< 2 Amakhosi 2 >

1 Kwasekusithi iNkosi isizamenyusela uElija emazulwini ngesivunguzane, uElija wahamba loElisha bevela eGiligali.
Yehova ali pafupi kutenga Eliya kupita kumwamba mu kamvuluvulu, Eliya ndi Elisa anali pa ulendo wopita ku Giligala.
2 UElija wasesithi kuElisha: Akuhlale lapha, ngoba iNkosi ingithumile eBhetheli. Kodwa uElisha wathi: Kuphila kukaJehova lokuphila komphefumulo wakho, kangiyikukutshiya. Basebesehlela eBhetheli.
Eliya anawuza Elisa kuti, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Beteli.” Koma Elisa anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapita ku Beteli.
3 Lamadodana abaprofethi ayeseBhetheli aphuma eza kuElisha, athi kuye: Uyazi yini ukuthi iNkosi izayisusa inkosi yakho lamuhla ekhanda lakho? Wasesithi: Yebo, mina ngiyazi; thulani.
Ana a aneneri a ku Beteli anabwera kwa Elisa namufunsa kuti, “Kodi ukudziwa kuti lero Yehova akuchotsera mbuye wako?” Elisa anayankha kuti, “Inde ndikudziwa, koma musakambe zimenezi.”
4 UElija wasesithi kuye: Elisha, akuhlale lapha, ngoba iNkosi ingithumile eJeriko. Kodwa wathi: Kuphila kukaJehova lokuphila komphefumulo wakho, kangiyikukutshiya. Basebefika eJeriko.
Ndipo Eliya anati kwa Elisa, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Yeriko.” Koma Elisa anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapita ku Yeriko.
5 Amadodana abaprofethi aseJeriko asesondela kuElisha, athi kuye: Uyazi yini ukuthi lamuhla iNkosi izasusa inkosi yakho ekhanda lakho? Wasesithi: Yebo, mina ngiyazi; thulani.
Ana a aneneri amene anali ku Yeriko anapita kwa Elisa, namufunsa kuti, “Kodi ukudziwa kuti lero Yehova akuchotsera mbuye wako?” Elisa anayankha kuti, “Inde ndikudziwa, koma inu musakambe zimenezi.”
6 UElija wasesithi kuye: Akuhlale lapha, ngoba iNkosi ingithumile eJordani. Kodwa wathi: Kuphila kukaJehova lokuphila komphefumulo wakho, kangiyikukutshiya. Basebehamba bobabili.
Ndipo Eliya anati kwa Elisa, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Yorodani.” Elisa anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapitirira ulendo wawo.
7 Amadoda angamatshumi amahlanu awamadodana abaprofethi asesiyakuma khatshana maqondana labo; bona bobabili basebesima eJordani.
Anthu makumi asanu mwa ana a aneneri anawatsatira nayima chapatali moyangʼanana nawo ndipo Eliya ndi Elisa anayima mʼmphepete mwa Yorodani.
8 UElija wasethatha isembatho sakhe, wasigoqa, watshaya amanzi, asedabuka ngapha langapha; bobabili basebechapha emhlabathini owomileyo.
Eliya anatenga chovala chake nachipinda, napanda madzi ndi chovalacho. Madziwo anagawikana, ena kwina ena kwina, ndipo awiriwo anawoloka powuma.
9 Kwasekusithi sebechaphile uElija wathi kuElisha: Cela engizakwenzela khona ngingakasuswa kuwe. UElisha wathi: Ake kuthi isabelo esiphindwe kabili somoya wakho sibe phezu kwami.
Atawoloka, Eliya anati kwa Elisa, “Ndifotokozere, ndikuchitire chiyani ndisanachotsedwe pamaso pako?” Elisa anayankha kuti, “Ndikupemphani kuti mundipatse magawo awiri a mphamvu za mzimu wanu wa uneneri.”
10 Wasesithi: Ucele ulutho olulukhuni; uba ungibona lapha ngisuswa kuwe, kuzakuba njalo kuwe; kodwa uba kungenjalo, kakuyikuba njalo.
Eliya anati, “Wapempha chinthu chapatali, komabe ukandiona pamene ndikuchotsedwa pamaso pako, mphamvu wapemphayi idzakhala yako, koma ukapanda kundiona sizidzachitika.”
11 Kwasekusithi besahamba, behamba bekhuluma, khangela-ke, kwaba lenqola yomlilo lamabhiza omlilo, kwabehlukanisa bobabili. UElija wasesenyukela emazulwini ngesivunguzane.
Akuyenda ndi kumakambirana, mwadzidzidzi galeta lamoto ndi akavalo amoto anaonekera ndi kuwasiyanitsa awiriwo, ndipo Eliya anapita kumwamba mʼkamvuluvulu.
12 UElisha wasekubona wamemeza wathi: Baba wami! Baba wami! Inqola yakoIsrayeli labamabhiza ayo! Njalo kazabe esambona. Wasebamba izigqoko zakhe, wazidabula zaba yiziqa ezimbili.
Elisa anaona zimenezi ndipo anafuwula kuti, “Abambo anga! Abambo anga! Magaleta a Israeli ndi anthu ake okwera pa akavalo!” Ndipo Elisa sanamuonenso Eliyayo. Pamenepo Elisa anagwira zovala zake nazingʼamba pakati.
