< 2 Amakhosi 15 >
1 Ngomnyaka wamatshumi amabili lesikhombisa kaJerobhowamu, inkosi yakoIsrayeli, uAzariya indodana kaAmaziya, inkosi yakoJuda, waba yinkosi.
Mʼchaka cha 27 cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Azariya mwana wa Amaziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Wayeleminyaka elitshumi lesithupha lapho esiba yinkosi; wasebusa iminyaka engamatshumi amahlanu lambili eJerusalema. Lebizo likanina lalinguJekoliya weJerusalema.
Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 16 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 52. Amayi ake anali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
3 Wasesenza okulungileyo emehlweni eNkosi njengakho konke uAmaziya uyise akwenzayo.
Iyeyo anachita zabwino pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
4 Kodwa indawo eziphakemeyo kazisuswanga; abantu babelokhu benikela imihlatshelo betshisa impepha endaweni eziphakemeyo.
Komabe malo opembedzerako mafano sanawachotse ndipo anthu anapitirizabe kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 UJehova wayitshaya inkosi, yasisiba ngumlephero kwaze kwaba lusuku lokufa kwayo. Yahlala endlini eyehlukanisiweyo. UJothamu indodana yenkosi wasephatha indlu, esahlulela abantu belizwe.
Ndipo Yehova analanga mfumu ndi nthenda ya khate mpaka tsiku limene inamwalira. Tsono mfumuyo inkakhala mʼnyumba yakeyake yapadera. Mwana wake Yotamu ndiye amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu ndiponso ndiye amene ankalamulira anthu mʼdzikomo.
6 Ezinye-ke zezindaba zikaAzariya, lakho konke akwenzayo, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoJuda?
Ntchito zina za Azariya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
7 UAzariya waselala laboyise, bamngcwaba kuboyise emzini kaDavida. UJothamu indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Azariya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
8 Ngomnyaka wamatshumi amathathu lesificaminwembili kaAzariya inkosi yakoJuda uZekhariya indodana kaJerobhowamu wabusa phezu kukaIsrayeli eSamariya inyanga eziyisithupha.
Mʼchaka cha 38 cha Azariya mfumu ya Yuda, Zekariya mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira miyezi isanu ndi umodzi.
9 Wasesenza okubi emehlweni eNkosi njengokwenza kwaboyise; kasukanga ezonweni zikaJerobhowamu indodana kaNebati owenza uIsrayeli one.
Ndipo iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira makolo ake. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
10 UShaluma indodana kaJabeshi wasemenzela ugobe, wamtshaya phambi kwabantu wambulala, wasebusa esikhundleni sakhe.
Salumu mwana wa Yabesi anachitira chiwembu Zekariya. Anamukantha anthu akuona, namupha, ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
11 Ezinye-ke zezindaba zikaZekhariya, khangela, zibhaliwe egwalweni lwemilando yamakhosi akoIsrayeli.
Ntchito zina za Zekariya, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
12 Leli yilizwi leNkosi eyalikhuluma kuJehu isithi: Amadodana akho azahlala esihlalweni sobukhosi sikaIsrayeli kuze kube sesizukulwaneni sesine. Kwaba njalo-ke.
Awa ndiwo mawu a Yehova amene anayankhula kwa Yehu kuti, “Ana ako adzalamulira Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
13 UShaluma indodana kaJabeshi waba yinkosi ngomnyaka wamatshumi amathathu lesificamunwemunye kaUziya inkosi yakoJuda; wabusa inyanga egcweleyo eSamariya.
Salumu mwana wa Yabesi anakhala mfumu mʼchaka cha 39 cha ulamuliro wa Uziya mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Samariya mwezi umodzi.
14 Ngoba uMenahema indodana kaGadi wenyuka esuka eTiriza, weza eSamariya, wamtshaya uShaluma indodana kaJabeshi eSamariya wambulala; wabusa esikhundleni sakhe.
Ndipo Menahemu mwana wa Gadi anachoka ku Tiriza napita ku Samariya nakantha Salumu mwana wa Yabesi ku Samariya, namupha ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwake.
