< 2 Amakhosi 18 >
1 Kwasekusithi ngomnyaka wesithathu kaHosheya indodana kaEla, inkosi yakoIsrayeli, uHezekhiya indodana kaAhazi inkosi yakoJuda waba yinkosi.
Mʼchaka chachitatu cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Hezekiya mwana wa Ahazi mfumu ya Yuda analowa ufumu.
2 Wayeleminyaka engamatshumi amabili lanhlanu lapho esiba yinkosi; wabusa iminyaka engamatshumi amabili lesificamunwemunye eJerusalema. Lebizo likanina lalinguAbhi indodakazi kaZekhariya.
Anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Abi, mwana wa Zekariya.
3 Wasesenza okulungileyo emehlweni eNkosi njengakho konke uDavida uyise akwenzayo.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
4 Yena wasusa indawo eziphakemeyo, wabhidliza insika eziyizithombe, wagamula izixuku, wachoboza inyoka yethusi uMozisi ayeyenzile, ngoba kuze kube yilezonsuku abantwana bakoIsrayeli babeyitshisela impepha; wayibiza ngokuthi nguNehushitani.
Anachotsa malo opembedzerako mafano, anaphwanya miyala yachipembedzo ndiponso anadula mafano a Asera. Iye anaphwanya njoka yamkuwa imene Mose anapanga, pakuti mpaka kufikira nthawi imeneyi Aisraeli amafukiza lubani kwa njoka imeneyi. (Imatchedwa Nehusitani).
5 Wathembela eNkosini, uNkulunkulu kaIsrayeli; okwathi emva kwakhe kakubanga khona onjengaye emakhosini wonke akoJuda, loba ayengaphambi kwakhe.
Hezekiya anadalira Yehova Mulungu wa Israeli. Kotero panalibe wina wofanana naye pakati pa mafumu onse a Yuda, asanakhale mfumu kapena atakhala kale mfumu.
6 Ngoba wanamathela eNkosini, kaphambukanga ekuyilandeleni, kodwa wagcina imilayo yayo iNkosi eyayilaya uMozisi.
Iye anakangamira Yehova ndipo sanamusiye koma anasunga malamulo amene Yehova anapatsa Mose.
7 LeNkosi yaba laye; loba ngaphi lapho aphumela khona waphumelela. Wavukela inkosi yeAsiriya, kayisebenzelanga.
Ndipo Yehova anali naye ndipo kulikonse kumene anapita zinthu zinkamuyendera bwino. Iye anagalukira mfumu ya ku Asiriya ndipo sanayitumikirenso.
8 Yena watshaya amaFilisti waze wafika eGaza lemingcele yayo, kusukela emphotshongweni wabalindi kuze kube semzini obiyelweyo.
Iye anakantha Afilisti kuyambira ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa. Anakafika mpaka ku Gaza ndi ku malire ake.
9 Kwasekusithi ngomnyaka wesine wenkosi uHezekhiya, owawungumnyaka wesikhombisa kaHosheya indodana kaEla, inkosi yakoIsrayeli, uShalimaneseri inkosi yeAsiriya wenyuka wamelana leSamariya, wayivimbezela.
Mʼchaka chachinayi cha Mfumu Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chiwiri cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Salimenezeri, mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Samariya ndi kuwuzinga
10 Basebeyithumba ekupheleni kweminyaka emithathu. Ngomnyaka wesithupha kaHezekhiya, owawungumnyaka wesificamunwemunye kaHosheya inkosi yakoIsrayeli, iSamariya yathunjwa.
Asiriya analanda mzindawu patatha zaka zitatu. Choncho mzinda wa Samariya unalandidwa chaka chachisanu ndi chimodzi cha Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya mfumu ya Israeli.
11 Inkosi yeAsiriya yathumbela uIsrayeli eAsiriya, yababeka eHala leHabori umfula weGozani, lemizini yamaMede.
Mfumu ya ku Asiriya inatenga Aisraeli kupita nawo ku ukapolo ku Asiriya ndipo anakawakhazika ku Hala, ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
12 Ngoba bengalilalelanga ilizwi leNkosi uNkulunkulu wabo, kodwa baseqa isivumelwano sayo, konke uMozisi inceku yeNkosi eyayikulayile; kabalalelanga, kabenzanga.
