< U-Eksodusi 28 >
1 Wena-ke sondeza kuwe uAroni umnewenu lamadodana akhe kanye laye, phakathi kwabantwana bakoIsrayeli, ukuze bangisebenzele njengabapristi, uAroni, uNadabi loAbihu, uEleyazare loIthamari, amadodana kaAroni.
“Aaroni mʼbale wako ndi ana ake aamuna, Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara uwapatule pakati pa Aisraeli. Abwere kwa iwe kuti anditumikire monga ansembe.
2 Umenzele-ke uAroni umnewenu izembatho ezingcwele, ezobukhosi lezokucecisa.
Umusokere mʼbale wako, Aaroni, zovala zopatulika kuti azioneka mwaulemerero ndi molemekezeka.
3 Wena-ke khuluma labo bonke abahlakaniphileyo ngenhliziyo, engibagcwalise ngomoya wenhlakanipho, ukuze benze izembatho zikaAroni zokumehlukanisela ukungisebenzela njengompristi.
Uwawuze anthu onse aluso amene Ine ndawapatsa nzeru pa ntchito yosoka kuti apange zovala za Aaroni za pa mwambo womupatula, kuti iye anditumikire monga wansembe.
4 Lalezi yizembatho abazazenza; isembatho sesifuba le-efodi, lebhatshi, lesigqoko esilamabala, iqhiye, lebhanti; bamenzele uAroni umnewenu izembatho ezingcwele, lezamadodana akhe, ukuze angisebenzele njengompristi.
Zovala zoti apange ndi izi: chovala chapachifuwa, efodi, mkanjo, mwinjiro wolukidwa, nduwira ndi lamba. Apangire mʼbale wako Aaroni ndi ana ake aamuna zovala zopatulikazi kuti iwo anditumikire monga ansembe.
5 Bona-ke kabathathe igolide lokuluhlaza okwesibhakabhaka lokuyibubende lokubomvu lelembu elicolekileyo kakhulu.
Iwo agwiritse ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira ndi yosalala yofewa.
6 Besebesenza i-efodi ngegolide, okuluhlaza okwesibhakabhaka, lokuyibubende, okubomvu, lelembu elicolekileyo lentambo ephothiweyo, umsebenzi wengcitshi.
“Apange efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yolukidwa mwaluso.
7 Sizakuba lezichibi ezimbili zamahlombe, zihlangane emaceleni aso womabili, ukuze sihlanganiswe.
Efodiyo ikhale ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.
8 Ibhanti elelukwe ngobungcitshi le-efodi lakhe, elikuye, lizakuba njengomsebenzi walo, liyinto yinye, ngegolide, okuluhlaza okwesibhakabhaka, lokuyibubende, lokubomvu, lelembu elicolekileyo lentambo ephothiweyo.
Lamba womangira efodi akhale wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Akhale wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala.
9 Njalo uzathatha amatshe amabili ama-onikse, ubaze kuwo amabizo amadodana kaIsrayeli,
“Utenge miyala iwiri ya onikisi ndipo uzokotepo mayina a ana a Israeli.
10 ayisithupha kumabizo awo phezu kwelinye ilitshe, lamabizo ayisithupha aseleyo phezu kwelinye ilitshe, njengokuzalwa kwawo.
Mayina asanu ndi limodzi akhale pa mwala umodzi, ndipo mayina asanu ndi limodzi pa mwala winawo motsata mabadwidwe awo.
11 Njengomsebenzi wombazi wamatshe, njengokubazwa kwendandatho elophawu, uzawabaza amatshe womabili, ngamabizo amadodana kaIsrayeli, uwenze amiswe ezisekelweni zegolide ezitshiliweyo.
Mayina a ana a Israeli uwazokote pa miyala iwiriyo, monga momwe amachitira mmisiri wozokota miyala. Ndipo uyike miyalayo mu zoyikamo zake zagolide.
12 Njalo uzabeka amatshe womabili ezichibini zamahlombe ze-efodi, amatshe esikhumbuzo ebantwaneni bakoIsrayeli; loAroni uzathwala amabizo abo emahlombe akhe womabili phambi kweNkosi, kube yisikhumbuzo.
Umangirire miyala iwiriyi pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli. Aaroni azinyamula mayinawo mʼmapewa ake kuti akhale chikumbutso pamaso pa Yehova.
13 Wenze lezisekelo ezitshiliweyo zegolide,
Upange zoyikamo za maluwa agolide,
14 lamaketane amabili egolide elicwengekileyo, uwenze ukuthi abe njengamagoda, umsebenzi ophothiweyo, amaketane aphothiweyo uwabophele ezisekelweni ezitshiliweyo zegolide.
ndiponso maunyolo awiri a golide wabwino kwambiri, wopetedwa ngati zingwe ndipo uwalumikize ku zoyikamozo.
