< 2 Amakhosi 11 >

1 UAthaliya unina kaAhaziya esebonile ukuthi indodana yakhe ifile, wasukuma wachitha yonke inzalo yesikhosini.
Ataliya amayi ake a Ahaziya ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakawononga banja lonse la mfumu.
2 Kodwa uJehosheba indodakazi yenkosi uJoramu, udadewabo kaAhaziya, wathatha uJowashi indodana kaAhaziya, wameba phakathi kwamadodana enkosi abulawayo, yena lomlizane wakhe ekamelweni lokulala. Basebemfihla ebusweni bukaAthaliya ukuze angabulawa.
Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa Mfumu Yehoramu, mlongo wake wa Ahaziya, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, namusunga kutali ndi ana a mfumu amene ankati awaphewo. Anamuyika iye pamodzi ndi mlezi wake mʼchipinda chogona chamʼkati kubisira Ataliya kotero iye sanaphedwe.
3 Wayelaye-ke efihliwe endlini yeNkosi iminyaka eyisithupha; uAthaliya wasebusa phezu kwelizwe.
Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi mlezi wake mʼnyumba ya Yehova kwa zaka zisanu ndi chimodzi pamene Ataliya ankalamulira dzikolo.
4 Ngomnyaka wesikhombisa uJehoyada wasethuma wathatha izinduna zamakhulu, lamaKariti kanye labalindi, wabaletha kuye endlini yeNkosi. Wenza isivumelwano labo, wabafungisa endlini yeNkosi, wabatshengisa indodana yenkosi.
Koma mʼchaka chachisanu ndi chiwiri, Yehoyada anatumiza mawu kukayitana atsogoleri olamulira asilikali 100 olondera mfumu ndiponso alonda olonda nyumba yaufumu ndipo anabwera nawo mʼNyumba ya Yehova. Iye anapangana nawo pangano ndipo anawalumbiritsa mʼnyumba ya Yehova. Kenaka anawaonetsa mwana wamwamuna wa mfumu uja.
5 Wasebalaya esithi: Nansi into elizayenza: Ingxenye eyodwa kwezintathu yenu elingena ngesabatha izakuba ngabalindi bomlindo wendlu yenkosi,
Yehoyada anawalamulira kuti, “Chimene muti muchite ndi ichi: Inu magulu atatu amene muti mudzakhale pa ntchito tsiku la Sabata, gulu loyamba lidzalondera nyumba ya mfumu,
6 lengxenye eyodwa kwezintathu izakuba sesangweni leSuri, lengxenye eyodwa kwezintathu esangweni ngemva kwabalindi; ngokunjalo lizalinda umlindo wendlu, ingafohlelwa.
gulu lachiwiri lidzalondera Chipata cha Suri, ndipo gulu lachitatu lidzalondera chipata cha kumbuyo kwa asilikali amene amasinthana polondera nyumbayo.
7 Lengxenye ezimbili zenu lonke eliphuma ngesabatha, bona bazagcina umlindo wendlu yeNkosi mayelana lenkosi.
Ndipo inu amene muli mʼmagulu ena awiri amene simugwira ntchito pa tsiku la Sabata, nonse mudzalondere mfumu ku nyumbayo.
8 Lizazingelezela inkosi inhlangothi zonke, ngulowo lalowo elezikhali esandleni sakhe; lozangena kokuhleliweyo uzabulawa. Libe lenkosi ekuphumeni kwayo lekungeneni kwayo.
Mudzakhale mozungulira mfumuyo, munthu aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake. Wina aliyense amene adzakuyandikireni adzayenera kuphedwa. Muzikhala pafupi ndi mfumu kulikonse kumene ikupita.”
9 Induna zamakhulu zasezisenza njengakho konke uJehoyada umpristi akulayayo; zathatha, yileyo laleyo abantu bayo abangena ngesabatha lalabo abaphuma ngesabatha, zafika kuJehoyada umpristi.
Atsogoleri olamulira asilikali 100 aja anachitadi zonse monga analamulira wansembe Yehoyada. Aliyense anatenga anthu ake, iwo amene amakagwira ntchito pa tsiku la Sabata ndi amene amapita kukapuma ndipo anabwera kwa wansembe Yehoyada.
10 Umpristi wasenika izinduna zamakhulu imikhonto lezihlangu ezazingezenkosi uDavida ezazisendlini yeNkosi.
Ndipo wansembeyo anawapatsa asilikaliwo mikondo ndi zishango zimene zinali za mfumu Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Yehova.
