< U-Eksodusi 15 >

1 Khona oMozisi labantwana bakoIsrayeli bahlabelela lelihubo eNkosini; bakhuluma bathi: Ngizahlabelela iNkosi, ngoba iphakeme isibili. Ibhiza lomgadi walo ikuphosele olwandle.
Ndipo Mose ndi Aisraeli anayimbira Yehova nyimbo iyi: “Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wakwezeka mʼchigonjetso. Kavalo ndi wokwera wake, Iye wawaponya mʼnyanja.
2 INkosi ingamandla lehubo lami, isibe kimi lusindiso, lo nguNkulunkulu wami, ngakho ngizamdumisa, unguNkulunkulu kababa, ngakho ngizamphakamisa.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; ndiye chipulumutso changa. Iye ndiye Mulungu wanga, ndipo ndidzamutamanda, Mulungu wa makolo anga, ine ndidzamukweza.
3 INkosi yindoda yempi, iNkosi libizo layo.
Yehova ndi wankhondo; Yehova ndilo dzina lake.
4 Inqola zikaFaro lebutho lakhe ikuphosele olwandle, lokhetho lwezinduna zakhe lwacwiliswa oLwandle oluBomvu.
Magaleta a Farao ndi asilikali ake ankhondo Iye wawaponya mʼnyanja. Akatswiri ankhondo amphamvu a Farao amizidwa mʼNyanja Yofiira.
5 Inziki zabasibekela; behlela ekujuleni njengelitshe.
Nyanja yakuya inawaphimba; Iwo anamira pansi ngati mwala.”
6 Isandla sakho sokunene, Nkosi, sidunyisiwe ngamandla; isandla sakho sokunene, Nkosi, sisiphahlazile isitha.
Yehova, dzanja lanu lamanja ndi laulemerero chifukwa cha mphamvu zake. Ndithu Yehova, dzanja lanu lamanja linaphwanya mdani.
7 Njalo ngobukhulu bokuphakama kwakho uchithile abakuvukelayo; uthumele ulaka lwakho oluvuthayo, lwabaqeda njengezidindi.
Ndi ulemerero wanu waukulu, munagonjetsa okutsutsani. Inu munatumiza mkwiyo wanu waukulu; ndipo unawapsereza ngati udzu.
8 Langokuvuthela kwamakhala akho amanzi abuthelelwa; impophoma zema njengenqumbi; izinziki zajiya enhliziyweni yolwandle.
Ndi mpweya wotuluka mʼmphuno mwanu madzi anawunjikana pamodzi. Nyanja yakuya ija inasanduka madzi owuma gwaa kufika pansi.
9 Isitha sathi: Ngizaxotsha, ngifice, ngehlukanise impango; isiloyiso sami sizasutha bona, ngizahwatsha inkemba yami, isandla sami sizababhubhisa.
Mdaniyo anati, “Ine ndidzawalondola, ndipo ndidzawagwira. Ndidzagawa chuma chawo; ndiye chokhumba changa chidzakwaniritsidwa. Ine ndidzasolola lupanga langa, ndi mkono wanga ndidzawawononga.”
10 Waphephetha ngomoya wakho, ulwandle lwabasibekela; batshona njengomnuso emanzini alamandla.
Koma Inu munawuzira mphepo yanu, ndipo nyanja inawaphimba. Iwo anamira ngati chitsulo mʼmadzi amphamvu.
11 Ngubani onjengawe, Nkosi, phakathi kwabonkulunkulu? Ngubani onjengawe olodumo ebungcweleni, owesabekayo ezindunyisweni, esenza izimangaliso?
Ndithu Yehova, pakati pa milungu, ndani afanana nanu? Inu amene muli woyera, ndiponso wotamandika wolemekezeka, chifukwa cha ntchito zanu, zazikulu ndi zodabwitsa?
12 Welulile isandla sakho sokunene, umhlaba wabaginya.
Munatambasula dzanja lanu lamanja ndipo dziko linawameza.
13 Ukhokhele ngomusa wakho lesisizwe osihlengileyo; wasihola ngamandla akho endaweni yakho yokuhlala yobungcwele bakho.
Ndi chikondi chanu chosasinthika mudzatsogolera anthu amene munawawombola. Ndi mphamvu zanu munawatsogolera ku malo anu woyera.
14 Izizwe zizwile, ziyathuthumela; umhelo ubabambile abahlali beFilisti.
Anthu amitundu ina anamva za mbiriyi ndipo ananjenjemera ndi mantha, mantha woopsa agwira anthu a dziko la Filisiti.
15 Ngalesosikhathi izinduna zeEdoma zizasanganiseka, iziphathamandla zakoMowabi, ukuthuthumela kwazibamba, bonke abahlali beKhanani bazancibilika.
Tsopano mafumu a ku Edomu agwidwa ndi mantha aakulu, otsogolera a dziko la Mowabu akunjenjemera ndi mantha, ndipo anthu a ku Kanaani asungunuka ndi mantha.
