< 1 Amakhosi 18 >

1 Kwasekusithi emva kwensuku ezinengi ilizwi leNkosi lafika kuElija ngomnyaka wesithathu lisithi: Hamba, uziveze kuAhabi, sengizanisa izulu ebusweni bomhlaba.
Patapita masiku ambiri, mʼchaka chachitatu cha chilala, Yehova anayankhula ndi Eliya kuti, “Pita ukadzionetse kwa Ahabu ndipo ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi.”
2 UElija wasesiya ukuziveza kuAhabi. Njalo indlala yayilamandla eSamariya.
Choncho Eliya anapita kukadzionetsa kwa Ahabu. Tsono nthawi imeneyi njala inakula kwambiri mu Samariya,
3 UAhabi wasebiza uObhadiya owayephezu kwendlu yakhe. UObhadiya wayeyesaba-ke kakhulu iNkosi.
ndipo Ahabu anayitana Obadiya amene ankayangʼanira nyumba yake yaufumu. (Obadiya ankaopa Yehova kwambiri.
4 Ngoba kwathi lapho uJezebeli ebhubhisa abaprofethi beNkosi, uObhadiya wathatha abaprofethi abalikhulu, wabafihla ngamadoda angamatshumi amahlanu ebhalwini, wabondla ngesinkwa langamanzi.
Pamene Yezebeli ankapha aneneri a Yehova, Obadiya anatenga aneneri 100 ndi kuwabisa mʼmapanga awiri, phanga lililonse aneneri makumi asanu, ndipo ankawapatsa chakudya ndi madzi).
5 UAhabi wasesithi kuObhadiya: Hamba elizweni uye emithonjeni yonke yamanzi lezifuleni zonke; mhlawumbe singathola utshani, silondoloze amabhiza lezimbongolo kuphila, ukuze singabhubhisi okwezifuyo.
Ahabu anawuza Obadiya kuti, “Pita mʼdziko kulikonse kumene kuli zitsime za madzi ndi ku zigwa zonse. Mwina mwake tingapeze udzu oti nʼkumadyetsa akavalo ndi abulu kuti akhale ndi moyo, kuti tisaphe chiweto chilichonse.”
6 Basebesehlukaniselana ilizwe ukuthi badabule phakathi kwalo; uAhabi wahamba ngenye indlela yedwa, uObhadiya laye wahamba ngenye indlela yedwa.
Choncho anagawana dziko loti apiteko, Ahabu anapita mbali ina, Obadiya nʼkupita ina.
7 Kwasekusithi uObhadiya esendleleni, khangela-ke, uElija wamhlangabeza; wamnanzelela, wawa ngobuso bakhe wathi: Nguwe yini, nkosi yami, Elija?
Obadiya akuyenda mʼnjira anakumana ndi Eliya. Ndipo taonani, Obadiya anamuzindikira Eliyayo, naweramira pansi ndipo anati, “Kodi ndinu, mbuye wanga Eliya?”
8 Wasesithi kuye: Yimi. Hamba uyetshela inkosi yakho ukuthi: Khangela, uElija ulapha.
Eliya anayankha kuti, “Inde. Pita kawuze mbuye wako kuti, ‘Eliya wabwera.’”
9 Wasesithi: Ngoneni ukuthi unikele inceku yakho esandleni sikaAhabi ukuthi angibulale?
Obadiya anafunsa kuti, “Kodi ndalakwa chiyani kuti inu mupereke mtumiki wanu kwa Ahabu kuti akaphedwe?
10 Kuphila kukaJehova uNkulunkulu wakho, kakulasizwe lombuso inkosi yami engathumelanga kukho ukukudinga. Lapho besithi: Kakho; yafungisa lowombuso lalesosizwe ukuthi kabakutholanga.
Pali Yehova Mulungu wanu wamoyo, kulibe mtundu wa anthu kapena ufumu uliwonse kumene mbuye wanga sanatumeko anthu okakufunafunani. Ndipo pamene mtundu wa anthu kapena ufumu unena kuti kuno kulibe, Ahabu ankawalumbiritsa kuti atsimikizedi kuti inuyo kulibe kumeneko.
