< 2 USamuyeli 12 >

1 INkosi yasithuma uNathani kuDavida. Wasefika kuye wathi kuye: Kwakukhona amadoda amabili emzini owodwa; enye inothile, lenye ingumyanga.
Tsono Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Atafika kwa Davide anati, “Panali anthu awiri mʼmizinda ina, wina wolemera ndi wina wosauka.
2 Enothileyo yayilezimvu lenkomo ezinengi kakhulu.
Munthu wolemerayo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri,
3 Kodwa engumyanga yayingelalutho ngaphandle kwewundlu elincinyane elilodwa elisikazi eyayilithengile, yalondla; lakhula layo, njalo labantwana bayo ndawonye. Ladla okocezu lwayo, lanatha okwenkezo yayo; lalala esifubeni sayo, lalinjengendodakazi kiyo.
koma wosaukayo analibe chilichonse kupatula kankhosa kamodzi kakakazi kamene anakagula. Iye anakasunga ndipo kanakula naye pamodzi ndi ana ake. Kamadya chakudya chake, kamamwera chikho chake ndipo kamagona mʼmanja mwake. Kanali ngati mwana wamkazi kwa iyeyo.
4 Kwasekufika isihambi endodeni enothileyo; yasiyekela ukuthatha ezimvini zayo lenkomeni zayo ukulungisela isihambi esasifike kiyo, kodwa yathatha iwundlu elisikazi lendoda engumyanga, yalilungisela umuntu owayefike kiyo.
“Ndipo mlendo anafika kwa munthu wolemera uja, koma munthu wolemerayo sanafune kutenga imodzi mwa nkhosa kapena ngʼombe zake kuti akonzere chakudya mlendo amene anafika kwa iye. Mʼmalo mwake anatenga mwana wankhosa wamkazi wa munthu wosauka uja nakonzera chakudya mlendo uja amene anabwera kwa iye.”
5 Ulaka lukaDavida lwaseluvuthela lowomuntu kakhulu, wathi kuNathani: Kuphila kukaJehova, isibili umuntu owenze lokho uyindodana yokufa.
Davide anapsa mtima kwambiri chifukwa cha munthuyo ndipo anati kwa Natani, “Pali Yehova, munthu amene anachita zimenezi ayenera kufa basi!
6 Njalo uzalibuyisela iwundlu elisikazi liphindwe kane, ngenxa yokuthi enze le into langenxa yokuthi engabanga lozwelo.
Iye ayenera kulipira mwana wankhosa wamkaziyo kanayi, chifukwa anachita chinthu chimenechi ndipo analibe chifundo.”
7 UNathani wasesithi kuDavida: Nguwe lowomuntu! Itsho njalo iNkosi uNkulunkulu kaIsrayeli: Ngakugcoba waba yinkosi phezu kukaIsrayeli, ngakukhulula esandleni sikaSawuli.
Kenaka Natani anati kwa Davide, “Munthuyo ndinu! Yehova, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakudzoza kukhala mfumu ya Israeli, ndipo ndinakupulumutsa mʼdzanja la Sauli.
8 Ngakunika indlu yenkosi yakho labafazi benkosi yakho esifubeni sakho, ngakunika indlu kaIsrayeli lekaJuda; uba-ke bekukuncinyane, bengingakwengezelela okunje lokunje.
Ndinakupatsanso banja la mbuye wako ndiponso akazi a mbuye wako mʼmanja mwako. Ine ndinakupatsanso banja la Israeli ndi Yuda. Ndipo ngati zinthu zonse izi zinali zochepa, Ine ndikanakupatsa zambiri.
9 Udeleleleni ilizwi leNkosi ukuthi wenze okubi emehlweni ayo? U-Uriya umHethi umtshayile ngenkemba, lomkakhe wamthatha waba ngumkakho, laye umbulele ngenkemba yabantwana bakoAmoni.
Nʼchifukwa chiyani unanyoza mawu a Yehova pochita chimene chili choyipa pamaso pake? Iwe unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndipo unatenga mkazi wake kukhala wako. Uriyayo unamupha ndi lupanga la Aamoni.
