< UDutheronomi 14 >

1 Lingabantwana beNkosi uNkulunkulu wenu. Kaliyikuzisika, lingenzi impabanga phakathi laphakathi kwamehlo enu ngenxa yabafileyo.
Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
2 Ngoba uyisizwe esingcwele eNkosini uNkulunkulu wakho; leNkosi ikukhethile ukuthi ube yisizwe esikhethekileyo kuyo, ngaphezu kwezizwe zonke ezisebusweni bomhlaba.
pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
3 Ungadli loba yikuphi okunengekayo.
Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
4 Yilezi inyamazana elingazidla: Inkabi, imvu, lembuzi,
Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
5 indluzele, lomziki, lomziki olempondo ezilembaxambaxa, lembuzi yeganga, lomtshwayeli, lenkabi yeganga, legogo,
mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
6 layo yonke inyamazana edabula isondo, edabula okudabukileyo kube zinklagu ezimbili, eyetshisayo phakathi kwezinyamazana; leyo lingayidla.
Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
7 Kodwa lezi kaliyikuzidla kuzo ezetshisayo, lakuzo ezidabula isondo elidabukileyo: Ikamela lomvundla lembila, ngoba ziyetshisa kodwa kazidabulanga isondo; zingcolile kini.
Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
8 Lengulube, ngoba idabula isondo kodwa kayetshisi; ingcolile kini. Lingadli okwenyama yazo, lingathinti izidumbu zazo.
Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
9 Lezi lingazidla kuzo zonke ezisemanzini: Zonke ezilempiko lamaxolo lingazidla.
Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
10 Kodwa loba yikuphi okungelampiko lamaxolo lingakudli; kungcolile kini.
Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
11 Zonke inyoni ezihlambulukileyo lingazidla.
Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
12 Kodwa yilezi elingayikudla kuzo: Ukhozi lelinqe lengqungqulu edla inhlanzi,
Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
13 lomzwazwa, lohelwane, lelinqe ngohlobo lwalo,
nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
14 lalo lonke iwabayi ngohlobo lwalo,
mtundu uliwonse wa khwangwala,
15 lesikhova, lomandukulo, lenkanku, lokhozi ngohlobo lwalo,
kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
16 isikhova esincinyane, lesikhova esikhulu, lesikhova esimhlophe,
kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
17 lewunkwe, lelinqe elikhulu, letshayamanzi,
tsekwe, vuwo, dembo,
18 lengabuzane, lehemu ngohlobo lwalo, lemvenduna, lolulwane.
indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
19 Lazo zonke izibungu ezilempiko zingcolile kini; kazingadliwa.
Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
20 Zonke izinyoni ezihlambulukileyo lingazidla.
Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
21 Lingabokudla langcuba; ungayinika owemzini ophakathi kwamasango akho ukuthi ayidle, loba uyithengise kowezizwe; ngoba uyisizwe esingcwele eNkosini uNkulunkulu wakho. Ungapheki izinyane lembuzi ngochago lukanina.
Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
22 Uzanikela ngoqotho okwetshumi kwesithelo sonke senhlanyelo yakho, insimu ekuthelayo iminyaka ngeminyaka.
Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
23 Njalo uzakudla phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho, endaweni ezayikhetha ukuthi ibeke ibizo layo khona, okwetshumi kwamabele akho, okwewayini lakho elitsha, lokwamafutha akho, lamazibulo enkomo zakho lawezimvu zakho, ukuze ufunde ukuyesaba iNkosi uNkulunkulu wakho insuku zonke.
Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
24 Uba-ke indlela inde kakhulu kuwe, uze wehluleke ukukuthwala, ngoba ikhatshana kakhulu lawe indawo iNkosi uNkulunkulu wakho ezayikhetha ukuthi ibeke ibizo layo khona, lapho iNkosi uNkulunkulu wakho ikubusisile,
Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
25 uzakuguqula-ke kube yimali, ubophele imali esandleni sakho, uye endaweni iNkosi uNkulunkulu wakho ezayikhetha,
ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
26 uthenge ngaleyomali loba kuyini umphefumulo wakho okufisayo, izinkabi loba izimvu loba iwayini loba okunathwayo okulamandla, loba kuyini umphefumulo wakho okufisayo; udle khona phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho, uthabe wena lendlu yakho.
Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
27 LomLevi ophakathi kwamasango akho, ungamdeli, ngoba kalasabelo lelifa kanye lawe.
Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
28 Ekupheleni kweminyaka emithathu uzakhupha konke okwetshumi kwezithelo zakho ngalowomnyaka, ukugcine phakathi kwamasango akho.
Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
29 LomLevi, lokhu engelasabelo lelifa kanye lawe, lowemzini, lentandane, lomfelokazi, abaphakathi kwamasango akho, bazakuza, badle, basuthe, ukuze iNkosi uNkulunkulu wakho ikubusise emsebenzini wonke wesandla sakho owenzayo.
kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.

< UDutheronomi 14 >