< 2 USamuyeli 17 >

1 UAhithofeli wasesithi kuAbisalomu: Ake ngikhethe amadoda azinkulungwane ezilitshumi lambili, ngisukume ngixotshane loDavida ngalobubusuku.
Ahitofele anati kwa Abisalomu, “Mundilole ndisankhe asilikali 12,000, ndinyamuke usiku womwe uno kuti ndithamangire Davide.
2 Ngizamehlela esakhathele ebuthakathaka ezandleni, ngimethuse; labo bonke abantu abalaye bazabaleka; ngizatshaya inkosi kuphela.
Ndipo ndikamuthira nkhondo atatopa ndiponso atataya mtima. Ndikamuchititsa mantha ndipo anthu onse amene ali naye akathawa. Ine ndikakantha mfumu yokhayo,
3 Ngizabuyisela abantu bonke kuwe. Umuntu omdingayo ufanana lokubuya kwabo bonke. Bonke abantu bazakuba sekuthuleni.
ndipo anthu onse ndidzabwera nawo kwa inu, ngati mkwati amene akubwerera kwa mwamuna wake. Imfa ya munthu mmodzi yekha idzakhalitsa anthu onse pa mtendere.”
4 Lalelilizwi lalilungile emehlweni kaAbisalomu lemehlweni abo bonke abadala bakoIsrayeli.
Malangizo awa anaoneka abwino kwa Abisalomu ndi kwa akuluakulu onse a Israeli.
5 UAbisalomu wasesithi: Bizani-ke loHushayi umArki, sizwe ukuthi laye uthini ngomlomo.
Koma Abisalomu anati, “Muyitanenso Husai Mwariki kuti timve zimene iye adzanena.”
6 UHushayi esefikile kuAbisalomu, uAbisalomu wakhuluma kuye esithi: UAhithofeli ukhulume ngalindlela: Senze ilizwi lakhe yini? Uba kungenjalo, khuluma wena.
Husai atabwera kwa iye, Abisalomu anati, “Ahitofele wapereka malangizo ake. Kodi tichite zimene wanena? Ngati sichoncho, tiwuze maganizo ako.”
7 UHushayi wasesithi kuAbisalomu: Iseluleko uAhithofeli aselulekileyo ngalesisikhathi kasisihle.
Husai anayankha Abisalomu kuti, “Malangizo amene Ahitofele wapereka si abwino pa nthawi ino.
8 UHushayi wathi futhi: Wena uyamazi uyihlo labantu bakhe ukuthi bangamaqhawe, ukuthi bathukuthele enhliziyweni, njengebhere elithathelwe imidlwane egangeni. Futhi uyihlo yindoda yempi; kayikulala labantu ebusuku.
Inu mukudziwa bwino abambo anu ali ndi ankhondo awo. Iwo ndi anthu ankhondo komanso ndi woopsa ngati chimbalangondo chimene chalandidwa ana ake. Kuwonjezera apa abambo anu ndi katswiri wa nkhondo. Iwo sanagone pamodzi ndi asilikali awo.
9 Khangela, khathesinje ucatshile komunye wemigodi, loba kwenye yezindawo. Kuzakuthi lapho abanye babo bewile ekuqaleni, kuthi loba ngubani ozwayo athi: Bekulokubulawa ebantwini abalandela uAbisalomu.
Onani, ngakhale tsopano lino abisala mʼphanga lina ku malo ena ake. Ngati iwo atayamba kuthira nkhondo asilikali anu, aliyense amene adzamve zimenezi adzati, ‘Gulu lalikulu lankhondo lotsatira Abisalomu laphedwa.’
10 Kuthi laye olobuqhawe, onhliziyo yakhe injengenhliziyo yesilwane, ancibilike lokuncibilika; ngoba uIsrayeli wonke uyazi ukuthi uyihlo uliqhawe, lalabo abalaye balobuqhawe.
Tsono ngakhale msilikali wolimba mtima kwambiri, amene mtima wake uli ngati wa mkango, adzagwidwa ndi mantha aakulu pakuti Aisraeli akudziwa kuti abambo anu ndi ankhondo ndipo kuti iwo amene ali nawo ndi anthu olimba mtima.
11 Ngakho ngiyeluleka ukuthi uIsrayeli wonke abuthane, abuthane kuwe kusukela koDani kuze kufike eBherishebha, ngangetshebetshebe eliselwandle ngobunengi, wena ngokwakho ubususiya empini.
