< 2 Amakhosi 10 >
1 Njalo uAhabi wayelamadodana angamatshumi ayisikhombisa eSamariya. UJehu wasebhala izincwadi, wazithumela eSamariya kubabusi beJizereyeli, abadala, lakubondli bamadodana kaAhabi, esithi:
Tsono Ahabu anali ndi ana aamuna 70 a ku Samariya. Ndipo Yehu analemba makalata nawatumiza ku Samariya kwa atsogoleri a mu mzinda wa Yezireeli, kwa akuluakulu ndiponso kwa amene ankalera ana a Ahabu, nati,
2 Ngakho-ke nxa lincwadi ifika kini, lokhu amadodana enkosi yenu akini, futhi izinqola lamabhiza kukini, lomuzi obiyelweyo, lezikhali,
“Inu mukangolandira kalatayi, popeza ana a mbuye wanu ali ndi inu ndiponso muli ndi magaleta ndi akavalo, mzinda wotetezedwa ndi zida zankhondo,
3 ziboneleni-ke ongcono kakhulu lofaneleyo kulabo bonke ebantwaneni benkosi yenu, limbeke esihlalweni sobukhosi sikayise, lilwele indlu yenkosi yenu.
sankhani mwana wa mbuye wanu amene ndi wooneka bwino ndiponso woyenera, mulowetseni ufumu wa abambo ake. Kenaka muchite nkhondo kuteteza nyumba ya mbuye wanu.”
4 Kodwa besaba kakhulukazi bathi: Khangelani, amakhosi amabili kawemanga phambi kwakhe; thina-ke sizakuma njani?
Koma anthuwo anachita mantha kwambiri ndipo anati, “Taonani, mafumu awiri sanathe kulimbana naye, nanga ife tingathe bwanji?”
5 Umphathi wendlu lomphathi womuzi labadala labondli babantwana bathumela kuJehu besithi: Siyizinceku zakho, sizakwenza konke okutshoyo kithi. Kasiyikubeka muntu abe yinkosi. Yenza okuhle emehlweni akho.
Choncho woyangʼanira nyumba ya mfumu, bwanamkubwa wa mzinda, akuluakulu ena ndiponso olera anawo anatumiza uthenga uwu kwa Yehu: “Ife ndife atumiki anu ndipo tidzachita chilichonse chomwe mutiwuze. Sitidzasankha munthu wina aliyense kukhala mfumu ndipo chitani chimene mukuganiza kuti nʼchabwino kwa inu.”
6 Wasebabhalela incwadi okwesibili esithi: Uba lingabami, lilalela ilizwi lami, thathani amakhanda alawomadoda, amadodana enkosi yenu, lize kimi eJizereyeli ngalesisikhathi kusasa. Lamadodana enkosi, abantu abangamatshumi ayisikhombisa, ayelezikhulu zomuzi ezaziwakhulisa.
Ndipo Yehu anawalembera kalata yachiwiri yonena kuti, “Ngati inu muli mbali yanga ndi kuti mudzandimvera, mudule mitu ya ana a mbuye wanu ndipo mubwere nayo kwa ine ku Yezireeli mawa nthawi ngati yomwe ino.” Tsono ana a mfumu onse 70 anali pamodzi ndi akuluakulu a mu mzindamo, amene ankawalera.
7 Kwasekusithi ekufikeni kwencwadi kubo, bathatha amadodana enkosi, babulala abantu abangamatshumi ayisikhombisa, bafaka amakhanda awo ezitsheni, bawesa kuye eJizereyeli.
Kalatayo itafika, anthuwo anatenga ana a mfumu 70 aja ndi kuwapha onse. Anayika mitu yawo mʼmadengu ndi kuyitumiza ku Yezireeli kwa Yehu.
8 Kwasekusiza isithunywa sambikela sisithi: Sebewalethile amakhanda amadodana enkosi. Wasesithi: Abekeni abe zinqumbi ezimbili ekungeneni kwesango kuze kube sekuseni.