15 Ezinye-ke zezindaba zikaShaluma, logobe lwakhe alwenzayo, khangela, kubhaliwe egwalweni lwemilando yamakhosi akoIsrayeli.
Ntchito zina za Salumu ndiponso za chiwembu chimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
16 Khona uMenahema wasetshaya iThifisa, lakho konke okwakukiyo, lemingcele yayo kusukela eTiriza, ngoba bengamvulelanga. Ngakho wayitshaya; bonke abesifazana bayo abakhulelweyo wabaqhaqha.
Nthawi imeneyo Menahemu, kuchokera ku Tiriza, anakathira nkhondo mzinda wa Tipisa ndi anthu onse amene anali mʼmenemo ndi dera lonse lozungulira chifukwa iwo anakana kutsekula zipata zawo. Iye anatenga katundu yense mu mzinda wa Tipisa ndi kutumbula akazi onse oyembekezera.
17 Ngomnyaka wamatshumi amathathu lesificamunwemunye kaAzariya inkosi yakoJuda uMenahema indodana kaGadi waba yinkosi phezu kukaIsrayeli; wabusa iminyaka elitshumi eSamariya.
Mʼchaka cha 39 cha Azariya mfumu ya Yuda, Menahemu mwana wa Gadi anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira mu Samariya zaka khumi.
18 Wasesenza okubi emehlweni eNkosi; kasukanga ezonweni zikaJerobhowamu indodana kaNebati owenza uIsrayeli one, insuku zakhe zonke.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Nthawi yonse ya ulamuliro wake sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
19 UPhuli inkosi yeAsiriya weza wamelana lelizwe; uMenahema wasenika uPhuli amathalenta esiliva ayinkulungwane ukuze isandla sakhe sibe laye ukuqinisa umbuso esandleni sakhe.
Tsono Puli mfumu ya ku Asiriya inadzathira nkhondo dzikolo ndipo Menahemu anapatsa Puliyo makilogalamu 34,000 a siliva kuti amuthandize ndi kulimbikitsa ufumu wake.
20 UMenahema wasekhuphisa uIsrayeli imali, yabo bonke abantu abalamandla enothweni, ukupha inkosi yeAsiriya; amashekeli esiliva angamatshumi amahlanu kuleyo laleyondoda. Inkosi yeAsiriya yasibuyela, kayaze yahlala lapho elizweni.
Menahemu anapeza ndalamazo kudzera mu msonkho umene ankakhometsa Aisraeli. Munthu aliyense wachuma ankapereka masekeli a siliva makumi asanu kwa mfumu ya ku Asiriya. Choncho mfumu ya ku Asiriya inabwerera ndipo sinakhalenso mʼdzikomo.
21 Ezinye-ke zezindaba zikaMenahema, lakho konke akwenzayo, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoIsrayeli?
Ntchito zina za Menahemu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
22 UMenahema waselala laboyise; uPhekahiya indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Menahemu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Pekahiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
23 Ngomnyaka wamatshumi amahlanu kaAzariya inkosi yakoJuda uPhekahiya indodana kaMenahema waba yinkosi phezu kukaIsrayeli eSamariya, wabusa iminyaka emibili.
Mʼchaka cha makumi asanu a Azariya mfumu ya Yuda, Pekahiya mwana wa Menahemu anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka ziwiri.
24 Wasesenza okubi emehlweni eNkosi; kasukanga ezonweni zikaJerobhowamu indodana kaNebati owenza uIsrayeli one.
Pekahiya anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, omwe anachimwitsa nawo Israeli.
25 Kodwa uPheka indodana kaRemaliya, induna yakhe, wamenzela ugobe wamtshaya eSamariya enqabeni yendlu yenkosi, kanye loArigobi loAriye, njalo kanye laye abantu abangamatshumi amahlanu bamaGileyadi. Wambulala, waba yinkosi esikhundleni sakhe.