Izi zinachitika chifukwa sanamvere zonena za Yehova Mulungu wawo, koma anaphwanya pangano lake ndi zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anawalamula. Iwo sanamvere malamulowo kapena kuwagwiritsa ntchito.
13 Langomnyaka wetshumi lane wenkosi uHezekhiya, uSenakheribi inkosi yeAsiriya wenyuka wamelana layo yonke imizi yakoJuda ebiyelweyo, wayithumba.
Mʼchaka chakhumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, nayilanda.
14 UHezekhiya inkosi yakoJuda wasethumela enkosini yeAsiriya eLakishi esithi: Ngonile; buyela usuke kimi; okubeka phezu kwami ngizakuthwala. Inkosi yeAsiriya yasibeka phezu kukaHezekhiya inkosi yakoJuda amathalenta esiliva angamakhulu amathathu, lamathalenta angamatshumi amathathu egolide.
Choncho Hezekiya mfumu ya Yuda anatumiza uthenga kwa mfumu ya ku Asiriya ku Lakisi wonena kuti, “Ine ndalakwa. Chokani kuno ndipo ndidzakupatsani chilichonse chimene munene.” Mfumu ya ku Asiriya inalamula mfumu Hezekiya, mfumu ya Yuda, kuti azipereka makilogalamu a siliva okwana 3,000 ndi makilogalamu a golide 1,000.
15 UHezekhiya wasemnika sonke isiliva esatholakala endlini kaJehova lenothweni yendlu yenkosi.
Mfumu Hezekiya inapereka siliva yense amene anapezeka mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba zosungiramo chuma cha mfumu.
16 Ngalesosikhathi uHezekhiya waquma igolide ezivalweni zethempeli leNkosi, lemigubazini uHezekhiya inkosi yakoJuda ayekunamathisele, walinika inkosi yeAsiriya.
Nthawi imeneyi Hezekiya mfumu ya Yuda anakanganula golide amene anakuta zitseko ndi mphuthu za chipata cha Nyumba ya Yehova namupereka kwa mfumu ya ku Asiriya.
17 Inkosi yeAsiriya yasithuma uTharithani loRabi-Sarisi loRabi-Shake besuka eLakishi besiya enkosini uHezekhiya belebutho elinzima eJerusalema. Benyuka-ke bafika eJerusalema. Sebenyuke bafika bema emgelweni wechibi eliphezulu, elisemgwaqweni omkhulu wensimu yomwatshi.
Mfumu ya ku Asiriya inatuma Taritani, Rabusarisi ndi Rabusake pamodzi ndi gulu lalikulu la ankhondo, kwa Mfumu Hezekiya ku Yerusalemu kuchokera ku Lakisi. Iwo anafika ku Yerusalemu nakayima pafupi ndi ngalande ya madzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu waukulu wopita ku malo a Munda wa Mmisiri Wochapa.
18 Sebebize inkosi, kwaphumela kibo uEliyakhimi indodana kaHilikhiya owayengumphathi wendlu, loShebina umbhali, loJowa indodana kaAsafi umabhalane.
Iwo anayitana mfumu, ndipo Eliyakimu mwana wa Hilikiya woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa anthuwo.
19 URabi-Shake wasesithi kibo: Khulumani khathesi kuHezekhiya: Itsho njalo inkosi enkulu, inkosi yeAsiriya ithi: Yisibindi bani lesi, othembela kuso?
Ndipo Rabusake anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “‘Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, ‘Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?’
20 Uthi, kodwa yilizwi lendebe nje: Kulecebo lamandla empi. Usuthembe bani ukuthi ungivukele?
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
21 Khangela-ke, wena uthembele odondolweni lomhlanga owephukileyo, oluyiGibhithe, uba umuntu eseyama phezu kwalo, luzangena esandleni sakhe lusihlabe. Unjalo uFaro inkosi yeGibhithe kubo bonke abathembela kuye.
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.’”
22 Kodwa uba lisithi kimi: ENkosini uNkulunkulu wethu siyathemba; angithi yiyo elezindawo zayo eziphakemeyo lamalathi ayo uHezekhiya awasusileyo, wathi kuJuda leJerusalema: Phambi kwalelilathi lizakhonza eJerusalema?
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, “Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu.” Kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, “Muzipembedza pa guwa lansembe ili mu Yerusalemu?”
23 Ngakho-ke, akunike isibambiso enkosini yami, inkosi yeAsiriya, njalo ngizakunika amabhiza azinkulungwane ezimbili, uba wena ulakho ukunika abagadi bawo.
“‘Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
24 Pho, uzabuyisela emuva njani ubuso benduna eyodwa yabancinyane nje benceku zenkosi yami; wena-ke uthembele eGibhithe ngezinqola labagadi bamabhiza?
Ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo?
25 Kambe ngenyukile yini ukumelana lalindawo ngingelaJehova ukuyichitha? UJehova uthe kimi: Yenyuka umelane lalelilizwe, ulichithe.
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga malo ano popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.’”
26 UEliyakhimi indodana kaHilikhiya loShebina loJowa basebesithi kuRabi-Shake: Akukhulume lenceku zakho ngesiSiriya, ngoba siyasizwa; ungakhulumi lathi ngesiJuda endlebeni zabantu abasemdulini.
Pamenepo Eliyakimu mwana wa Hilikiya, Sebina ndi Yowa anawuza Rabusakeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
27 Kodwa uRabi-Shake wathi kubo: Inkosi yami ingithumile yini enkosini yakho lakuwe ukukhuluma lamazwi? Kakusebantwini yini abahlezi phezu komduli ukuze badle ubulongwe babo, banathe umchamo wabo kanye lani?
Koma Rabusake anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
28 URabi-Shake wasesima wamemeza ngelizwi elikhulu ngesiJuda, wakhuluma esithi: Zwanini ilizwi lenkosi enkulu, inkosi yeAsiriya.
Tsono Rabusake anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
29 Itsho njalo inkosi: UHezekhiya kangalikhohlisi, ngoba kayikuba lakho ukulikhulula esandleni sayo.
Zimene mfumu ikunena ndi izi: ‘Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni mʼdzanja langa.
30 Njalo uHezekhiya angalenzi lithembele eNkosini esithi: INkosi izasikhulula lokusikhulula, lalumuzi kawuyikunikelwa esandleni senkosi yeAsiriya.
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
31 Lingamlaleli uHezekhiya, ngoba itsho njalo inkosi yeAsiriya: Yenzani isivumelwano sokuthula lami, liphume lize kimi; dlanini-ke, ngulowo lalowo okwevini lakhe langulowo lalowo okomkhiwa wakhe, linathe, ngulowo lalowo amanzi omthombo wakhe;
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
32 ngize ngifike ngilithathe ngilise elizweni elifanana lelizwe lakini, ilizwe lamabele lewayini elitsha, ilizwe lesinkwa lezivini, ilizwe lamafutha emihlwathi loluju, ukuze liphile lingafi. Lingamlaleli uHezekhiya ngoba eliyenga esithi: INkosi izasikhulula.
mpaka nditabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanuli, dziko la tirigu ndi vinyo watsopano, dziko la chakudya ndi minda ya mipesa, dziko la mitengo ya olivi ndi uchi. Sankhani moyo osati imfa! “Musamvere zonena Hezekiya, pakuti iye akukusocheretsani ponena kuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’
33 Onkulunkulu bezizwe sebake bawakhulula yini ngulowo lalowo ilizwe lakhe esandleni senkosi yeAsiriya?
Kodi mulungu wa anthu a mtundu wina uliwonse wapulumutsapo dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
34 Bangaphi onkulunkulu beHamathi leArpadi? Bangaphi onkulunkulu beSefavayimi, beHena, leIva? Kambe bayikhulule yini iSamariya esandleni sami?
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu, Hena ndi Ivani? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
35 Ngobani kubo bonke onkulunkulu balawomazwe abakhulule ilizwe labo esandleni sami, ukuthi iNkosi ikhulule iJerusalema esandleni sami?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja langa? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
36 Kodwa abantu bathula, kabaze bamphendula lalizwi, ngoba umlayo wenkosi wawuyikuthi: Lingamphenduli.
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
37 UEliyakhimi indodana kaHilikhiya owayengumphathi wendlu, loShebina umbhali, loJowa indodana kaAsafi umabhalane, basebesiza kuHezekhiya izigqoko zidatshuliwe, bamtshela amazwi kaRabi-Shake.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu, mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza Hezekiya zonse zimene anayankhula Rabusake uja.