Mthenga uja atafika, anamuwuza Yehu kuti, “Abweretsa mitu ya ana a mfumu.” Ndipo Yehu analamula kuti, “Unjikani mituyo mʼmilu iwiri pa chipata cha mzinda ndipo ikhale pamenepo mpaka mmawa.”
9 Kwasekusithi ekuseni waphuma wema wathi ebantwini bonke: Lina lilungile. Khangelani, mina ngenzela inkosi yami ugobe, ngayibulala; pho, ngubani obulele bonke laba?
Mmawa mwake Yehu anatuluka. Iye anayimirira pamaso pa anthu onse ndipo anati, “Inu ndinu osalakwa. Ndine amene ndinachita chiwembu mbuye wanu ndi kumupha, koma kodi wapha anthu onsewa ndani?
10 Yazini khathesi ukuthi kakuyikuwela lutho emhlabathini okwelizwi leNkosi, iNkosi eyalikhuluma ngendlu kaAhabi, ngoba iNkosi yenzile eyakukhulumayo ngesandla senceku yayo uElija.
Koma dziwani tsono, kuti mawu amene Yehova anayankhula kunena za banja la Ahabu sadzapita padera. Yehova wachita chimene analonjeza kudzera mwa mtumiki wake Eliya.”
11 UJehu wasetshaya bonke ababesele endlini kaAhabi eJizereyeli, lazo zonke izikhulu zakhe, labazana laye, labapristi bakhe, akaze amtshiyela oseleyo.
Choncho Yehu anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Yezireeli, pamodzinso ndi akuluakulu ake onse, abwenzi ake ndiponso ansembe ake, sanasiyeko ndi mmodzi yemwe wamoyo.
12 Wasesukuma wahamba waya eSamariya. Endlini yokugunda yabelusi endleleni,
Kenaka Yehu ananyamuka kupita ku Samariya. Atafika pa malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa,
13 uJehu wahlangana labafowabo bakaAhaziya inkosi yakoJuda, wathi: Lingobani? Basebesithi: Singabafowabo bakaAhaziya, sehlela ukubingelela abantwana benkosi, labantwana bendlovukazi.
Yehu anakumana ndi abale ena a Ahaziya mfumu ya Yuda nawafunsa kuti, “Kodi ndinu yani?” Iwo anayankha kuti, “Ndife abale ake a Ahaziya, ndipo tabwera kulonjera banja la mfumu ndi ana a mfumukazi.”
14 Wasesithi: Babambeni bephila. Basebebabamba bephila, bababulalela emgodini weBeti-Ekedi, amadoda angamatshumi amane lambili, katshiyanga loyedwa wabo.
Yehu analamula kuti, “Atengeni amoyo!” Choncho anawatenga amoyo ndipo anakawaphera ku chitsime cha ku malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa; anthu onse 42. Iye sanasiyepo ndi mmodzi yemwe wamoyo.
15 Esesukile lapho wahlangana loJehonadabi indodana kaRekabi ezemhlangabeza; wambingelela wathi kuye: Inhliziyo yakho iqondile yini, njengoba inhliziyo yami ikanye lenhliziyo yakho? UJehonadabi wasesithi: Injalo. Uba kunjalo, ngipha isandla sakho. Wasemnika isandla sakhe; wasemkhweza enqoleni kuye.
Yehu atachoka kumeneko anakumana ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu, amene amabwera kudzakumana naye. Yehu anamulonjera nati kwa iye, “Kodi mtima wako uli bwino monga momwe mtima wanga ugwirizana nawo mtima wako?” Yehonadabu anayankha kuti, “Inde ndikugwirizana nawe.” Yehu anati, “Ngati ndi choncho, gwire dzanja.” Ndipo iye anaterodi, ndipo Yehu anamugwira dzanja namulowetsa mʼgaleta lake.
16 Wasesithi: Hamba lami, ubone ukuyitshisekela kwami iNkosi. Basebemgadisa enqoleni yakhe.
Yehu anati, “Tiye kuno uwone mmene ndikudziperekera kwa Yehova.” Ndipo anayenda naye mʼgaleta mwake.