10 Ngakho-ke inkemba kayiyikusuka endlini yakho kuze kube nininini, ngenxa yokuthi ungidelele, wathatha umkaUriya umHethi ukuthi abe ngumkakho.
Ndipo tsopano lupanga silidzachoka pa nyumba yako, chifukwa unandinyoza ine ndi kutenga mkazi wa Uriya Mhiti kukhala wako.’
11 Itsho njalo iNkosi: Khangela, ngizakuvusela okubi kuvela endlini yakho, ngithathe omkakho phambi kwamehlo akho, ngibanike umakhelwane wakho, alale labomkakho phambi kwalelilanga.
“Yehova akuti, ‘Ine ndidzabweretsa tsoka pa iwe lochokera mʼbanja lako. Ndidzatenga akazi ako iwe ukuona ndi kuwapereka kwa wina amene ali pafupi nawe, ndipo iye adzagona ndi akazi ako masanasana Aisraeli onse akuona.
12 Ngoba wena wakwenza ensitha, kodwa mina ngizakwenza le into phambi kukaIsrayeli wonke laphambi kwelanga.
Iwe unachita zimenezi mwamseri koma Ine ndidzachita izi masanasana Aisraeli onse akuona.’”
13 UDavida wasesithi kuNathani: Ngonile eNkosini. UNathani wasesithi kuDavida: LeNkosi isusile isono sakho; kawuyikufa.
Kenaka Davide anati kwa Natani, “Ine ndachimwira Yehova.” Natani anayankha kuti, “Yehova wachotsa tchimo lanu. Simufa ayi.
14 Loba kunjalo, ngoba wenze izitha zeNkosi zidelele lokudelela ngalindaba, laye umntwana ozalelwe wena uzakufa lokufa.
Komabe, popeza pochita zimenezi mwachititsa kuti adani a Yehova amunyoze, mwana amene akubalireniyo adzafa.”
15 UNathani wasesiya endlini yakhe. INkosi yasimtshaya umntwana umkaUriya amzalela uDavida, wagula kakhulu.
Natani atapita kwawo, Yehova anakantha mwana amene mkazi wa Uriya anabereka ndipo anayamba kudwala.
16 Ngakho uDavida wamncengela umntwana kuNkulunkulu; uDavida wasezila izilo lokudla, wangena, walala emhlabathini ubusuku bonke.
Davide anapempherera mwanayo kwa Mulungu. Iye anasala chakudya ndipo analowa mʼnyumba mwake nagona pansi usiku wonse.
17 Abadala bendlu yakhe basebesukuma baya kuye ukumvusa emhlabathini; kodwa kafunanga, futhi kadlanga ukudla labo.
Akuluakulu a banja lake anayima pambali pake kuti amudzutse, koma iye anakana, ndipo sanadye chakudya chilichonse pamodzi ndi iwo.
18 Kwasekusithi ngosuku lwesikhombisa umntwana wafa. Izinceku zikaDavida zasezisesaba ukumtshela ukuthi umntwana ufile; ngoba zathi: Khangela, umntwana esaphila sakhuluma laye, kalalelanga ilizwi lethu; pho, singamtshela njani ukuthi umntwana ufile? Angazilimaza.
Mwana anamwalira pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Antchito a Davide anaopa kumuwuza kuti mwanayo wamwalira, popeza ankaganiza kuti, “Pamene mwanayu anali ndi moyo, ife tinayankhula Davide koma sanatimvere. Nanga tingamuwuze bwanji kuti mwana wamwalira? Mwina atha kudzipweteka.”
19 Kodwa uDavida ebona ukuthi inceku zakhe ziyanyenyezelana, uDavida waqedisisa ukuthi umntwana usefile; ngakho uDavida wathi ezincekwini zakhe: Umntwana usefile yini? Zasezisithi: Usefile.
