< 1 KuThimothi 4 >
1 UMoya-ke utsho ngokucacileyo ukuthi ngezikhathi zokucina abanye bazahlehlela nyovane ekholweni, balalele omoya abaduhisayo lemfundiso zamadimoni,
Mzimu akunena momveka bwino kuti mʼmasiku otsiriza anthu ena adzataya chikhulupiriro chawo ndi kutsatira mizimu yonyenga ndi zinthu zophunzitsidwa ndi ziwanda.
2 ekuzenziseni kwabaqambimanga, betshiswe kwezabo izazela ngensimbi etshisayo,
Ziphunzitso zimenezi zimachokera ku chinyengo cha anthu onama, amene chikumbumtima chawo chinamatidwa ndi chitsulo cha moto.
3 besalela ukuthathana, bezila ukudla uNkulunkulu akudalileyo ekwemukelweni lokubonga ngabakholwayo labazi iqiniso;
Iwo amaletsa anthu ukwati ndi kuwalamula kuti asamadye zakudya zina, zimene Mulungu analenga kuti amene anakhulupirira ndi kudziwa choonadi, azidye moyamika.
4 ngoba sonke isidalwa sikaNkulunkulu sihle, kakulahlwa lutho, uba lwemukelwa kanye lokubonga;
Pakuti chilichonse chimene Mulungu analenga ndi chabwino, ndipo chilichonse chisasalidwe, akamachilandira moyamika,
5 ngoba luyangcweliswa ngelizwi likaNkulunkulu langomkhuleko.
pakuti chimayeretsedwa ndi mawu a Mulungu ndi pemphero.
6 Uba ubeluleka lezizinto abazalwane uzakuba yisikhonzi esihle sikaJesu Kristu, wondliwe emazwini okholo, lawemfundiso enhle oyilandelayo ngokunanzelela.
Ngati abale uwalangiza zimenezi, udzakhala mtumiki wabwino wa Khristu Yesu, woleredwa mʼchoonadi cha chikhulupiriro ndi mʼchiphunzitso chabwino chimene wakhala ukutsata.
7 Kodwa wale inganekwane ezimbi lezezalukazi. Uzejwayeze ukukhonza uNkulunkulu;
Koma upewe nkhani zachabe ndi nthano za amayi okalamba; mʼmalo mwake udziphunzitse kukhala moyo wolemekeza Mulungu.
8 ngoba ukwejwayeza umzimba kulokusiza okuncinyane; kodwa ukukhonza uNkulunkulu kusiza ezintweni zonke, kulesithembiso sempilo yalamuhla lezayo.
Pakuti kulimbitsa thupi kumapindulitsapo pangʼono, koma moyo woopa Mulungu umapindulitsa pa zonse. Umatilonjeza moyo pa moyo uno ndiponso pa moyo umene ukubwerawo.
9 Lithembekile ilizwi njalo lifanele konke ukwemukelwa.
Amenewa ndi mawu odalirika ndi oyenera kuwalandira kwathunthu.
10 Ngoba ngalokho lathi siyasebenza nzima futhi siyathukwa ngoba sithembele kuNkulunkulu ophilayo onguMsindisi wabo bonke abantu, ikakhulu wabakholwayo.
Nʼchifukwa chake timagwira ntchito molimbika ndi kuyesetsa, chifukwa tayika chiyembekezo chathu mwa Mulungu wamoyo, amene ndi Mpulumutsi wa anthu onse, koma makamaka wa amene amakhulupirira.
11 Laya ngalezizinto ufundise.
Lamulira ndi kuphunzitsa zinthu zimenezi.
12 Kungabi lamuntu odelela ubutsha bakho, kodwa woba yisibonelo kwabakholwayo elizwini, ekuhambeni, ethandweni, emoyeni, ekholweni, ekuhlambulukeni.
Usalole kuti wina akupeputse chifukwa ndiwe wachinyamata, koma khala chitsanzo kwa okhulupirira pa mayankhulidwe, pa makhalidwe, pa chikondi, pa chikhulupiriro ndi pa kuyera mtima.
13 Ngize ngifike, nanzelela ekubaleni, ekulayeni, ekufundiseni.
Mpaka nditabwera, udzipereke powerenga mawu a Mulungu kwa anthu, kulalikira ndi kuphunzitsa.
14 Ungadeleli isiphiwo esikuwe, owasiphiwa ngesiprofetho kanye lokubekwa izandla zobudala.
Usanyozere mphatso yako yomwe inapatsidwa kwa iwe kudzera mʼmawu auneneri pamene gulu la akulu ampingo linakusanjika manja.
15 Nakana ngalezizinto, ube kulezizinto, ukuze ukuqhubeka kwakho kubonakale phakathi kwabo bonke.
Uzichita zimenezi mosamalitsa ndi modzipereka kwathunthu, kuti aliyense aone kuti ukupita mʼtsogolo.
16 Zinanzelele wena lemfundiso. Hlala kulezizinto; ngoba ngokwenza lokho uzazisindisa wena kanye lalabo abakuzwayo.
Samala kwambiri moyo wako ndi ziphunzitso zako. Uzichitabe zimenezi chifukwa ukatero, udzadzipulumutsa ndiponso udzapulumutsa okumvetsera.