< U-Eksodusi 29 >

1 Yile-ke into ozayenza kubo ukubehlukanisa ukuthi bangisebenzele njengabapristi. Thatha ijongosi elilodwa ithole lenkomo, lenqama ezimbili ezingelasici,
“Pofuna kumupatula Aaroni ndi ana ake kuti akhale ansembe onditumikira Ine, uchite izi: Utenge ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa ziwiri zazimuna zopanda chilema.
2 lesinkwa esingelamvubelo, lamaqebelengwana angelamvubelo ahlanganiswe lamafutha, lezinkwana eziyizipatalala ezingelamvubelo ezinindwe ngamafutha, uzenze ngempuphu ecolekileyo yengqoloyi;
Utengenso buledi wopanda yisiti, makeke wopanda yisiti wopakidwa mafuta. Zonsezi uzipange ndi ufa wosalala wa tirigu.
3 ukufake esitsheni esisodwa, ukusondeze ngesitsha, kanye lejongosi lenqama ezimbili.
Uziyike mʼdengu ndipo ubwere nazo kwa Ine pamodzi ndi ngʼombe yayimuna ija ndi nkhosa ziwiri zazimuna zija.
4 Usondeze uAroni lamadodana akhe emnyango wethente lenhlangano, ubagezise ngamanzi;
Kenaka ubwere naye Aaroni ndi ana ake pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo uwasambitse ndi madzi.
5 uthathe izembatho, ugqokise uAroni isigqoko, lebhatshi le-efodi, le-efodi, lesembatho sesifuba, umbophe ngebhanti elelukwe ngobungcitshi le-efodi,
Tenga zovala ndipo umuveke Aaroni mwinjiro, mkanjo wa efodi, efodiyo ndi chovala chapachifuwa. Umumange mʼchiwuno lamba wa efodi wolukidwa mwaluso uja.
6 umthwalise iqhiye ekhanda lakhe, umthwalise umqhele ongcwele phezu kweqhiye.
Umuveke nduwira kumutu, ndiponso uyike chizindikiro chopatulika chija pa nduwirayo.
7 Uthathe amafutha okugcoba, uwathele ekhanda lakhe, umgcobe.
Utenge mafuta wodzozera ndipo uwatsanulire pamutu pake kumudzoza.
8 Usondeze lamadodana akhe, uwagqokise izigqoko.
Ubwere ndi ana ake aamuna ndipo uwavekenso minjiro
9 Ubabophe ngamabhanti, uAroni lamadodana akhe, ubabophele izingowane, lobupristi bube ngobabo ngesimiso saphakade. Ubehlukanise-ke uAroni lamadodana akhe.
ndi nduwira. Kenaka umange malamba Aaroniyo pamodzi ndi ana ake ndi kuwaveka nduwira. Motero unsembe udzakhala wawo malingana ndi lamulo ili losatha. “Umu ndi mmene udzadzozere Aaroni ndi ana ake aamuna.
10 Uzasondeza ijongosi phambi kwethente lenhlangano; njalo uAroni lamadodana akhe babeke izandla zabo enhlokweni yejongosi;
“Ubwere ndi ngʼombe yayimuna pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo Aaroni ndi ana ake asanjike manja awo pamutu pake.
11 ubusulihlaba ijongosi phambi kweNkosi emnyango wethente lenhlangano,
Uphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
12 uthathe okwegazi lejongosi, ulifake empondweni zelathi ngomunwe wakho, uthululele lonke igazi esisekelweni selathi.
Utenge magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chako pa nyanga zaguwa lansembe ndipo magazi otsalawo uwakhutulire pa tsinde laguwalo.
13 Uzathatha idanga lonke, lamahwahwa aphezu kwesibindi, lezinso zombili, lamahwahwa aphezu kwazo, ukutshise elathini.
Kenaka utenge mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake. Zonsezi uzitenthe pa guwapo.
14 Kodwa inyama yejongosi lesikhumba salo lomswane walo ukutshise ngomlilo ngaphandle kwenkamba; kungumnikelo wesono.
Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake uziwotche kunja kwa msasa. Iyi ndi nsembe yopepesera machimo.
