< 1 USamuyeli 3 >
1 Umfana uSamuweli wayesebenzela iNkosi phambi kukaEli. Lelizwi leNkosi laliligugu ngalezonsuku; kwakungekho lombono osabaleleyo.
Samueli ankatumikira Yehova moyangʼaniridwa ndi Eli. Masiku amenewo mawu a Yehova sankamveka pafupipafupi. Kuona zinthu mʼmasomphenya sikunkachitikanso kawirikawiri.
2 Kwasekusithi ngalolosuku uEli elele endaweni yakhe, lamehlo akhe eseqala ukufiphala engelakubona,
Tsiku lina Eli, amene maso anali ofowoka ndi kuti sankatha kuona bwino, anagona pa malo ake.
3 lesibane sikaNkulunkulu sasingakacitshwa, njalo uSamuweli wayelele ethempelini leNkosi, lapho okwakukhona umtshokotsho kaNkulunkulu,
Nthawiyi nʼkuti nyale ya Mulungu isanazimitsidwe. Samueli anali gone mu Nyumba ya Yehova, kumene kunali Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
4 iNkosi yambiza uSamuweli, owathi: Khangela ngilapha.
Yehova anayitana Samueli. Iye anayankha kuti, “Wawa.”
5 Wasegijimela kuEli, wathi: Khangela ngilapha, ngoba ungibizile. Wasesithi: Kangibizanga, buyela ulale. Wasesiyalala.
Ndipo iyeyo anathamangira kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera ndamva kuyitana.” Koma Eli anati, “Ine sindinakuyitane, bwerera kagone.” Ndipo iye anapita kukagona.
6 INkosi yasibuya imbiza uSamuweli futhi. USamuweli wasevuka waya kuEli, wathi: Khangela ngilapha, ngoba ungibizile. Kodwa wathi: Kangibizanga, ndodana yami; buyela ulale.
Yehova anayitananso, “Samueli!” Ndipo Samueli anadzuka ndi kupita kwa Eli nati, “Ndabwera popeza ndamva mukundiyitana.” Eli nati, “Mwana wanga, ine sindinakuyitane, bwerera kagone.”
7 Kodwa uSamuweli wayengakayazi iNkosi, lelizwi leNkosi lalingakembulwa kuye.
Nthawiyi nʼkuti Samueli asanadziwe Yehova ndipo Mawu a Yehova nʼkuti asanawululidwe kwa iye.
8 INkosi yasimbiza futhi uSamuweli ngokwesithathu. Wasevuka waya kuEli wathi: Khangela ngilapha, ngoba ungibizile. UEli waseqedisisa ukuthi iNkosi imbizile umfana.
Yehova anayitananso Samueli kachitatu ndipo Samueli anadzuka ndikupita kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera popeza mwandiyitana ndithu.” Apo Eli anazindikira kuti Yehova ndiye ankayitana mnyamatayo.
9 Ngakho uEli wathi kuSamuweli: Hamba uyelala; kuzakuthi-ke nxa ikubiza uzakuthi: Khuluma Nkosi, ngoba inceku yakho iyezwa. Wasehamba uSamuweli, walala endaweni yakhe.
Tsono Eli anamuwuza Samueli kuti, “Pita ukagone ndipo akakuyitananso ukanene kuti, ‘Yankhulani Yehova, pakuti mtumiki wanu ndikumvetsera.’” Choncho Samueli anapita ndi kukagona pamalo pake.
10 INkosi yasisiza, yema, yabiza njengakwezinye izikhathi: Samuweli, Samuweli! Wasesithi uSamuweli: Khuluma, ngoba inceku yakho iyezwa.
Yehova anabwera ndi kuyima pomwepo, ndi kuyitana monga nthawi zina zija, “Samueli! Samueli!” Ndipo Samueli anayankha, “Yankhulani, pakuti mtumiki wanu akumvetsera.”
11 INkosi yasisithi kuSamuweli: Khangela, ngizakwenza into koIsrayeli ezakhenceza indlebe zombili zalowo wonke oyizwayo.
Ndipo Yehova anati kwa Samueli, “Taona, patsala pangʼono kuti ndichite chinthu china mu Israeli chimene chidzadabwitsa aliyense amene adzamve.
12 Ngalolosuku ngizakwenza ngimelene loEli konke engakukhuluma ngendlu yakhe; ngiqalise ngiqede.
Tsiku limenelo ndidzachitadi zonse zimene ndinayankhula zokhudza banja la Eli kuyambira poyamba mpaka pomaliza.
13 Ngoba ngimtshelile ukuthi ngizagweba indlu yakhe kuze kube nininini ngesiphambeko asaziyo, ngoba amadodana akhe azenza aqalekiswa, kodwa kawakhuzanga.
Pakuti ndinamudziwitsa kuti Ine ndikhoza kulanga banja lake kwamuyaya chifukwa cha zoyipa zimene ana ake ankadziyipitsa nazo. Iye ankadziwa zimenezi koma osawaletsa.
14 Ngakho-ke ngifungile kuyo indlu kaEli ukuthi ububi bendlu kaEli kabuyikuhlangulwa ngomhlatshelo langomnikelo kuze kube phakade.
Nʼchifukwa chake ndinalumbira kuti, ‘Zoyipa zimene banja la Eli linandichita sizidzafafanizidwa mpaka muyaya ngakhale adzapereke nsembe kapena zopereka zina.’”
15 USamuweli waselala kwaze kwasa; wavula iminyango yendlu yeNkosi, kodwa uSamuweli wesaba ukumtshela uEli umbono.
Samueli anagona mpaka mmawa. Atadzuka anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova. Iye anachita mantha kumuwuza Eli za masomphenya ake.
16 UEli wasembiza uSamuweli, wathi: Samuweli, ndodana yami. Wasesithi: Khangela ngilapha.
Koma Eli anamuyitana nati, “Samueli mwana wanga.” Samueli anayankha kuti, “Wawa.”
17 Wasesithi: Yinto bani eyikhulume kuwe? Ake ungangifihleli; kenze njalo uNkulunkulu kuwe, ngokunjalo engezelele, uba ungifihlela ulutho lwazo zonke izinto akutshele zona.
Tsono Eli anafunsa kuti, “Yehova wakuwuza chiyani? Usandibisire. Mulungu akulange ndithu ngati undibisira chilichonse cha zimene wakuwuza.”
18 Ngakho uSamuweli wasemtshela zonke izinto, kamfihlelanga lutho. Wasesithi: YiNkosi, kayenze lokho okulungileyo emehlweni ayo.
Choncho Samueli anamuwuza zonse, sanamubisire kalikonse. Ndipo Eli anati, “Iye ndi Yehova, mulekeni achite chimene chamukomera.”
19 Wakhula-ke uSamuweli, leNkosi yayilaye, kayiyekelanga lelilodwa lamazwi ayo liwele emhlabathini.
Yehova anali ndi Samueli pamene amakula, ndipo zonse zimene ankayankhula zinkachitikadi.
20 UIsrayeli wonke-ke kusukela koDani kuze kube seBherishebha wazi ukuthi uSamuweli uqinisiwe ukuthi abe ngumprofethi weNkosi.
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dera la Dani mpaka ku Beeriseba anazindikira kuti Yehova analozadi chala pa Samueli kuti akhale mneneri wake.
21 INkosi yaphinda yabonakala eShilo, ngoba iNkosi yazibonakalisa kuSamuweli eShilo ngelizwi leNkosi.
Yehova anapitiriza kuoneka ku Silo, ndipo kumeneko anadziwulula yekha kwa Samueli mwa mawu ake.