< UDutheronomi 2 >
1 Sasesiphenduka, sasuka saya enkangala, indlela yoLwandle oluBomvu, njengokutsho kweNkosi kimi; njalo sayibhoda intaba yeSeyiri insuku ezinengi.
Kenaka tinabwerera ndi kuyamba ulendo wolowera ku chipululu motsatira njira ya ku Nyanja Yofiira, monga mmene Yehova anatilamulira. Kwa nthawi yayitali tinayendayenda cha ku dziko la mapiri la Seiri.
2 INkosi yasikhuluma kimi isithi:
Ndipo Yehova anati kwa ine,
3 Selibhode intaba le okweneleyo; phendukelani lina enyakatho.
“Mwazungulira mokwanira dziko la mapiri, tsopano tembenukirani kumpoto.
4 Balaye-ke abantu usithi: Lidabula umngcele wabafowenu, abantwana bakaEsawu abahlala eSeyiri. Njalo bazalesaba, ngakho lizinanzelele kakhulu,
Apatse anthu malamulo awa: ‘Muli pafupi kudutsa mʼchigawo cha abale anu adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Iwowa adzachita nanu mantha koma musamale kwambiri.
5 lingalwi labo; ngoba kangiyikulinika okwelizwe labo, lelingangokunyathela kwangaphansi konyawo, ngoba ngimnikile uEsawu intaba yeSeyiri ibe yilifa.
Musayambane nawo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo ngakhale poti mungoyika phazi. Ndamupatsa Esau dziko lamapiri la Seiri kuti likhale lakelake.
6 Lizathenga ukudla kubo ngemali ukuze lidle, lithenge kubo lamanzi ngemali ukuze linathe.
Inu muyenera kuwalipira ndi siliva pa chakudya chimene mudye ndi madzi amene mumwe.’”
7 Ngoba iNkosi uNkulunkulu wakho ikubusisile emsebenzini wonke wesandla sakho; iyazi ukuhamba kwakho kulinkangala enkulu. Le iminyaka engamatshumi amane iNkosi uNkulunkulu wakho ibilawe, kawuswelanga lutho.
Yehova Mulungu wanu wakudalitsani mʼntchito zonse za manja anu. Iye wakuyangʼanirani pa ulendo wanu wodutsa mʼchipululu chachikulu. Yehova Mulungu wanu wakhala nanu mʼzaka makumi anayi, ndipo simunasowe kalikonse.
8 Uba sisedlula sisuka kubafowethu, abantwana bakaEsawu abahlala eSeyiri, ngendlela yegceke sisuke eElathi njalo sisuka eEziyoni-Geberi, saphenduka, sadlula ngendlela yenkangala yakoMowabi.
Choncho tinapitiriza ulendo modutsa abale athu, adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Tinapatukira njira ya ku Araba imene imachokera ku Elati ndi Ezioni Geberi ndipo tinayenda njira ya ku chipululu cha Mowabu.
9 INkosi yasisithi kimi: Ungahlukuluzi uMowabi, ungalwi labo empini; ngoba kangiyikukunika okwelizwe labo kube yilifa, ngoba ngibanikile abantwana bakaLothi iAri ibe yilifa.
Ndipo Yehova anati kwa ine, “Musawavutitse Amowabu kapena kuwaputa kuti muchite nawo nkhondo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo. Ndinapereka Ari kwa adzukulu a Loti ngati chuma chawo.”
10 Kwakuhlala khona endulo amaEmi, abantu abakhulu, labanengi, labade, njengamaAnaki;
(Aemi, anthu amphamvu ndi ochuluka komanso ataliatali ngati Aanaki amakhala kumeneko.
11 babebalwa njengeziqhwaga labo njengamaAnaki, kodwa amaMowabi ababiza ngokuthi ngamaEmi.
Ngati Aanaki, nawonso ankawayesa kuti anali Arefai, koma Amowabu ankawatcha iwo Aemi.
12 LamaHori ayehlala eSeyiri endulo, kodwa abantwana bakaEsawu bawakhupha emfuyweni yabo, bawachitha phambi kwabo, bahlala endaweni yawo, njengokwenza kukaIsrayeli elizweni lelifa lakhe, iNkosi eyabanika lona.
Ahori amakhala ku Seiri koma adzukulu a Esau anawapirikitsa. Iwo anawononga Ahori pamaso pawo nawakhalira pamalo pawo monga Aisraeli anachitira mʼdziko limene Yehova anawapatsa ngati chuma chawo).