15 Ubusuthatha inqama ibenye; njalo uAroni lamadodana akhe babeke izandla zabo phezu kwenhloko yenqama.
“Utenge nkhosa yayimuna imodzi ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna asanjike manja awo pamutu pake.
16 Ubusuyihlaba inqama, uthathe igazi layo, ulifafaze elathini uligombolozele.
Uyiphe ndipo utenge magazi ake ndi kuwaza mbali zonse zaguwalo.
17 Uyiqume inqama ngeziqa zayo, ugezise imibilini yayo lemilenze yayo, ukubeke phezu kweziqa zayo laphezu kwenhloko yayo,
Uyidule nkhosayo nthulinthuli, kutsuka matumbo ake ndi miyendo yake. Ukatero, pamodzi ndi mutu wake, uziyike pamwamba pa nthulizo.
18 utshise inqama yonke elathini. Kungumnikelo wokutshiswa eNkosini, kuluqhatshi olumnandi, umnikelo owenzelwe iNkosi ngomlilo.
Ndipo uwotche nkhosa yonseyo pa guwa lansembe. Iyi ndi nsembe yopsereza ya kwa Yehova. Ili ndi fungo lokoma, loperekedwa pa moto kwa Yehova.
19 Uzathatha inqama yesibili; uAroni lamadodana akhe babesebebeka izandla zabo phezu kwenhloko yenqama.
“Utenge nkhosa yayimuna ina ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna asanjike manja awo pamutu pake.
20 Uyihlabe-ke inqama, uthathe okwegazi layo, ulifake eqwangeni lwendlebe kaAroni, leqwangeni lwendlebe yokunene yamadodana akhe, lesithupheni sesandla sabo sokunene, lezwaneni olukhulu lonyawo lwabo lokunene, ufafaze igazi elathini uligombolozele.
Uyiphe ndipo utenge magazi ake ena ndi kupaka ndewere za makutu a kudzanja lamanja la Aaroni ndi ana ake aamuna. Upakenso pa zala zawo zazikulu za kudzanja lawo lamanja, ndi zala zazikulu za kuphazi lakudzanja lawo lamanja. Kenaka uwaze magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
21 Uthathe okwegazi eliselathini lokwamafutha okugcoba, ukufafaze phezu kukaAroni, laphezu kwezembatho zakhe, laphezu kwamadodana akhe, laphezu kwezembatho zamadodana akhe kanye laye, ukuze abe ngcwele lezembatho zakhe, lamadodana akhe lezembatho zamadodana akhe kanye laye.
Ndipo utenge magazi ena amene ali pa guwa lansembe komanso pa mafuta ena odzozera ndipo uwawaze pa Aaroni ndi zovala zake ndi ana ake ndi zovala zawo. Ndiye kuti iyeyo ndi ana ake aamuna adzakhala opatulika pamodzi ndi zovala zawo.
22 Uthathe enqameni amahwahwa, lomsila ononileyo, ledanga, lamahwahwa esibindi, lezinso zombili, lamahwahwa aphezu kwazo, lomlenze wokunene, ngoba iyinqama yokwehlukaniswa;
“Pa nkhosa yayimuna ija utengepo mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake, ndiponso ntchafu yakumanja. Iyi ndi nkhosa ya mwambo wodzoza.
23 lesinkwa esiyindilinga esisodwa, leqebelengwana elilodwa elesinkwa esilamafutha, lesinkwana esiyisipatalala esisodwa, esitsheni sezinkwa ezingelamvubelo esiphambi kweNkosi,
Utengenso mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene lili pamaso pa Yehova, buledi mmodzi, buledi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi.
24 ukubeke konke ezandleni zikaAroni lezandleni zamadodana akhe, ukuzunguze ukuze kube ngumnikelo wokuzunguzwa phambi kweNkosi.
Izi zonse uzipereke mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake, ndipo iwo aziweyule pamaso pa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
25 Ukuthathe ezandleni zabo, ukutshise phezu kwelathi phezu komnikelo wokutshiswa, ukuze kube luqhatshi olumnandi phambi kweNkosi; kungumnikelo owenzelwe iNkosi ngomlilo.