“Kotero ine ndikukulangizani kuti: Aisraeli onse, kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba; ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja, asonkhane kwa inu ndipo muwatsogolera kupita ku nkhondo.
12 Ngakho sizamehlela kwenye yezindawo lapho angatholakala khona, simehlele njengamazolo ewela emhlabathini; njalo kungasali kuye lebantwini bonke abalaye loyedwa.
Ndipo ife tidzapita kukamuthira nkhondo kulikonse kumene tikamupeze, ndipo ife tikamuthira nkhondo ngati mame pa nthaka. Palibe amene adzakhale wamoyo kaya iye kapena ankhondo ake.
13 Uba-ke engena emzini, uIsrayeli wonke uzaletha amagoda kulowomuzi, siwuhudulele esifuleni, kungabe kusatholwa lalitshana khona.
Iye akakathawira mu mzinda, Aisraeli onse adzabweretsa zingwe ku mzindawo, ndipo ife tidzawugwetsera ku chigwa mpaka sipadzapezeka ngakhale kachidutswa.”
14 UAbisalomu lawo wonke amadoda akoIsrayeli basebesithi: Iseluleko sikaHushayi umArki singcono kuleseluleko sikaAhithofeli. Ngoba iNkosi uNkulunkulu yayilayile ukuthi kufutshiswe iseluleko esihle sikaAhithofeli ukuze iNkosi imehlisele okubi uAbisalomu.
Abisalomu ndi ankhondo ena onse a Israeli anati, “Malangizo a Husai Mwariki ndi abwino kuposa a Ahitofele.” Pakuti Yehova anatsimikiza kutsutsa malangizo onse abwino a Ahitofele ndi cholinga choti zimuvute Abisalomu.
15 UHushayi wasesithi kuZadoki lakuAbhiyatha abapristi: UAhithofeli weluleke uAbisalomu labadala bakoIsrayeli kanje lakanje; mina-ke ngeluleka kanje lakanje.
Husai anawuza ansembe Zadoki ndi Abiatara kuti, “Ahitofele analangiza Abisalomu ndi akuluakulu a Israeli zakuti, koma ine ndawalangiza kuchita zakutizakuti.
16 Ngakho-ke thumani masinyane litshele uDavida lithi: Ungalali emagcekeni enkangala kulobubusuku, futhi chapha lokuchapha, hlezi inkosi iginywe labantu bonke abalayo.
Tsopano tumizani wamthenga msangamsanga kuti akamuwuze Davide kuti, ‘Musakagone powolokera Yorodani ku chipululu koma mukawoloke. Mukapanda kutero, mfumu ndi anthu onse amene ali naye adzaphedwa.’”
17 OJonathani loAhimahazi babemile-ke eEnirogeli; incekukazi yeza yabatshela, bona-ke bahamba babikela inkosi uDavida; ngoba babengelakubonwa bengena emzini.
Yonatani ndi Ahimaazi amakhala ku Eni Rogeli. Tsono wantchito wamkazi ndiye amapita kukawawuza ndipo iwo amayenera kupita kukamuwuza mfumu Davide, pakuti iwowo sankayenera kuonekera polowa mu mzinda.
18 Kodwa umfana othile wababona, wabikela uAbisalomu; kodwa bahamba masinyane bobabili, bayafika endlini yomuntu eBahurimi, owayelomthombo egumeni lakhe; behlela khona.
Koma mnyamata wina anawaona ndipo anakawuza Abisalomu. Kotero anthu awiriwo anachoka mofulumira ndipo anapita ku nyumba ya munthu wina ku Bahurimu. Iye anali ndi chitsime ku mpanda kwake ndipo iwo analowamo.
19 Owesifazana wasethatha wendlala isimbombozo phezu komlomo womthombo, wachaya amabele agigiweyo phezu kwaso; ngakho linto kayaziwanga.
Mkazi wake anatenga chophimba ndipo anachiyika pamwamba pa chitsimecho nawazapo tirigu. Palibe amene anadziwa chilichonse za izi.
20 Lapho zifika izinceku zikaAbisalomu kowesifazana endlini, zathi: Bangaphi oAhimahazi loJonathani? Owesifazana wasesithi kizo: Bachaphe isifula samanzi. Sezidingile, zingabatholanga, zabuyela eJerusalema.
