< 2 Amakhosi 12 >

1 Ngomnyaka wesikhombisa kaJehu uJehowashi waba yinkosi; wabusa iminyaka engamatshumi amane eJerusalema. Lebizo likanina lalinguZibiya weBherishebha.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri cha Yehu, Yowasi anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka makumi anayi. Amayi ake anali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 UJehowashi wasesenza okulungileyo emehlweni eNkosi zonke izinsuku zakhe uJehoyada umpristi amfundisa ngazo.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova masiku onse amene wansembe Yehoyada ankamulangiza.
3 Kodwa indawo eziphakemeyo kazisuswanga; abantu babelokhu benikela imihlatshelo betshisa impepha endaweni eziphakemeyo.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo opembedzerako mafanowo.
4 UJehowashi wasesithi kubapristi: Yonke imali yezinto ezehlukanisiweyo elethwa endlini kaJehova, imali yalowo lalowo odlulayo kwababaliweyo, imali yalowo lalowo umuntu ayilinganisileyo, yonke imali, okuvela enhliziyweni yaloba nguwuphi umuntu ukuyiletha endlini yeNkosi;
Yowasi anati kwa ansembe, “Tolerani ndalama zonse zimene zimaperekedwa monga chopereka chopatulika ku Nyumba ya Yehova, ndalama zonse zamsonkho wa munthu aliyense, ndalama zomwe munthu amapereka akalonjeza ndiponso ndalama zimene munthu amapereka mwaufulu ku Nyumba ya Yehova.
5 abapristi kabayithathe kubo, ngulowo lalowo komejwayeleyo, balungise izikhala zendlu, loba kungaphi lapho okutholwa khona izikhala.
Wansembe aliyense alandire ndalamazo kuchokera kwa abwenzi ake, ndipo zigwiritsidwe ntchito yokonzera chilichonse chimene chipezeke kuti ndi chowonongeka mʼnyumbayo.”
6 Kodwa kwathi ngomnyaka wamatshumi amabili lantathu wenkosi uJehowashi abapristi babengakalungisi izikhala zendlu.
Koma pofika chaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi, ansembewo anali asanakonze nyumbayo.
7 Inkosi uJehowashi yasibiza uJehoyada umpristi labapristi, yathi kibo: Kungani lingalungisi izikhala zendlu? Ngakho-ke lingathathi imali kwelibejwayeleyo kodwa liyinikele izikhala zendlu.
Choncho Mfumu Yowasi inayitanitsa wansembe Yehoyada ndi ansembe ena ndipo inafunsa kuti, “Chifukwa chiyani simukukonza malo owonongeka a mʼnyumbayi? Musasungenso ndalama zina zochokera kwa abwenzi anu, koma muzipereke kuti akonzere nyumbayi.”
8 Abapristi basebevuma ukuthi kabasayikuthatha imali ebantwini lokuthi kabayikulungisa izikhala zendlu.
Ansembe anavomera kuti salandiranso ndalama kuchokera kwa anthu ndipo kuti sindiwo amene ati akonzenso nyumbayo.
9 UJehoyada umpristi wasethatha ibhokisi elilodwa, wabhoboza isikhala esivalweni salo, walibeka eceleni kwelathi ngakwesokunene nxa umuntu engena endlini yeNkosi. Abapristi-ke abalinda umbundu bafaka kulo yonke imali eyalethwa endlini yeNkosi.
Koma wansembe Yehoyada anatenga bokosi ndipo anabowola chivundikiro chake. Anayika bokosilo pambali pa guwa lansembe, kudzanja lamanja la aliyense amene akulowa mʼNyumba ya Yehovayo. Ansembe amene ankalondera pa khomopo ankaponya mʼbokosi ndalama zonse zimene ankabwera nazo ku nyumba ya Yehova.
10 Kwakusithi sebebona ukuthi imali isinengi ebhokisini, umabhalane wenkosi, lompristi omkhulu benyuke, bayibophe bayibale imali eyatholwa endlini yeNkosi.
Nthawi zonse akaona kuti mʼbokosimo muli ndalama zambiri, mlembi wa mfumu ndi mkulu wa ansembe ankabwera ndipo ankawerenga ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku Nyumba ya Yehova ndi kuziyika mʼmatumba.
