< 2 Imilando 25 >
1 UAmaziya eseleminyaka engamatshumi amabili lanhlanu waba yinkosi; wabusa iminyaka engamatshumi amabili lesificamunwemunye eJerusalema. Lebizo likanina lalinguJehowadani weJerusalema.
Amaziya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
2 Wasesenza okuqondileyo emehlweni eNkosi, kodwa kungeyisikho ngenhliziyo epheleleyo.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osati ndi mtima wonse.
3 Kwasekusithi umbuso usuqinisiwe kuye, wabulala inceku zakhe ezazibulele inkosi uyise.
Pamene mphamvu zonse zaufumu zinali mʼmanja mwake, iye anapha akuluakulu amene anapha abambo ake, mfumu ija.
4 Kodwa kababulalanga abantwana bazo, kodwa wenza njengokubhaliweyo emlayweni wogwalo lukaMozisi lapho iNkosi eyalaya khona isithi: Oyise kabayikufa ngenxa yabantwana, labantwana kabayikufa ngenxa yaboyise, kodwa wonke uzafela isono sakhe.
Komabe iye sanaphe ana awo koma anatsatira zolembedwa mʼbuku la Mose, mʼmene Yehova analamula kuti, “Makolo sadzaphedwa chifukwa cha ana awo kapena ana kuphedwa chifukwa cha makolo awo. Aliyense adzafera machimo ake.”
5 UAmaziya wasebuthanisa uJuda, wabamisa ngokwendlu yaboyise baba zinduna zezinkulungwane lezinduna zamakhulu, kuye wonke uJuda loBhenjamini. Wababala kusukela koleminyaka engamatshumi amabili kusiya phezulu, wabathola bezinkulungwane ezingamakhulu amathathu zabakhethiweyo, abaphuma impi, ababamba umkhonto lesihlangu esikhulu.
Amaziya anasonkhanitsa anthu a ku Yuda ndipo anawapatsa zochita molingana ndi mabanja awo kukhala anthu olamulira 1,000, ndi olamulira 100 pa Ayuda onse ndi Benjamini. Ndipo iye anawerenga amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo napeza kuti analipo amuna 300,000 okonzeka kugwira ntchito ya usilikali, okhoza kugwiritsa ntchito mkondo ndi chishango.
6 Wabuya waqhatsha koIsrayeli amaqhawe alamandla azinkulungwane ezilikhulu ngamathalenta esiliva alikhulu.
Iye analembanso ntchito anthu odziwa nkhondo 100,000 ochokera ku Israeli pa mtengo wa makilogalamu 3,400 a siliva.
7 Kodwa kwafika umuntu kaNkulunkulu kuye, esithi: Nkosi, ibutho lakoIsrayeli kalingahambi lawe, ngoba iNkosi kayilaye uIsrayeli, kusitsho bonke abantwana bakoEfrayimi.
Koma munthu wa Mulungu anabwera kwa iye ndipo anati, “Inu mfumu, asilikali awa ochokera ku Israeli asapite ndi inu, pakuti Yehova sali ndi Israeli kapena ndi aliyense wa anthu a Efereimu.
8 Kodwa uba uhamba, kwenze, qinela impi; uNkulunkulu uzakwenza ukhubeke phambi kwesitha; ngoba kulamandla kuNkulunkulu okusiza lokukhubekisa.
Ngakhale mupite ndi kuchita nkhondo molimba mtima, Mulungu adzakugonjetsani pamaso pa adani anu, pakuti Mulungu ali ndi mphamvu yothandiza kapena kugonjetsa.”
9 UAmaziya wasesithi emuntwini kaNkulunkulu: Pho, senzeni ngamathalenta alikhulu engiwanike iviyo lakoIsrayeli? Umuntu kaNkulunkulu wasesithi: INkosi ilokunengi kulalokhu okokukunika.
Amaziya anafunsa munthu wa Mulungu kuti, “Koma nanga za makilogalamu aja a siliva amene ndapereka kwa asilikali a Israeli?” Munthu wa Mulungu anayankha kuti, “Yehova atha kukupatsani zambiri kuposa zimenezo.”
10 UAmaziya wasebehlukanisa, kusitsho iviyo elalifike kuye livela koEfrayimi, ukuze baye endaweni yabo. Ngakho ulaka lwabo lwamvuthela kakhulu uJuda, babuyela endaweni yabo bevutha ulaka.
