< 1 USamuyeli 8 >

1 Kwasekusithi uSamuweli esemdala wabeka amadodana akhe ukuze abe ngabahluleli koIsrayeli.
Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
2 Lebizo lendodana yakhe elizibulo lalinguJoweli, lebizo leyesibili yakhe linguAbhiya; ayengabahluleli eBherishebha.
Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
3 Kodwa amadodana akhe ayengahambi ngendlela zakhe, kodwa aphambukela enzuzweni embi, emukela isivalamlomo, aphambula isahlulelo.
Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
4 Kwasekubuthana abadala bonke bakoIsrayeli, beza kuSamuweli eRama,
Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
5 bathi kuye: Khangela, wena usumdala, lamadodana akho kawahambi ngendlela zakho; ngakho sibekele inkosi ukuze isahlulele njengazo zonke izizwe.
Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
6 Kodwa leyonto yayimbi emehlweni kaSamuweli lapho besithi: Sinike inkosi ukusahlulela. USamuweli wasekhuleka eNkosini.
Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
7 INkosi yasisithi kuSamuweli: Lalela ilizwi labantu kukho konke abakutshoyo kuwe, ngoba kakusuwe abakwalayo, kodwa bala mina ukuze ngingabusi phezu kwabo.
Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
8 Ngokwezenzo zonke abazenzileyo kusukela ngosuku engabenyusa ngalo eGibhithe kuze kube lamuhla, bangitshiyile bakhonza abanye onkulunkulu; benza njalo lakuwe.
Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
9 Ngakho khathesi, lalela ilizwi labo; kodwa nxa ubafakazele kakhulu, ubazise indlela yenkosi ezabusa phezu kwabo.
Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
10 USamuweli wasetshela abantu abacela kuye inkosi wonke amazwi eNkosi.
Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
11 Wasesithi: Le izakuba yindlela yenkosi ezabusa phezu kwenu; izathatha amadodana enu izibekele wona enqoleni zayo lakubagadi bamabhiza ayo, agijime phambi kwezinqola zayo.
Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
12 Izazibekela wona abe yizinduna zezinkulungwane lezinduna zamatshumi amahlanu, lokulima amasimu ayo, lokuvuna isivuno sayo, lokwenza izikhali zayo zempi, lezikhali zezinqola zayo.
Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
13 Izathatha amadodakazi enu iwenze abe ngabenzi bamakha, labapheki, labaphekizinkwa.
Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
14 Izathatha amasimu enu, lezivini zenu lezivande zenu zemihlwathi, ezinhle, ikunike inceku zayo.
Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
15 Izathatha okwetshumi yenhlanyelo yenu leyezivini zenu, iyinike induna zayo lenceku zayo.
Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
16 Izathatha inceku zenu lencekukazi zenu lamajaha enu angcono labobabhemi benu, ikusebenzise emsebenzini wayo.
Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
17 Izathatha okwetshumi kwemihlambi yenu; lina-ke libe yizinceku zayo.
Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
18 Njalo lizakhala ngalolosuku ngenxa yenkosi yenu elizikhethele yona; kodwa iNkosi kayiyikuliphendula mhlalokho.
Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
19 Kodwa abantu bala ukulilalela ilizwi likaSamuweli, bathi: Hatshi, kodwa kuzakuba lenkosi phezu kwethu,
Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
20 ukuze lathi sibe njengezizwe zonke, lenkosi yethu isahlulele, iphume phambi kwethu, ilwe izimpi zethu.
Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
21 USamuweli esewazwile wonke amazwi abantu, wawalandisa endlebeni zeNkosi.
Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
22 INkosi yasisithi kuSamuweli: Lalela ilizwi labo, ubabekele inkosi. USamuweli wasesithi emadodeni akoIsrayeli: Hambani liye ngulowo lalowo emzini wakhe.
Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”

< 1 USamuyeli 8 >