< 2 Imilando 19 >

1 UJehoshafathi inkosi yakoJuda wasebuyela endlini yakhe ngokuthula eJerusalema.
Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu,
2 UJehu indodana kaHanani umboni wasephuma ukumhlangabeza, wathi enkosini uJehoshafathi: Unganceda yini omubi, uthande labo abazonda iNkosi? Ngenxa yalokhu-ke kulolaka phezu kwakho oluvela ebusweni beNkosi.
mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu.
3 Loba kunjalo izinto ezinhle zitholwe kuwe, ngoba ususile izixuku elizweni, walungisa inhliziyo yakho ukumdinga uNkulunkulu.
Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”
4 UJehoshafathi wasehlala eJerusalema; wabuya waphuma wahamba phakathi kwabantu, kusukela eBherishebha kusiya entabeni yakoEfrayimi, wababuyisela eNkosini, uNkulunkulu waboyise.
Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
5 Wasemisa abahluleli elizweni kuyo yonke imizi ebiyelweyo yakoJuda, kumuzi ngomuzi.
Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda.
6 Wasesithi kubahluleli: Bonani elikwenzayo, ngoba kalehluleleli umuntu kodwa iNkosi, elani endabeni yokwahlulela.
Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo.
7 Ngakho-ke uvalo ngeNkosi kalube phezu kwenu, linanzelele likwenze, ngoba eNkosini uNkulunkulu wethu kakulabubi lokukhangela ubuso lokwemukela izivalamlomo.
Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”
8 Futhi leJerusalema uJehoshafathi wasemisa abanye kumaLevi labapristi lakunhloko zaboyise zakoIsrayeli kusahlulelo seNkosi lakumibango, sebebuyele eJerusalema.
Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu.
9 Wasebalaya esithi: Lizakwenza njalo ekuyesabeni iNkosi, ngobuqotho langenhliziyo epheleleyo.
Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova.
10 Lawuphi umbango oza kini ovela kubafowenu abahlala emizini yabo, phakathi kwegazi legazi, phakathi komthetho lomlayo, izimiso lezahlulelo, lizabaxwayisa ukuze bangabi lecala eNkosini, lolaka lwehlele phezu kwenu laphezu kwabafowenu. Lizakwenza njalo, futhi lingabi lacala.
Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.
11 Khangelani-ke, uAmariya umpristi oyinhloko uphezu kwenu kulo lonke udaba lukaJehova, loZebhadiya indodana kaIshmayeli, umbusi wendlu yakoJuda, kulo lonke udaba lwenkosi; labaphathi amaLevi baphambi kwenu. Qinani likwenze; iNkosi-ke izakuba lolungileyo.
“Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”

< 2 Imilando 19 >