11 Khathesi-ke uthi: Hamba utshele inkosi yakho ukuthi: Khangela, uElija ulapha.
Koma tsopano mukundiwuza kuti ndipite kwa mbuye wanga ndi kukanena kuti, ‘Eliya wabwera.’
12 Kuzakuthi-ke sengisukile kuwe, uMoya weNkosi akuthwale akuse lapho engingazi khona; lapho sengifike ngatshela uAhabi, angakutholi, uzangibulala; kodwa mina inceku yakho ngiyayesaba iNkosi kusukela ebutsheni bami.
Ine sindikudziwa kumene Mzimu wa Yehova udzakupititsani ine ndikachoka. Ngati ndipita kukamuwuza Ahabu ndipo iye wosadzakupezani, adzandipha. Komatu ine mtumiki wanu ndakhala ndi kupembedza Yehova kuyambira ubwana wanga.
13 Kakutshelwanga inkosi yami yini engakwenzayo lapho uJezebeli ebulala abaprofethi beNkosi, ukuthi ngafihla amadoda alikhulu kubaprofethi beNkosi, ngamadoda angamatshumi amahlanu ebhalwini, ngabondla ngesinkwa langamanzi?
Mbuye wanga, kodi simunamve zimene ndinachita pamene Yezebeli ankapha aneneri a Yehova? Ine ndinabisa aneneri 100 a Yehova mʼmapanga awiri, mʼphanga lililonse aneneri makumi asanu, ndipo ndinkawapatsa chakudya ndi madzi akumwa.
14 Khathesi-ke uthi: Hamba uyetshela inkosi yakho ukuthi: Khangela uElija ulapha. Abesengibulala.
Ndiye inu tsopano mukundiwuza kuti ndipite kwa mbuye wanga ndi kukanena kuti, ‘Eliya wabwera.’ Iyeyo adzandipha ndithu!”
15 UElija wasesithi: Kuphila kukaJehova wamabandla engimi phambi kwakhe, oqotho lamuhla ngizaziveza kuye.
Eliya anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse wamoyo, amene ndimamutumikira, ine lero ndidzaonekera ndithu pamaso pa Ahabu.”
16 Ngakho uObhadiya wahamba ukuhlangabeza uAhabi, wamtshela; loAhabi wayahlangabeza uElija.
Choncho Obadiya anapita kukakumana ndi Ahabu, namuwuza, ndipo Ahabu anapita kukakumana ndi Eliya.
17 Kwasekusithi uAhabi ebona uElija, uAhabi wathi kuye: Nguwe yini ongumhluphi kaIsrayeli?
Pamene Ahabu anaona Eliya, anati kwa iye, “Kodi ndiwedi, munthu wovutitsa Israeli uja?”
18 Wasesithi: Kangimhluphanga uIsrayeli, kodwa nguwe lendlu kayihlo, ngokuyitshiya kwenu imilayo yeNkosi, lalandela oBhali.
Eliya anayankha kuti, “Ine sindinavutitse Israeli, koma ndinuyo ndi banja lanu. Mwasiya malamulo a Yehova ndipo mwatsatira Abaala.
19 Ngakho-ke thuma, ubuthanisele kimi uIsrayeli wonke entabeni iKharmeli, labaprofethi bakaBhali abangamakhulu amane lamatshumi amahlanu labaprofethi bezixuku abangamakhulu amane abadla etafuleni likaJezebeli.
Tsopano sonkhanitsani anthu a mʼdziko lonse la Israeli kuti akumane nane pa Phiri la Karimeli. Ndipo mubwere nawo aneneri a Baala 450 ndi aneneri a fano la Asera 400, amene amadya pa tebulo la Yezebeli.”
20 Ngakho uAhabi wathuma phakathi kwabo bonke abantwana bakoIsrayeli, wabuthanisa abaprofethi entabeni iKharmeli.
Choncho Ahabu anatumiza mawu mʼdziko lonse la Israeli, ndipo anasonkhanitsa aneneri a Baala ku Phiri la Karimeli.
