< UDanyeli 8 >

1 Ngomnyaka wesithathu wokubusa kwenkosi uBelishazari kwabonakala umbono kimi, mina Daniyeli, emva kwalowo owabonakala kimi kuqala.
Chaka chachitatu cha ulamuliro wa mfumu Belisazara, Ine Danieli, ndinaonanso masomphenya, ena atatha amene anandionekera poyamba.
2 Ngabona-ke embonweni; kwasekusithi, sengibonile, ngiseShushani isigodlo, esisesabelweni seElamu; ngasengibona embonweni, mina ngangingasemfuleni iUlayi.
Ndinaona mʼmasomphenya kuti ndinali mu mzinda wotetezedwa wa Susa mʼchigawo cha Elamu. Mʼmasomphenyawo ndinaona nditayima pafupi ndi mtsinje wa Ulai.
3 Ngasengiphakamisa amehlo ami, ngabona, khangela-ke, kwema phambi komfula inqama elempondo ezimbili. Impondo zombili zaziphakeme, kodwa olunye lwaluphakeme okwedlula olunye, njalo oluphakemeyo lwenyuka muva.
Nditakweza maso ndinaona nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri, itayima pafupi ndi mtsinje. Nyanga zakezo zinali zazitali. Nyanga imodzi inali yotalika kuposa inzake, ndipo iyi inaphuka inzakeyo itamera kale.
4 Ngabona inqama ihlaba ikhangele ngentshonalanga langenyakatho langeningizimu; ukuze kungabi lezinyamazana ezingema phambi kwayo, njalo kungekho ongophula esandleni sayo; kodwa yenza njengentando yayo, yazikhulisa.
Ndinaona nkhosa yayimunayo ikuthamanga mwaukali kupita kumadzulo, kumpoto ndi kummwera. Palibe chirombo chimene chikanatha kulimbana nayo, ndipo palibe akanatha kulanditsa kanthu kwa iyo. Iyo inachita monga inafunira ndipo inali ndi mphamvu zambiri.
5 Kwathi mina ngisacabanga, khangela-ke, kweza impongo yembuzi ivela ngentshonalanga phezu kobuso bomhlaba wonke, njalo kayiwuthintanga umhlabathi. Njalo limpongo yayilophondo olunanzelelekayo phakathi laphakathi kwamehlo ayo.
Pamene ndinali kulingalira za zinthu zimenezi, mwadzidzidzi mbuzi yayimuna inatulukira cha kumadzulo, kudutsa dziko lonse lapansi mwaliwiro ikuyenda mʼmalele mokhamokha. Mbuzi yayimunayo inali ndi nyanga yayikulu pakati pa maso ake.
6 Yasisiza enqameni eyayilempondo ezimbili, engangiyibone imi phambi komfula, yagijimela kuyo ngolaka lwamandla ayo.
Inabwera molunjika nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri ija imene ndinaona itayima pafupi ndi mtsinje. Ndipo inayithamangira mwaukali.
7 Ngasengiyibona isondela ngasenqameni, yathukuthela kakhulu imelene layo, yayitshaya inqama, yephula impondo zayo zombili. Kwakungaselamandla enqameni okuma phambi kwayo; kodwa impongo yayiwisela emhlabathini, yayinyathelela phansi; njalo kwakungekho owayengayophula inqama esandleni sayo.
Inafika pafupi ndipo inalimbana nayo mwaukali nkhosa yayimuna ija nʼkuthyola nyanga zake ziwiri. Nkhosa yayimunayo inalibenso mphamvu zogonjetsera mbuziyo; choncho mbuzi ija inagwetsa nkhosayo pansi nʼkuyipondaponda, ndipo palibe akanatha kulanditsa nkhosayo kwa mbuziyo.
8 Ngakho impongo yembuzi yazikhulisa kakhulukazi; yathi isilamandla, uphondo olukhulu lwephuka; njalo endaweni yalo kwenyuka ezine ezinanzelelekayo ngasemimoyeni emine yamazulu.