Choncho Amaziya anachotsa asilikali amene anabwera kwa iye kuchokera ku Efereimu ndipo anawatumiza kwawo. Iwo anakwiyira anthu a ku Yuda ndipo anapita kwawo atapsa mtima kwambiri.
11 UAmaziya waseziqinisa, wakhokhela abantu bakhe, waya esihotsheni setshwayi, watshaya abantwana beSeyiri, izinkulungwane ezilitshumi.
Ndipo Amaziya analimba mtima ndipo anatsogolera gulu lake lankhondo ku Chigwa cha Mchere, kumene anapha anthu 10,000 a ku Seiri.
12 Abantwana bakoJuda basebethumba abazinkulungwane ezilitshumi abaphilayo, babasa engqongeni yeliwa, babaphosa besengqongeni yeliwa, baze baphahlazeka bonke.
Gulu la ankhondo la Yuda linagwiranso anthu amoyo 10,000, napita nawo pamwamba pa thanthwe ndipo anawaponya pansi kotero kuti onse ananyenyeka.
13 Kodwa abantu beviyo uAmaziya ayelibuyisele emuva ukuthi bangahambi laye empini, bahlasela imizi yakoJuda, kusukela eSamariya kuze kube seBhethi-Horoni, batshaya abazinkulungwane ezintathu zabo, baphanga impango enengi.
Pa nthawi imeneyi asilikali amene Amaziya anawabweza ndipo sanawalole kuti achite nawo nkhondo, anakathira nkhondo mizinda ya Yuda kuyambira ku Samariya mpaka ku Beti-Horoni. Iwo anapha anthu 3,000 ndipo anafunkha katundu wambiri.
14 Kwasekusithi emva kokubuya kukaAmaziya ekutshayeni amaEdoma, waletha onkulunkulu babantwana beSeyiri, wabamisa baba ngonkulunkulu bakhe, wabakhothamela, wabatshisela impepha.
Amaziya atabwerera kuja anakapha Aedomu, anabweretsa milungu ya anthu a ku Seiri. Ndipo anayika kuti ikhale milungu yake, ankayipembedza ndi kupereka nsembe zopsereza.
15 Ngalokhu ulaka lweNkosi lwamvuthela uAmaziya, yathuma kuye umprofethi owathi kuye: Ubadingelani onkulunkulu babantu abangophulanga abantu babo esandleni sakho?
Yehova anakwiyira Amaziya, ndipo anamutumizira mneneri amene anati, “Nʼchifukwa chiyani mukupembedza milungu ya anthu awa, imene sinathe kupulumutsa anthu ake mʼdzanja lanu?”
16 Kodwa kwathi ekhuluma laye, wathi kuye: Sikubekile yini ukuthi ube ngumeluleki wenkosi? Ziyekelele! Kungani bezakutshaya? Umprofethi waseyekela wathi: Ngiyazi ukuthi uNkulunkulu unqume ukukubhubhisa, ngoba wenze lokhu, kawulalelanga iseluleko sami.
Iye ali kuyankhula, mfumu inati, “Kodi ife takusankha iwe kuti ukhale mlangizi wa mfumu? Khala chete! Ufuna kuphedweranji?” Choncho mneneriyo analeka koma anati, “Ine ndikudziwa kuti Mulungu watsimikiza kukuwonongani chifukwa mwachita izi ndipo simunamvere uphungu wanga.”
17 UAmaziya inkosi yakoJuda wasethatha iseluleko, wathumela kuJowashi indodana kaJehowahazi indodana kaJehu, inkosi yakoIsrayeli, esithi: Woza, sikhangelane ubuso.
Amaziya mfumu ya ku Yuda, atafunsa alangizi ake, anatumiza mawu awa kwa Yowasi mwana wa Yehowahazi mwana wa Yehu, mfumu ya Israeli: “Bwera udzakumane nane maso ndi maso.”
18 UJowashi inkosi yakoIsrayeli wasethumela kuAmaziya inkosi yakoJuda esithi: Ukhula oluhlabayo oluseLebhanoni lwathumela emsedarini oseLebhanoni lusithi: Phana indodana yami indodakazi yakho ibe ngumkayo; kodwa isilo seganga esasiseLebhanoni sedlula, salugxoba ukhula oluhlabayo.
