< 1 Amakhosi 5 >
1 UHiramu inkosi yeTire wasethuma inceku zakhe kuSolomoni, ngoba wayezwile ukuthi bamgcobile ukuthi abe yinkosi esikhundleni sikayise, ngoba uHiramu wayemthanda uDavida insuku zonke.
Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
2 USolomoni wasethumela kuHiramu esithi:
Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
3 Wena uyazi ukuthi uDavida ubaba wayengelakwakhela ibizo leNkosi uNkulunkulu wakhe indlu ngenxa yezimpi ezazimzingelezele, iNkosi yaze yazifaka ngaphansi kwengaphansi yenyawo zakhe.
“Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
4 Kodwa khathesi iNkosi uNkulunkulu inginikile ukuphumula inhlangothi zonke; kakulasitha, njalo kakulabubi obenzakalayo.
Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
5 Khangela-ke, ngizimisele ukwakhela ibizo leNkosi uNkulunkulu wami indlu njengokutsho kweNkosi kuDavida ubaba isithi: Indodana yakho engizayibeka esihlalweni sakho sobukhosi esikhundleni sakho, yona izakwakhela ibizo lami indlu.
Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
6 Ngakho-ke laya ukuthi bangigamulele imisedari eLebhanoni, lenceku zami zizakuba lenceku zakho; leholo lenceku zakho ngizakunika njengakho konke okutshoyo. Ngoba wena uyakwazi ukuthi kakho phakathi kwethu okwaziyo ukugamula izihlahla njengabeSidoni.
“Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
7 Kwasekusithi uHiramu esizwa amazwi kaSolomoni wathokoza kakhulu wathi: Kayibusiswe iNkosi lamuhla emnikileyo uDavida indodana ehlakaniphileyo phezu kwalesisizwe esikhulu.
Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
8 UHiramu wasethumela kuSolomoni esithi: Ngizwile lokho ongithumele ngakho; mina ngizakwenza zonke iziloyiso zakho mayelana lezigodo zemisedari lamayelana lezigodo zamafiri.
Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
9 Inceku zami zizazehlisa zisuka eLebhanoni zisiya elwandle; mina-ke ngizazenza okundendayo olwandle ukuya endaweni ozayiqamba kimi, ngizithukulule lapho; wena-ke uzazithathela khona, wena uzakwenza isifiso sami ngokupha abendlu yami ukudla.
Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
10 Ngakho uHiramu wamnika uSolomoni izigodo zemisedari lezigodo zamafiri njengokwezifiso zakhe zonke.
Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
11 LoSolomoni wanika uHiramu amakhori engqoloyi azinkulungwane ezingamatshumi amathathu lambili, ukudla kwabendlu yakhe, lamakhori angamatshumi amabili amafutha akhanyiweyo. Ngokunjalo uSolomoni wamupha uHiramu iminyaka ngeminyaka.
ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
12 INkosi yasimnika uSolomoni inhlakanipho njengokutsho kwayo kuye. Kwasekusiba khona ukuthula phakathi kukaHiramu loSolomoni; benza isivumelwano bobabili.
Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
13 Inkosi uSolomoni yabutha izibhalwa kuIsrayeli wonke; lezibhalwa zazingabantu abazinkulungwane ezingamatshumi amathathu.
Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
14 Yasibathuma eLebhanoni, abazinkulungwane ezilitshumi ngenyanga ngamazopho, inyanga beseLebhanoni, inyanga ezimbili besekhaya. LoAdoniramu wayephezu kwezibhalwa.
Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
15 Futhi uSolomoni wayelabayizinkulungwane ezingamatshumi ayisikhombisa abathwala imithwalo, lababazi abazinkulungwane ezingamatshumi ayisificaminwembili ezintabeni,
Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
16 ngaphandle kwezinduna zabaphathi bakaSolomoni, ababephethe umsebenzi, izinkulungwane ezintathu lamakhulu amathathu, ezazibusa abantu ababesenza umsebenzi.
ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
17 Inkosi yasilaya, baletha amatshe amakhulu, amatshe aligugu, okubeka isisekelo sendlu, amatshe abaziweyo.
Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
18 Abakhi bakaSolomoni labakhi bakaHiramu lamaGebhali basebebaza, balungisa izigodo lamatshe ukwakha indlu.
Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.