< 2 Imilando 5 >
1 Usuphelile umsebenzi wonke uSolomoni ayewenzela indlu yeNkosi, wangenisa izinto ezingcwelisiweyo zikaDavida uyise, lesiliva legolide lazo zonke izitsha wazibeka esiphaleni senotho sendlu kaNkulunkulu.
Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.
2 Ngalesosikhathi uSolomoni wabuthanisa eJerusalema abadala bakoIsrayeli, lazo zonke inhloko zezizwe, izinduna zaboyise babantwana bakoIsrayeli, ukuthi benyuse umtshokotsho wesivumelwano seNkosi usuke emzini kaDavida oyiZiyoni.
Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide.
3 Wonke amadoda akoIsrayeli asebuthana enkosini emkhosini owenyanga yesikhombisa.
Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
4 Labo bonke abadala bakoIsrayeli beza, amaLevi asewuthwala umtshokotsho,
Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano,
5 awuletha umtshokotsho lethente lenhlangano lazo zonke izitsha ezingcwele ezazisethenteni; abapristi lamaLevi basebekwenyusa.
ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula,
6 Inkosi uSolomoni lenhlangano yonke yakoIsrayeli eyayibuthene phambi komtshokotsho basebenikela imihlatshelo yezimvu lezinkabi ezingelakubhalwa lezingelakubalwa ngobunengi.
ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.
7 Abapristi basebewungenisa umtshokotsho wesivumelwano seNkosi endaweni yawo, endaweni yelizwi yendlu, kungcwele yezingcwele, kwaze kwaba ngaphansi kwempiko zamakherubhi.
Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi.
8 Ngoba amakherubhi elulela impiko zawo phezu kwendawo yomtshokotsho; amakherubhi awembesa umtshokotsho lemijabo yawo ngaphezulu.
Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira.
9 Basebeselula imijabo, izihloko zemijabo zaze zabonakala emtshokotshweni phambi kwendawo yelizwi, kodwa zingabonakali ngaphandle; ukhona lapho-ke kuze kube lamuhla.
Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino.
10 Kwakungelalutho emtshokotshweni, ngaphandle kwezibhebhe ezimbili uMozisi azifaka khona eHorebe lapho iNkosi eyenza khona isivumelwano labantwana bakoIsrayeli ekuphumeni kwabo eGibhithe.
Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
11 Kwasekusithi abapristi bephuma endaweni engcwele, ngoba bonke abapristi abatholakalayo babezihlambulule bengagcinanga izigaba,
Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera.
12 lamaLevi angabahlabeleli babo bonke - akoAsafi, akoHemani, akoJeduthuni, lakumadodana abo lakubafowabo - begqoke amalembu acolekileyo amhlophe, belezinsimbi ezincencethayo lezigubhu zezintambo lamachacho, bema ngempumalanga kwelathi; njalo kanye labo kulabapristi abalikhulu lamatshumi amabili bekhalisa izimpondo.
Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi.
13 Kwasekusithi bekhalisa izimpondo behlabelela kanyekanye ukuzwakalisa umsindo owodwa, ukudumisa lokubonga iNkosi, lalapho bephakamisa ilizwi ngezimpondo langezinsimbi ezincencethayo lezinto zokuhlabelela, lalapho bedumisa iNkosi ukuthi ilungile lokuthi umusa wayo umi kuze kube phakade, indlu yagcwaliswa liyezi, indlu yeNkosi,
Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti, “Yehova ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.” Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo,
14 abapristi kabaze baba lakho ukuma ukukhonza ngenxa yeyezi, ngoba inkazimulo yeNkosi yagcwalisa indlu kaNkulunkulu.
choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.