11 Abalindi basebesima, ngulowo lalowo elezikhali esandleni sakhe, kusukela kwesokunene sendlu kusiya kwesokhohlo sendlu, ngaselathini langasendlini, enkosini inhlangothi zonke.
Alondawo, aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake, anayima mozungulira mfumu, pafupi ndi guwa lansembe ndi nyumbayo, kuchokera mbali ya kummwera mpaka mbali ya kumpoto kwa nyumbayo.
12 Waseyikhupha indodana yenkosi, wayethesa umqhele, wayinika ubufakazi; bayibeka yaba yinkosi, bayigcoba, batshaya izandla, basebesithi: Kayiphile inkosi!
Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumuyo namuveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano ndi kumuyika kukhala mfumu. Iwo anamudzoza ndipo anthu anamuwombera mʼmanja akufuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
13 UAthaliya esizwa umsindo wabalindi lowabantu waya ebantwini endlini yeNkosi;
Ataliya atamva phokoso limene alonda ndi anthuwo amachita, anapita ku Nyumba ya Yehova kumene kunali anthuwo.
14 wabona, khangela-ke, inkosi yayimi ngasensikeni njengomkhuba, lezinduna labavutheli bezimpondo bengasenkosini, labantu bonke belizwe bethokoza bavuthela izimpondo. UAthaliya wasedabula izigqoko zakhe, wamemeza wathi: Ugobe! Ugobe!
Iye anayangʼana naona mfumu itayima pa chipilala, potsata mwambo waufumu. Atsogoleri a asilikali ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderalo ankasangalala ndi kuyimba malipenga. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake nafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
15 UJehoyada umpristi waselaya induna zamakhulu, abaphathi bebutho, wathi kubo: Mkhupheleni ngaphandle kokuhleliweyo, lomlandelayo limbulale ngenkemba. Ngoba umpristi wathi: Kangabulawelwa endlini kaJehova.
Wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a asilikali 100 amene amayangʼanira asilikaliwo kuti, “Mutulutseni ameneyo pakati panu ndipo muphe ndi lupanga aliyense amene adzamutsata.” Pakuti nʼkuti wansembeyo atanena kuti, “Ataliyayo asaphedwere mʼNyumba ya Yehova.”
16 Basebembamba ngezandla, wasehamba ngendlela yokungena kwamabhiza endlini yenkosi, wabulawelwa khonapho.
Choncho anamugwira pamene amafika pa malo amene akavalo amalowera ku nyumba ya mfumu ndipo anamuphera pamenepo.
17 UJehoyada wasesenza isivumelwano phakathi kukaJehova lenkosi labantu ukuthi babe ngabantu bakaJehova; laphakathi kwenkosi labantu.
Tsono Yehoyada anachititsa pangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu kuti adzakhala anthu a Yehova. Iye anachititsanso pangano pakati pa mfumu ndi anthu.
18 Bonke abantu belizwe basebengena endlini kaBhali, bayidilizela phansi; amalathi akhe lezithombe zakhe baziphahlaza ngokupheleleyo, loMathani umpristi kaBhali bambulala phambi kwamalathi. Umpristi wasebeka abaphathi phezu kwendlu yeNkosi.
Anthu onse a mʼdzikomo anapita ku nyumba ya Baala nakayigwetsa. Iwo anaphwanya kotheratu maguwa ansembe ndi mafano ake ndipo anapha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwa pomwepo. Pamenepo wansembe Yehoyada anasankha oyangʼanira Nyumba ya Yehova.
19 Wasethatha izinduna zamakhulu lamaKariti labalindi labo bonke abantu belizwe, bayehlisa inkosi isuka endlini kaJehova, beza ngendlela yesango labalindi endlini yenkosi. Yasihlala esihlalweni sobukhosi samakhosi.
Iye anatenga atsogoleri a asilikali 100 aja, alonda olonda nyumba yaufumu pamodzi ndi anthu onse a mʼdzikomo ndipo onse pamodzi anayitulutsa mfumu mʼNyumba ya Yehova ndi kukalowa ku nyumba yaufumu podzera pa chipata cha alonda. Ndipo mfumuyo inakhala pa mpando wake waufumu.
20 Bonke abantu belizwe basebethokoza. Umuzi wasusiba lokuthula, sebembulele uAthaliya ngenkemba ngasendlini yenkosi.
Choncho anthu onse a mʼdzikomo anasangalala. Ndipo mu mzindamo munakhala bata chifukwa Ataliya nʼkuti ataphedwa ndi lupanga ku nyumba ya mfumu.
21 UJehowashi wayeleminyaka eyisikhombisa lapho esiba yinkosi.
Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anayamba kulamulira.

< 2 Amakhosi 11 >