15 Ubususenza isembatho sesifuba sokwahlulela, kube ngumsebenzi wengcitshi, uyenze njengomsebenzi we-efodi, ngegolide, okuluhlaza okwesibhakabhaka, lokuyibubende, lokubomvu, langelembu elicolekileyo lentambo ephothiweyo uzasenza.
“Upange chovala chapachifuwa chogwiritsa ntchito poweruza mlandu ndipo uchipange mwaluso kwambiri. Uchipange ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino.
16 Kasilingane inhlangothi zozine, siphindwe kabili, ubude baso bube yikwelulwa kweminwe, lobubanzi baso bube yikwelulwa kweminwe.
Kutalika kwake kukhale kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, ndipo chikhale chopinda pawiri.
17 Njalo uhlele kuso inhlelo zamatshe, imizila emine yamatshe; umzila wesardiyusi, itopazi le-emeraldi, umzila wokuqala.
Uyikepo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba ukhale ndi miyala ya rubi, topazi ndi berili.
18 Lomzila wesibili ube lerubi, isafire, lendayimana,
Mzere wachiwiri pakhale miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi;
19 lomzila wesithathu ube lejasinte, i-agate, le-ametiste,
mzere wachitatu pakhale miyala ya opera, agate ndi ametisiti.
20 lomzila wesine ube lebherule, le-onikse, lejaspi; amatshe la azasekelwa ngegolide ezisekelweni zawo ezitshiliweyo.
Mzere wachinayi pakhale miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi uyiike mu zoyikamo zagolide.
21 Lamatshe azakuba lamabizo amadodana kaIsrayeli, alitshumi lambili, lamabizo awo; njengokubazwa kwendandatho elophawu, yilelo lalelo lebizo lalo; azakuba ngawezizwe ezilitshumi lambili.
Miyalayo ikhalepo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse uzokotedwe ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
22 Wenze-ke esembathweni sesifuba amaketane aphothiweyo omsebenzi wegoda egolide elicwengekileyo,
“Upange timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.
23 wenze futhi phezu kwesembatho sesifuba amasongo amabili egolide, uwafake amasongo amabili emaceleni womabili esembatho sesifuba.
Upangenso mphete ziwiri zagolide ndipo uzimangirire pa ngodya ziwiri za pa chovala chapachifuwa.
24 Ufake amaketane amabili egolide aphothiweyo emasongweni amabili emaceleni esembatho sesifuba;
Umangirire timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho.
25 kodwa izihloko zombili zamaketane womabili aphothiweyo uzifake ezisekelweni ezimbili ezitshiliweyo, uzibeke ezichibini ze-efodi, phambili kwayo kanye.
Ndipo mbali ina ya timaunyoloto umangirire pa zoyikapo zake ziwiri zija ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.
26 Uzakwenza njalo amasongo amabili egolide, uwafake emaceleni womabili esembatho sesifuba, emphethweni waso ongaphakathi kwe-efodi.
Upangenso mphete ziwiri zagolide, ndipo uzilumikize ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija.
27 Wenze futhi amasongo amabili egolide, uwafake ezichibini ezimbili ze-efodi, ngaphansi ngaphambili kwaso, eduze kokuhlangana kwazo, phezu kwebhanti elelukwe ngobungcitshi le-efodi.
Upangenso mphete zina ziwiri zagolide ndipo uzilumikize kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi.
28 Bazabophela-ke isembatho sesifuba ngamasongo aso emasongweni e-efodi ngentambo eluhlaza okwesibhakabhaka, ukuze sibe phezu kwebhanti elelukwe ngobungcitshi, njalo isembatho sesifuba singakhumuki e-efodini.
Tsono umangirire mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi.
29 Njalo uAroni uzathwala amabizo abantwana bakoIsrayeli esembathweni sesifuba sokwahlulela phezu kwenhliziyo yakhe, nxa engena endaweni engcwele, kube yisikhumbuzo phambi kweNkosi njalonjalo.
“Pamene Aaroni akulowa kumalo opatulika azivala chovala chapachifuwa cha zoweruzira chija chimene chalembedwa mayina a ana a Israeli kuti Yehova awakumbukire nthawi zonse.
30 Uzafaka-ke esembathweni sesifuba sokwahlulela iUrimi leThumimi, njalo kube phezu kwenhliziyo kaAroni, nxa engena phambi kweNkosi; ngakho uAroni uzakuthwala ukwahlulelwa kwabantwana bakoIsrayeli phezu kwenhliziyo yakhe phambi kweNkosi njalonjalo.
Ndiponso uyike Urimu ndi Tumimu mu chovala chapachifuwa cha zoweruziracho, kuti zikhale pamtima pa Aaroni. Choncho Aaroniyo adzakhala akutenga nthawi zonse zida zomuthandizira kuweruza ana a Israeli pamene adzafika pamaso pa Yehova.
