< UDutheronomi 31 >
1 UMozisi wasehamba wakhuluma lamazwi kuIsrayeli wonke,
Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
2 wathi kubo: Ngileminyaka elikhulu lamatshumi amabili lamuhla; kangiselamandla okuphuma lokungena. LeNkosi yathi kimi: Kawuyikuyichapha le iJordani.
“Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
3 INkosi uNkulunkulu wakho, yona izachapha phambi kwakho, yona izachitha lezizizwe zisuke phambi kwakho, ukuze udle ilifa lazo. UJoshuwa, yena uzachapha phambi kwakho, njengokutsho kweNkosi.
Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
4 LeNkosi izakwenza kuzo njengokwenza kwayo kuSihoni lakuOgi, amakhosi amaAmori, lelizweni lawo, ewachithileyo.
Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
5 INkosi izazinikela-ke phambi kwenu, ukuze lenze kuzo njengokwemilayo yonke engililaye yona.
Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
6 Qinani, lime isibindi, lingesabi, lingatshaywa luvalo ngenxa yazo; ngoba iNkosi uNkulunkulu wakho, yiyo ehamba lawe; kayiyikukulahla, kayiyikukudela.
Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
7 UMozisi wasembiza uJoshuwa, wathi kuye phambi kwamehlo kaIsrayeli wonke: Qina, ume isibindi; ngoba wena uzangena lalababantu elizweni iNkosi eyalifungela oyise ukubanika lona; uzabenza badle ilifa lalo.
Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
8 Njalo iNkosi, yiyo ehamba phambi kwakho; yona izakuba lawe, ingakulahli, ingakudeli; ungesabi, ungakhathazeki.
Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
9 UMozisi wasewubhala lumlayo, wawunika abapristi, amadodana kaLevi, ababethwala umtshokotsho wesivumelwano seNkosi, lakubo bonke abadala bakoIsrayeli.
Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
10 UMozisi wasebalaya esithi: Ekupheleni kweminyaka eyisikhombisa, ngesikhathi esimisiweyo somnyaka wenkululeko, emkhosini wamadumba,
Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
11 lapho uIsrayeli wonke esefike ukubonakala phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho endaweni ezayikhetha, uwubale lumlayo phambi kukaIsrayeli wonke endlebeni zabo.
pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
12 Buthanisa abantu, abesilisa labesifazana labantwana, lowemzini wakho ophakathi kwamasango akho, ukuze bezwe, lokuze bafunde, bayesabe iNkosi uNkulunkulu wenu, bagcine ukwenza wonke amazwi alumlayo.
Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
13 Labantwana babo abangaziyo bezwe, bafunde ukuyesaba iNkosi uNkulunkulu wenu, zonke izinsuku zokuphila kwenu, elizweni elichapha iJordani lisiya kulo ukudla ilifa lalo.
Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
14 INkosi yasisithi kuMozisi: Khangela, insuku zakho zokufa sezisondele; biza uJoshuwa, zimiseni ethenteni lenhlangano ukuze ngimlaye. UMozisi loJoshuwa bahamba-ke, bazimisa ethenteni lenhlangano.
Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
15 INkosi yasibonakala ethenteni ensikeni yeyezi; lensika yeyezi yema phezu komnyango wethente.
Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
16 INkosi yasisithi kuMozisi: Khangela, uzalala laboyihlo; lalababantu bazasukuma baphinge ngokulandela onkulunkulu bezizweni belizwe, lapho abaya khona phakathi kwabo, bangitshiye, bephule isivumelwano sami engisenze labo.
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
17 Lentukuthelo yami izabavuthela ngalolosuku, ngibatshiye, ngibafihlele ubuso bami, ukuze babe yikudla, behlelwe ngokubi okunengi lezinhlupheko, baze bathi ngalolosuku: Angithi lobububi busehlele ngoba uNkulunkulu wethu kakho phakathi kwethu?
Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
18 Lami ngizafihla lokufihla ubuso bami ngalolosuku ngenxa yobubi bonke ababenzileyo, ngoba bephendukele kwabanye onkulunkulu.
Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
19 Ngakho-ke zibhaleleni lingoma, uyifundise abantwana bakoIsrayeli; uyifake emlonyeni wabo ukuze lingoma ibe yibufakazi kimi obumelene labantwana bakoIsrayeli.
“Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
20 Lapho sengibangenisile elizweni engalifungela oyise, eligeleza uchago loluju, sebedlile basutha, bazimuka, bazaphendukela kwabanye onkulunkulu, babakhonze, bangidelele, bephule isivumelwano sami.
Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
21 Kuzakuthi-ke, nxa sebehlelwe ngokubi okunengi lezinhlupheko, lingoma izaphendula phambi kobuso babo ibe yibufakazi; ngoba kayiyikukhohlakala emlonyeni wenzalo yabo. Ngoba ngiyawazi amacebo abo abawenzayo lamuhla, ngingakabangenisi elizweni engifunge ngalo.
Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
22 UMozisi wasebhala lingoma ngalolosuku, wayifundisa abantwana bakoIsrayeli.
Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
23 Yasilaya uJoshuwa indodana kaNuni yathi: Qina, ume isibindi, ngoba wena uzabangenisa abantwana bakoIsrayeli elizweni engabafungela lona; lami ngizakuba lawe.
Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
24 Kwasekusithi uMozisi eseqedile ukubhala amazwi alumlayo egwalweni, aze aphela,
Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
25 uMozisi walaya amaLevi ayethwala umtshokotsho wesivumelwano seNkosi esithi:
analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
26 Thathani lolugwalo lomlayo, lilubeke eceleni komtshokotsho wesivumelwano seNkosi uNkulunkulu wenu, ukuze lube khona, kube yibufakazi obumelene lawe.
“Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
27 Ngoba mina ngiyazi umvukela wakho, lentamo yakho elukhuni; khangelani, ngisaphila lani lamuhla, belingabavukeli beNkosi; pho, kangakanani emva kokufa kwami?
Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
28 Buthanisani kimi bonke abadala bezizwe zenu lenduna zenu ukuze ngikhulume lamazwi endlebeni zabo, ngibize amazulu lomhlaba ukuba ngabafakazi bamelane labo.
Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
29 Ngoba ngiyazi ukuthi emva kokufa kwami lizakona lokona, liphambuke endleleni engililaye yona; lizakwehlelwa ngokubi ngensuku ezizayo, ngoba lizakwenza okubi emehlweni eNkosi, liyithukuthelise ngomsebenzi wezandla zenu.
Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
30 UMozisi wasekhuluma amazwi alingoma endlebeni zebandla lonke lakoIsrayeli, aze aphela.
Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva: