< 1 USamuyeli 22 >

1 UDavida wasesuka lapho, waphephela ebhalwini lweAdulamu. Lapho abafowabo lendlu yonke kayise bekuzwa lokho, behlela kuye lapho.
Davide anachoka kumeneko nathawira ku phanga la Adulamu. Abale ake ndi banja lonse la abambo ake anamva izi, anapita kumene kunali Davide.
2 Kwasekubuthana kuye wonke umuntu ocindezelweyo, laye wonke umuntu owayelesikwelede, laye wonke umuntu owayebuhlungu emphefumulweni, wasesiba yinduna phezu kwabo, kwaze kwaba laye phose abantu abangamakhulu amane.
Ndipo aliyense amene anali pa mavuto, kapena ndi ngongole kapenanso amene anali wosakondwa anasonkhana kwa iye, ndipo iye anakhala mtsogoleri wawo. Onse pamodzi analipo amuna 400.
3 UDavida wasesuka lapho waya eMizipa yakoMowabi, wathi enkosini yakoMowabi: Ngiyacela ukuthi ubaba lomama baphume lani, ngize ngazi ukuthi uNkulunkulu uzangenzelani.
Kuchokera kumeneko Davide anapita ku Mizipa ku Mowabu ndipo anapempha mfumu ya Mowabu kuti, “Bwanji abambo ndi amayi anga akhale nanu mpaka ine nditadziwa chimene Mulungu adzachite nane?”
4 Wasebaletha phambi kwenkosi yakoMowabi, basebehlala layo insuku zonke uDavida esenqabeni.
Choncho iye anawasiya kwa mfumu ya Mowabu ndipo anakhala naye nthawi yonse imene Davide ankabisala ku phanga kuja.
5 Umprofethi uGadi wasesithi kuDavida: Ungahlali enqabeni; hamba wena ngena elizweni lakoJuda. UDavida wasehamba wangena eguswini leHerethi.
Koma mneneri Gadi anawuza Davide kuti, “Usakhale ku phanga kuno. Pita ku dziko la Yuda.” Kotero Davide anachoka ndi kupita ku nkhalango ya Hereti.
6 USawuli wasesizwa ukuthi uDavida uyaziwa labantu ababelaye. USawuli wayehlezi eGibeya ngaphansi kwesihlahla setamarisiki eRama, elomkhonto esandleni sakhe, lazo zonke inceku zakhe zazimi laye.
Tsono Sauli anamva kuti Davide ndi anthu ake apezeka. Nthawiyo nʼkuti Sauli atakhala pansi pa mtengo wa bwemba pa phiri la ku Gibeya, mkondo uli mʼdzanja lake ndi ankhondo ake atayima chomuzungulira.
7 USawuli wasesithi ezincekwini zakhe ezazimi laye: Ake lizwe, bakoBhenjamini: Kambe indodana kaJese izalinika lonke amasimu lezivini, ilibeke lonke libe zinduna zezinkulungwane lezinduna zamakhulu,
Tsono Sauli anafunsa ankhondo ake aja kuti, “Tamverani inu anthu a fuko la Benjamini! Kodi mwana wa Yese adzakupatsani nonsenu minda ndi minda ya mpesa? Kodi nonsenu adzakuyikani kukhala atsogoleri a magulu ankhondo?
8 ngokuthi lonke lingenzele ugobe, njalo kakho owembule endlebeni yami ukuthi indodana yami yenza isivumelwano lendodana kaJese; kakho loyedwa kini ongizwelayo, lowembula endlebeni yami, ukuthi indodana yami ingivusela inceku yami ukuthi icathame njengalamuhla?
Mwinatu nʼchifukwa chake mwagwirizana zondichita chiwembu. Palibe amene anandiwuza pamene mwana wanga ankapanga pangano ndi mwana wa Yese. Palibe aliyense amene ankalabadirako za ine kapena kundiwuza kuti mwana wanga wautsa mtima wa wantchito wanga kuti andiwukire monga wachitira lero.”
9 Kwasekuphendula uDowegi umEdoma owayemi lenceku zikaSawuli, wathi: Ngayibona indodana kaJese isiza eNobi kuAhimeleki indodana kaAhitubi.
Koma Doegi Mwedomu anayima pafupi ndi nduna za Sauli nati, “Ine ndinaona mwana wa Yese atabwera kwa Ahimeleki mwana wa Ahitubi ku Nobi.
10 Wasembuzela eNkosini, wamnika umphako, lenkemba kaGoliyathi umFilisti wamnika yona.
Ahimelekiyo anafunsa kwa Yehova chomwe Davide ayenera kuchita. Iye anamupatsa zakudya ndiponso lupanga la Goliati Mfilisiti uja.”
11 Inkosi uSawuli yasithuma ukubiza uAhimeleki umpristi, indodana kaAhitubi, lendlu yonke kayise, abapristi ababeseNobi; bonke basebesiza enkosini.
Pamenepo mfumu inayitanitsa wansembe Ahimeleki mwana wa Ahitubi ndi banja lonse la abambo ake, amene anali ansembe ku Nobi. Ndipo onse anabwera kwa mfumu.
