< 2 USamuyeli 24 >
1 Lwaselubuya lwamvuthela uIsrayeli ulaka lukaJehova, wabavusela uDavida, esithi: Hamba ubale uIsrayeli loJuda.
Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”
2 Ngakho inkosi yathi kuJowabi induna yebutho eyayilaye: Hamba khathesi ubhode ezizweni zonke zakoIsrayeli, kusukela koDani kuze kube seBherishebha, libale abantu ukuze ngazi inani labantu.
Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 UJowabi wasesithi enkosini: Aluba iNkosi uNkulunkulu wakho ingandisa ebantwini, loba bebanengi kangakanani, kuphindwe ngokulikhulu, ukuthi amehlo enkosi yami, inkosi, akubone. Kodwa inkosi yami, inkosi, ithokozelani kulinto?
Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”
4 Kodwa ilizwi lenkosi lalilamandla phezu kukaJowabi laphezu kwezinduna zebutho. Ngakho uJowabi lenduna zebutho baphuma phambi kwenkosi ukuze babale abantu, uIsrayeli.
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.
5 Basebechapha iJordani, bamisa inkamba eAroweri, ngakwesokunene komuzi ophakathi kwesifula seGadi, lamaqondana leJazeri.
Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.
6 Basebefika eGileyadi lelizweni leTahetimi-Hodishi; bafika eDani-Jahani, babhoda ngaseSidoni,
Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni.
7 bafika enqabeni yeTire lemizini yonke yamaHivi leyamaKhanani; baphuma baya eningizimu yakoJuda, eBherishebha.
Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.
8 Sebebhode badabula ilizwe lonke, bafika eJerusalema ekupheleni kwenyanga eziyisificamunwemunye lensuku ezingamatshumi amabili.
Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.
9 UJowabi waseyinika inkosi inani lokubalwa kwabantu; njalo kwakukhona koIsrayeli amaqhawe ayizinkulungwane ezingamakhulu ayisificaminwembili ahwatsha inkemba; lamadoda akoJuda ayengamadoda ayizinkulungwane ezingamakhulu amahlanu.
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.
10 Inhliziyo kaDavida yasimtshaya emva kokuthi esebale abantu. UDavida wasesithi eNkosini: Ngonile kakhulu ngalokho engikwenzileyo. Ngakho-ke, Nkosi, ngiyakuncenga, susa ububi benceku yakho, ngoba ngenze ngobuthutha obukhulu.
Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
11 Kwathi uDavida esevukile ekuseni, kwafika ilizwi leNkosi kuGadi umprofethi, umboni kaDavida, lisithi:
Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti,
12 Hamba uthi kuDavida: Itsho njalo iNkosi ithi: Ngikubekela okuthathu; zikhethele okukodwa kukho, ukuthi ngikwenze kuwe.
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
13 UGadi wasefika kuDavida, wamtshela wathi kuye: Kufike kuwe yini iminyaka eyisikhombisa yendlala elizweni lakini? Loba ubalekele izitha zakho inyanga ezintathu zixotshana lawe? Ingabe kube khona umatshayabhuqe wesifo okwensuku ezintathu elizweni lakini? Khathesi cabanga, ubone ukuthi yimpendulo bani engizayibuyisela kongithumileyo.
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”
14 UDavida wasesithi kuGadi: Ngicindezelekile kakhulu; ake siwele esandleni seNkosi, ngoba izisa zayo zinkulu, kodwa kangingaweli esandleni somuntu.
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”
15 Ngakho iNkosi yasibeka umatshayabhuqe wesifo kuIsrayeli, kusukela ekuseni kwaze kwaba sesikhathini esimisiweyo; kwasekusifa ebantwini abantu abayizinkulungwane ezingamatshumi ayisikhombisa kusukela koDani kwaze kwaba seBherishebha.
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba.
16 Lapho ingilosi iselulela isandla sayo eJerusalema ukuyibhubhisa, iNkosi yazisola ngalobobubi, yathi engilosini eyayibhubhisa abantu: Sekwanele. Khathesi finyeza isandla sakho. Ingilosi yeNkosi yayisebaleni lokubhulela likaArawuna umJebusi.
Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
17 UDavida wasekhuluma eNkosini lapho ebona ingilosi eyayitshaya abantu, wathi: Khangela, mina ngonile, njalo mina ngenze okubi; pho, lezizimvu zenzeni? Isandla sakho ake simelane lami njalo simelane lendlu kababa.
Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”
18 UGadi wasefika kuDavida ngalolosuku, wathi kuye: Yenyuka, umisele iNkosi ilathi ebaleni lokubhulela likaArawuna umJebusi.
Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.”
19 UDavida wasesenyuka njengokutsho kukaGadi, njengokulaya kweNkosi.
Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.
20 UArawuna waselunguza, wabona inkosi lenceku zayo beqhubeka besiza kuye; uArawuna wasephuma wakhothama phambi kwenkosi ngobuso bakhe emhlabathini.
Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.
21 UArawuna wasesithi: Kungani inkosi yami, inkosi, ize encekwini yayo? UDavida wasesithi: Ukuthi ngithenge kuwe ibala lokubhulela, ukuthi ngakhele iNkosi ilathi, ukuze inhlupheko ithinteke ingafiki ebantwini.
Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?” Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”
22 UArawuna wasesithi kuDavida: Inkosi yami, inkosi, kayithathe inikele lokho okuhle emehlweni ayo; bona, nanzi inkabi zomnikelo wokutshiswa, lezimbulo lezinto zenkabi kube zinkuni.
Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni.
23 Konke lokhu, nkosi, uArawuna wakunika inkosi; uArawuna wasesithi enkosini: INkosi uNkulunkulu wakho kayikwemukele.
Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”
24 Inkosi yasisithi kuArawuna: Hatshi, kodwa ngizakuthenga lokukuthenga kuwe ngentengo; njalo kangiyikunikela iminikelo yokutshiswa engangibizanga lutho eNkosini uNkulunkulu wami. UDavida waselithenga ibala lokubhulela lezinkabi ngamashekeli esiliva angamatshumi amahlanu.
Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.” Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu.
25 UDavida wasesakhela khona iNkosi ilathi, wanikela iminikelo yokutshiswa leminikelo yokuthula. Ngakho iNkosi yancengeka ngelizwe, inhlupheko yasithinteka phezu kukaIsrayeli.
Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.