< 1 USamuyeli 1 >

1 Kwakukhona-ke indoda ethile yeRamathayimi-Zofimu entabeni yakoEfrayimi; lebizo layo lalinguElkana indodana kaJerohamu, indodana kaElihu, indodana kaTohu, indodana kaZufi umEfrayimi.
Panali munthu wina wochokera ku Ramataimu, Mzofimu wa ku dziko la mapiri la Efereimu. Iyeyu dzina lake anali Elikana ndipo anali mwana wa Yerohamu, mwana wa Elihu, mwana wa Tohu, mwana wa Zufu wa fuko la Efereimu.
2 Njalo yayilabafazi ababili; ibizo lomunye lalinguHana, lebizo lomunye lalinguPenina. Njalo uPenina wayelabantwana, kodwa uHana wayengelabantwana.
Iye anali ndi akazi awiri, Hana ndi Penina. Penina anali ndi ana, koma Hana analibe.
3 Leyondoda yenyuka-ke isuka emzini wayo iminyaka ngeminyaka ukuyakhonza lokuhlabela iNkosi yamabandla eShilo, njalo kwakukhona lapho amadodana amabili kaEli, uHofini loPhinehasi, abapristi beNkosi.
Chaka ndi chaka Elikana ankachoka ku mudzi kwawo kupita ku Silo kukapembedza ndi kukapereka nsembe kwa Yehova Wamphamvuzonse. Ku Siloko kunali ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi amene anali ansembe a Yehova.
4 Kwakusithi mhla uElkana ehlaba, wanika uPenina umkakhe lawo wonke amadodana akhe lamadodakazi akhe izabelo;
Tsiku lopereka nsembe likafika Elikana amapereka magawo a nsembeyo kwa mkazi wake Penina ndi kwa ana ake onse aamuna ndi aakazi.
5 kodwa uHana wamnika isabelo esiphindwe kabili, ngoba wayemthanda uHana; kodwa iNkosi yayisivalile isizalo sakhe.
Ngakhale ankamukonda Hana, koma ankamupatsa gawo limodzi popeza Yehova sanamupatse ana.
6 Lesitha sakhe laso samcaphula ngentukuthelo ukuze simkhathaze, ngoba iNkosi yayisivalile isizalo sakhe.
Tsono popeza Yehova sanamupatse Hana ana, mkazi mnzakeyo ankamuyamba dala ndi cholinga chomukwiyitsa.
7 Wayesenza njalo-ke iminyaka ngeminyaka; kusukela lapho esenyukela endlini yeNkosi, ngokunjalo samcaphula. Ngakho walila, kadlanga.
Izi zimachitika chaka ndi chaka. Hana ankati akamapita ku Nyumba ya Yehova mkazi mnzakeyo ankamunyogodola. Choncho Hana ankangokhalira kulira osafuna ndi kudya komwe.
8 UElkana umkakhe wasesithi kuye: Hana, ulilelani? Njalo kawudli ngani? Kungani-ke inhliziyo yakho idabukile? Mina kangingcono kuwe kulamadodana alitshumi yini?
Tsono mwamuna wake Elikana ankamufunsa kuti, “Hana ukulira chifukwa chiyani? Wakhumudwa ndi chiyani kuti sukufuna ndi kudya komwe? Kodi ine kwa iwe sindili woposa ana aamuna khumi?”
9 Ngakho uHana wasukuma emva kokudla eShilo langemva kokunatha. UEli umpristi wayehlezi-ke esihlalweni phansi kwensika yethempeli leNkosi.
Tsiku lina atatha kudya ndi kumwa ku Silo kuja, Hana anayimirira kukapemphera. Nthawiyi nʼkuti wansembe Eli atakhala pa mpando pa khomo la Nyumba ya Yehova.
10 Njalo wayelobuhlungu emphefumulweni, wasekhuleka eNkosini ekhala lokukhala inyembezi.
Hana anavutika mʼmoyo mwake, ndipo anapemphera kwa Yehova akulira kwambiri.
11 Wasefunga isifungo wathi: Nkosi yamabandla, uba ungabona lokubona ukuhlupheka kwencekukazi yakho, ungikhumbule, ungakhohlwa incekukazi yakho, kodwa unike incekukazi yakho inzalo yesilisa, ngizamnika iNkosi insuku zonke zempilo yakhe, lempuco kayiyikwedlula ekhanda lakhe.
Ndipo iye analumbira kuti, “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ngati muyangʼana kusauka kwa mtumiki wanune, ndi kuyankha pemphero langa osandiyiwala ine mtumiki wanu pondipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzamupereka mwanayo kwa inu Yehova masiku onse a moyo wake. Lumo silidzapita pa mutu pake.”
12 Kwasekusithi esaqhubeka ukukhuleka phambi kweNkosi, uEli waqaphelisa umlomo wakhe.
Akupemphera choncho kwa Yehova, Eli ankamuyangʼana pakamwa.
13 UHana wayekhulumela-ke enhliziyweni yakhe, kwanyikinyeka indebe zakhe kuphela, kodwa ilizwi lakhe lalingezwakali; ngakho uEli wacabanga ukuthi udakiwe.
Hana ankapemphera chamumtima ndipo milomo yake inkangogwedera koma mawu ake samamveka. Choncho Eli anaganiza kuti anali ataledzera.
14 UEli wasesithi kuye: Koze kube nini udakwa? Susa iwayini lakho kuwe.
Ndipo anamufunsa Hana kuti, “Kodi mukhala chiledzerere mpaka liti? Pitani, ayambe wakuchokani vinyo mwamwayo.”