13 Khathesi, sukumani lina lichaphe isifula iZeredi. Ngakho sachapha isifula iZeredi.
Ndipo Yehova anati, “Tsopano nyamukani ndipo muwoloke Chigwa cha Zeredi.” Choncho tinawoloka chigwacho.
14 Lensuku esahamba ngazo sisuka eKadeshi-Bhaneya saze sachapha isifula iZeredi zaziyiminyaka engamatshumi amathathu lesificaminwembili, kwaze kwaphela isizukulwana sonke samadoda empi sisuka phakathi kwenkamba, njengokufunga kweNkosi kuwo.
Panapita zaka 38 kuchokera pa nthawi imene tinachoka ku Kadesi Barinea mpaka pamene tinawoloka Chigwa cha Zeredi. Pa nthawi imeneyi nʼkuti mʼbado wonse wa anthu ankhondowo utawonongeka ku msasa monga Yehova anawalumbirira.
15 Ngoba isibili isandla seNkosi sasimelene lawo, ukuwachitha esuka phakathi kwenkamba, aze aphela.
Dzanja la Yehova linatsutsana nawo mpaka wonse anathera ku msasa.
16 Kwasekusithi lapho wonke amadoda empi esephelile esifa esuka phakathi kwabantu,
Tsono atafa munthu wotsiriza mwa anthu ankhondowo,
17 INkosi yasikhuluma kimi isithi:
Yehova anati kwa ine,
18 Lamuhla uzakwedlula iAri, umngcele wakoMowabi,
“Lero mudutsa malire a Mowabu ku Ari podzera ku Ari.
19 lapho ususondele maqondana labantwana bakoAmoni, ungabahlukuluzi, ungalwi labo, ngoba kangiyikukunika okwelizwe labantwana bakoAmoni kube yilifa, ngoba ngilinike abantwana bakaLothi libe yilifa.
Mukafika kwa Aamoni, musawavutitse kapena kuwaputa, popeza sindidzakupatsani gawo lililonse la dziko la Aamoni. Ine ndalipereka dzikoli ngati chuma kwa adzukulu a Loti.”
20 Lalelo labalwa njengelizwe leziqhwaga. Iziqhwaga zahlala kulo endulo, kodwa amaAmoni bazibiza ngokuthi ngamaZamuzumu;
(Ilinso ankaliyesa dziko la Arefai amene ankakhala kumeneko. Koma Aamoni ankawatcha iwo Azamuzumi.
21 abantu abakhulu, labanengi, labade, njengamaAnaki; kodwa iNkosi yabachitha phambi kwabo, babakhupha emfuyweni yabo, bahlala endaweni yabo,
Iwo anali anthu amphamvu ndiponso ochuluka, ataliatali ngati Aanaki. Yehova anawawononga ndi kuwachotsa pamaso pa Aamoni, amene anawapirikitsa nawakhalira pa malo pawo.
22 njengalokho eyakwenzela abantwana bakaEsawu, ababehlala eSeyiri, lapho yawachitha amaHori esuka phambi kwabo, bawakhupha emfuyweni yabo, bahlala endaweni yawo kuze kube lamuhla.
Yehova anachitanso chimodzimodzi ndi adzukulu a Esau omwe anakhazikika ku Seiri atawononga Ahori powachotsa pamaso pawo. Iwo anawapirikitsa Ahoriwo ndi kuwakhalira pamalo pawo mpaka lero.
23 LamaAvi, ayehlala eHazerimi kuze kube seGaza; amaKafitori, aphuma eKafitori, awachitha, ahlala endaweni yawo.
Ndipo za Aavi omwe ankakhala mʼmidzi yofika mpaka ku Gaza, anagonjetsedwa ndi Akafitori wochokera ku Akafitori nakhala pamalo pawo).
24 Sukumani, lisuke lichaphe isifula iArinoni. Bona, nginikele esandleni sakho uSihoni, inkosi yeHeshiboni, umAmori, lelizwe lakhe; qala ukudla ilifa lalo, ulwe laye empini.
“Tsopano nyamukani, muwoloke khwawa la Arinoni. Taona ndapereka mʼmanja mwako Sihoni Mwamori mfumu ya Hesiboni ndi dziko lake lonse. Yambapo kutenga chuma chake ndi kumenyana naye nkhondo.
25 Lamuhla ngizaqalisa ukufaka uvalo ngawe lokwesabeka kwakho phezu kobuso bezizwe, ngaphansi kwamazulu wonke, ezizakuzwa umbiko ngawe, zithuthumele, ziqhaqhazele ngenxa yakho.
