< 2 USamuyeli 8 >
1 Kwasekusithi emva kwalokho uDavida watshaya amaFilisti, wawehlisela phansi; uDavida wasethatha iMethegama esandleni samaFilisti.
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 Wasetshaya amaMowabi, wawalinganisa ngentambo, ewalalisa emhlabathini; walinganisa intambo ezimbili ukubulala, lentambo epheleleyo ukuwayekela ephila. Ngokunjalo amaMowabi aba zinceku zikaDavida, eletha izipho.
Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
3 UDavida wasetshaya uHadadezeri indodana kaRehobi inkosi yeZoba, ekuhambeni kwakhe ukubuyisela amandla akhe emfuleni iYufrathi.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 UDavida wasethumba kuye inqola eziyinkulungwane, labagadi bamabhiza abangamakhulu ayisikhombisa, lamadoda ahamba ngenyawo ayizinkulungwane ezingamatshumi amabili; waquma imisipha yawo wonke amabhiza enqola, kodwa watshiya kuwo izinqola ezilikhulu.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 Lapho amaSiriya aweDamaseko efika ukusiza uHadadezeri inkosi yeZoba, uDavida watshaya amadoda ayizinkulungwane ezingamatshumi amabili lambili kumaSiriya.
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 UDavida wasebeka amabutho enqaba eSiriya yeDamaseko; njalo amaSiriya aba zinceku zikaDavida, eletha izipho. INkosi yasimlondoloza uDavida loba ngaphi lapho aya khona.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 UDavida wasethatha izihlangu zegolide ezazisezincekwini zikaHadadezeri, waziletha eJerusalema.
Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 Inkosi uDavida yasithatha ithusi elinengi kakhulu eBeta leBerothayi, imizi kaHadadezeri.
Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
9 Lapho uToyi inkosi yeHamathi esizwa ukuthi uDavida wayetshaye ibutho lonke likaHadadezeri,
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
10 uToyi wasethuma uJoramu indodana yakhe enkosini uDavida ukuyibuza impilo lokuyibusisa, ngoba yayilwe loHadadezeri yamtshaya (ngoba uHadadezeri waba lezimpi loToyi); njalo esandleni sakhe kwakulezitsha zesiliva lezitsha zegolide lezitsha zethusi.
anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
11 Lazo inkosi uDavida yazehlukanisela iNkosi kanye lesiliva legolide eyayilehlukanisile livela ezizweni zonke eyayizehlisele phansi,
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
12 eSiriya, lakoMowabi, lakubantwana bakoAmoni, lakumaFilisti, leAmaleki, lempangweni kaHadadezeri indodana kaRehobi, inkosi yeZoba.
Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
13 UDavida wasezenzela ibizo ekubuyeni kwakhe ekutshayeni amaSiriya, esihotsheni seTshwayi, izinkulungwane ezilitshumi lesificaminwembili.
Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
14 Wasebeka inqaba zamabutho eEdoma; kuyo yonke iEdoma wabeka inqaba zamabutho, labo bonke abeEdoma baba zinceku zikaDavida. INkosi yasimlondoloza uDavida loba ngaphi lapho aya khona.
Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
15 UDavida wabusa-ke phezu kukaIsrayeli wonke; uDavida wayesenza ukwahlulela lokulunga kubo bonke abantu bakhe.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
16 Njalo uJowabi indodana kaZeruya wayephezu kwebutho; loJehoshafathi indodana kaAhiludi wayengumabhalane;
Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
17 loZadoki indodana kaAhitubi loAhimeleki indodana kaAbhiyatha babengabapristi; loSeraya wayengumbhali;
Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
18 loBhenaya indodana kaJehoyadawayephezu kwamaKerethi lamaPelethi; lamadodana kaDavida ayeyiziphathamandla.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.