< 1 Amakhosi 1 >
1 Inkosi uDavida yayisindala ilensuku ezinengi; basebeyembesa ngezembatho, kodwa kayikhudumalanga.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 Inceku zayo zasezisithi kuyo: Inkosi yami, inkosi, kayidingelwe intombazana emsulwa, ukuthi ime phambi kwenkosi, iyonge, ilale esifubeni sakho, ukuze inkosi yami, inkosi, ikhudumale.
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 Zasezidinga intombazana enhle emingceleni yonke yakoIsrayeli, zathola uAbishagi umShunami, zamletha enkosini.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 Intombazana yayinhle kakhulu sibili, yaba ngumongi wenkosi, yayisebenzela; kodwa inkosi kayiyazanga.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 UAdonija indodana kaHagithi waseziphakamisa esithi: Mina ngizakuba yinkosi. Wasezilungisela inqola labagadi bamabhiza, lamadoda angamatshumi amahlanu ukugijima phambi kwakhe.
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6 Uyise wayengazanga amdanise lakanye esithi: Wenzeleni kanje? Laye futhi wayelesimo esihle kakhulu, lonina wamzala emva kukaAbisalomu.
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 Lamazwi akhe ayeloJowabi indodana kaZeruya njalo loAbhiyatha umpristi, basebencedisa, bamlandela uAdonija.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 Kodwa uZadoki umpristi, loBhenaya indodana kaJehoyada, loNathani umprofethi, loShimeyi, loReyi, lamaqhawe uDavida ayelawo, babengekho kuAdonija.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 UAdonija wahlaba izimvu lezinkabi lokunonisiweyo elitsheni leZohelethi eliseceleni kweEni-Rogeli, wanxusa bonke abafowabo, amadodana enkosi, lawo wonke amadoda akoJuda, inceku zenkosi;
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 kodwa oNathani umprofethi loBhenaya lamaqhawe loSolomoni umfowabo kabanxusanga.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 Ngakho uNathani wakhuluma kuBathisheba unina kaSolomoni esithi: Kawuzwanga yini ukuthi uAdonija indodana kaHagithi uyabusa, lenkosi yethu uDavida kayikwazi?
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 Ngakho-ke woza, ake ngikuphe iseluleko, ukuze usindise impilo yakho lempilo yendodana yakho uSolomoni.
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 Hamba ungene enkosini uDavida uthi kuyo: Wena nkosi yami, nkosi, kawufunganga yini kuncekukazi yakho usithi: Qotho, uSolomoni indodana yami uzabusa emva kwami, njalo yena uzahlala esihlalweni sami sobukhosi? Pho, kungani kubusa uAdonija?
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 Khangela, ulokhu usakhuluma lapho lenkosi, ngingene lami emva kwakho, ngiqinise amazwi akho.
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 UBathisheba wasengena enkosini ekamelweni. Inkosi yayisindala kakhulu, loAbishagi umShunami wayeyisebenzela inkosi.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 UBathisheba waseguqa wakhothamela inkosi; inkosi yasisithi: Ulani?
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 Wasesithi kuyo: Nkosi yami, wena wafunga ngoJehova uNkulunkulu wakho kuncekukazi yakho usithi: Qotho uSolomoni indodana yakho uzabusa emva kwami, njalo yena uzahlala esihlalweni sami sobukhosi.
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 Kodwa khathesi khangela, uAdonija uyabusa, khathesi-ke, nkosi yami, nkosi, kawukwazi.
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 Usehlabe izinkabi lokunonisiweyo lezimvu ezinengi, wanxusa wonke amadodana enkosi loAbhiyatha umpristi loJowabi induna yebutho; kodwa uSolomoni inceku yakho kamnxusanga.
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 Wena-ke, nkosi yami, nkosi, amehlo kaIsrayeli wonke aphezu kwakho ukuthi ubatshele ukuthi ngubani ozahlala esihlalweni sobukhosi senkosi yami, inkosi, emva kwayo,
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 hlezi kuzakuthi lapho inkosi yami, inkosi, izalala laboyise, mina lendodana yami uSolomoni sizakuba yizoni.
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 Khangela-ke, elokhu esakhuluma lenkosi, loNathani umprofethi wangena.
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 Basebeyibikela inkosi besithi: Khangela uNathani umprofethi. Esengene phambi kwenkosi wakhothama phambi kwenkosi ngobuso bakhe emhlabathini.
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 UNathani wasesithi: Nkosi yami, nkosi, wena utshilo yini ukuthi: UAdonija uzabusa emva kwami, njalo yena uzahlala esihlalweni sami sobukhosi?
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 Ngoba wehlile lamuhla, uhlabile izinkabi lokunonisiweyo lezimvu ezinengi, wanxusa wonke amadodana enkosi, lenduna zebutho, loAbhiyatha umpristi; khangela-ke, bayadla bayanatha phambi kwakhe, njalo bathi: Kayiphile inkosi uAdonija!
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 Kodwa mina, mina inceku yakho loZadoki umpristi loBhenaya indodana kaJehoyada loSolomoni inceku yakho, kasinxusanga.
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 Lindaba yenziwe yinkosi yami, inkosi, yini? Njalo kawazisanga inceku yakho ukuthi ngubani ozahlala esihlalweni sobukhosi senkosi yami, inkosi, emva kwayo?
