< 2 Amakhosi 8 >

1 UElisha wasekhuluma kowesifazana ondodana yakhe ayeyenze yaphila, esithi: Sukuma, uhambe wena lendlu yakho, uyehlala njengowezizwe lapho ongahlala khona njengowezizwe, ngoba iNkosi ibize indlala, ezafika njalo elizweni iminyaka eyisikhombisa.
Ndipo Elisa anawuza mayi amene anamuukitsira mwana wake kuti, “Choka kuno pamodzi ndi banja lako ndipo ukakhale kulikonse ukufuna, chifukwa Yehova akubweretsa njala ya zaka zisanu ndi ziwiri mʼdziko muno.”
2 Owesifazana wasukuma-ke, wenza njengokutsho komuntu kaNkulunkulu; wahamba yena lendlu yakhe, wahlala njengowezizwe elizweni lamaFilisti iminyaka eyisikhombisa.
Mayiyo ananyamuka nachita zimene munthu wa Mulungu ananena. Iye pamodzi ndi banja lake anachoka nakakhala ku dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.
3 Kwasekusithi ekupheleni kweminyaka eyisikhombisa, owesifazana waphenduka evela elizweni lamaFilisti; waphuma ukuyakhala enkosini ngendlu yakhe langensimu yakhe.
Zitatha zaka zisanu ndi ziwirizo anabwera kuchokera ku dziko la Afilisti ndipo anapita kwa mfumu kukafunsa za nyumba yake ndi munda wake.
4 Inkosi yayikhuluma-ke loGehazi inceku yomuntu kaNkulunkulu isithi: Akungilandisele izinto zonke ezinkulu uElisha asezenzile.
Ndipo mfumu inkayankhula ndi Gehazi, mtumiki wa munthu wa Mulungu kuti, “Tandiwuza zinthu zikuluzikulu zimene Elisa wachita.”
5 Kwasekusithi esatshela inkosi ukuthi wavusa njani ofileyo, khangela-ke, owesifazana ondodana yakhe ayeyivuse ekufeni wakhala enkosini ngendlu yakhe langensimu yakhe. UGehazi wasesithi: Nkosi yami, nkosi, nguye lo owesifazana, njalo yiyo le indodana yakhe uElisha ayiphilisayo.
Pamene Gehazi ankayiwuza mfumuyo momwe Elisa anaukitsira anthu akufa, mayi amene mwana wake Elisa anamuukitsa kwa akufayo analowa kudzafunsa mfumu za nyumba yake ndi munda wake. Gehazi anati, “Mbuye wanga mfumu, mayi wake ndi uyu ndipo mwana wakeyo ndi uyu amene Elisa anamuukitsa kwa akufa.”
6 Lapho inkosi ibuza owesifazana, wayilandisela. Inkosi yasimmisela induna ethile, isithi: Buyisela konke okwakungokwakhe, laso sonke isivuno sensimu kusukela mhla esuka elizweni kuze kube lamuhla.
Mfumu inafunsa mayiyo za nkhaniyi ndipo iye anayifotokozera mfumuyo. Ndipo mfumu inasankha munthu woti ayendetse nkhani yake ndipo inati, “Mubwezereni zonse zimene zinali zake, kuphatikizapo phindu lonse lochokera mʼmunda wake, kuyambira tsiku limene anachoka mpaka tsopano lino.”
7 UElisha wasefika eDamaseko, njalo uBenihadadi inkosi yeSiriya wayegula. Wasetshelwa kwathiwa: Umuntu kaNkulunkulu ufikile lapha.
