< 2 Amakhosi 14 >

1 Ngomnyaka wesibili kaJowashi indodana kaJehowazi, inkosi yakoIsrayeli, uAmaziya indodana kaJowashi inkosi yakoJuda waba yinkosi.
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Wayeleminyaka engamatshumi amabili lanhlanu lapho esiba yinkosi; wabusa iminyaka engamatshumi amabili lesificamunwemunye eJerusalema. Lebizo likanina lalinguJehowadani weJerusalema.
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 Wasesenza okulungileyo emehlweni eNkosi, kodwa kungenjengoDavida uyise; wenza njengakho konke uJowashi uyise akwenzayo.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 Loba kunjalo indawo eziphakemeyo kazisuswanga; abantu babelokhu benikela imihlatshelo betshisa impepha endaweni eziphakemeyo.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 Kwasekusithi umbuso wakhe usuqinisiwe esandleni sakhe, watshaya inceku zakhe ezazitshaye inkosi uyise.
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 Kodwa abantwana bababulali kababulalanga, njengokubhaliweyo ogwalweni lomlayo kaMozisi lapho iNkosi eyalaya khona isithi: Oyise kabayikubulawa ngenxa yabantwana, labantwana kabayikubulawa ngenxa yaboyise, kodwa wonke umuntu uzabulawelwa isono sakhe.
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 Yena wasetshaya amaEdoma azinkulungwane ezilitshumi esihotsheni setshwayi, wathumba iSela ngempi, wabiza ibizo layo ngokuthi yiJokhitheyeli, kuze kube lamuhla.
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 Khona uAmaziya wathuma izithunywa kuJehowashi indodana kaJehowahazi indodana kaJehu, inkosi yakoIsrayeli, esithi: Woza sikhangelane ubuso ngobuso.
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 UJehowashi inkosi yakoIsrayeli wasethumela kuAmaziya inkosi yakoJuda esithi: Ukhula oluhlabayo oluseLebhanoni lwathumela emsedarini oseLebhanoni lusithi: Nika indodakazi yakho endodaneni yami ibe ngumkayo; kwasekusedlula isilo seganga esiseLebhanoni, salugxoba ukhula oluhlabayo.
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 Uyitshayile lokuyitshaya iEdoma, inhliziyo yakho isikuphakamisile; dumiseka, uhlale endlini yakho; ngoba kungani uzivusela ububi ukuze uwe wena loJuda kanye lawe?
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 Kodwa uAmaziya kezwanga. Ngakho uJehowashi inkosi yakoIsrayeli wenyuka, yena-ke loAmaziya inkosi yakoJuda bakhangelana ubuso ngobuso eBeti-Shemeshi eyakoJuda.
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 UJuda wasetshaywa phambi kukaIsrayeli; basebebaleka, ngulowo lalowo waya ethenteni lakhe.
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 UJehowashi inkosi yakoIsrayeli wasembamba uAmaziya inkosi yakoJuda, indodana kaJehowashi indodana kaAhaziya, eBeti-Shemeshi; wafika eJerusalema, wadilizela phansi umduli weJerusalema, kusukela esangweni lakoEfrayimi kusiya esangweni lengonsi, ingalo ezingamakhulu amane.
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 Wasethatha lonke igolide lesiliva, lezitsha zonke ezatholakala endlini kaJehova lezendlini zenotho zendlu yenkosi, kanye labayisibambiso, wasebuyela eSamariya.
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 Ezinye-ke zezindaba zikaJehowashi azenzayo, lamandla akhe, lokuthi walwa njani loAmaziya inkosi yakoJuda, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoIsrayeli?
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 UJehowashi waselala laboyise, wangcwatshelwa eSamariya emakhosini akoIsrayeli. UJerobhowamu indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 UAmaziya indodana kaJowashi, inkosi yakoJuda, wasephila iminyaka elitshumi lanhlanu emva kokufa kukaJehowashi indodana kaJehowahazi inkosi yakoIsrayeli.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 Ezinye-ke zezindaba zikaAmaziya, kazibhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoJuda?
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 Basebemenzela ugobe eJerusalema, wabalekela eLakishi; kodwa bathuma bamlandela eLakishi, bambulalela khona.
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 Basebemthwala ngamabhiza, wangcwatshelwa eJerusalema kuboyise emzini kaDavida.
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 Bonke abantu bakoJuda basebethatha uAzariya, owayeleminyaka elitshumi lesithupha, bambeka waba yinkosi esikhundleni sikayise uAmaziya.
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 Yena wakha iElathi, wayibuyisela koJuda emva kokulala kwenkosi laboyise.
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 Ngomnyaka wetshumi lanhlanu kaAmaziya indodana kaJowashi inkosi yakoJuda uJerobhowamu indodana kaJowashi inkosi yakoIsrayeli waba yinkosi eSamariya; wabusa iminyaka engamatshumi amane lanye.
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 Wasesenza okubi emehlweni eNkosi; kasukanga ezonweni zonke zikaJerobhowamu indodana kaNebati owenza uIsrayeli one.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 Yena wabuyisela umngcele wakoIsrayeli kusukela ekungeneni kweHamathi kuze kufike elwandle lwamagceke, njengokwelizwi leNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli, eyalikhuluma ngesandla senceku yayo uJona indodana kaAmithayi umprofethi, owayevela eGathi-Heferi.
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 Ngoba iNkosi yabona ukuhlupheka kukaIsrayeli, kwakubaba kakhulu, ngoba kwakungekho ovalelweyo, njalo engekho okhululekileyo, njalo kungelamsizi kaIsrayeli.
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 INkosi yayingatshongo-ke ukuthi izalesula ibizo likaIsrayeli ngaphansi kwamazulu; kodwa yabasindisa ngesandla sikaJerobhowamu indodana kaJowashi.
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 Ezinye-ke zezindaba zikaJerobhowamu, lakho konke akwenzayo, lamandla akhe, ukuthi walwa njani, lokuthi wayibuyisela njani koIsrayeli iDamaseko leHamathi, engeyeJuda, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoIsrayeli?
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 UJerobhowamu waselala laboyise, emakhosini akoIsrayeli. UZekhariya indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Amakhosi 14 >