Lero lomwe lino ndidzayamba kuyika chiopsezo ndi mantha pa mitundu yonse pansi pa thambo kuti akuope. Iwowo adzamva zambiri yako ndipo adzanjenjemera ndi kuwawidwa mtima chifukwa cha iwe.”
26 Ngasengithuma izithunywa zisuka enkangala yeKedemothi kuSihoni inkosi yeHeshiboni, zilamazwi okuthula, zisithi:
Ine ndinatuma amithenga kuchokera ku chipululu cha Kedemoti kupita kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni kukanena mawu ofuna mtendere ndipo ndinati,
27 Ake ngidabule elizweni lakho; ngizahamba ngomgwaqo kuphela, ngingaphambukeli ngakwesokunene loba ngakwesokhohlo.
“Tiloleni tidutse mʼdziko mwanu. Ife tidzangodutsa ndi msewu waukulu, ndipo sitidzapatukira kumanja kapena kumanzere.
28 Uzangithengisela ukudla ngemali ukuze ngidle, ungiphe amanzi ngemali ukuze nginathe; kuphela ngizadabula ngenyawo zami,
Mutigulitse chakudya kuti tidye ndi madzi kuti timwe pa mtengo wa siliva. Mungotilola kuti tidutse, tikuyenda pansi
29 njengalokhu abantwana bakaEsawu abahlala eSeyiri lamaMowabi ahlala eAri benza kimi, ngize ngichaphe iJordani, ngingene elizweni iNkosi uNkulunkulu wethu esinika lona.
monga mmene anatichitira adzukulu a Esau okhala ku Seiri ndi Amowabu okhala ku Ari mpaka titawoloka Yorodani kufika ku dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa.”
30 Kodwa uSihoni inkosi yeHeshiboni kasivumelanga ukuthi sidlule kuye; ngoba iNkosi uNkulunkulu wakho yenza umoya wakhe waba lukhuni, yenza lenhliziyo yakhe yaba lenkani, ukuze imnikele esandleni sakho, njengalamuhla.
Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanalole kuti tidutse. Popeza Yehova Mulungu wanu analimbitsa mzimu wake, nawumitsa mtima wake kuti amupereke mʼmanja mwanu monga wachitira lero lino.
31 INkosi yathi kimi: Bona, sengiqalisile ukunikela phambi kwakho uSihoni lelizwe lakhe; qalisa ukudla ilifa, ukuze udle ilifa lelizwe lakhe.
Yehova anati kwa ine, “Taona ndayamba kumupereka Sihoni ndi dziko lake kwa iwe. Tsopano yamba kugonjetsa ndi kulanda dziko lake.”
32 Kwasekuphuma uSihoni ukumelana lathi, yena labantu bakhe bonke, ukulwa eJahazi.
Sihoni ndi ankhondo ake atabwera kudzakumana nafe mwankhondo pa Yahazi,
33 INkosi uNkulunkulu wethu yasimnikela phambi kwethu; sasesimtshaya lamadodana akhe labantu bakhe bonke.
Yehova Mulungu anamupereka iye kwa ife ndipo tinankantha, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse lankhondo.
34 Ngalesosikhathi sasesithumba yonke imizi yakhe, satshabalalisa wonke umuzi, abesilisa labesifazana labantwanyana; kasitshiyanga insali;
Pa nthawi imeneyi tinamulanda mizinda yake yonse ndi kuyiwononga kwathunthu, amuna, akazi ndi ana. Palibe amene anapulumuka.
35 sazithumbela izifuyo kuphela, lempango yemizi esayithumbayo.
Koma ziweto ndi zinthu zonse zimene tinalanda mʼmizinda imene tinagonjetsayo, tinazitenga kukhala zathu.
36 Kusukela eAroweri esekhunjini lwesifula iArinoni, lomuzi osesifuleni, kuze kube seGileyadi kwakungekho muzi owawuphakeme kakhulu kithi. INkosi uNkulunkulu wethu yayinikela yonke phambi kwethu.
Kuchokera ku Aroeri mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni ndi ku mzinda wa ku mtsinjeko mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe ndi mzinda ndi umodzi omwe umene unatikanika kuwugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anatipatsa onsewo.
37 Kuphela kawusondelanga elizweni labantwana bakoAmoni, endaweni yonke yesifula iJaboki, lemizini esezintabeni, lakukuphi iNkosi uNkulunkulu wethu esenqabela khona.
Molingana ndi lamulo la Yehova Mulungu wathu, simunalowerere dziko lililonse la Aamoni, ngakhale dera lonse la ku mtsinje wa Yaboki kapena dera lozungulira dera la ku mizinda ya ku mapiri.