Kenaka uzitenge mʼmanja mwawo ndipo uzipsereze pa guwa lansembe, pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza kuti ipereke fungo lokoma kwa Yehova. Ichi ndiye chopereka chachakudya kwa Yehova.
26 Uzathatha isifuba senqama yokwehlukaniswa engekaAroni, usizunguze sibe ngumnikelo wokuzunguzwa phambi kweNkosi, njalo sibe yisabelo sakho.
Kenaka utenge chidale cha nkhosa yayimuna imene inaperekedwa pamwambo wodzoza Aaroni, uchiweyule kuti chikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndipo chidzakhala gawo lako.
27 Uzasingcwelisa isifuba somnikelo wokuzunguzwa lomlenze womnikelo wokuphakanyiswa ozunguzwayo lophakanyiswayo, okwenqama yokwehlukaniswa, okwalokho okungokukaAroni lokwalokho okungokwamadodana akhe;
“Uzipatule ziwalo zonse za nkhosa ya pa mwambo wodzoza Aaroni ndi ana ake. Chidale chimene unaweyula chija ndiponso ntchafu imene inaperekedwa ija.
28 njalo kuzakuba ngokukaAroni lokwamadodana akhe, kube yisimiso saphakade kuvela kubantwana bakoIsrayeli; ngoba kungumnikelo wokuphakanyiswa; kuzakuba ngumnikelo wokuphakanyiswa ovela kubantwana bakoIsrayeli, eminikelweni yabo yokuthula; umnikelo wabo wokuphakanyiswa eNkosini.
Nsembe izi ndi zimene Aisraeli azipereka kwa Aaroni ndi ana ake mwa zonse zimene azipereka nthawi zonse. Mwa zopereka za mtendere zimene ana a Aisraeli adzapereka kwa Yehova, zimenezi zikhale gawo lawo.
29 Lezembatho ezingcwele zikaAroni zizakuba ngezamadodana akhe emva kwakhe, ukuze agcotshwe embethe zona, lokuze ehlukaniswe embethe zona.
“Zovala zopatulika za Aaroni zidzakhala za ana ake aamuna iye atafa kuti adzavale podzozedwa ndi polandira udindo wawo.
30 Insuku eziyisikhombisa umpristi endaweni yakhe, ovela kumadodana akhe, uzazembatha, nxa engena ethenteni lenhlangano ukukhonza endaweni engcwele.
Mwana amene adzalowa mʼmalo mwake monga wansembe pamene adzabwerera kudzalowa mu tenti ya msonkhano kudzatumikira ku malo wopatulika, adzavala zovala zimenezi masiku asanu ndi awiri.
31 Uzathatha-ke inqama yokwehlukaniswa, upheke inyama yayo endaweni engcwele.
“Utenge nkhosa yayimuna ya pamwambo wodzoza ansembe ndipo uyiphike pamalo opatulika.
32 Njalo uAroni lamadodana akhe bazakudla inyama yenqama lesinkwa esisesitsheni emnyango wethente lenhlangano,
Aaroni ndi ana ake adye nyama ya nkhosa yayimunayi pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu pa khomo la tenti ya msonkhano.
33 badle lezozinto okwenziwa ngazo inhlawulo yokuthula, ukubehlukanisa, ukubangcwelisa; kodwa owemzini angazidli ngoba zingcwele.
Adye zonse zimene anazipereka kwa Yehova pamwambo wopepesera machimo powadzoza ndi kuwapatula. Munthu wamba asadye chifukwa ndi zopatulika.
34 Njalo uba kusala okwenyama yokwehlukaniswa kumbe okwesinkwa kuze kuse, tshisa okuseleyo ngomlilo; kungadliwa, ngoba kungcwele.
Ndipo ngati nyama ina ya nkhosa ya pamwambo wodzoza ansembe kapena buledi zatsala mpaka mmawa, muziwotche, asazidye chifukwa ndi zopatulika.