Koma Yowasi mfumu ya Israeli inayankha Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Nthawi ina kamtengo kaminga ka ku Lebanoni kanatumiza mawu kwa mkungudza wa ku Lebanoni kuti, ‘Pereka mwana wako wamkazi kwa mwana wanga kuti amukwatire!’ Koma chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa minga uja.
19 Uthi: Khangela, uyitshayile iEdoma; ngakho inhliziyo yakho iyakuphakamisa ukuthi uzincome; khathesi hlala endlini yakho; kungani uzazingenisa ebubini ukuze uwe, wena loJuda elawe?
Iwe ukuti wagonjetsa Edomu, ndipo tsopano ukudzikuza ndi kudzitamandira, koma khala kwanu komweko! Nʼchifukwa chiyani ukufuna mavuto ndi kudzichititsa kuti ugwe pamodzinso ndi Yuda?”
20 Kodwa uAmaziya kalalelanga; ngoba kwakungokukaNkulunkulu ukuze abanikele esandleni sabo, ngoba babedinge onkulunkulu beEdoma.
Komabe Amaziya sanamvere pakuti ndi Mulungu amene anakonzeratu kuti awapereke kwa Yehowasi, chifukwa iwo amapembedza milungu ya ku Edomu.
21 UJowashi inkosi yakoIsrayeli wasesenyuka, bakhangelana ubuso, yena loAmaziya inkosi yakoJuda, eBeti-Shemeshi engeyakoJuda.
Kotero Yowasi mfumu ya Israeli inakamuthira nkhondo. Iye ndi Amaziya anayangʼanana maso ndi maso ku Beti-Semesi ku Yuda.
22 UJuda wasetshaywa phambi kukaIsrayeli, babaleka, ngulowo waya ethenteni lakhe.
Yuda anagonjetsedwa ndi Israeli ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
23 UJowashi inkosi yakoIsrayeli wasembamba uAmaziya inkosi yakoJuda, indodana kaJowashi, indodana kaJehowahazi, eBeti-Shemeshi, wamletha eJerusalema, wadilizela phansi okomduli weJerusalema, kusukela esangweni lakoEfrayimi kuze kube sesangweni lengonsi, izingalo ezingamakhulu amane.
Yehowahazi mfumu ya Israeli inagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Yehowasi anabwera naye ku Yerusalemu ndipo anagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira pa Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, khoma lotalika mamita 180.
24 Wasethatha lonke igolide lesiliva, lezitsha zonke ezatholakala endlini kaNkulunkulu kuObedi-Edoma, lokuligugu kwendlu yenkosi, labayisibambiso, wabuyela eSamariya.
Iye anatenga golide ndi siliva yense ndi zida zonse zimene zimapezeka mʼNyumba ya Mulungu zimene ankazisamalira Obedi-Edomu, pamodzinso ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu ndipo anatenga anthu ngati chikole.
25 UAmaziya indodana kaJowashi inkosi yakoJuda wasephila iminyaka elitshumi lanhlanu emva kokufa kukaJowashi indodana kaJehowahazi inkosi yakoIsrayeli.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo kwa zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
26 Ezinye-ke zezindaba zikaAmaziya, ezokuqala lezokucina, khangela, kazibhalwanga yini egwalweni lwamakhosi akoJuda lawakoIsrayeli?
Ntchito zina za mfumu Amaziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli?
27 Njalo kusukela esikhathini uAmaziya aphambuka ngaso ekulandeleni iNkosi bamenzela ugobe eJerusalema; wasebalekela eLakishi; kodwa bathumela emva kwakhe eLakishi, bambulalela khona.
Kuyambira nthawi imene Amaziya analeka kutsatira Yehova anthu anamukonzera chiwembu mu Yerusalemu ndipo anathawira ku Lakisi, koma adaniwo anatumiza anthu ku Lakisiko ndipo anamupha komweko.
28 Basebemthwala ngamabhiza, bamngcwaba kuboyise emzini kaJuda.
Iwo anabwera naye ali pa kavalo ndipo anayikidwa mʼmanda ndi makolo ake mu mzinda wa Yuda.