Elisa anapita ku Damasiko, ndipo Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu ankadwala. Mfumuyo itawuzidwa kuti, “Munthu wa Mulungu wabwera kuno kuchokera kutali,”
8 Inkosi yasisithi kuHazayeli: Thatha esandleni sakho isipho, uyehlangabeza umuntu kaNkulunkulu, ubusubuza eNkosini ngaye usithi: Ngizasila yini kulumkhuhlane?
inawuza Hazaeli kuti, “Tenga mphatso ndipo pita ukakumane ndi munthu wa Mulungu. Ukandifunsire kwa Yehova kudzera mwa iye kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
9 UHazayeli wasesiyamhlangabeza, wathatha isipho esandleni sakhe, ngitsho esakho konke okuhle kweDamaseko, imithwalo yamakamela engamatshumi amane, weza wema phambi kwakhe, wathi: Indodana yakho uBenihadadi inkosi yeSiriya ingithumile kuwe isithi: Ngizasila yini kulumkhuhlane?
Choncho Hazaeli anapita kukakumana ndi Elisa, atasenzetsa ngamira 40 mphatso za zinthu zosiyanasiyana zabwino kwambiri za ku Damasiko. Iye analowa mʼnyumba ya Elisa ndi kuyima pamaso pake, ndipo anati, “Mwana wanu Beni-Hadadi wandituma kuti ndidzakufunseni kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
10 UElisha wasesithi kuye: Hamba uthi kuye: Ungasila lokusila, kodwa iNkosi ingibonisile ukuthi uzakufa lokufa.
Elisa anayankha kuti, “Pita ndipo ukamuwuze kuti, ‘Udzachira ndithu,’ koma Yehova wandionetsa kuti adzafabe.”
11 Wasemjolozela waze waba lenhloni. Umuntu kaNkulunkulu waselila.
Elisa anamuyangʼana kwambiri Hazaeli mpaka anachita manyazi. Pamenepo munthu wa Mulungu anayamba kulira.
12 UHazayeli wasesithi: Inkosi yami ililelani? Wasesithi: Ngoba ngiyazi ububi ozabenza ebantwaneni bakoIsrayeli; uzathungela inqaba zabo ngomlilo, ubulale amajaha abo ngenkemba, uphahlaze abantwanyana babo, uqhaqhe abesifazana babo abakhulelweyo.
Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?” Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”
13 Kodwa uHazayeli wathi: Kodwa iyini inceku yakho eyinja nje, ukuthi yenze linto enkulu? UElisha wasesithi: INkosi ingibonisile ukuthi uzakuba yinkosi phezu kweSiriya.
Ndipo Hazaeli anati, “Kodi kapolo wanune, amene ndine wonyozeka ngati galu, ndingathe bwanji kuchita chinthu chachikulu chotere?” Elisa anayankha kuti, “Yehova wandionetsa kuti iwe udzakhala mfumu ya ku Aramu.”
14 Wasesuka kuElisha weza enkosini yakhe eyathi kuye: UElisha utheni kuwe? Wasesithi: Ungitshele ukuthi uzasila lokusila.
Choncho Hazaeli anasiyana ndi Elisa ndi kubwerera kwa mbuye wake. Beni-Hadadi atafunsa kuti, “Elisa wakuwuza chiyani?” Hazaeli anayankha kuti, “Elisa wandiwuza kuti inu mudzachira ndithu.”
15 Kwasekusithi kusisa wathatha ingubo, wayigxamuza emanzini, wayendlala phezu kobuso bakhe waze wafa. UHazayeli wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Koma mmawa mwake Hazaeli anatenga nsalu yokhuthala ndi kuyiviyika mʼmadzi ndipo anaphimba nayo nkhope ya mfumu, kotero mfumuyo inafa. Hazaeli analowa ufumu mʼmalo mwake.
16 Njalo ngomnyaka wesihlanu kaJoramu indodana kaAhabi inkosi yakoIsrayeli, lapho uJehoshafathi eyinkosi yakoJuda, uJehoramu indodana kaJehoshafathi inkosi yakoJuda waba yinkosi.
Chaka chachisanu cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya ku Israeli, Yehosafati ali mfumu ya ku Yuda, Yehoramu mwana wake anakhala mfumu ya Ayuda.
17 Wayeleminyaka engamatshumi amathathu lambili lapho esiba yinkosi, wabusa iminyaka eyisificaminwembili eJerusalema.
Yehoramu analowa ufumu ali ndi zaka 32, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
18 Wasehamba ezindleleni zamakhosi akoIsrayeli njengokwenza kwendlu kaAhabi, ngoba indodakazi kaAhabi yayingumkakhe; wenza okubi emehlweni eNkosi.