17 Ekufikeni kwakhe eSamariya wabatshaya bonke ababesele kuAhabi eSamariya waze wamqeda, njengokwelizwi leNkosi eyalikhuluma kuElija.
Yehu atafika ku Samariya, anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Samariya; anawawonongeratu potsata mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Eliya.
18 UJehu wasebuthanisa bonke abantu, wathi kibo: UAhabi wakhonza kancinyane uBhali: UJehu uzamkhonza kakhulu.
Ndipo Yehu anasonkhanitsa anthu onse pamodzi nawawuza kuti, “Ahabu ankatumikira Baala pangʼono chabe; Yehu adzamutumikira kwambiri.
19 Ngakho-ke ngibizelani abaprofethi bakaBhali bonke, izinceku zakhe zonke labo bonke abapristi bakhe, kungabi lamuntu ongekho, ngoba ngilomhlatshelo omkhulu kuBhali; loba ngubani ongayikuba khona kayikuphila. Kodwa uJehu wakwenza ngobuqili ukuze abulale izinceku zikaBhali.
Tsopano itanani aneneri a Baala onse, atumiki ake onse ndi ansembe ake onse. Pasapezeke ndi mmodzi yemwe wotsala chifukwa ine ndidzapereka nsembe yayikulu kwa Baala. Aliyense amene alephere kubwera adzaphedwa.” Koma Yehu anachita zimenezi mwachinyengo ndi cholinga choti awononge atumiki onse a Baala.
20 UJehu wasesithi: Mehlukaniseleni umhlangano onzulu uBhali. Basebewumemezela.
Yehu anati, “Itanitsani msonkhano wodzalemekeza Baala.” Ndipo analengeza za msonkhanowo.
21 UJehu wasethumela kuye wonke uIsrayeli; zonke izinceku zikaBhali zasezisiza, kakwaze kwasala loyedwa ongabuyanga. Bangena endlini kaBhali, yaze yagcwala indlu kaBhali kusukela emsamo kusiya emnyango.
Pamenepo Yehu anatumiza mawu ku dziko lonse la Israeli ndipo atumiki onse a Baala anabwera; palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala. Iwo anadzaza nyumba ya Baala. Nyumbayo inadzaziratu kuchokera ku khoma lina mpaka ku khoma lina.
22 Wasesithi kulowo owayephethe indlu yezembatho: Khuphela bonke abakhonzi bakaBhali izembatho. Wasebakhuphela izembatho.
Ndipo Yehu anawuza munthu wosunga mikanjo kuti, “Bweretsa mikanjo yokwanira atumiki onse a Baala.” Ndipo iye anabweretsa mikanjoyo.
23 Wasengena uJehu eloJehonadabi indodana kaRekabi endlini kaBhali, wathi kuzinceku zikaBhali: Hlolani libone ukuthi kakukho kini abezinceku zeNkosi lapha, kodwa izinceku zikaBhali kuphela.
Kenaka Yehu ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu analowa mʼnyumba ya Baala. Yehu anawawuza atumiki a Baala kuti, “Yangʼanitsitsani ndipo muone kuti muno musapezeke atumiki a Yehova, koma mukhale atumiki okhawo a Baala.”
24 Sebengene ukwenza imihlatshelo leminikelo yokutshiswa, uJehu wazimisela amadoda angamatshumi ayisificaminwembili ngaphandle, wasesithi: Umuntu oyekela enye kumadoda engiwabeka ezandleni zenu iphunyuke, impilo yakhe izakuba sendaweni yempilo yayo.
Choncho Yehu analowa kukapereka nsembe zina ndi nsembe zopsereza. Nthawi iyi nʼkuti Yehu atayika anthu 80 kunja kwa nyumbayo ndi chenjezo lakuti, “Ngati wina aliyense wa inu adzathawitsa wina aliyense wa anthu amene ndayika kuti muziwayangʼanira, munthu woteroyo adzaphedwa.”
