< 2 Amakhosi 22 >
1 UJosiya wayeleminyaka eyisificaminwembili lapho esiba yinkosi; wabusa iminyaka engamatshumi amathathu lanye eJerusalema. Lebizo likanina lalinguJedida indodakazi kaAdaya weBhozikhathi.
Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati.
2 Wasesenza okulungileyo emehlweni eNkosi, wahamba ngayo yonke indlela kaDavida uyise, kaze aphambukela ngakwesokunene langakwesokhohlo.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.
3 Kwasekusithi ngomnyaka wetshumi lesificaminwembili wenkosi uJosiya, inkosi yathuma uShafani indodana kaAzaliya indodana kaMeshulamu, umabhalane, endlini yeNkosi, esithi:
Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati,
4 Yenyukela kuHilikhiya umpristi omkhulu ukuthi ahlanganise imali elethwe endlini yeNkosi, abalindi bombundu womnyango ababeyiqoqe ebantwini.
“Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu.
5 Kabayinikele esandleni sabenzi bomsebenzi abamiswe phezu kwendlu yeNkosi, kabayinike abenzi bomsebenzi osendlini yeNkosi, ukulungisa izikhala zendlu,
Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova,
6 kubabazi, lakubakhi, lakubabazi bamatshe, lokuthenga amapulanka lamatshe abaziweyo ukulungisa indlu.
amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova.
7 Kodwa akubalelwananga labo imali eyayinikelwe esandleni sabo ngoba benza ngokuthembeka.
Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”
8 UHilikhiya umpristi omkhulu wasesithi kuShafani umabhalane: Sengifice ugwalo lomlayo endlini yeNkosi. UHilikhiya wasenika uShafani ugwalo, waselufunda.
Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga.
9 UShafani umabhalane wasefika enkosini, wabuyisela ilizwi enkosini wathi: Izinceku zakho seziyithulule imali eficwe endlini, zayinikela esandleni sabenzi bomsebenzi abamiswe phezu kwendlu yeNkosi.
Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.”
10 UShafani umabhalane wasebika enkosini esithi: UHilikhiya umpristi unginike ugwalo. UShafani waselufunda phambi kwenkosi.
Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.
11 Kwasekusithi inkosi isizwile amazwi ogwalo lomlayo, yadabula izigqoko zayo.
Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake.
12 Inkosi yasilaya uHilikhiya umpristi loAhikhamu indodana kaShafani loAkhibhori indodana kaMikhaya loShafani umabhalane loAsaya inceku yenkosi, isithi:
Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti,
13 Hambani liyengibuzela eNkosini mina labantu loJuda wonke mayelana lamazwi alolugwalo oluficiweyo; ngoba yinkulu intukuthelo yeNkosi esesiyibaselwe, ngoba obaba kabawalalelanga amazwi alolugwalo, ukwenza konke okubhaliweyo mayelana lathi.
“Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”
14 Ngakho uHilikhiya umpristi loAhikhamu loAkhibhori loShafani loAsaya baya kuHulida umprofethikazi umkaShaluma indodana kaTikiva indodana kaHarihasi, umgcini wezigqoko. Wayehlala-ke eJerusalema esiGabeni seSibili. Basebekhuluma laye.
Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.
15 Wasesithi kibo: Itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli: Mtsheleni lowomuntu olithume kimi:
Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti,
16 Itsho njalo iNkosi: Khangela, ngizakwehlisela okubi kulindawo laphezu kwabakhileyo bayo, wonke amazwi ogwalo inkosi yakoJuda elufundileyo.
‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga.
17 Ngenxa yokuthi bangidelile, batshisela abanye onkulunkulu impepha, ukuze bangithukuthelise ngawo wonke umsebenzi wezandla zabo. Ngakho intukuthelo yami izavutha imelene lale indawo, ingacitshwa.
Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’
18 Kodwa enkosini yakoJuda elithumileyo ukubuza eNkosini, lizakutsho njalo kuyo: Itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli: Mayelana lamazwi eliwezwileyo:
Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva:
19 Ngoba inhliziyo yakho ibithambile, wazithoba phambi kweNkosi, lapho usizwa engikukhulume ngimelene lalindawo labakhileyo bayo, ukuthi bazakuba yincithakalo lesiqalekiso, wadabula izigqoko zakho, wakhala inyembezi phambi kwami, lami-ke ngizwile, kutsho iNkosi.
Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova.
20 Ngakho, khangela, ngizakubuthela kuboyihlo, njalo uzabuthelwa engcwabeni lakho ngokuthula, lamehlo akho kawayikubona bonke ububi engizabehlisela phezu kwalindawo. Basebebuyisela ilizwi enkosini.
Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’” Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.