< 1 Amakhosi 19 >
1 UAhabi wasetshela uJezebeli konke uElija ayekwenzile, labo bonke ababulalayo, bonke abaprofethi, ngenkemba.
Tsono Ahabu anawuza Yezebeli zonse zimene anachita Eliya ndi momwe anaphera aneneri onse ndi lupanga.
2 Khona uJezebeli wathuma isithunywa kuElija esithi: Kabenze njalo onkulunkulu, bengezelele njalo, uba ngalesisikhathi kusasa ngingenzi impilo yakho ibe njengempilo yomunye wabo.
Choncho Yezebeli anatuma mthenga kwa Eliya kuti akamuwuze kuti, “Milungu indilange, ndipo indilange koopsa, ngati mawa nthawi ngati yomwe ino sindidzakupha iwe monga unaphera aneneriwo.”
3 Esekubonile, wasukuma, wahamba ngenxa yempilo yakhe, wafika eBherishebha engeyakoJuda, watshiya khona inceku yakhe.
Eliya ataona zimenezi, ananyamuka nathawa kupulumutsa moyo wake. Atafika ku Beeriseba ku Yuda, anasiya mtumiki wake kumeneko,
4 Kodwa yena wahamba uhambo losuku enkangala, wafika wahlala ngaphansi kwesihlahla serotemu, wacela ukuthi umphefumulo wakhe ufe, wathi: Kwanele, khathesi, Nkosi, thatha impilo yami, ngoba kangingcono kulabobaba.
ndipo Eliyayo anayenda ulendo wa tsiku limodzi mʼchipululu. Anafika pa kamtengo ka tsache, nakhala pansi pa tsinde lake napemphera kuti afe. Iye anati, “Yehova, ine ndatopa nazo. Chotsani moyo wanga. Ineyo sindine wopambana makolo anga.”
5 Esecambalele elele ngaphansi kwesihlahla esithile serotemu, khangela-ke, khonokho ingilosi yamthinta, yathi kuye: Vuka udle.
Ndipo Eliya anagona tulo tofa nato pa tsinde pa kamtengoko. Ndipo taonani, mngelo anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye.”
6 Wasethalaza, khangela-ke, ekhanda lakhe iqebelengwana losiwe emalahleni, lesigxingi samanzi; wasesidla wanatha, waphinda walala.
Eliya anayangʼana, ndipo taonani kumutu kwake kunali buledi wootcha pa makala ndi botolo la madzi. Iye anadya ndi kumwa, nʼkugonanso.
7 Ingilosi yeNkosi yasifika ngokwesibili, yamthinta yathi: Vuka udle; ngoba uhambo lwakho lukhulu kakhulu kuwe.
Mngelo wa Yehova anabweranso kachiwiri, anamukhudza, namuwuza kuti, “Dzuka udye, popeza ulendowu ndi wautali.”
8 Wasevuka wadla wanatha, wahamba ngamandla alokhokudla insuku ezingamatshumi amane lobusuku obungamatshumi amane, waze wafika eHorebe intaba kaNkulunkulu.
Tsono Eliya anadzuka nadya ndi kumwa. Atapeza mphamvu chifukwa cha chakudyacho, anayenda masiku 40, usana ndi usiku mpaka anafika ku Horebu, phiri la Mulungu.
9 Wasengena lapho ebhalwini, walala khona ubusuku. Khangela-ke, ilizwi leNkosi lafika kuye lathi kuye: Wenzani lapha, Elija?
Kumeneko analowa mʼphanga, nakhala komweko. Ndipo taonani, Yehova anayankhula naye kuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
10 Wathi: Bengitshiseka lokutshisekela iNkosi, uNkulunkulu wamabandla, ngoba abantwana bakoIsrayeli basitshiyile isivumelwano sakho, badiliza amalathi akho, babulala abaprofethi bakho ngenkemba; yimi ngedwa engiseleyo, njalo badinga impilo yami ukuyisusa.
Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
11 Wasesithi: Phuma ume entabeni phambi kweNkosi. Khangela-ke, iNkosi yadlula. Umoya omkhulu olamandla wasudabula izintaba, waqhekeza amadwala phambi kweNkosi; kodwa iNkosi yayingekho emoyeni. Lemva komoya ukunyikinyeka komhlaba; kodwa iNkosi yayingekho ekunyikinyekeni komhlaba.
Yehova anati, “Tuluka ndipo ukayime pa phiri pamaso pa Yehova, pakuti Yehova ali pafupi kudutsa pamenepo.” Tsono mphepo yayikulu ndi yamphamvu inawomba ningʼamba mapiri ndi kuswa matanthwe pamaso pa Yehova, koma Yehova sanali mʼmphepomo. Itapita mphepoyo panachita chivomerezi, koma Yehova sanali mʼchivomerezicho.