Mbuziyo inayamba kudzikuza kwambiri chifukwa cha mphamvu zake koma pamene mphamvuzo zinakula kwambiri nyanga yake yayikulu inathyoka, ndipo mʼmalo mwake panamera nyanga zinayi moloza mbali zonse zinayi.
9 Njalo kolunye lwazo kwaphuma uphondo oluncinyane, olwakhula kakhulukazi, ngaseningizimu langasempumalanga langaselizweni elihle.
Pa imodzi mwa nyangazo panatuluka nyanga imene inali yocheperapo koma inakula kwambiri kuloza kummwera ndi kummawa ndi kuloza dziko lokongola.
10 Lwaselukhula kwaze kwaba sebuthweni lamazulu; lwaseluwisela emhlabathini okwebutho lokwezinkanyezi, lwakunyathelela phansi.
Inakula mpaka inafikira gulu lankhondo la kumwamba, ndipo inagwetsera ena a gulu lankhondolo ndi ena a gulu la nyenyezi ku dziko lapansi ndi kuwapondaponda.
11 Yebo, lwazikhulisa kwaze kwaba sesiphathamandleni sebutho, langalo umhlatshelo oqhubekayo wasuswa, lendawo yendlu yaso engcwele yadilizelwa phansi.
Inadzikuza yokha mpaka kufikira kwa mfumu ya gululo: inathetsa nsembe zimene zinkaperekedwa tsiku ndi tsiku, ndipo inagwetsa nyumba yake yopatulika.
12 Kwasekunikelwa ibutho limelene lomhlatshelo oqhubekayo ngenxa yesiphambeko, laphosela emhlabathini iqiniso, lenza, laphumelela.
Gulu lake la nkhondo linathetsa nsembe zoperekera machimo za tsiku ndi tsiku; chipembedzo choonadi chinaponderezedwa pansi. Nyangayi inapambana mu zonse zimene inachita.
13 Ngasengisizwa ongcwele oyedwa ekhuluma, njalo omunye ongcwele wathi kulowo othile owakhulumayo: Koze kube nini uzakuba khona lumbono mayelana lomhlatshelo oqhubekayo, lesiphambeko sencithakalo, ukunikela indawo engcwele kanye lebutho ukuthi kunyathelelwe phansi?
Kenaka ndinamva wina akuyankhula; ndipo woyera winanso anamufunsa kuti, “Kodi zimene ndikuziona mʼmasomphenyazi zidzatha liti? Nsembe zoperekera machimo za tsiku ndi tsiku zidzakhala zoletsedwa mpaka liti? Nanga chonyansa chosokoneza chidzakhalapo mpaka liti? Kodi gulu la ankhondo lidzapondereza malo opatulika mpaka liti?”
14 Wasesithi kimi: Kuze kube zintambama lekuseni okuzinkulungwane ezimbili lamakhulu amathathu; kube sekuhlanjululwa indawo engcwele.
Iye anandiyankha kuti, “Zidzachitika patapita masiku 2,300; pambuyo pake malo opatulika adzabwezeretsedwa monga kale.”
15 Kwasekusithi mina Daniyeli sengiwubonile umbono ngadinga ukuqedisisa, khangela-ke, kwema phambi kwami okunjengesimo somuntu.
Ine Danieli ndikuyangʼanitsitsa masomphenyawa ndi kuyesa kuwazindikira, kuwamvetsa, ndinangoona wina wooneka ngati munthu atayima patsogolo panga.
16 Ngasengisizwa ilizwi lomuntu phakathi kwezinkumbizeUlayi, elamemeza lathi: Gabriyeli, yenza lo aqedisise umbono.
Ndipo ndinamva mawu a munthu kuchokera mʼmbali mwa mtsinje wa Ulai akuyitana kuti, “Gabrieli, muwuze munthuyu tanthauzo la masomphenyawo.”
17 Wasesiza eceleni kwalapho engangimi khona. Esefikile, ngethuka, ngathi mbo ngobuso bami. Kodwa wathi kimi: Qedisisa, ndodana yomuntu, ngoba umbono ungowesikhathi sokucina.
Atayandikira kumene ndinayima, ndinachita mantha ndi kugwa chafufumimba. Iye anati, “Mwana wa munthu, zindikira kuti masomphenyawa akunena za nthawi yachimaliziro.”
