< UDutheronomi 17 >
1 Ungahlabeli iNkosi uNkulunkulu wakho inkabi kumbe imvu okukuyo isici, loba yiyiphi into embi, ngoba kuyisinengiso eNkosini uNkulunkulu wakho.
Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.
2 Uba kutholakala phakathi kwakho, loba phakathi kwaliphi lamasango akho, iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika wona, owesilisa loba owesifazana owenza okubi emehlweni eNkosi uNkulunkulu wakho, ngokweqa isivumelwano sayo,
Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake,
3 abesesiyakhonza abanye onkulunkulu, abakhothamele, loba ilanga kumbe inyanga, kumbe enye yebutho lamazulu, engingakulayanga,
ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba,
4 ube usukubikelwa, ukuzwe, uzakubuzisisa, khangela-ke, kuliqiniso, indaba iqinisekile, lesosinengiso senziwe koIsrayeli,
ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli,
5 uzayikhupha leyondoda kumbe lowo owesifazana, abenze leyonto embi, emasangweni akho, leyondoda kumbe lowo owesifazana, ubakhande ngamatshe baze bafe.
mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala.
6 Ngomlomo wabafakazi ababili loba wabafakazi abathathu ofanele ukufa uzabulawa; kayikubulawa ngomlomo womfakazi oyedwa.
Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi.
7 Isandla sabafakazi sizakuba ngesokuqala phezu kwakhe ukumbulala, lemva kwalokho isandla sabo bonke abantu. Ngalokhu uzakhupha ububi phakathi kwakho.
Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
8 Uba kulodaba olulukhuni kakhulu kuwe ekwahluleleni, phakathi kwegazi legazi, phakathi kwesahlulelo lesahlulelo, laphakathi kokutshaya lokutshaya, indaba zokuphikisana emasangweni akho, khona uzasukuma uye endaweni iNkosi uNkulunkulu wakho ezayikhetha,
Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
9 uze kubapristi abangamaLevi lakumahluleli ozakuba ekhona ngalezonsuku, uzabuza; babesebekutshela isinqumo sesahlulelo.
Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita.
10 Njalo uzakwenza njengokwesinqumo abazakutshela sona kuleyondawo iNkosi ezayikhetha; njalo unanzelele ukwenza njengakho konke abazakufundisa khona.
Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo.
11 Njengokomthetho abazakufundisa wona, lanjengokwesahlulelo abazakutshela sona, uzakwenza. Kawuyikuphambuka kusinqumo abazakutshela sona, uye ngakwesokunene kumbe ngakwesokhohlo.
Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere.
12 Lendoda eyenza ngokuziqhenya ukuze ingalaleli umpristi omi ukukhonza khona iNkosi uNkulunkulu wakho, kumbe umahluleli, leyondoda izakufa. Ngalokhu uzakhupha ububi koIsrayeli.
Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli.
13 Njalo bonke abantu bazakuzwa, besabe, bangaphindi ukuziqhenya.
Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.
14 Lapho usufikile elizweni iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona ukuthi udle ilifa lalo, uhlale kilo, ubususithi: Ngizazimisela inkosi njengazo zonke izizwe ezingizingelezeleyo;
Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,”
15 umbeke lokumbeka abe yinkosi phezu kwakho, yena iNkosi uNkulunkulu wakho ezamkhetha. Evela phakathi kwabafowenu umbeke abe yinkosi phezu kwakho; kawulakumbeka owezizweni phezu kwakho ongesumfowenu.
mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli.
16 Kodwa angazandiseli amabhiza, njalo angababuyiseli abantu eGibhithe ukuze andise amabhiza, ngoba iNkosi ithe kini: Kalisayikubuyela futhi ngaleyondlela.
Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.”
17 Futhi angazandiseli abafazi, ukuze inhliziyo yakhe ingaphambuki; njalo angazandiseli kakhulu isiliva legolide.
Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.
18 Kuzakuthi esehlala esihlalweni sobukhosi sombuso wakhe, uzazibhalela impinda yalumlayo egwalweni, okuvela kulokho okuphambi kwabapristi abangamaLevi.
Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi.
19 Njalo luzakuba laye, njalo abale kulo insuku zonke zempilo yakhe, ukuze afunde ukuyesaba iNkosi uNkulunkulu wakhe, agcine wonke amazwi alumlayo lezimiso lezi, akwenze,
Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa.
20 ukuze inhliziyo yakhe ingaziphakamisi phezu kwabafowabo, lokuze angaphambuki emthethweni aye ngakwesokunene loba ngakwesokhohlo, ukuze elule izinsuku embusweni wakhe, yena labantwana bakhe, phakathi kukaIsrayeli.
Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.