25 Kwasekusithi eseqedile ukwenza iminikelo yokutshiswa, uJehu wasesithi kubalindi lezinduneni: Ngenani libatshaye, kungaphumi muntu. Basebebatshaya ngobukhali benkemba; abalindi lezinduna basebebaphosela phandle, baya emzini wendlu kaBhali.
Yehu atangotsiriza kupereka nsembe yopsereza, analamula alonda ndi akulu a ankhondo kuti, “Lowani ndipo mukawaphe ndipo musalole kuti wina athawe.” Choncho iwo anawapha ndi lupanga. Alonda ndi akulu a ankhondo anaponya mitembo ya anthuwo panja ndipo anakalowa mʼkati mwenimweni mwa nyumba ya Baala.
26 Bakhupha endlini kaBhali insika eziyizithombe, bazitshisa.
Iwo anakatulutsa mwala wopatulika umene unali mʼnyumba ya Baala ndipo anawutentha.
27 Badiliza insika kaBhali eyisithombe, badiliza indlu kaBhali, bayenza yaba yindlu yokuyela ngaphandle kuze kube lamuhla.
Anawononga mwala wopatulika wa Baala ndi kugwetsa nyumba ya Baala, ndipo anthu anayisandutsa chimbudzi mpaka lero lino.
28 Ngokunjalo uJehu wachitha uBhali wamkhupha koIsrayeli.
Motero Yehu anawononga Baala mu Israeli.
29 Kodwa ezonweni zikaJerobhowamu indodana kaNebati owenza uIsrayeli one, uJehu kasukanga ekuzilandeleni, amathole egolide ayeseBhetheli lawayekoDani.
Koma Yehuyo sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati amene anachimwitsa nawo Israeli kupembedza mafano a golide a ana angʼombe ku Beteli ndi ku Dani.
30 INkosi yasisithi kuJehu: Ngoba wenze kuhle ngokwenza okulungileyo emehlweni ami, wenza endlini kaAhabi njengakho konke okwakusenhliziyweni yami, amadodana akho kuze kube sesizukulwaneni sesine azahlala esihlalweni sobukhosi sakoIsrayeli.
Yehova anati kwa Yehu, “Chifukwa wachita bwino pokwaniritsa kuchita zabwino pamaso panga ndipo wachitira banja la Ahabu zonse zimene zinali mʼmaganizo anga, zidzukulu zako zidzakhala pa mpando waufumu wa Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
31 Kodwa uJehu kaqaphelisanga ukuhamba emlayweni weNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli, ngenhliziyo yakhe yonke; kasukanga ezonweni zikaJerobhowamu owenza uIsrayeli one.
Komatu Yehu sanasamalire kusunga lamulo la Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wake wonse. Iyeyo sanaleke machimo a Yeroboamu amene anachimwitsa nawo Israeli.
32 Ngalezonsuku iNkosi yaqala ukuquma isusa koIsrayeli. UHazayeli wasebatshaya kuyo yonke imingcele yakoIsrayeli,
Masiku amenewo Yehova anayamba kuchepetsa dziko la Israeli. Hazaeli anagonjetsa Aisraeli,
33 kusukela eJordani empumalanga, ilizwe lonke leGileyadi, abakoGadi labakoRubeni labakoManase, kusukela eAroweri engasesifuleni seArinoni, leGileyadi leBashani.
kuyambira kummawa kwa Yorodani, dziko lonse la Giliyadi (chigawo cha Gadi, Rubeni ndi Manase), kuchokera ku Aroeri pafupi ndi chigwa cha Arinoni kudutsa Giliyadi mpaka ku Basani.
34 Ezinye-ke zezindaba zikaJehu, lakho konke akwenzayo, lamandla akhe wonke, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoIsrayeli?
Ntchito zina za Yehu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
35 UJehu waselala laboyise, bamngcwabela eSamariya. UJehowahazi indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Yehu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ku Samariya. Ndipo Yehowahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
36 Lesikhathi uJehu abusa ngaso phezu kukaIsrayeli eSamariya sasiyiminyaka engamatshumi amabili lesificaminwembili.
Yehu analamulira Aisraeli ku Samariya zaka 28.