18 Kwathi esakhuluma lami, ngangilele ubuthongo obukhulu ngobuso bami emhlabathini; kodwa wangithinta, wangimisa endaweni yami yokuma.
Pamene ankandiyankhula ndinadzigwetsa pansi chafufumimba, nʼkugona tulo tofa nato. Kenaka anandikhudza ndi kundiyimiritsa.
19 Wasesithi: Khangela, ngizakwenza wazi okuzakuba sekupheleni kwentukuthelo, ngoba ukucina kuzakuba ngesikhathi esimisiweyo.
Iye anati, “Ine ndikuwuza zimene zidzachitike ukadzatha mkwiyo, chifukwa masomphenyawa ndi a nthawi ya chimaliziro.”
20 Inqama oyibonileyo elempondo ezimbili ngamakhosi eMede lePerisiya.
Nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri imene unayiona, ikuyimira mafumu a Amedi ndi Aperezi.
21 Njalo impongo eyisiyephu iyinkosi yeGirisi, lophondo olukhulu oluphakathi laphakathi kwamehlo ayo luyinkosi yokuqala.
Mbuzi yayimuna ija ndi mfumu ya Agriki, ndipo nyanga yayikulu pakati pa maso ake aja ndi mfumu yoyamba.
22 Ngolwephukayo, njengoba kwema ezine endaweni yalo, kuzakuma imibuso emine kuso isizwe, kodwa hatshi ngamandla alo.
Kunena za nyanga inathyoka ija ndi nyanga zinayi zimene zinaphuka mʼmalo mwake zikutanthauza maufumu anayi amene adzatuluka mʼdziko lake; koma sizidzafanana mphamvu ndi ufumu woyambawo.
23 Njalo ekucineni kwemibuso yazo, lapho abaphambeki sebephelele, izakuma inkosi elukhuni ngobuso, eqedisisa imizekeliso.
“Pa masiku otsiriza a maufumuwa, machimo awo atachulukitsa, padzadzuka mfumu yaukali ndi yochenjera kwambiri.
24 Lamandla ayo azaqina, kodwa hatshi ngamandla ayo. Njalo izachitha ngokumangalisayo, iphumelele, yenze, ichithe abalamandla lesizwe sabangcwele.
Idzakhala yamphamvu kwambiri koma osati mphamvu za iyo yokha. Idzawononga koopsa ndipo idzapambana mu chilichonse chimene idzachite. Mfumuyi idzawononga anthu amphamvu ndi anthu oyera omwe.
25 Langobuqili bayo izaphumelelisa inkohliso esandleni sayo, izikhulise enhliziyweni yayo, ichithe abanengi ngokuthula, futhi izamelana leNkosana yamakhosana, kodwa izakwephulwa kungelasandla.
Chifukwa cha kuchenjera kwake chinyengo chidzachuluka pa nthawi ya ulamuliro wake, ndipo idzadzikuza kuposa onse. Pamene oyera mtima adzaona ngati kuti ali otetezedwa, iyo idzawononga ambiri ndi kuwukira ngakhale Mfumu ya mafumu. Komabe idzawonongedwa, koma osati ndi mphamvu za munthu.
26 Njalo umbono wantambama lowekuseni olandisiweyo uliqiniso; wena-ke valela umbono, ngoba ungowensuku ezinengi.
“Masomphenya okhudza madzulo ndi mmawa amene unawaona aja ndi woona, koma uwasunge masomphenyawa mwachinsinsi popeza ndi onena za masiku a mʼtsogolo kwambiri.”
27 Mina-ke Daniyeli, ngaphela amandla ngagula okwensuku ezithile; emva kwalokho ngasukuma, ngenza umsebenzi wenkosi; njalo ngamangala kakhulu ngombono, kodwa kakho owaqedisisayo.
Ine Danieli ndinafowoka ndipo ndinadwala masiku angapo. Kenaka ndinadzuka ndi kupitiriza ntchito za mfumu. Ndinada nkhawa ndi masomphenyawo; ndipo sindinathe kuwamvetsa.

< UDanyeli 8 >