31 Uzakwenza ibhatshi lonke le-efodi ngokuluhlaza okwesibhakabhaka;
“Uyipangire efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo.
32 njalo sibe lesikhala sekhanda ngaphakathi kwaso, isikhala sibe lomphetho osizingelezeleyo, umsebenzi owelukiweyo, sibe njengesikhala sebhatshi lensimbi, ukuze singadabuki.
Mkanjowo ukhala ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo pakhale chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike.
33 Lemiphethweni yaso wenze amapomegranati ngokuluhlaza okwesibhakabhaka lokuyibubende lokubomvu, emiphethweni yaso osizingelezeleyo, lamabhera egolide phakathi kwawo asizingelezeleyo,
Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, upange mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira zokhala ndi maberu agolide pakati pake.
34 ibhera legolide lepomegranati, ibhera legolide lepomegranati, emiphethweni yebhatshi kuzingelezele.
Choncho pazikhala mphonje imodzi kenaka belu limodzi, kuzungulira mpendero wa mkanjo wonse.
35 UAroni kasembathele-ke ukukhonza, lokukhenceza kwaso kuzwakale lapho engena endaweni engcwele phambi kweNkosi, lalapho ephuma, ukuze angafi.
Aaroni azivala mkanjowo pamene akutumikira ngati wansembe. Kulira kwa maberu kuzimveka pamene akulowa mʼmalo opatulika pamaso pa Yehova ndiponso pamene akutuluka, kuti asafe.
36 Uzakwenza njalo incence ngegolide elicwengekileyo, ubaze kuyo ukubazwa kwendandatho elophawu: UBUNGCWELE ENKOSINI.
“Upange duwa lagolide wabwino kwambiri kukhala ngati chidindo ndipo uzokotepo mawu akuti, Cohoperekedwa kwa Yehova.
37 Uyifake phezu kwentambo eluhlaza okwesibhakabhaka, ukuze ibe phezu kweqhiye, ibe ngaphambili kweqhiye.
Ulimange ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira ya Aaroni, ndipo duwalo likhale kutsogolo kwa nduwirayo.
38 Izakuba sebunzini likaAroni, ukuze uAroni athwale ububi bezinto ezingcwele, abantwana bakoIsrayeli abazazingcwelisa, kuzo zonke izipho zabo ezingcwele; njalo izahlala isebunzini lakhe, ukuze bemukeleke phambi kweNkosi.
Lidzakhala pa mphumi ya Aaroni, motero iye adzasenza cholakwa chilichonse cha pa zopereka zilizonse zimene Aisraeli amazipatulira Yehova. Aaroni azivala chikwangwanichi pa mphumi pake nthawi zonse kuti Yehova alandire zopereka za anthu ake.
39 Uzakweluka njalo isigqoko ngelembu elicolekileyo kakhulu elilamabala, wenze leqhiye ngelembu elicolekileyo kakhulu, lebhanti, umsebenzi womfekethisi ngenalithi.
“Uluke mwinjiro wa nsalu yofewa yosalala ndiponso upange nduwira ya nsalu yofewa yosalala. Lamba wake akhale wolukidwa bwino ndi munthu waluso.
40 Wenzele-ke amadodana kaAroni izigqoko, uwenzele amabhanti, lezingowane uwenzele, kube ngokobukhosi lokuceca.
Upangirenso ana a Aaroni mwinjiro, malamba ndi nduwira kuti azioneka mwaulemu ndi molemekezeka.
41 Umgqokise zona uAroni umnewenu lamadodana akhe kanye laye, ubagcobe, ubehlukanise, ubangcwelise ukuze bangisebenzele njengabapristi.
Zovala zimenezi umuveke Aaroni, mʼbale wako ndi ana ake. Kenaka uwadzoze, uwapatse udindo ndi kuwapatula kuti anditumikire ngati ansembe anga.
42 Ubenzele labokabhudula bangaphansi belembu elicolekileyo okusibekela inyama yobunqunu, aqale ekhalweni afike emathangazini;
“Uwapangire akabudula a nsalu yofewa oyambira mʼchiwuno kulekeza mʼntchafu kuti asamaonetse maliseche.
43 njalo uAroni lamadodana akhe bawagqoke lapho bengena ethenteni lenhlangano kumbe lapho besondela elathini ukukhonza endaweni engcwele, hlezi bathwale ububi, bafe. Kuzakuba yisimiso esilaphakade kuye lakuyo inzalo yakhe emva kwakhe.
Aaroni ndi ana ake ayenera kuvala akabudulawo pamene akulowa mu tenti ya msonkhano kapena pamene akupita ku guwa lansembe kukatumikira malo oyera kuopa kuti angachimwe ndi kufa. “Ili likhale lamulo la nthawi zonse kwa Aaroni ndi zidzukulu zake.”