Ndipo Peka mwana wa Remaliya, mtsogoleri wake wa ankhondo, anamuchita chiwembu. Iye pamodzi ndi anthu makumi asanu a ku Giliyadi anapha Pekahiya pamodzi ndi Arigobu ndi Ariyeli mʼchipinda choteteza nyumba ya mfumu mu Samariya. Kotero Peka anapha Pekahiya ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
26 Ezinye-ke zezindaba zikaPhekahiya, lakho konke akwenzayo, khangela, kubhaliwe egwalweni lwemilando yamakhosi akoIsrayeli.
Ntchito zina za Pekahiya ndi zonse zimene anachita zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
27 Ngomnyaka wamatshumi amahlanu lambili kaAzariya inkosi yakoJuda uPheka indodana kaRemaliya waba yinkosi phezu kukaIsrayeli eSamariya; wabusa iminyaka engamatshumi amabili.
Mʼchaka cha 52 cha Azariya mfumu ya Yuda, Peka mwana wa Remaliya anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira zaka makumi awiri.
28 Wasesenza okubi emehlweni eNkosi; kasukanga ezonweni zikaJerobhowamu indodana kaNebati owenza uIsrayeli one.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
29 Ensukwini zikaPheka inkosi yakoIsrayeli kwafika uTigilathi Pileseri inkosi yeAsiriya, wathatha iIjoni, leAbeli-Beti-Mahaka, leJanowa, leKedeshi, leHazori, leGileyadi, leGalili, ilizwe lonke lakoNafithali; wabathumbela eAsiriya.
Nthawi ya Peka mfumu ya Israeli, Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kudzalanda Iyoni, Abeli-Beti-Maaka, Yanowa, Kedesi ndi Hazori. Mfumu ya ku Asiriya inatenga Giliyadi ndi Galileya, kuphatikizanso madera onse a Nafutali ndipo anatumiza Aisraeli ku Asiriya.
30 UHosheya indodana kaEla wasesenza ugobe emelene loPheka indodana kaRemaliya, wamtshaya wambulala, waba yinkosi esikhundleni sakhe ngomnyaka wamatshumi amabili kaJothamu, indodana kaUziya.
Kenaka Hoseya mwana wa Ela anachitira chiwembu Peka mwana wa Remaliya. Anamukantha ndi kumupha ndipo anakhala mfumu mʼmalo mwake mʼchaka makumi awiri cha Yotamu mwana wa Uziya.
31 Ezinye-ke zezindaba zikaPheka, lakho konke akwenzayo, khangela, kubhaliwe egwalweni lwemilando yamakhosi akoIsrayeli.
Ntchito zina za Peka ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 Ngomnyaka wesibili kaPheka indodana kaRemaliya inkosi yakoIsrayeli uJothamu indodana kaUziya inkosi yakoJuda waba yinkosi.
Mʼchaka chachiwiri cha Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli, Yotamu mwana wa Uziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
33 Wayeleminyaka engamatshumi amabili lanhlanu lapho esiba yinkosi; wabusa iminyaka elitshumi lesithupha eJerusalema. Lebizo likanina lalinguJerusha indodakazi kaZadoki.
Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Amayi ake anali Yerusa mwana wa Zadoki.
34 Wasesenza okulungileyo emehlweni eNkosi; wenza njengakho konke uUziya uyise ayekwenzile.
Iye anachita zabwino pamaso pa Yehova monga anachitira Uziya abambo ake.
35 Kodwa indawo eziphakemeyo kazisuswanga; abantu babelokhu benikela imihlatshelo betshisa impepha endaweni eziphakemeyo. Yena wakha isango elingaphezulu endlini yeNkosi.
Komabe malo opembedzera mafano sanawachotse ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
36 Ezinye-ke zezindaba zikaJothamu, azenzayo, kazibhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoJuda?
Ntchito zina za Yotamu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
37 Ngalezonsuku iNkosi yaqala ukuthumela koJuda uRezini inkosi yeSiriya loPheka indodana kaRemaliya.
(Nthawi imeneyo, Yehova anayamba kumatuma Rezini mfumu ya Aaramu ndi Peka mwana wa Remaliya kudzamenyana ndi Yuda).
38 UJothamu waselala laboyise, wangcwatshelwa kuboyise emzini kaDavida uyise. UAhazi indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Yotamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Ahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.