15 UHana wasephendula wathi: Hatshi, nkosi yami, ngingowesifazana odabukileyo emoyeni; kanginathanga wayini loba okunathwayo okulamandla, kodwa bengithulula umphefumulo wami phambi kweNkosi.
Koma Hana anayankha kuti, “Sichoncho mbuye wanga. Ndakhala ndikumukhuthulira Yehova chisoni changa. Sindinamwe vinyo kapena chakumwa choledzeretsa chilichonse, popeza nthawi yonseyi ndakhala ndikupereka kwa Yehova nkhawa yayikulu ndi mavuto anga.
16 Ungayithathi incekukazi yakho njengendodakazi kaBheliyali, ngoba ebunengini bosizi lwami lenkathazo yami sengikhulume kwaze kwaba khathesi.
Musaganize kuti mtumiki wanu ndi kukhala mkazi wachabechabe. Ine ndakhala ndi kupereka nkhawa yanga yayikulu ndi zowawa zanga.”
17 UEli wasephendula wathi: Hamba ngokuthula; uNkulunkulu wakoIsrayeli akunike isicelo sakho osicele kuye.
Eli anayankha, “Pitani mu mtendere, ndipo Mulungu wa Israeli akupatseni zimene mwamupemphazo.”
18 Wasesithi: Incekukazi yakho kayithole umusa emehlweni akho. Ngakho owesifazana wahamba ngendlela yakhe, wadla; lobuso bakhe abaze busanyukumala ngakho.
Hana anati, “Mundikomerebe mtima mtumiki wanune.” Kenaka anachoka nakadya, ndipo sanaonekenso wachisoni.
19 Basebevuka ekuseni kakhulu, bakhonza phambi kweNkosi, basebebuyela bafika emzini wabo eRama. UElkana wasemazi uHana umkakhe, leNkosi yamkhumbula.
Elikana ndi banja lake anadzuka mmawa mwake nakapemphera pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anabwerera kwawo ku Rama. Elikana anakhala pamodzi ndi mkazi wake, ndipo Yehova anamukumbuka Hanayo.
20 Kwasekusithi ekuqhubekeni kwesikhathi uHana wakhulelwa, wabeletha indodana, wayitha ibizo layo uSamuweli; ngoba wathi: Ngimcelile eNkosini.
Motero Hana anakhala ndi pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Samueli, popeza anati, “Ndinachita kumupempha kwa Yehova.”
21 Lendoda uElkana lendlu yakhe yonke benyukela ukuyahlabela iNkosi umhlatshelo weminyaka ngeminyaka, lesifungo sakhe.
Elikana ndi banja lake lonse anapita kukapereka nsembe ya pa chaka kwa Yehova ndi kukakwaniritsa malonjezo ake.
22 Kodwa uHana kenyukanga, ngoba wathi kumkakhe: Kangiyikuhamba aze alunyulwe umfana; khona ngizamletha ukuze abonakale phambi kweNkosi, abesehlala khona kuze kube nininini.
Koma Hana sanapite nawo popeza anawuza mwamuna wake kuti, “Mwanayu akadzaleka kuyamwa, ndidzapita naye ndi kukamupereka pamaso pa Yehova ndipo adzakhala kumeneko moyo wake wonse.”
23 UElkana umkakhe wasesithi kuye: Yenza okulungileyo emehlweni akho; hlala uze umlumule; kuphela, iNkosi kayiqinise ilizwi lakho. Ngokunjalo owesifazana wahlala, wayimunyisa indodana yakhe waze wayilumula.
Elikana mwamuna wake anamuwuza kuti, “Chita chimene chakukomera. Tsala kuno mpaka utamusiyitsa kuyamwa, Yehova yekha akwaniritse mawu ake.” Choncho mkaziyo anatsala ku nyumba ndi kusamalira mwana wake mpaka atamuletsa kuyamwa.
24 Wasesenyuka layo eseyilumule, elamajongosi amathathu, le-efa elilodwa lempuphu, lembodlela yewayini, wayiletha endlini yeNkosi eShilo; lomfana wayemncinyane.
Atamuletsa kuyamwa, Hana anatenga mwanayo ali wachichepere, ndikupita naye ku nyumba ya Yehova ku Silo. Anatenga ngʼombe yamphongo ya zaka zitatu, ufa wa makilogalamu khumi, ndi thumba lachikopa la vinyo.
25 Balihlaba ijongosi, bamletha umntwana kuEli.
Tsono anapha ngʼombe yamphongo ija ndi kupereka mwana uja kwa Eli.
26 Wasesithi: Hawu nkosi yami, kuphila komphefumulo wakho, nkosi yami, yimi owesifazana owayemi lawe lapha, ekhuleka eNkosini.
Ndipo Hana anati kwa Eli, “Mbuye wanga, ine ndikunenetsadi pamaso panu kuti ndine mkazi uja amene anayima pamaso panu ndi kumapemphera kwa Yehova.
27 Ngakhulekela lo umfana, njalo iNkosi inginikile isicelo sami engasicela kuyo.
Ndinapempha mwana uyu, ndipo Yehova wandipatsa chimene ndinamupempha.
28 Ngakho lami ngimnikele eNkosini, zonke izinsuku ekhona; wacelwa eNkosini. Wasekhonza iNkosi lapho.
Ndiye tsopano ine ndikumupereka kwa Yehova. Pa moyo wake wonse adzakhala wa Yehova.” Ndipo onse anapembedza Yehova kumeneko.

< 1 USamuyeli 1 >