< 2 Imilando 26 >
1 Bonke abantu bakoJuda basebethatha uUziya owayeleminyaka elitshumi lesithupha, bambeka waba yinkosi esikhundleni sikayise uAmaziya.
Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
2 Yena wakha iElothi, wayibuyisela koJuda emva kokulala kwenkosi laboyise.
Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
3 U-Uziya wayeleminyaka elitshumi lesithupha lapho esiba yinkosi; wabusa iminyaka engamatshumi amahlanu lambili eJerusalema. Lebizo likanina lalinguJekoliya weJerusalema.
Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
4 Wasesenza okuqondileyo emehlweni eNkosi njengakho konke uAmaziya uyise ayekwenzile.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
5 Njalo wayemdinga uNkulunkulu ensukwini zikaZekhariya owayelokuqedisisa emibonweni kaNkulunkulu; langezinsuku zokudinga kwakhe iNkosi, uNkulunkulu wamphumelelisa.
Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
6 Wasephuma walwa lamaFilisti, wadilizela phansi umduli weGathi lomduli weJabine lomduli weAshidodi, wakha imizi eAshidodi laphakathi kwamaFilisti.
Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
7 UNkulunkulu wasemsiza ukumelana lamaFilisti, lokumelana lamaArabhiya ayehlala eGuri-Bhali, lamaMewuni.
Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
8 AmaAmoni asesipha umthelo kuUziya, lebizo lakhe lahamba laze lafika engenelweni leGibhithe, ngoba waziqinisa waze waba sengqongeni.
Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
9 Futhi uUziya wakha imiphotshongo eJerusalema esangweni lengonsi lesangweni lesigodi lengonsini, wayiqinisa.
Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
10 Wakha lemiphotshongo enkangala, wagebha imithombo eminengi, ngoba wayelenkomo ezinengi esihotsheni kanye lemagcekeni, abalimi lezisebenzi zezivini ezintabeni leKharmeli, ngoba wayengothanda umhlabathi.
Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
11 Futhi uUziya wayelebutho elilwayo eliphuma impi ngamaviyo ngokwenani lokubalwa kwabo ngesandla sikaJeyiyeli umabhalane loMahaseya umbusi phansi kwesandla sikaHananiya, omunye wezinduna zenkosi.
Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
12 Inani lonke lezinhloko zaboyise lamaqhawe alamandla lalizinkulungwane ezimbili lamakhulu ayisithupha.
Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
13 Laphansi kwesandla sazo kwakulamandla ebutho elizinkulungwane ezingamakhulu amathathu lesikhombisa lamakhulu amahlanu elalisilwa ngamandla obuqhawe ukusiza inkosi limelene lesitha.
Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
14 U-Uziya wasebalungisela, ibutho lonke, izihlangu lemikhonto lamakhowa lamabhatshi ensimbi lamadandili lamatshe ezavutha.
Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
15 EJerusalema wasesenza imitshina, eyaqanjwa ngohlakaniphileyo, ukuthi ibe phezu kwemiphotshongo laphezu kwezingonsi ukuphosa ngemitshoko langamatshe amakhulu. Lebizo lakhe laphuma laze laba khatshana, ngoba wasizwa ngokumangalisayo waze waqina.
Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
16 Kodwa eseqinile, inhliziyo yakhe yaziphakamisela encithakalweni. Ngoba waphambuka eNkosini uNkulunkulu wakhe, wasengena ethempelini leNkosi ukuze atshise impepha phezu kwelathi lempepha.
Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
17 UAzariya umpristi wasengena emva kwakhe elabapristi beNkosi abangamatshumi ayisificaminwembili, amadoda alamandla.
Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
18 Basebemelana loUziya inkosi, bathi kuye: Kakusikho okwakho, Uziya, ukutshisela iNkosi impepha, kodwa ngokwabapristi, amadodana kaAroni abehlukaniselwe ukutshisa impepha. Phuma endaweni engcwele, ngoba uphambukile; njalo kakusikho kodumo lwakho oluvela eNkosini uNkulunkulu.
Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
19 Wasethukuthela uUziya, njalo kwakulodengezi esandleni sakhe ukuze atshise impepha; esebathukuthelele abapristi, kwabonakala ubulephero ebunzini lakhe phambi kwabapristi endlini yeNkosi, ngaphezu kwelathi lempepha.
Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
20 UAzariya umpristi oyinhloko labo bonke abapristi basebemkhangela, khangela-ke, wayelobulephero ebunzini lakhe; basebemkhupha lapho masinyane, yebo laye uqobo waphangisa ukuphuma, ngoba iNkosi yayimtshayile.
Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
21 U-Uziya inkosi waba ngumlephero kwaze kwaba lusuku lokufa kwakhe; wahlala endlini eyehlukanisiweyo engumlephero, ngoba waqunywa wasuka endlini kaJehova. Njalo uJothamu indodana yakhe wayephezu kwendlu yenkosi, esahlulela abantu belizwe.
Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
22 Ezinye-ke zezindaba zikaUziya, ezokuqala lezokucina, uIsaya umprofethi, indodana kaAmozi, wazibhala.
Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
23 U-Uziya waselala laboyise; basebemngcwaba kuboyise ensimini yokungcwaba eyayingeyamakhosi, ngoba bathi: Ungumlephero. UJothamu indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.