Iye anatsatira khalidwe la mafumu a ku Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, popeza iye anakwatira mwana wa Ahabu. Yehoramu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
19 Kodwa iNkosi kayithandanga ukuchitha uJuda ngenxa kaDavida inceku yayo, njengokuthembisa kwayo kuye ukuthi izanika isibane kuye zonke izinsuku, lemadodaneni akhe.
Komabe, chifukwa cha mtumiki wake Davide, Yehova sanafune kuwononga Yuda popeza Yehova analonjeza Davide kuti adzamupatsa nyale pamodzi ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
20 Ensukwini zakhe iEdoma yahlamuka isuka phansi kwesandla sakoJuda, yabeka inkosi phezu kwayo.
Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira ulamuliro wa Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
21 UJoramu wasewelela eZayiri lazo zonke inqola zilaye; yena wavuka ebusuku watshaya amaEdoma ayemzingelezele, lenduna zezinqola; labantu babalekela emathenteni abo.
Choncho Yehoramu anapita ku Zairi pamodzi ndi magaleta ake onse. Ndipo iye anakantha Aedomu amene anamuzungulira pamodzi ndi oyendetsa magaleta ake usiku. Koma ankhondo ake anathawa napita ku misasa yawo.
22 Ngakho iEdoma yahlamuka isuka phansi kwesandla sakoJuda kuze kube lamuhla. Khona iLibhina yahlamuka ngalesosikhathi.
Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira Yuda. Nthawi yomweyo mzinda wa Libina unawukiranso.
23 Ezinye-ke zezindaba zikaJoramu, lakho konke akwenzayo, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoJuda?
Ndipo ntchito zina za Yehoramu ndi zonse zomwe anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
24 UJoramu waselala laboyise, wangcwatshelwa kuboyise emzini kaDavida. UAhaziya indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Choncho Yehoramu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 Ngomnyaka wetshumi lambili kaJoramu indodana kaAhabi inkosi yakoIsrayeli uAhaziya indodana kaJehoramu, inkosi yakoJuda, waba yinkosi.
Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israeli, Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
26 UAhaziya wayeleminyaka engamatshumi amabili lambili lapho esiba yinkosi, wabusa umnyaka owodwa eJerusalema. Lebizo likanina lalinguAthaliya, indodakazi kaOmri inkosi yakoIsrayeli.
Ahaziya anali ndi zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Amayi ake anali Ataliya, chidzukulu cha Omiri mfumu ya Israeli.
27 Wasehamba ngendlela yendlu kaAhabi, wenza okubi emehlweni eNkosi, njengendlu kaAhabi, ngoba wayengumkhwenyana wendlu kaAhabi.
Iye anatsatira makhalidwe a banja la Ahabu ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga linachitira banja la Ahabu, pakuti anali mkamwini wa banja la Ahabu.
28 Wasehamba loJoramu indodana kaAhabi ukulwa loHazayeli inkosi yeSiriya eRamothi-Gileyadi; amaSiriya aselimaza uJoramu.
Ahaziya anapita pamodzi ndi Yoramu mwana wa Ahabu kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yoramu.
29 UJoramu inkosi wabuyela ukwelatshwa eJizereyeli amanxeba amaSiriya ayemtshaye wona eRama ekulweni kwakhe loHazayeli inkosi yeSiriya. UAhaziya indodana kaJehoramu inkosi yakoJuda wasesehla ukubona uJoramu indodana kaAhabi eJizereyeli, ngoba wayegula.
Choncho mfumu Yoramu inabwerera ku Yezireeli kuti ikachire mabala ake amene Aaramu anamuvulaza ku Rama pa nkhondo yake ndi Hazaeli mfumu ya Aramu. Tsono Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya ku Yuda anapita ku Yezireeli kuti akamuone Yoramu mwana wa Ahabu, popeza nʼkuti akudwala.

< 2 Amakhosi 8 >