzozere munthu wamba mafuta amenewa, ndipo musadzapange mafuta wofanana ndi amenewa. Mafutawa ndi wopatulika ndipo akhale woyera kwa inu.
33 Loba ngubani owenza anjengawo, loba ewafaka kowemzini, uzaqunywa asuke ebantwini bakibo.
Wina aliyense amene adzapanga mafuta wonunkhira wofanana nawo kapena kudzozera mafutawa munthu wamba osati wansembe ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.”
34 INkosi yasisithi kuMozisi: Zithathele amakha amnandi, isitakete leonika legalibanu, amakha amnandi lenhlaka ecengekileyo, kube yizabelo ezilinganayo;
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Tenga muyeso wofanana wa zinthu zonunkhira izi: sitakate, onika, galibanumu pamodzi ndi lubani weniweni.
35 wenze kube yimpepha, amakha axutshanisiweyo njengokwenza komenzi wamakha, itshwayiwe, icengekile, ingcwele;
Uziphatikize pamodzi zonsezi ndi kupanga lubani monga amachitira mmisiri wopanga zonunkhira. Athire mchere ndipo akhale woyera ndi wopatulika.
36 uchole okwayo kucolisiseke, ubeke okwayo phambi kobufakazi ethenteni lenhlangano, lapho engizahlangana khona lawe; izakuba yingcwelengcwele kini.
Upere gawo lina mosalala kwambiri ndipo utapepo pangʼono ndi kuyika patsogolo pa Bokosi la Chipangano mu tenti ya msonkhano, kumene ine ndidzakumane nawe. Lubani ameneyu kwa inu adzakhala wopatulika kwambiri.
37 Kodwa impepha ozayenza, lingazenzeli yona njengokwenziwa kwayo; izakuba ngcwele kuwe, yenzelwe iNkosi.
Musapange lubani wanu potsatira njira iyi. Lubani yense wopangidwa mwa njira iyi akhale wopatulika, woperekedwa kwa Yehova.
38 Loba ngubani ozakwenza enjengayo ukuyinuka, uzaqunywa asuke ebantwini bakibo.
Aliyense amene adzapanga wofanana naye kuti asangalale ndi fungo lake ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.”