21 UElija wasesondela ebantwini bonke wathi: Koze kube nini liqhula emicabangweni emibili? Uba iNkosi inguNkulunkulu, landelani yona; kodwa uba kunguBhali, mlandeleni. Kodwa abantu kabamphendulanga ngalizwi.
Eliya anapita patsogolo pa anthuwo ndipo anati, “Kodi mudzakhala anthu a mitima iwiri mpaka liti? Ngati Yehova ndi Mulungu, mutsateni; koma ngati Baala ndi Mulungu, mutsateni.” Koma anthu aja sanayankhe.
22 UElija wasesithi ebantwini: Mina ngedwa ngingumprofethi weNkosi oseleyo; kodwa abaprofethi bakaBhali ngamadoda angamakhulu amane lamatshumi amahlanu.
Pamenepo Eliya ananena kwa iwo kuti, “Ine ndilipo ndekha mneneri wa Yehova, koma Baala ali ndi aneneri 450.
23 Ngakho kabasinike amajongosi amabili, bazikhethele ijongosi elilodwa, baliqume iziqa, bazibeke phezu kwenkuni, bangafaki mlilo; lami ngizalungisa elinye ijongosi, ngilibeke phezu kwenkuni, ngingafaki mlilo.
Tibweretsereni ngʼombe zazimuna ziwiri. Iwo asankhepo okha ngʼombe imodzi, ndipo ayidule nthulinthuli ndi kuziyika pa nkhuni nthulizo, koma osakolezapo moto. Ndipo ine ndidzadula nthulinthuli ngʼombe inayo ndi kuyika pa nkhuni koma sindikolezapo moto.
24 Njalo bizani ibizo likankulunkulu wenu, lami ngizabiza ibizo leNkosi; uNkulunkulu ozaphendula ngomlilo nguye uNkulunkulu. Bonke abantu basebephendula bathi: Lelilizwi lilungile.
Kenaka inu muyitane dzina la mulungu wanu, ndipo ine ndidzayitana dzina la Yehova. Mulungu amene ati ayankhe potumiza moto, iyeyo ndiye Mulungu.” Pamenepo anthu onse anati, “Izi mwanena zamveka bwino.”
25 UElija wasesithi kubaprofethi bakaBhali: Zikhetheleni ijongosi elilodwa, lililungise kuqala, ngoba libanengi, libize ibizo likankulunkulu wenu, kodwa lingafaki mlilo.
Eliya anawuza aneneri a Baala kuti, “Yambani ndinu. Sankhani ngʼombe yayimuna imodzi, muyikonze, popeza mulipo ambiri. Muyitane dzina la mulungu wanu, koma musakoleze moto.”
26 Basebethatha ijongosi ababelinikiwe, balilungisa, babiza ibizo likaBhali kusukela ekuseni kwaze kwaba semini, besithi: Bhali, siphendule! Kodwa kakubanga lalizwi, kakubanga lophendulayo. Basebeseqa phezu kwelathi elalenziwe.
Choncho iwo anatenga ngʼombe yayimunayo imene anawapatsa, nayikonza. Kenaka anayitana dzina la Baala kuyambira mmawa mpaka masana. Iwo anafuwula kuti, “Inu Baala, tiyankheni ife.” Koma panalibe yankho; palibe amene anayankha. Ndipo anavinavina mozungulira guwa lansembe limene anapanga.
27 Kwasekusithi emini uElija wadlala ngabo wathi: Memezani ngelizwi elikhulu, ngoba ungunkulunkulu; ngoba uyanakana, loba umonyukile, kumbe usekuhambeni, mhlawumbe ulele, njalo kudingeka ukuthi avuswe.
Nthawi yamasana Eliya anayamba kuwanyogodola ndipo anati, “Fuwulani kwambiri. Ndithudi, iye ndi mulungu! Mwinatu akulingalira kwambiri, kapena watanganidwa, kapena ali paulendo. Mwina wagona ndipo nʼkofunika kuti adzutsidwe.”