11 Basebenikela imali elinganisiweyo ezandleni zabenzi bomsebenzi, zababonisi bendlu yeNkosi, bayikhuphela kubabazi bezigodo lakubakhi ababesebenza endlini yeNkosi,
Ankati akadziwa kuti ndalamazo zilipo zingati, ankazipereka kwa anthu amene ankayangʼanira ntchito yokonza nyumbayo. Ndalamazo ankalipira anthu amene ankagwira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova, amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba,
12 lakwabakha ngamatshe lakubabazi bamatshe, lokuthenga izigodo lamatshe abaziweyo ukulungisa izikhala zendlu yeNkosi, lakukho konke okwakhutshelwa indlu ukuyilungisa.
amisiri a miyala ndiponso anthu ophwanya miyala. Iwo ankagula matabwa ndi miyala yosema yokonzera Nyumba ya Yehova ndipo ankalipira zinthu zonse zofunika pokonzanso nyumbayo.
13 Kodwa kayenzelwanga indlu yeNkosi imiganu yesiliva, izindlawu, imiganu yokufafaza, izimpondo zokukhaliswa, laziphi izitsha zegolide lezitsha zesiliva zemali eyalethwa endlini yeNkosi,
Koma ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku nyumbayo sanagulire siliva wopangira mabeseni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, malipenga kapena ziwiya zina zilizonse zagolide kapena zasiliva za ku Nyumba ya Yehova.
14 kodwa bayinika abenzi bomsebenzi, basebelungisa ngayo indlu yeNkosi.
Ndalamazi anazipereka kwa anthu antchito amene anazigwiritsa ntchito yokonzera nyumbayo.
15 Njalo kababalelananga labantu abanikela imali esandleni sabo, ukupha abenzi bomsebenzi, ngoba benza ngokuthembeka.
Koma sanawafunse kuti afotokoze kagwiritsidwe ntchito ka ndalama zolipira amene ankagwira ntchito, chifukwa anthuwo ankagwira ntchitoyo mokhulupirika kwambiri.
16 Imali yomnikelo wecala lemali yeminikelo yesono kayilethwanga endlini yeNkosi; yayingeyabapristi.
Ndalama zomwe zinkaperekedwa pa nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo sanabwere nazo ku Nyumba ya Yehova pakuti zinali za ansembe.
17 Ngalesosikhathi uHazayeli inkosi yeSiriya wenyuka walwa emelene leGathi, wayithumba. UHazayeli wasekhangelisa ubuso bakhe ukwenyuka amelane leJerusalema.
Pa nthawi imeneyo, Hazaeli, mfumu ya Aramu anapita kukathira nkhondo mzinda wa Gati nawulanda. Kenaka Hazaeli anatembenuka kupita kukathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu.
18 Kodwa uJehowashi inkosi yakoJuda wathatha zonke izinto ezingcwelisiweyo uJehoshafathi loJoramu loAhaziya oyise, amakhosi akoJuda, ababezingcwelisile, lezakhe izinto ezingcwelisiweyo, legolide lonke elatholwa enothweni yendlu kaJehova lendlu yenkosi, wakuthumela kuHazayeli inkosi yeSiriya. Wasesenyuka wasuka eJerusalema.
Koma Yowasi mfumu ya Yuda anatenga zinthu zonse zopatulika zomwe anazipatula Yehosafati, Yehoramu, ndi Ahaziya abambo ake, mafumu a Yuda ndi mphatso zonse zomwe iye mwini anazipereka: golide yense amene anapezeka mʼnyumba yosungiramo chuma cha mʼnyumba ya Yehova ndi zomwe zinali mʼnyumba ya mfumu, nazipereka kwa Hazaeli mfumu ya Aramu. Pamenepo iye anachoka ku Yerusalemuko.
19 Ezinye-ke zezindaba zikaJowashi, lakho konke akwenzayo, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoJuda?
Ndipo ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
20 Inceku zakhe zasezisukuma zenza ugobe, zamtshaya uJowashi endlini yeMilo eyehlela eSila.
Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu ndi kumupha ku Beti Milo, pa njira yotsikira ku Silo.
21 Ngoba oJozakari indodana kaShimeyathi loJehozabadi indodana kaShomeri, inceku zakhe, bamtshaya, wafa; basebemngcwaba kuboyise emzini kaDavida. UAmaziya indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Yozakara mwana wa Simeati ndi Yehozabadi mwana wa Someri atumiki ake anamukantha nafa. Ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Amakhosi 12 >