< U-Eksodusi 2 >
1 Kwasekusuka indoda yendlu yakoLevi, yathatha indodakazi yakoLevi.
Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo.
2 Owesifazana wasethatha isisu, wazala indodana; eseyibonile ukuthi inhle, wayifihla inyanga ezintathu.
Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu.
3 Kwathi engaselakuyifihla wayithathela isitsha semizi, wasibhada ngengcino langethara, wafaka umntwana kuso, wasibeka emihlangeni ekhunjini lomfula.
Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo.
4 Udadewabo wasezimisa khatshana ukuze azi okuzakwenziwa kuye.
Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.
5 Kwasekusehla indodakazi kaFaro ukuyageza emfuleni; lamantombazana ayo ahamba eceleni komfula. Isibonile isitsha phakathi kwemihlanga, yathuma incekukazi yayo yasithatha.
Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge.
6 Kwathi isivula, yabona umntwana, khangela-ke, umfanyana wakhala inyembezi. Yasimhawukela yathi: Lo ngomunye wabafana bamaHebheru.
Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”
7 Udadewabo wasesithi endodakazini kaFaro: Ngihambe yini ngiyekubizela umfazi omunyisayo kumaHebherukazi ukuze akumunyisele umfana?
Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”
8 Indodakazi kaFaro yasisithi kuye: Hamba. Intombi yasihamba, yabiza unina womfana.
Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo.
9 Indodakazi kaFaro yasisithi kuye: Thatha uhambe lalo umntwana, ungimunyisele yena; njalo mina ngizakupha iholo lakho. Owesifazana wasemthatha umntwana, wammunyisa.
Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera.
10 Umfana esekhulile, wamletha endodakazini kaFaro, wasesiba yindodana yayo. Yasisitha ibizo layo yathi nguMozisi, yathi: Ngoba ngamkhupha emanzini.
Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”
11 Kwasekusithi ngalezonsuku, uMozisi esekhulile, waphuma waya kubafowabo, wakhangela imithwalo yabo; futhi wabona umGibhithe etshaya umHebheru kubafowabo.
Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake.
12 Wathalaza ngapha langapha; esebonile ukuthi kakulamuntu, wamtshaya umGibhithe, wamfihla etshebetshebeni.
Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga.
13 Waphuma langosuku lwesibili, khangela-ke, amaHebheru amabili esilwa; wasesithi kowonileyo: Umtshayelani umakhelwane wakho?
Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”
14 Wasesithi: Ngubani okubeke ube yisiphathamandla lomahluleli phezu kwethu? Wena uzimisele ukungibulala yini njengalokho ubulele umGibhithe? UMozisi wasesesaba wathi: Isibili udaba luyaziwa.
Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”
15 Kwathi uFaro eseluzwile udaba, wadinga ukumbulala uMozisi. Kodwa uMozisi wabalekela ubuso bukaFaro, wahlala elizweni leMidiyani; wahlala emthonjeni.
Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime.
16 Njalo umpristi weMidiyani wayelamadodakazi ayisikhombisa; eza ukukha, agcwalisa imikolo ukunathisa umhlambi kayise.
Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo.
17 Kwasekufika abelusi, bawaxotsha; kodwa uMozisi wasukuma, wawasiza wanathisa umhlambi wawo.
Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.
18 Lapho efika kuRehuweli uyise, wathi: Kungani libuye masinyane kangaka lamuhla?
Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”
19 Asesithi: Indoda engumGibhithe isophulile esandleni sabelusi; futhi yasikhela lokusikhela, yanathisa umhlambi.
Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”
20 Wasesithi emadodakazini akhe: Kambe ingaphi? Kanti liyitshiyeleni indoda? Ibizeni, ukuze idle isinkwa.
Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”
21 UMozisi wasevuma ukuhlala lendoda; wasemnika uMozisi uZipora indodakazi yakhe.
Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake.
22 Wasezala indodana; wayitha ibizo layo uGereshoma, ngoba wathi: Ngangingowemzini elizweni lemzini.
Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”
23 Kwasekusithi emva kwalezinsuku ezinengi, inkosi yeGibhithe yafa. Labantwana bakoIsrayeli babubula ngenxa yobugqili, bakhala; lokukhala kwabo kwenyukela kuNkulunkulu ngenxa yobugqili.
Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu.
24 UNkulunkulu wasesizwa ukububula kwabo, uNkulunkulu wakhumbula isivumelwano sakhe loAbrahama, loIsaka, njalo loJakobe.
Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
25 UNkulunkulu wasebona abantwana bakoIsrayeli, uNkulunkulu wabazi.
Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.