35 Uzakwenza njalo-ke kuAroni lakumadodana akhe njengakho konke engikulaya khona; insuku eziyisikhombisa uzabehlukanisa.
“Uchitire Aaroni ndi ana ake aamuna zonse zimene ndakulamulazi. Uchite mwambo wowapatula kukhala ansembe masiku asanu ndi awiri.
36 Insuku ngensuku unikele ijongosi lomnikelo wesono wenhlawulo yokuthula; uhlambulule ilathi lapho ulenzela inhlawulo yokuthula, uligcobe ukuze ulingcwelise.
Tsiku lililonse uzipereka ngʼombe yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo kuti machimowo akhululukidwe. Ndiponso upatule guwalo popereka nsembe yopepesera ndi kulidzoza mafuta kuti likhale lopatulika.
37 Ulenzele ilathi inhlawulo yokuthula insuku eziyisikhombisa, ulingcwelise, lelathi lizakuba yingcwelengcwele; konke okulithintayo ilathi kuzakuba ngcwele.
Pa masiku asanu ndi awiri uzipereka pa guwapo nsembe zoyeretsera guwalo, ukatero ndiye kuti uzilipatula. Ndipo guwa lansembelo lidzakhala loyera kwambiri, ndipo chilichonse chimene chidzakhudza guwalo chidzayeretsedwa.
38 Yilokhu-ke ozakunikela phezu kwelathi: Amawundlu amabili alomnyaka owodwa insuku ngensuku njalonjalo.
“Tsiku ndi tsiku pa guwa lansembe uzipereka izi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri.
39 Elinye iwundlu uzalinikela ekuseni, lelinye iwundlu ulinikele kusihlwa,
Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
40 lokwetshumi kwempuphu ecolekileyo kuxubene lengxenye yesine yehini yamafutha agigiweyo, lengxenye yesine yehini yewayini kube ngumnikelo wokunathwayo, welinye iwundlu.
Pamodzi ndi mwana wankhosa woyambayo, muzipereka kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi pamodzi ndi lita imodzi ya vinyo ngati chopereka chachakumwa.
41 Lelinye iwundlu ulinikele kusihlwa, wenze kulo njengomnikelo wokudla wekuseni, lanjengomnikelo wawo wokunathwayo, kube luqhatshi olumnandi, umnikelo owenzelwe iNkosi ngomlilo.
Upereke mwana wankhosa winayo madzulo pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa kuti ikhale fungo lokoma la chopereka chachakudya kwa Yehova.
42 Uzakuba ngumnikelo wokutshiswa njalonjalo ezizukulwaneni zenu, emnyango wethente lenhlangano phambi kweNkosi, lapho engizahlangana khona lani, ukukhuluma lawe lapho.
“Zopereka zopsereza zimenezi ziziperekedwa nthawi zonse, pa mibado yonse. Muzidzazipereka pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano. Pa guwa lansembe, Yehova adzakumana nanu ndi kuyankhula nanu.
43 Lalapho ngizahlangana labantwana bakoIsrayeli, njalo kungcweliswe yinkazimulo yami.
Pameneponso Ine ndidzakumana ndi Aisraeli, ndipo guwalo lidzakhala lopatulika chifukwa cha ulemerero wanga.
44 Njalo ngizangcwelisa ithente lenhlangano lelathi, ngizangcwelisa loAroni lamadodana akhe, ukuze bangisebenzele njengabapristi.
“Tsono Ine ndidzapatula tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Ndidzapatulanso Aaroni pamodzi ndi ana ake kuti akhale ansembe anga onditumikira.
45 Ngizahlala phakathi kwabantwana bakoIsrayeli, ngibe nguNkulunkulu kubo.
Ndidzakhala pakati pa Aisraeli ndikukhala Mulungu wawo.
46 Bazakwazi-ke ukuthi ngiyiNkosi uNkulunkulu wabo, eyabakhupha elizweni leGibhithe ukuze ngihlale phakathi kwabo; ngiyiNkosi uNkulunkulu wabo.
Adzadziwa kuti ine ndine Mulungu wawo amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto kuti ndikhale pakati pawo. Ine ndine Yehova, Mulungu wawo.”

< U-Eksodusi 29 >