12 Lemva kokunyikinyeka komhlaba umlilo; kodwa iNkosi yayingekho emlilweni. Njalo emva komlilo ilizwi elincinyane elinyenyezayo.
Chitapita chivomerezicho, panafika moto, koma Yehova sanali mʼmotomo. Ndipo utapita motowo, panamveka kamphepo kayaziyazi.
13 Kwasekuthi uElija elizwa, wathandela ubuso bakhe ngesembatho sakhe, waphuma wema emlonyeni wobhalu. Khangela-ke, leza kuye ilizwi lathi: Wenzani lapha, Elija?
Eliya atamva kamphepoko, anakokera chovala chake naphimba kumutu. Anatuluka ndipo anayima pa khomo la phanga. Ndipo panamveka mawu akuti, “Eliya, ukuchita chiyani kuno?”
14 Wathi: Bengitshisekela lokutshisekela iNkosi, uNkulunkulu wamabandla, ngoba abantwana bakoIsrayeli basitshiyile isivumelwano sakho, badiliza amalathi akho, babulala abaprofethi bakho ngenkemba; yimi ngedwa engiseleyo, njalo badinga impilo yami ukuyisusa.
Iye anayankha kuti, “Ndakhala wodzipereka kwambiri kwa Yehova Mulungu Wamphamvuzonse. Aisraeli asiya pangano lanu, agwetsa maguwa anu ansembe, ndipo apha aneneri anu ndi lupanga. Ndatsala ine ndekha ndipo tsopano akufuna kundipha.”
15 INkosi yasisithi kuye: Hamba, ubuyele ngendlela yakho uye enkangala yeDamaseko; lapho usufikile ugcobe uHazayeli abe yinkosi phezu kweSiriya,
Yehova anati kwa Eliyayo, “Bwerera njira imene unadzera, ndipo upite ku Chipululu cha ku Damasiko. Ukakafika kumeneko, ukadzoze Hazaeli kuti akhale mfumu ya ku Aramu.
16 loJehu indodana kaNimshi umgcobe abe yinkosi phezu kukaIsrayeli, loElisha indodana kaShafati weAbeli-Mehola umgcobe abe ngumprofethi esikhundleni sakho.
Ukadzozenso Yehu mwana wa Nimisi kuti akhale mfumu ya Israeli, ndiponso ukadzoze Elisa mwana wa Safati wa ku Abeli-Mehola kuti akhale mneneri wolowa mʼmalo mwako.
17 Kuzakuthi-ke ozaphepha enkembeni kaHazayeli uJehu uzambulala, lozaphepha enkembeni kaJehu uElisha uzambulala.
Yehu adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Hazaeli, ndipo Elisa adzapha aliyense amene adzapulumuke ku lupanga la Yehu.
18 Kodwa ngitshiyile koIsrayeli abazinkulungwane eziyisikhombisa, wonke amadolo angazanga aguqe kuBhali, lawo wonke umlomo ongazanga umange.
Komabe ndasunga anthu 7,000 ku Israeli, anthu onse amene mawondo awo sanagwadirepo Baala, onse amene pakamwa pawo sipanapsompsoneko fano lake.”
19 Wasesuka lapho, wafica uElisha indodana kaShafati; wayelima ngezipani zenkabi zamajogwe alitshumi lambili phambi kwakhe, yena wayelesetshumi lambili. UElija wesesedlula eceleni kwakhe, waphosela isembatho sakhe phezu kwakhe.
Kotero Eliya anachoka kumeneko, nakapeza Elisa mwana wa Safati. Iye ankatipula ndi mapulawo khumi ndi awiri okokedwa ndi ngʼombe ziwiriziwiri zapamagoli, ndipo iye mwini ankayendetsa goli la khumi ndi chiwiri. Eliya anapita kumene anali namuveka chofunda chake.
20 Wasetshiya izinkabi, wagijima elandela uElija, wathi: Ake ngange ubaba lomama, besengikulandela. Wasesithi kuye: Hamba ubuyele, ngoba ngenzeni kuwe?
Pomwepo Elisa anasiya ngʼombe zake nathamangira Eliya. Iye anati, “Mundilole kuti ndikatsanzike abambo ndi amayi anga, ndipo kenaka ndidzakutsatani.” Eliya anayankha kuti, “Bwerera. Ine ndachita chiyani kwa iwe?”
21 Wasebuyela ekumlandeleni, wathatha isipani senkabi, wasihlaba, langezikhali zenkabi wapheka inyama yazo, wayinika abantu, bayidla. Wasesuka elandela uElija, wamsebenzela.
Choncho Elisa anamusiya Eliyayo nabwerera kwawo. Anatenga ngʼombe zake ziwiri zapagoli nazipha. Anatenga magoli a mapulawo ake nasonkhera moto kuphikira nyamayo ndipo anayipereka kwa anthu kuti adye. Ndipo ananyamuka natsatira Eliya ndi kukhala mtumiki wake.