Anthu a Abisalomu atafika kwa mkaziyo pa nyumbapo anafunsa kuti, “Kodi Ahimaazi ndi Yonatani ali kuti?” Mkaziyo anawayankha kuti, “Awoloka mtsinje.” Anthuwo anafunafuna koma sanapeze munthu, kotero anabwerera ku Yerusalemu.
21 Kwasekusithi sezihambile, benyuka emthonjeni baya bayitshela inkosi uDavida, bathi kuDavida: Sukani lichaphe amanzi masinyane, ngoba uAhithofeli weluleke njalo emelene lani.
Anthu aja atapita, awiriwo anatuluka mʼchitsimemo ndipo anapita kukawuza mfumu Davide nati kwa iye, “Nyamukani, muwoloke mtsinje msangamsanga. Ahitofele wapereka malangizo akutiakuti kutsutsana nanu.”
22 UDavida wasesuka, labo bonke abantu ababelaye, bachapha iJordani; kuze kube sekukhanyeni kokusa kwakungasalanga loyedwa, ongayichaphanga iJordani.
Kotero Davide ndi anthu onse amene anali nawo ananyamuka ndi kuwoloka Yorodani. Pofika mmamawa, panalibe munthu amene anatsala asanawoloke Yorodani!
23 Lapho uAhithofeli ebona ukuthi iseluleko sakhe asilandelwanga, wabophela isihlalo kubabhemi, wasuka waya endlini yakhe emzini wakhe, walaya indlu yakhe, waziphanyeka, wafa, wangcwatshelwa engcwabeni likayise.
Ahitofele ataona kuti malangizo ake sanatsatidwe, iye anakwera bulu wake napita ku mzinda wa kwawo ku nyumba yake. Iye anakonza mʼnyumba mwakemo ndi kudzimangirira. Kotero anafa nayikidwa mʼmanda a abambo ake.
24 UDavida wasefika eMahanayimi; uAbisalomu wasechapha iJordani, yena lamadoda wonke akoIsrayeli kanye laye.
Davide anapita ku Mahanaimu, ndipo Abisalomu anawoloka Yorodani pamodzi ndi ankhondo ena onse a Israeli.
25 UAbisalomu wayebeke-ke uAmasa phezu kwebutho esikhundleni sikaJowabi. Njalo uAmasa wayeyindodana yomuntu obizo lakhe lalinguIthira umIsrayeli, owangena kuAbigali indodakazi kaNahashi, udadewabo kaZeruya, unakaJowabi.
Abisalomu anasankha Amasa kukhala mkulu wa ankhondo mʼmalo mwa Yowabu. Amasa anali mwana wa munthu wotchedwa Itira Mwisraeli amene anakwatira Abigayeli mwana wa Nahasi mlongo wake wa Zeruya, amayi ake a Yowabu.
26 Ngakho uIsrayeli loAbisalomu bamisa inkamba elizweni leGileyadi.
Aisraeli ndi Abisalomu anamanga zithando mʼdziko la Giliyadi.
27 Kwasekusithi uDavida esefikile eMahanayimi, uShobi indodana kaNahashi weRaba yabantwana bakoAmoni, loMakiri indodana kaAmiyeli weLodebari, loBarizilayi umGileyadi weRogelimi,
Davide atafika ku Mahanaimu, Sobi mwana wa Nahasi wochokera ku Raba ku dziko la Amoni ndi Makiri mwana wa Amieli wochokera ku Lodebara, ndi Barizilai Mgiliyadi wochokera ku Rogelimu
28 baletha amacansi, lemiganu, lendiwo zebumba, lengqoloyi, lebhali, lempuphu, lamabele akhanzingiweyo, lendumba, lamalentili, lokunye okukhanzingiweyo,
anabweretsa zofunda, mabeseni ndi miphika. Iwo anabweretsanso kwa Davide ndi anthu ake zakudya izi: tirigu ndi barele, ufa ndi tirigu wokazinga, nyemba ndi mphodza,
29 lenyosi, lamasi, lezimvu, letshizi yenkomo, kusenzelwa uDavida labantu ababelaye ukuze badle; ngoba bathi: Abantu balambile badiniwe bomile enkangala.
uchi ndi chambiko, nkhosa ndi mafuta olimba a mkaka wangʼombe. Pakuti anati, “Anthuwa ali ndi njala ndipo atopa, alinso ndi ludzu muno mʼchipululu.”

< 2 USamuyeli 17 >