13 Wasedobha isembatho sikaElija esawa kuye, wabuyela, wema ekhunjini lweJordani.
Iye anatola chovala cha Eliya chomwe chinagwa nabwerera ndi kukayima mʼmphepete mwa Yorodani.
14 Wasethatha isembatho sikaElija esawa kuye, watshaya amanzi esithi: Ingaphi iNkosi, uNkulunkulu kaElija? Yena-ke esewatshayile amanzi, ehlukana ngapha langapha; uElisha wasechapha.
Ndipo Elisa anatenga chovala chomwe chinagwa kuchokera kwa Eliya napanda nacho madzi. Iye anafunsa kuti, “Ali kuti Mulungu wa Eliya?” Atapanda madzi, madziwo anagawika pakati, ena kwina ena kwina, ndipo iye anawoloka.
15 Kwathi amadodana abaprofethi ayeseJeriko maqondana laye embona athi: Umoya kaElija uhlezi phezu kukaElisha. Asesiza ukumhlangabeza, akhothamela emhlabathini phambi kwakhe.
Ndipo ana a aneneri ochokera ku Yeriko atamuona anati, “Mzimu wa Eliya wakhazikika pa Elisa.” Ndipo anapita kukakumana naye nagwada ndi kuweramitsa mitu yawo pansi pamaso pake.
16 Asesithi kuye: Khangela khathesi, kulamadoda aqinileyo angamatshumi amahlanu kanye lenceku zakho; akuwayekele ahambe adinge inkosi yakho; mhlawumbe uMoya weNkosi uyenyusile wayiphosela kwenye yezintaba, loba kwesinye sezihotsha. Wasesithi: Lingathumi.
Ndipo anawuza Elisa kuti, “Ife atumiki anu tili ndi anthu amphamvu makumi asanu. Aloleni apite kuti akafunefune mbuye wanu. Mwina Mzimu wa Yehova wamutenga ndi kukamuponya ku phiri lina kapena ku chigwa china.” Elisa anayankha kuti, “Ayi, musawatume.”
17 Sebemphikelele waze waba lenhloni, wathi: Thumani. Basebethuma amadoda angamatshumi amahlanu; adinga insuku ezintathu, kodwa awamtholanga.
Koma anamukakamizabe mpaka Elisayo anachita manyazi moti sakanatha kukana. Choncho iye anati, “Atumizeni.” Ndipo anatumiza anthu makumi asanu amene anakafunafuna Eliya kwa masiku atatu koma sanamupeze.
18 Asebuyela kuye ehlezi eJeriko, wathi kuwo: Kangitshongo yini kini ukuthi: Lingahambi?
Atabwerera kwa Elisa (chifukwa anali akanali ku Yeriko), iye anawawuza kuti, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musapite?”
19 Amadoda omuzi asesithi kuElisha: Ake ukhangele, indawo yalumuzi inhle njengoba inkosi yami ibona; kodwa amanzi mabi, lomhlabathi kawuvundanga.
Anthu a mu mzindamo anati kwa Elisa, “Mbuye wathu, taonani mzinda uno uli pamalo pabwino, monga mukuoneramu, koma madzi ake ndi oyipa, nthaka yakenso ndi yosabereka.”
20 Wasesithi: Ngilethelani umganu omutsha, lifake itshwayi kuwo. Basebewuletha kuye.
Iye anati, “Patseni mbale yatsopano ndipo muyikemo mchere.” Ndipo anabweretsa mbaleyo kwa iye.
21 Wasephuma waya emthonjeni wamanzi, waphosela itshwayi kuwo, wathi: Itsho njalo iNkosi: Ngiwelaphile amanzi la; kakusayikuba khona ukufa lokungatheli okuvela lapho.
Kenaka Elisa anapita ku kasupe wa madziwo, nathiramo mchere mʼkasupemo nati, “Yehova akuti, ‘Ndachiritsa madzi awa. Madzi amenewa sadzabweretsanso imfa kapena kuchititsa kuti nthaka ikhale yosabereka.’”
22 Amanzi aseselatshwa kuze kube lamuhla, njengelizwi likaElisha alikhulumayo.
Kotero madziwo ndi abwino mpaka lero, molingana ndi mawu amene Elisa anayankhula.
23 Wasesenyuka esuka lapho waya eBhetheli; kwathi esenyuka endleleni kwaphuma abantwanyana emzini, bamklolodela bathi kuye: Yenyuka, mpabanga ndini! Yenyuka, mpabanga ndini!
Kuchokera kumeneko Elisa anapita ku Beteli. Ndipo pamene ankayenda mu msewu, anyamata ena achichepere anatuluka mu mzindamo nʼkumamuseka. Iwo ankanena kuti, “Choka iwe, wachidazi! Choka iwe wachidazi”
24 Wasenyemukula, wababona wabaqalekisa ngebizo leNkosi. Kwaphuma amabhere amabili amasikazi ehlathini, adabula abafana abangamatshumi amane lambili kubo.
Iye anatembenuka nawayangʼana ndipo anawatemberera mʼdzina la Yehova. Nthawi yomweyo panatulukira zimbalangondo ziwiri kuchokera kuthengo, ndi kuphapo anyamata 42.
25 Wasesuka lapho, waya entabeni iKharmeli, esuka lapho wabuyela eSamariya.
Ndipo iye anapita ku phiri la Karimeli. Pochoka kumeneko anabwerera ku Samariya.

< 2 Amakhosi 2 >