12 USawuli wasesithi: Ake ulalele, ndodana kaAhitubi. Wasesithi: Khangela ngilapha, nkosi yami.
Sauli anati, “Tsono tamvera, mwana wa Ahitubi.” Iye anayankha kuti, “Inde mbuye wanga.”
13 USawuli wasesithi kuye: Kungani lingenzela ugobe, wena lendodana kaJese, njengoba wayinika isinkwa lenkemba, wayibuzela kuNkulunkulu, ukuthi ingivukele icathame njengalamuhla?
Sauli anamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani iwe ndi mwana wa Yese mwandiwukira ine? Wamupatsa buledi ndi lupanga. Wafunsiranso kwa Yehova zoti andiwukire ndi kundibisalira monga wachita leromu?”
14 UAhimeleki waseyiphendula inkosi wathi: Pho, ngubani kuzo zonke inceku zakho othembekileyo njengoDavida, ongumkhwenyana wenkosi, oqhubeka ekukulaleleni, lohloniphekayo endlini yakho?
Ahimeleki anayankha mfumu kuti, “Kodi ndani mwa ankhondo anu onse amene ali wokhulupirika monga Davide? Iye uja ndi mkamwini wa mfumu, kapitawo wa asilikali okutetezani ndiponso munthu amene amalemekezedwa mʼbanja lanu?
15 Ngiyaqalisa lamuhla yini ukumbuzela kuNkulunkulu? Kakube khatshana lami! Inkosi kayingabeki udaba encekwini yayo lendlini yonke kababa; ngoba inceku yakho yayingazi lutho ngaloludaba, oluncinyane kumbe olukhulu.
Kodi tsiku limeneli linali loyamba kuti ndimufunsire kwa Yehova? Ayi sichoncho! Mfumu musandinenere kanthu kalikonse koyipa kapena banja la abambo anga, pakuti sindikudziwa kanthu kena kalikonse ka zimenezi.”
16 Inkosi yasisithi: Ahimeleki, uzakufa lokufa, wena lendlu yonke kayihlo.
Koma mfumu inati, “Iwe Ahimeleki ndi banja lonse la abambo ako mudzaphedwa ndithu.”
17 Inkosi yasisithi kuzigijimi ezazimi layo: Phendukani, libulale abapristi beNkosi; ngoba isandla sabo laso siloDavida, futhi ngoba babesazi ukuthi ubalekile, kodwa kabembulanga endlebeni yami. Kodwa inceku zenkosi kazithandanga ukwelula isandla sazo ukuthi zihlasele abapristi beNkosi.
Kenaka mfumu inalamulira alonda amene anali naye kuti, “Iphani ansembe a Yehovawa chifukwa iwo akugwirizana ndi Davide. Iwo amadziwa kuti Davide ankathawa koma sanandiwuze.” Koma antchito a mfumu aja sanasamule dzanja kuti aphe ansembe a Yehova.
18 Inkosi yasisithi kuDowegi: Phenduka wena, uhlasele abapristi. UDowegi umEdoma wasephenduka, yena wahlasela abapristi, wabulala ngalolosuku abantu abangamatshumi ayisificaminwembili lanhlanu ababegqoke i-efodi yelembu elicolekileyo.
Kotero mfumu inalamula Doegi kuti, “Uwaphe ndiwe ansembewa.” Choncho Doegi Mwedomu anapita ndi kuwapha. Tsiku limenelo iye anapha amuna 85 amene amavala efodi wa nsalu yofewa.
19 LeNobi, umuzi wabapristi, wayitshaya ngobukhali benkemba, kusukela endodeni kusiya kowesifazana, kusukela emntwaneni kusiya komunyayo, lezinkabi labobabhemi lezimvu, ngobukhali benkemba.
Kunena za Nobi, mzinda wa ansembe, Sauli anapha amuna ndi amayi, ana ndi makanda pamodzi ndi ngʼombe, abulu ndi nkhosa.
20 Kodwa omunye wamadodana kaAhimeleki indodana kaAhitubi waphepha, obizo lakhe lalinguAbhiyatha, wabaleka walandela uDavida.
Koma Abiatara mwana wa Ahimeleki mwana wa Ahitubi anapulumuka ndi kuthawira kwa Davide.
21 UAbhiyatha wasetshela uDavida ukuthi uSawuli ubulele abapristi beNkosi.
Abiatara anawuza Davide kuti Sauli wapha ansembe a Yehova.
22 UDavida wasesithi kuAbhiyatha: Ngakwazi ngalolosuku lapho uDowegi umEdoma elapho ukuthi uzamtshela lokumtshela uSawuli. Yimi engibangele ukufa kwawo wonke umphefumulo wendlu kayihlo.
Ndipo Davide anati kwa Abiatara, “Tsiku lija pamene Doegi Mwedomu anali kumene kuja, ine ndimadziwa kuti salephera kukamuwuza Sauli. Ine ndi amene ndaphetsa banja lonse la abambo ako.
23 Hlala lami, ungesabi, ngoba lowo odinga umphefumulo wami udinga umphefumulo wakho; kodwa uzalondolozeka ulami.
Iwe khala ndi ine, usaope munthu amene akufuna moyo wako komanso wanga. Udzatetezeka ukakhala ndi ine.”

< 1 USamuyeli 22 >