28 Basebememeza ngelizwi elikhulu, bazisika njengokomkhuba wabo ngezinkemba langemikhonto, kwaze kwantshaza igazi kubo.
Choncho iwo anafuwula kwambiri ndi kudzichekacheka ndi malupanga ndi mikondo, potsata miyambo yawo, mpaka kutuluka magazi.
29 Kwasekusithi sekwedlulile imini, baprofetha kwaze kwaba sekunikelweni komnikelo, kakubanga lelizwi, njalo kakubanga lophendulayo, njalo kakubanga lonakekelayo.
Nthawi yamasana inadutsa, ndipo anapitiriza kunenera mwakhama mpaka nthawi yopereka nsembe ya madzulo. Koma panalibe yankho. Palibe amene anayankha, kapena kulabadira zimenezo.
30 UElija wasesithi ebantwini bonke: Sondelani kimi. Bonke abantu basebesondela kuye. Waselungisa ilathi leNkosi elaselidilikile.
Pamenepo Eliya anati kwa anthu onse, “Senderani pafupi ndi ine.” Ndipo anthu onsewo anasendera pafupi ndi iye, ndipo iye anakonza guwa lansembe la Yehova limene linali litawonongeka.
31 UElija wasethatha amatshe alitshumi lambili, ngokwenani lezizwe zamadodana kaJakobe, okwafika kuye ilizwi leNkosi lisithi: Ibizo lakho lizakuba nguIsrayeli.
Eliya anatenga miyala 12, mwala uliwonse kuyimira fuko lililonse la Yakobo, amene Yehova anamuwuza kuti, “Dzina lako lidzakhala Israeli.”
32 Ngalawomatshe wasesakha ilathi ebizweni leNkosi, wenza umgelo ozingelezela ilathi, ngokwesilinganiso samaseya amabili enhlanyelo.
Ndi miyala imeneyo anamanga guwa mʼdzina la Yehova, ndipo anakumba ngalande yayikulu yolowa malita 15 a madzi kuzungulira guwalo.
33 Waselungisa inkuni, waliquma iziqa ijongosi, walibeka phezu kwenkuni, wasesithi: Gcwalisani izimbiza ezine ngamanzi, liwathele phezu komnikelo wokutshiswa laphezu kwenkuni.
Anayika nkhuni zija mʼmalo mwake nadula nthulinthuli ngʼombe yayimuna ija ndi kuyika nthulizo pa nkhunipo. Pamenepo Eliya anati, “Dzazani mitsuko inayi ndi madzi ndipo muwathire pa nyama ya nsembeyo ndi nkhunizo.”
34 Wasesithi: Kwenzeni okwesibili. Bakwenza okwesibili. Wathi: Kwenzeni okwesithathu. Basebekwenza okwesithathu.
Eliya anati, “Thiraninso kachiwiri.” Anthu aja anathiranso madziwo kachiwiri. Iye analamula kuti, “Thiraninso kachitatu.” Ndipo iwo anathiranso kachitatu.
35 Amanzi asehamba azingelezela ilathi, lomgelo lawo wawugcwalisa ngamanzi.
Madziwo anayenderera pansi kuzungulira guwa lansembe, nadzaza ngalande yonse.
36 Kwasekusithi ekunikelweni komnikelo uElija umprofethi wasondela wathi: Nkosi, Nkulunkulu kaAbrahama, uIsaka, loIsrayeli, kakwaziwe lamuhla ukuthi unguNkulunkulu koIsrayeli, lami ngiyinceku yakho, lokuthi ngizenzile zonke lezizinto njengokwelizwi lakho.
Pa nthawi yopereka nsembe, mneneri Eliya anasendera pafupi ndi guwa lansembe, napemphera kuti, “Inu Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, lero zidziwike kuti ndinu Mulungu mu Israeli ndipo kuti ine ndine mtumiki wanu, kuti ine ndachita zonsezi chifukwa mwalamula ndinu.
37 Ngiphendule, Nkosi, ungiphendule, ukuze lababantu bazi ukuthi wena uyiNkosi uNkulunkulu, lokuthi uyiphendulile futhi inhliziyo yabo.