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 Inkosi uDavida yasiphendula yathi: Ngibizelani uBathisheba. Wasengena phambi kobuso benkosi, wema phambi kwenkosi.
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 Inkosi yasifunga yathi: Kuphila kukaJehova ohlenge umphefumulo wami kuzo zonke inhlupheko,
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
30 ngitsho, njengoba ngafunga kuwe ngeNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli, ngisithi: Qotho, uSolomoni indodana yakho uzabusa emva kwami, njalo yena uzahlala esihlalweni sami sobukhosi esikhundleni sami; qotho ngizakwenza njalo lamuhla.
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 UBathisheba wasekhothama ngobuso emhlabathini, waguqela inkosi wathi: Kayiphile inkosi yami, inkosi uDavida kuze kube nininini!
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 Inkosi uDavida yasisithi: Ngibizelani uZadoki umpristi, loNathani umprofethi, loBhenaya indodana kaJehoyada. Basebengena phambi kwenkosi.
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 Inkosi yasisithi kibo: Thathani kanye lani inceku zenkosi yenu, ligadise uSolomoni indodana yami imbongolo engeyami, limehlisele eGihoni.
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 Kakuthi-ke uZadoki umpristi loNathani umprofethi bamgcobe khona abe yinkosi phezu kukaIsrayeli; beselivuthela uphondo lithi: Kayiphile inkosi uSolomoni!
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 Beselisenyuka emva kwakhe, njalo uzakuza ahlale esihlalweni sami sobukhosi, ngoba uzakuba yinkosi esikhundleni sami, njalo yena ngimbekile ukuthi abe ngumbusi phezu kukaIsrayeli laphezu kukaJuda.
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 UBhenaya indodana kaJehoyada waseyiphendula inkosi wathi: Ameni. Kayitsho njalo iNkosi, uNkulunkulu wenkosi yami, inkosi!
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 Njengoba uJehova ubelenkosi yami, inkosi, kabe njalo loSolomoni, asenze isihlalo sakhe sobukhosi sibe sikhulu kulesihlalo sobukhosi senkosi yami, inkosi uDavida.
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 Ngakho uZadoki umpristi, loNathani umprofethi, loBhenaya indodana kaJehoyada, lamaKerethi, lamaPelethi behla bamgadisa uSolomoni imbongolo yenkosi uDavida, bamusa eGihoni.
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 UZadoki umpristi wasethatha uphondo lwamafutha ethenteni, wamgcoba uSolomoni. Basebevuthela uphondo, bonke abantu bathi: Kayiphile inkosi uSolomoni!
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 Bonke abantu basebesenyuka emva kwakhe, bonke abantu basebevuthela imihlanga bethokoza ngentokozo enkulu, waze waqhekezeka umhlaba ngomsindo wabo.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 UAdonija labo bonke abanxusiweyo ababelaye basebewuzwa sebeqede ukudla. Lapho uJowabi esizwa ukukhala kophondo wathi: Ngowani umsindo womuzi oxokozelayo?
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 Lapho esakhuluma, khangela, kwafika uJonathani indodana kaAbhiyatha umpristi; uAdonija wathi: Ngena, ngoba uliqhawe, uletha imibiko emihle.
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 UJonathani wasephendula wathi kuAdonija: Qotho, inkosi yethu, inkosi uDavida, imbekile uSolomoni waba yinkosi;
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 njalo inkosi ithume kanye laye uZadoki umpristi, loNathani umprofethi, loBhenaya indodana kaJehoyada, lamaKerethi, lamaPelethi, bamgadisa imbongolo yenkosi.
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 Njalo uZadoki umpristi loNathani umprofethi bamgcobile waba yinkosi eGihoni, benyuka khona bethokoza; yikho umuzi uxokozela. Yiwo lowomsindo eliwuzwileyo.
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 Futhi uSolomoni usehlezi esihlalweni sobukhosi sombuso.
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 Futhi lenceku zenkosi zifikile ukubusisa inkosi yethu, inkosi uDavida, zisithi: UNkulunkulu wakho kalenze ibizo likaSolomoni libe ngcono kulebizo lakho, enze isihlalo sakhe sobukhosi sibe sikhulu kulesihlalo sakho sobukhosi. Inkosi yasikhothama embhedeni.
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 Futhi-ke yatsho njalo inkosi: Kayibusiswe iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli, enike lamuhla ohlala esihlalweni sami sobukhosi, amehlo ami ekubona.
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 Bonke abanxusiweyo ababeloAdonija basebethuthumela, basukuma, bahamba ngulowo lalowo ngendlela yakhe.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 UAdonija wasesesaba ngenxa kaSolomoni, wasukuma wahamba, wabamba impondo zelathi.
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 Wasebikelwa uSolomoni ukuthi: Khangela, uAdonija uyayesaba inkosi uSolomoni; ngoba khangela, usebambe impondo zelathi esithi: Inkosi uSolomoni kayifunge kimi lamuhla ukuthi kayiyikuyibulala inceku yayo ngenkemba.
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 USolomoni wasesithi: Uba eyindoda uqobo, kakuyikuwa okonwele lwakhe emhlabathini. Kodwa uba ububi butholakala kuye, uzakufa.
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 Inkosi uSolomoni yasithuma, bamehlisa elathini. Wasesiza wakhothama enkosini uSolomoni; uSolomoni wasesithi kuye: Yana endlini yakho.
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”