16 Ukwethuka lokwesaba kuzabehlela; ngobukhulu bengalo yakho bazathula njengelitshe, size sichaphe isizwe sakho, Nkosi, size sichaphe isizwe osithengileyo.
Onse agwidwa ndi mantha woopsa. Popeza anaona mphamvu zanu zazikulu, iwo ayima chilili ngati mwala mpaka anthu anu, Inu Yehova atadutsa; inde mpaka atadutsa anthu amene munawagula.
17 Uzabangenisa, ubahlanyele entabeni yelifa lakho, indawo oyenzileyo, Nkosi, ukuthi uhlale kuyo, indawo engcwele eziyimisileyo izandla zakho, Nkosi.
Inu mudzawalowetsa ndi kuwakhazikitsa pa phiri lanu. Pa malo pamene Inu Yehova munawapanga kuti muzikhalapo; malo wopatulika amene Inu Ambuye munawakonza ndi manja anu.
18 INkosi izabusa kuze kube phakade lanininini.
“Yehova adzalamula mpaka muyaya.”
19 Ngoba ibhiza likaFaro langena olwandle lenqola yakhe labagadi bakhe bamabhiza, iNkosi yasibuyisela amanzi olwandle phezu kwabo, kodwa abantwana bakoIsrayeli bahamba emhlabathini owomileyo phakathi kolwandle.
Akavalo a Farao, magaleta ndi oyendetsa akavalo atalowa mʼnyanja, Yehova anawabwezera madziwo mʼnyanja ndi kuwamiza, koma Aisraeli anawoloka nyanjayo powuma.
20 UMiriyamu umprofethikazi, udadewabo kaAroni, wasethatha isigujana esandleni sakhe; bonke abesifazana basebephuma ngemva kwakhe, lezigujana lemigido.
Ndipo Miriamu mneneri wamkazi, mlongo wa Aaroni anatenga zoyimbira ndipo akazi onse anamutsatira pambuyo, akuyimba ndi zoyimbira ndi kuvina.
21 UMiriyamu wasebaphendula wathi: Hlabelelani iNkosi, ngoba inqobe ngodumo. Ibhiza lomgadi walo ikuphosele olwandle.
Miriamu anawayimbira nyimbo iyi: “Imbirani Yehova, chifukwa iye wapambana. Kavalo ndi wokwerapo wake Iye wawamiza mʼnyanja.”
22 UMozisi wasemkhokhela uIsrayeli eqhubeka esuka eLwandle oluBomvu, baphuma baya enkangala yeShuri; bahamba insuku ezintathu enkangala, kabatholanga manzi.
Ndipo Mose anatsogolera Israeli kuchoka ku nyanja yofiira ndi kupita ku chipululu cha Suri. Anayenda mʼchipululu masiku atatu wosapeza madzi.
23 Kwathi lapho befika eMara babengelakuwanatha amanzi eMara, ngoba ayebaba; ngakho ibizo layo lathiwa yiMara.
Ndipo anafika ku Mara. Koma sanathe kumwa madzi akumeneko chifukwa anali owawa. (Ndi chifukwa chake malowo amatchedwa Mara).
24 Abantu basebekhonona bemelene loMozisi besithi: Sizanathani?
Tsono anthu aja anadandaulira Mose ndi kumufunsa kuti, “Kodi tikumwa chiyani?”
25 Wasekhala eNkosini. INkosi yasimtshengisa isihlahla, asiphosela emanzini, amanzi asesiba mnandi. Yabamisela khona isimiso lesimiselo, lalapho yabalinga,
Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, ndipo Yehova anamuonetsa kamtengo. Iye anakaponya mʼmadzimo ndipo madzi anakhala abwino. Kumeneko Yehova anawayikira lamulo ndi maweruziro. Kumenekonso Yehova anawayesa.
26 yasisithi: Uba lilalela lokulalela ilizwi leNkosi uNkulunkulu wenu, lenze okulungileyo emehlweni ayo, libeke indlebe emilayweni yayo, ligcine zonke izimiso zayo, kangiyikwehlisela phezu kwenu lasinye sezifo engazehlisela phezu kwamaGibhithe; ngoba ngiyiNkosi elelaphayo.
Yehova anati, “Ngati inu mudzamvetsa bwino mawu anga, kuchita zolungama, kumvera malamulo anga ndi kusamalitsa zimene ndikukuwuzani ndiye kuti Ine sindidzayika pa inu matenda amene ndinayika pa anthu a ku Igupto popeza ndine Yehova amene ndimakuchiritsani.”
27 Basebefika eElimi lapho okwakukhona imithombo elitshumi lambili yamanzi, lezihlahla zelala ezingamatshumi ayisikhombisa; basebemisa inkamba khona emanzini.
Kenaka anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa makumi asanu ndi awiri, ndipo anamanga misasa yawo kumeneko pafupi ndi madzi.

< U-Eksodusi 15 >