< 2 Imilando 16 >
1 Ngomnyaka wamatshumi amathathu lesithupha wokubusa kukaAsa uBahasha inkosi yakoIsrayeli wenyuka emelana loJuda, wakha iRama ukuze angavumeli ophumayo longenayo kuAsa inkosi yakoJuda.
Mʼchaka cha 36 cha ufumu wa Asa, Baasa mfumu ya Israeli inapita kukathira nkhondo dziko la Yuda. Anamangira mpanda mzinda wa Rama kuletsa aliyense kutuluka kapena kulowa mʼdziko la Asa mfumu ya Yuda.
2 UAsa wasekhupha isiliva legolide esiphaleni senotho sendlu kaJehova lendlu yenkosi, wathumela kuBenihadadi inkosi yeSiriya owayehlala eDamaseko, esithi:
Ndipo Asa anatenga siliva ndi golide ku malo osungirako a mʼNyumba ya Mulungu ndi ku nyumba yake yaufumu ndi kuzitumiza kwa Beni-Hadadi mfumu ya Aramu imene inkakhala mu Damasiko.
3 Kulesivumelwano phakathi kwami lawe laphakathi kukababa loyihlo; khangela, ngiyakuthumela isiliva legolide; hamba, yephula isivumelwano sakho loBahasha inkosi yakoIsrayeli ukuze enyuke asuke kimi.
Iye anati, “Pakhale pangano pakati pa inu ndi ine, monga zinalili pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Taonani, ine ndikutumiza kwa inu siliva ndi golide. Tsopano thetsani mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti achoke kwa ine.”
4 UBenihadadi waseyilalela inkosi uAsa, wathuma induna zamabutho ayelawo ukuyamelana lemizi yakoIsrayeli, zasezitshaya iIjoni leDani leAbeli-Mayimi, lemizi yonke eyiziphala yakoNafithali.
Beni-Hadadi anagwirizana ndi mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira nkhondo ake kukathira nkhondo mizinda ya Israeli. Iwo anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Maimu ndi mizinda yonse yosungira chuma ya Nafutali.
5 Kwasekusithi uBahasha esizwa wayekela ukwakha iRama, wawumisa umsebenzi wakhe.
Baasa atamva izi, anasiya kumanga Rama ndipo anayimitsa ntchito yakeyo.
6 UAsa inkosi wasethatha uJuda wonke, bathutha amatshe eRama lezigodo zayo uBahasha ayesakha ngakho; wasesakha ngakho iGeba leMizipa.
Ndipo mfumu Asa anabwera ndi Ayuda onse, ndipo anachotsa miyala ndi matabwa ku Rama amene Baasa amagwiritsa ntchito. Ndi zimenezi Asa ankamangira Geba ndi Mizipa.
7 Ngalesosikhathi uHanani umboni wasefika kuAsa inkosi yakoJuda, wathi kuye: Ngoba weyeme enkosini yeSiriya, ungeyamanga eNkosini uNkulunkulu wakho, ngalokho ibutho lenkosi yeSiriya liphunyukile esandleni sakho.
Nthawi imeneyi mlosi Hanani anabwera kwa Asa mfumu ya Yuda ndipo anati kwa iye, “Chifukwa chakuti munadalira mfumu ya Aramu osati Yehova Mulungu wanu, gulu la ankhondo la mfumu ya ku Aramu lapulumuka mʼmanja mwanu.
8 AmaEthiyophiya lamaLibiya ayengeyisilo ibutho elikhulu, elezinqola labagadi bamabhiza abanengi kakhulu yini? Kanti lapho weyeme eNkosini, yawanikela esandleni sakho.
Kodi Akusi ndi Alibiya sanali gulu lankhondo lamphamvu lokhala ndi magaleta ochuluka ndi okwera magaleta ake? Koma pamene inu munadalira Yehova, Iye anawapereka mʼdzanja lanu.
9 Ngoba iNkosi, amehlo ayo agijima aye le lale emhlabeni wonke ukuthi izitshengise ilamandla ngalabo abanhliziyo yabo iphelele kuyo. Wenze ngobuthutha kulokhu, ngoba kusukela khathesi kuzakuba lezimpi kuwe.
Pakuti Yehova amayangʼana uku ndi uku pa dziko lonse lapansi kuti alimbikitse iwo amene mitima yawo ayipereka kwathunthu kwa Iye. Inu mwachita chinthu chopusa ndipo kuyambira lero mudzakhala pa nkhondo.”
10 UAsa wasemcunukela umboni, wamfaka entolongweni, ngoba wamthukuthelela ngalokhu. UAsa wasecindezela abanye ebantwini ngalesosikhathi.
Asa anamupsera mtima mlosi uja chifukwa cha izi mwakuti anakwiya kwambiri namuyika mʼndende. Pa nthawi yomweyonso Asa anazunza mwankhanza anthu ena.
11 Khangela-ke, izindaba zikaAsa, ezokuqala lezokucina, khangela, zibhaliwe egwalweni lwamakhosi akoJuda lakoIsrayeli.
Ntchito zina za mfumu Asa, kuyambira pachiyambi mpaka kumapeto zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
12 UAsa waba lomkhuhlane enyaweni zakhe, ngomnyaka wamatshumi amathathu lesificamunwemunye wokubusa kwakhe, umkhuhlane wakhe waze wakhula kakhulu; kanti lekuguleni kwakhe kayidinganga iNkosi, kodwa izinyanga.
Mʼchaka cha 39 cha ufumu wake, Asa anayamba kudwala nthenda ya mapazi. Ngakhale nthendayo inali yaululu kwambiri, komabe iye sanafunefune Yehova, koma anafuna thandizo kwa asingʼanga.
13 UAsa waselala laboyise wafa ngomnyaka wamatshumi amane lanye wokubusa kwakhe.
Ndipo mʼchaka cha 41 cha ufumu wake, Asa anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake.
14 Basebemngcwaba emangcwabeni akhe ayezigebhele wona emzini kaDavida; bambeka embhedeni ayewugcwalise amaphunga amnandi lezinhlobonhlobo zamakha, ayenziwe ngokuhlakanipha kwezingcitshi zamakha; basebembasela umlilo omkhulu, omkhulukazi.
Iye anayikidwa mʼmanda amene anadzisemera yekha mu Mzinda wa Davide. Anagoneka mtembo wake pa chithatha chimene anayikapo zonunkhira zamitundumitundu, ndipo anasonkha chimoto chachikulu pomuchitira ulemu.