< U-Amosi 4 >
1 Zwanini lelilizwi, mankomokazi eBashani, elisentabeni yeSamariya, elicindezela abayanga, elichoboza abaswelayo, elithi emakhosini abo: Lethani sinathe.
Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
2 INkosi uJehova ifungile ngobungcwele bayo, ukuthi, khangelani, insuku zizafika phezu kwenu lapho abazalihudula ngezingwegwe, labalilandelayo ngengwegwe zokubamba inhlanzi.
Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
3 Njalo lizaphuma ngezikhala, ngulowo lalowo phambi kwakhe, liziphosele ngasesigodlweni, itsho iNkosi.
Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
4 Wozani eBhetheli, liphambeke, eGiligali landise iziphambeko; lilethe imihlatshelo yenu ekuseni, okwetshumi kwenu ngomnyaka wesithathu;
“Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
5 litshise umhlatshelo wokubonga ngokuvutshelweyo, limemezele iminikelo yesihle, lizwakalise; ngoba ngokunjalo likuthanda, bantwana bakoIsrayeli, itsho iNkosi uJehova.
Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
6 Ngakho mina ngilinikile futhi ukuhlanzeka kwamazinyo emizini yonke yenu, lenswelo yesinkwa endaweni zenu zonke; kanti kaliphendukelanga kimi, itsho iNkosi.
“Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
7 Futhi-ke mina ngaligodlela izulu, kuseselenyanga ezintathu kusiya ekuvuneni; ngalinisa komunye umuzi, kodwa kalinanga komunye umuzi; esinye isiqinti sanethwa, kodwa isiqinti esinganethwanga satsha.
“Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
8 Kwasekuzula imizi emibili loba emithathu yayanatha amanzi emzini owodwa, kodwa kayikholwanga; kanti kaliphendukelanga kimi, itsho iNkosi.
Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
9 Ngalitshaya ngokuhanguka langengumane; ukwanda kwezivande zenu, lezivini zenu, lezihlahla zenu zemikhiwa, lezihlahla zenu zemihlwathi, kwadliwa zintethe; kanti kaliphendukelanga kimi, itsho iNkosi.
“Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
10 Ngathumela phakathi kwenu umatshayabhuqe wesifo, ngokwendlela yeGibhithe, ngabulala amajaha enu ngenkemba, kanye lokuthunjwa kwamabhiza enu; njalo ngenza ivumba lenkamba yenu lenyuka ngitsho emakhaleni enu; kanti kaliphendukelanga kimi, itsho iNkosi.
“Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
11 Ngachitha abanye phakathi kwenu njengalokho uNkulunkulu wachitha iSodoma leGomora, lalinjengesikhuni esophulwe ekutsheni; kanti kaliphendukelanga kimi, itsho iNkosi.
“Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
12 Ngakho ngizakwenza ngokunjalo kuwe, Israyeli; ngenxa yokuthi ngizakwenza lokhu kuwe, zilungiselele ukuhlangana loNkulunkulu wakho, Israyeli.
“Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
13 Ngoba khangela, obumba izintaba, lodala umoya, lotshela umuntu ukuthi umcabango wakhe uyini, owenza ukusakube mnyama, onyathela ezindaweni eziphakemeyo zomhlaba, iNkosi, uNkulunkulu wamabandla, libizo lakhe.
Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.