< UDanyeli 11 >

1 Lami-ke, ngomnyaka wokuqala kaDariyusi umMede, ngema ukumqinisa lokumvikela.
Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
2 Khathesi sengizakutshela iqiniso. Khangela, kusezakuma amakhosi amathathu ePerisiya; njalo eyesine izanotha ngenotho enkulu okwedlula wonke. Kuthi isiqinile ngenotho yayo ibavuse bonke bamelane lombuso weGirisi.
“Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
3 Kuzasukuma-ke inkosi elamandla, ezabusa ngokubusa okukhulu, yenze ngokwentando yayo.
Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
4 Lalapho isukuma, umbuso wayo uzaqanyulwa, wehlukaniswe ngasemimoyeni emine yamazulu; kodwa ungabi ngowenzalo yayo, ungabi njengombuso ebiwubusa; ngoba umbuso wayo uzasitshunwa, ube ngowabanye ngaphandle kwalaba.
Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
5 Lenkosi yeningizimu izakuba lamandla, lomunye weziphathamandla zayo; yena-ke uzakuba lamandla kulayo, abuse; umbuso wakhe uzakuba ngumbuso omkhulu.
“Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
6 Lekupheleni kweminyaka bazahlangana, ngoba indodakazi yombusi weningizimu izakuza kumbusi wenyakatho ukuzakwenza isivumelwano esilinganayo, kodwa kayiyikugcina amandla engalo; futhi kayiyikuma, layo ingalo yakhe; kodwa izanikelwa, labayilethileyo, loyizeleyo, loyiqinisileyo ngalezizikhathi.
Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
7 Kodwa kuzasukuma ogatsheni lwempande zayo esikhundleni sakhe, ozabuya lebutho, angene enqabeni yenkosi yenyakatho, enze emelene labo, ehlule.
“Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
8 Labonkulunkulu babo kanye leziphathamandla zabo kanye lezitsha zabo eziloyisekayo ezesiliva legolide uzakuletha eGibhithe ekuthunjweni; yena-ke uzakuma okweminyaka kulenkosi yenyakatho.
Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
9 Ngokunjalo inkosi yeningizimu izangena embusweni, ibuyele elizweni layo.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
10 Kodwa amadodana ayo azadungeka, ahlanganise ixuku lamabutho amakhulu; ngeqiniso kufike omunye, agabhe, adabule; abuyele, adungeke, kuze kube senqabeni yakhe.
Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
11 Lenkosi yeningizimu izathukuthela kakhulu, iphume ilwe layo, lenkosi yenyakatho; yona izavusa ixuku elikhulu, kodwa lelixuku lizanikelwa esandleni sayo.
“Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
12 Selisusiwe lelixuku, inhliziyo yayo izaziphakamisa, iwisele phansi izinkulungwane ezingamatshumi amanengi, kodwa kayiyikuba lamandla.
Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
13 Ngoba inkosi yenyakatho izaphenduka, ivuse ixuku elikhulu kulelokuqala; njalo ekupheleni kwezikhathi zeminyaka izafika isibili ilebutho elikhulu lempahla ezinengi.
Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
14 Langalezozikhathi abanengi bazasukuma bemelane lenkosi yeningizimu. Labalesihluku babantu bakho bazaziphakamisa ukuze bawuqinise umbono, kodwa bazakhubeka.
“Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
15 Ngakho inkosi yenyakatho izafika, ibuthelele idundulu, ithumbe imizi ebiyelweyo. Futhi izingalo zeningizimu kaziyikuma, kanye labakhethiweyo bakhe, futhi kakuyikuba lamandla okuma.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
16 Kodwa eza ukuzamelana layo izakwenza ngokwentando yayo, engekho ongema phambi kwayo. Izakuma lelizweni elihle, lokutshabalaliswa kuzakuba sesandleni sayo.
Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
17 Njalo izamisa ubuso bayo ukungena ngamandla ombuso wayo wonke, labaqotho belayo, ngokunjalo izakwenza; futhi izayinika indodakazi yabafazi, ukuwuchitha; kodwa kayiyikuma, kayiyikuba ngeyayo.
Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
18 Emva kwalokho izaphendulela ubuso bayo ezihlengeni, ithumbe ezinengi; kodwa isiphathamandla sizakwenza ihlazo layo limphelele; ngaphandle kokuthi izabuyisela ihlazo layo kuyo.
Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
19 Ibisiphendulela ubuso bayo ngasezinqabeni zelizwe lakibo, kodwa izakhubeka iwe, njalo ingatholwa.
Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
20 Lapho kuzasukuma esikhundleni sayo odlulisa umthelisi kudumo lombuso; kodwa phakathi kwezinsuku ezinlutshwana uzabhujiswa, kungabi ngezintukuthelo, kungabi ngezimpi.
“Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
21 Lapho kuzasukuma esikhundleni sakhe odelelekileyo, abangayikumnika udumo lombuso, kodwa ezangena ngokuthula, awubambe umbuso ngamazwi abutshelezi.
“Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
22 Lezingalo zikazamcolo zizakhukhulwa phambi kobuso bakhe, zifohlozwe; yebo, laso isiphathamandla sesivumelwano.
Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
23 Langemva kokuhlangana laye uzasebenza ngenkohliso; ngoba ezakwenyuka, abe lamandla elesizwe esincane.
Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
24 Uzangena ngokuthula laphezu kwezindawo ezivunde kakhulu zesabelo; enze lokho oyise loba oyise baboyise abangakwenzanga; uzahlakaza phakathi kwabo impango lokuthunjiweyo lempahla; acebe amacebo akhe emelene lezinqaba, kodwa kuze kube yisikhathi.
Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
25 Futhi uzavusa amandla akhe lenhliziyo yakhe emelene lenkosi yeningizimu elebutho elikhulu; njalo inkosi yeningizimu izadungeka ilebutho elikhulu elilamandla amakhulu; kodwa kayiyikuma, ngoba bazaceba amacebo bemelene layo.
“Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
26 Yebo, labo abadla isabelo sokudla sayo bazayibhubhisa, lebutho layo lizakhukhula, labanengi bazakuwa bebulewe.
Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
27 Njalo inhliziyo zalamakhosi amabili zikukho okubi, njalo azakhuluma amanga etafuleni elilodwa; kodwa kakuyikuphumelela, ngoba isiphetho sisezakuba khona ngesikhathi esimisiweyo.
Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
28 Lapho ezabuyela elizweni lakhe elempahla ezinengi; kodwa inhliziyo yakhe izamelana lesivumelwano esingcwele; njalo uzakwenza, abesebuyela elizweni lakhe.
Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
29 Ngesikhathi esimisiweyo uzaphenduka, eze ngaseningizimu; kodwa kakuyikuba njengokwakuqala loba njengokokucina.
“Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
30 Ngoba imikhumbi yeKitimi izakuza imelane laye; ngakho uzadabuka, abuyele emuva, athukuthelele isivumelwano esingcwele; njalo uzakwenza, abesebuyela, anakane labo abadele isivumelwano esingcwele.
Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
31 Lezingalo zizakuma zivela kuye, zingcolise indawo engcwele eyinqaba, asuse umnikelo oqhubekayo, amise isinengiso esichithayo.
“Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
32 Lalabo abenza inkohlakalo bemelene lesivumelwano uzabangcolisa ngamazwi abutshelezi; kodwa abantu abamaziyo uNkulunkulu wabo bazaqina, benze.
Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
33 Njalo abaqedisisayo babantu bazafundisa abanengi; kanti bazakuwa ngenkemba, langelangabi, ngokuthunjwa, langokuphangwa, izinsuku ezinengi.
“Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
34 Kuzakuthi lapho besiwa, basizwe ngosizo oluncinyane, kodwa abanengi bazazihlanganisa labo ngamazwi abutshelezi.
Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
35 Kodwa abanye kwabaqedisisayo bazakuwa, ukubalinga, lokubahlambulula, lokubenza babe mhlophe, kuze kube yisikhathi sokuphela; ngoba kusezakuba ngokwesikhathi esimisiweyo.
Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
36 Njalo inkosi izakwenza njengokwentando yayo, iziphakamise, izikhulise ngaphezu kwabo bonke onkulunkulu, ikhulume izinto ezimangalisayo imelene loNkulunkulu wabonkulunkulu, iphumelele kuze kuphelele intukuthelo; ngoba lokho okumisiweyo kuzakwenziwa.
“Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
37 Futhi kayiyikunaka onkulunkulu baboyise, lesiloyiso sabesifazana, njalo kayiyikunaka loba nguwuphi unkulunkulu; ngoba izazikhulisa phezu kwabo bonke.
Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
38 Kodwa esikhundleni sakhe uzadumisa unkulunkulu wezinqaba, ngitsho unkulunkulu oyise ababengamazi amdumise ngegolide langesiliva langamatshe aligugu langezinto eziloyisekayo.
Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
39 Njalo izakwenza ezinqabeni ezilamandla ikanye lonkulunkulu wezizweni; amnanzelelayo amandisele udumo. Izabenza babuse phezu kwabanengi, yehlukanise ilizwe ngentengo.
Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
40 Langesikhathi sokuphela inkosi yeningizimu izamsunduza; kodwa inkosi yenyakatho izamelana layo njengesivunguzane, ilezinqola, labagadi bamabhiza, lemikhumbi eminengi; ingene emazweni, ikhukhule, idlule.
“Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
41 Njalo izangena elizweni elihle, njalo amazwe amanengi azakuwa; kodwa la azaphunyuka esandleni sakhe, iEdoma loMowabi lekhethelo labantwana bakoAmoni.
Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
42 Njalo izakwelulela isandla sayo emazweni, lelizwe leGibhithe kaliyikuphepha.
Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
43 Kodwa izabusa phezu kwamagugu afihliweyo egolide lawesiliva, laphezu kwazo zonke izinto eziligugu zeGibhithe. Njalo amaLibiya lamaEthiyophiya azakuba sezinyathelweni zakhe.
Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
44 Kodwa imibiko evela empumalanga levela enyakatho izamethusa, ngakho uzaphuma ngokuthukuthela okukhulu ukuyachitha lokutshabalalisa abanengi.
Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
45 Njalo uzagxumeka amathente esigodlo sakhe phakathi laphakathi kwezinlwandle entabeni enhle engcwele; kanti uzafika ekupheleni kwakhe, angabi lomsizi.
Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”

< UDanyeli 11 >