< 2 Imilando 20 >

1 Kwasekusithi emva kwalokho abantwana bakoMowabi labantwana bakoAmoni belabanye ngaphandle kwamaAmoni beza bamelana loJehoshafathi empini.
Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
2 Kwasekusiza abanye babikela uJehoshafathi besithi: Kuyeza ixuku elikhulu ukumelana lawe elivela phetsheya kolwandle, eSiriya; khangela-ke, liseHazazoni-Tamari, eyiEngedi.
Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
3 UJehoshafathi wasesesaba, wamisa ubuso bakhe ukudinga iNkosi, wamemezela ukuzila ukudla kuye wonke uJuda.
Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
4 UJuda wasezibuthanisa ukudinga eNkosini; lasemizini yonke yakoJuda baphuma beza ukudinga iNkosi.
Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
5 UJehoshafathi wasesima ebandleni lakoJuda leJerusalema endlini yeNkosi phambi kweguma elitsha.
Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
6 Wasesithi: Nkosi, Nkulunkulu wabobaba, wena kawusuye yini uNkulunkulu emazulwini? Yebo, kawubusi yini kuyo yonke imibuso yezizwe? Lesandleni sakho kukhona amandla lengalo, ukuze kungabi khona ongamelana lawe.
ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
7 KawusiNkulunkulu wethu yini? Uxotshile abahlali balelilizwe elifeni phambi kwabantu bakho uIsrayeli, walinika inzalo kaAbrahama umngane wakho kuze kube phakade.
Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
8 Basebehlala kilo, bakwakhela indawo engcwele kulo eyebizo lakho, besithi:
Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
9 Uba kusehlela phezu kwethu ububi, inkemba, isahlulelo, loba umatshayabhuqe wesifo, loba indlala, sizakuma phambi kwalindlu laphambi kwakho (ngoba ibizo lakho likulindlu), sikhale kuwe ekubandezelekeni kwethu, uzakuzwa-ke usindise.
‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
10 Ngakho-ke, khangela, abantwana bakoAmoni labakoMowabi labentabeni iSeyiri ongavumanga ukuthi uIsrayeli adlule phakathi kwabo lapho besuka elizweni leGibhithe, kodwa babafulathela kabababhubhisanga;
“Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
11 khangela-ke, basivuza beza ukuzasixotsha elifeni lakho owenze ukuthi silidle.
Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
12 Nkulunkulu wethu, kawuyikubahlulela yini? Ngoba amandla kawakho kithi okumelana lalelixuku elikhulu elize ukumelana lathi; njalo thina kasikwazi esingakwenza, kodwa amehlo ethu akuwe.
Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
13 UJuda wonke wasesima phambi kweNkosi, lensane zabo, omkabo labantwana babo.
Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
14 Khona uJahaziyeli indodana kaZekhariya indodana kaBhenaya indodana kaJeyiyeli indodana kaMathaniya, umLevi emadodaneni kaAsafi, uMoya weNkosi wafika phezu kwakhe phakathi kwebandla.
Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
15 Wasesithi: Lalelani lonke bakoJuda labahlali beJerusalema, lawe nkosi Jehoshafathi; itsho njalo iNkosi kini: Lina lingesabi lingatshaywa luvalo ngenxa yalelixuku elikhulu, ngoba impi kayisiyo yenu, kodwa ngekaNkulunkulu.
Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
16 Kusasa yehlani limelane labo; khangela, bayenyuka ngomqanso weZizi; lizabathola ekucineni kwesihotsha phambi kwenkangala yeJeruweli.
Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
17 Kakusikwenu ukulwa kule impi; zimiseni lime, libone usindiso lweNkosi lani, Juda leJerusalema. Lingesabi lingatshaywa luvalo; kusasa phumani limelene labo, ngoba iNkosi izakuba lani.
Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
18 UJehoshafathi wasekhothamisa ikhanda emhlabathini, laye wonke uJuda labahlali beJerusalema bawa phambi kweNkosi, beyikhonza iNkosi.
Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
19 AmaLevi kubantwana bakoKohathi lakubantwana bakoKora asesukuma ukudumisa iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli, ngelizwi elikhulu eliphezulu.
Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
20 Basebevuka ekuseni kakhulu, baphuma baya enkangala yeThekhowa; lekuphumeni kwabo uJehoshafathi wema wathi: Ngilalelani Juda labahlali beJerusalema. Kholwani eNkosini uNkulunkulu wenu, lizaqiniswa; likholwe kubaprofethi bayo, lizaphumelela.
Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
21 Esecebisene labantu wamisela iNkosi abahlabeleli, abazadumisa ubuhle bobungcwele, ekuphumeni phambi kwabahlomileyo, besithi: Dumisani iNkosi, ngoba umusa wayo umi kuze kube nininini.
Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
22 Kwathi lapho beqalisa ukuhlabelela lokudumisa, iNkosi yabeka abacathameli ukumelana labantwana bakoAmoni, uMowabi, lentaba iSeyiri, ababezemelana loJuda; basebetshaywa.
Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
23 Ngoba abantwana bakoAmoni labakoMowabi basukuma bamelana labahlali bentaba yeSeyiri ukutshabalalisa lokuchitha; njalo sebebaqedile abahlali beSeyiri, bancedisa ngulowo umakhelwane wakhe encithakalweni.
Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
24 UJuda esefikile enqabeni yokulinda enkangala bakhangela ngasexukwini, khangela-ke, kwakulezidumbu eziwele emhlabathini; njalo kungekho ophephileyo.
Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
25 UJehoshafathi labantu bakhe sebefikile ukuphanga impango bathola phakathi kwabo ngobunengi, impahla lazo, lezidumbu, lezinto eziligugu, baziphangela baze behluleka ukuzithwala. Njalo baba lensuku ezintathu bephanga impango ngoba yayinengi.
Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
26 Njalo ngosuku lwesine babuthana esihotsheni seBeraka, ngoba lapho bayibusisa iNkosi; ngenxa yalokho babiza ibizo laleyondawo ngokuthi yisihotsha seBeraka kuze kube lamuhla.
Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
27 Basebebuyela, wonke umuntu wakoJuda leJerusalema, loJehoshafathi enhlokweni yabo, ukuthi babuyele eJerusalema belentokozo, ngoba iNkosi yabathokozisa phezu kwezitha zabo.
Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
28 Basebengena eJerusalema belezigubhu zezintambo lamachacho lezimpondo, baya endlini yeNkosi.
Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
29 Uvalo ngoNkulunkulu lwaselusiba phezu kwayo yonke imibuso yamazwe lapho besizwa ukuthi iNkosi yalwa lezitha zikaIsrayeli.
Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
30 Ngakho umbuso kaJehoshafathi waba lokuthula, ngoba uNkulunkulu wakhe wamphumuza inhlangothi zonke.
Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
31 UJehoshafathi wabusa-ke phezu kukaJuda; wayeleminyaka engamatshumi amathathu lanhlanu lapho esiba yinkosi, wabusa iminyaka engamatshumi amabili lanhlanu eJerusalema. Lebizo likanina lalinguAzuba indodakazi kaShilehi.
Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
32 Wasehamba ngendlela kayise uAsa, kaphambukanga kuyo, esenza okulungileyo emehlweni eNkosi.
Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
33 Lanxa kunjalo indawo eziphakemeyo kazisuswanga; ngoba abantu babelokhu bengalungisanga inhliziyo yabo kuNkulunkulu waboyise.
Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
34 Ezinye-ke zezindaba zikaJehoshafathi, ezokuqala lezokucina, khangela, zibhaliwe ezindabeni zikaJehu indodana kaHanani ezagoqelwa egwalweni lwamakhosi akoIsrayeli.
Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
35 Lemva kwalokho uJehoshafathi inkosi yakoJuda wazihlanganisa loAhaziya inkosi yakoIsrayeli owenza ngenkohlakalo ekwenzeni.
Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
36 Wasezihlanganisa laye ukwenza imikhumbi yokuya eTarshishi; basebeyenza imikhumbi eEziyoni-Geberi.
Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
37 UEliyezeri indodana kaDodavahu weMaresha waseprofetha emelene loJehoshafathi esithi: Ngoba uzihlanganise loAhaziya, iNkosi yephulile imisebenzi yakho. Ngakho imikhumbi yephuka, ayaze yenelisa ukuya eTarshishi.
Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.

< 2 Imilando 20 >