Ndiyankheni, Inu Yehova, ndiyankheni, kuti anthu awa adziwe Inu Yehova, kuti ndinu Mulungu, ndipo kuti mutembenuziranso mitima yawo kwa Inu.”
38 Wasusehla umlilo weNkosi, waqothula umnikelo wokutshiswa lenkuni lamatshe lothuli, wakhotha lamanzi asemgelweni.
Pamenepo moto wa Yehova unagwa, nunyeketsa nsembe yopserezayo, nkhuni, miyala ndi dothi lomwe. Unawumitsanso madzi amene anali mʼngalande.
39 Kwathi abantu bonke bekubona bathi mbo ngobuso babo, bathi: UJehova nguye onguNkulunkulu; uJehova nguye onguNkulunkulu.
Anthu onse ataona zimenezi, anaweramitsa nkhope zawo pansi, nafuwula kuti, “Yehova ndiye Mulungu! Yehova ndiye Mulungu!”
40 UElija wasesithi kibo: Babambeni abaprofethi bakaBhali, kungaphunyuki lamunye wabo. Basebebabamba. UElija wasebehlisela esifuleni iKishoni, wababulalela khona.
Pamenepo Eliya analamula anthuwo kuti, “Gwirani aneneri a Baala. Musalole kuti wina aliyense athawe!” Anagwira onsewo ndipo Eliya anabwera nawo ku Chigwa cha Kisoni, nawapha kumeneko.
41 UElija wasesithi kuAhabi: Yenyuka, udle unathe, ngoba kulomsindo wobunengi bezulu.
Ndipo Eliya anati kwa Ahabu, “Pitani, kadyeni ndi kumwa, pakuti kukumveka mkokomo wa mvula.”
42 UAhabi wasesenyuka ukuyakudla lokunatha. UElija wasesenyukela engqongeni yeKharmeli; wakhothamela phansi emhlabathini, wafaka ubuso bakhe phakathi kwamadolo akhe.
Choncho Ahabu anapita kukadya ndi kumwa, koma Eliya anakwera pamwamba pa Phiri la Karimeli, ndipo anawerama mpaka pansi, nayika mutu wake pakati pa mawondo ake.
43 Wasesithi encekwini yakhe: Yenyuka khathesi, ukhangele ngaselwandle. Yasisenyuka, yakhangela, yathi: Kakulalutho. Wasesithi: Buyela, kasikhombisa.
Eliya anawuza mtumiki wake kuti, “Pita kayangʼane ku nyanja.” Ndipo iye anapita nakayangʼana. Mtumikiyo anati, “Kulibe kanthu.” Kasanu nʼkawiri Eliya anati, “Pitanso.”
44 Kwasekusithi ngesikhathi sesikhombisa yathi: Khangela, iyezana elingangesandla somuntu lisenyuka olwandle. Wasesithi: Yenyuka uyetshela uAhabi: Bophela inqola, wehle, hlezi izulu likuvalele.
Ulendo wachisanu ndi chiwiri mtumikiyo anafotokoza kuti, “Taonani, kamtambo kakangʼono kokhala ngati dzanja la munthu kakutuluka ku nyanja.” Pamenepo Eliya anati, “Pita, kamuwuze Ahabu kuti, ‘Konzani galeta lanu ndipo mutsike mvula isanakutsekerezeni.’”
45 Kwasekusithi kungakafiki lesosikhathi isibhakabhaka sasesisiba mnyama ngamayezi langomoya, kwaba lezulu elikhulu. UAhabi wasegada, waya eJizereyeli.
Nthawi imeneyi nʼkuti kuthambo kutayamba kusonkhana mitambo yakuda, mphepo inawomba, mvula yamphamvu inagwa ndipo Ahabu anakwera galeta napita ku Yezireeli.
46 Lesandla seNkosi sasiphezu kukaElija; wabopha ukhalo lwakhe, wagijima phambi kukaAhabi, uze ufike eJizereyeli.
Dzanja la Yehova linali pa Eliya ndipo atamangira lamba chovala chake, anathamanga ndi kumupitirira Ahabu mpaka kukhala woyamba kukafika ku Yezireeli.

< 1 Amakhosi 18 >