Davide anaona kuti antchito ake amanongʼonezana pakati pawo ndipo anazindikira kuti mwanayo wamwalira. Iye anafunsa kuti, “Kodi mwanayo wamwalira?” Iwo anayankha kuti, “Inde wamwalira.”
20 UDavida wasevuka emhlabathini, wageza, wagcoba, wantshintsha izigqoko zakhe, wangena endlini yeNkosi, wakhonza; wasesiya endlini yakhe, wacela, babeka ukudla phambi kwakhe, wadla.
Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.
21 Inceku zakhe zasezisithi kuye: Iyini le into oyenzileyo? Ngenxa yomntwana ophilayo uzile ukudla wakhala inyembezi; kodwa lapho umntwana esefile, uvukile wadla isinkwa.
Antchito ake anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuchita zinthu motere? Pamene mwana anali ndi moyo, munkasala chakudya ndi kulira, koma tsopano pamene mwana wamwalira inu mukudzuka ndi kudya!”
22 Wasesithi: Umntwana esaphila, ngizile ukudla, ngakhala inyembezi, ngoba ngathi: Ngubani owaziyo iNkosi ingangihawukela ukuthi umntwana aphile.
Iye anayankha kuti, “Pamene mwana anali ndi moyo ine ndinkasala zakudya ndi kulira. Ine ndinkaganiza kuti, ‘Akudziwa ndani? Yehova atha kundikomera mtima kuti mwanayo akhale ndi moyo.’
23 Kodwa khathesi usefile, ngizazilelani? Ngilakho ukumbuyisa yini futhi? Ngizakuya kuye, kodwa yena kayikubuyela kimi.
Koma tsopano wamwalira ndisaliranji chakudya? Kodi ndingathe kumubwezanso? Ine ndidzapita kumene kuli iyeko, koma iye sadzabwerera kwa ine.”
24 UDavida wasemduduza uBathisheba umkakhe, wangena kuye, walala laye; wazala indodana, wabiza ibizo layo wathi nguSolomoni. UJehova wasemthanda.
Ndipo Davide anatonthoza mkazi wake Batiseba, napita kwa iye ndi kugona naye. Iye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha dzina lake Solomoni. Yehova ankamukonda iye.
25 Wasethuma ngesandla sikaNathani umprofethi, wabiza ibizo layo wathi nguJedidiya, ngenxa kaJehova.
Ndipo chifukwa chakuti Yehova ankamukonda iyeyo, Yehovayo anatumiza mawu kwa mneneri Natani kuti akamutchule Yedidiya.
26 UJowabi walwa-ke leRaba eyabantwana bakoAmoni, wathumba umuzi wobukhosi.
Pa nthawi imeneyi Yowabu anamenyana ndi Raba ku Amoni ndipo analanda nsanja yaufumu.
27 UJowabi wasethuma izithunywa kuDavida wathi: Ngilwe leRaba, njalo ngathumba umuzi wamanzi.
Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.
28 Ngakho-ke buthanisa abantu abaseleyo, umise inkamba maqondana lomuzi, uwuthumbe, hlezi mina ngiwuthumbe umuzi, lebizo lami libizwe phezu kwawo.
Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”
29 UDavida wasebuthanisa bonke abantu, waya eRaba, walwa layo, wayithumba.
Kotero Davide anasonkhanitsa ankhondo onse ndipo anapita ku Raba kukawuthira nkhondo ndi kuwulanda.
30 Wasethatha umqhele wenkosi ekhanda lakhe, osisindo sawo sasilithalenta legolide lelitshe eliligugu, waba sekhanda likaDavida. Wasekhipha impango yomuzi enengi kakhulu.
Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo ndipo Davide anavala chipewacho. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide, ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
31 Wakhupha labantu ababephakathi kwawo, wababeka emasaheni, lezikhalini ezicijileyo zensimbi, lemahlokeni ensimbi, wabadlulisa emahondweni ezitina; wenza njalo kuyo yonke imizi yabantwana bakoAmoni. UDavida labo bonke abantu basebebuyela eJerusalema.
ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa, ndiponso yowomba njerwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka iye pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.

< 2 USamuyeli 12 >