< 1 Amakhosi 17 >
1 UElija umTishibi wabahlali beGileyadi wasesithi kuAhabi: Kuphila kukaJehova, uNkulunkulu kaIsrayeli, engimi phambi kwakhe, kakuyikuba khona lamazolo lezulu kuliminyaka, kuphela njengokwelizwi lami.
Ndipo mneneri Eliya wa ku Tisibe ku Giliyadi, anati kwa Ahabu, “Pali Yehova wamoyo, Mulungu wa Israeli, amene ndimamutumikira, sipadzakhala mame kapena mvula zaka zikubwerazi, pokhapokha ine nditanena.”
2 Ilizwi leNkosi laselifika kuye lisithi:
Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya kuti,
3 Suka lapha, wena uphendukele empumalanga, uzicatshise esifuleni iKerithi, esiphambi kweJordani.
“Choka kuno, upite kummawa, ukabisale mʼmbali mwa mtsinje wa Keriti, pafupi ndi Yorodani.
4 Kuzakuthi-ke unathe esifuleni; sengilaye amawabayi ukuthi akondle khona.
Uzikamwa mu mtsinjemo, ndipo ndalamula makwangwala kuti azikakudyetsa kumeneko.”
5 Wasehamba wenza njengokwelizwi leNkosi, ngoba wayahlala esifuleni iKerithi esiphambi kweJordani.
Choncho Eliya anachita zomwe Yehova anamuwuza. Anapita ku mtsinje wa Keriti, pafupi ndi Yorodani, nakakhala kumeneko.
6 Amawabayi asemlethela isinkwa lenyama ekuseni, lesinkwa lenyama ntambama; wanatha esifuleni.
Makwangwala ankabweretsera buledi ndi nyama mmawa ndi madzulo, ndipo ankamwa mu mtsinjemo.
7 Kwasekusithi emva kwesikhathi isifula satsha, ngoba kwakungelazulu elizweni.
Patapita masiku, mtsinjewo unaphwa chifukwa mvula sinagwe mʼdzikomo.
8 Ilizwi leNkosi laselifika kuye lisithi:
Yehova anayankhula naye kuti,
9 Sukuma uye eZarefathi engeyeSidoni, uhlale khona. Khangela, ngilayile owesifazana ongumfelokazi khona ukuthi akondle.
“Nyamuka tsopano, pita ku Zarefati ku Sidoni ndipo ukakhale kumeneko. Ndalamula mkazi wamasiye wa kumeneko kuti azikakudyetsa.”
10 Wasukuma-ke waya eZarefathi. Lapho efika esangweni lomuzi, khangela, owesifazana ongumfelokazi wayelapho etheza inkuni; wasembiza wathi: Ake ungikhele amanzi amalutshwana ngenkezo ukuze nginathe.
Choncho iye ananyamuka napita ku Zarefati. Atafika pa chipata cha mzindawo, taonani mkazi wamasiye amatola nkhuni. Anamuyitana ndi kumuwuza kuti, “Patseni madzi pangʼono mʼchikho kuti ndimwe.”
11 Kwathi esahamba ukuyawathatha, wambiza wathi: Ake ungiphathele ucezu lwesinkwa esandleni sakho.
Mayi wamasiye uja ankapita kukatunga madzi, Eliya anamuyitananso namuwuza kuti, “Chonde munditengerekonso buledi.”
12 Wasesithi: Kuphila kukaJehova uNkulunkulu wakho, kangilaqebelengwana, kuphela impuphu egcwala isandla embizeni lamafutha ayingcosana esiphisweni; khangela-ke ngitheza izinkuni ezimbili ukuze ngingene ngizilungisele khona mina lendodana yami, ukuze sidle sife.
Iye anayankha kuti “Pali Yehova Mulungu wanu wamoyo, ine ndilibe chakudya china chilichonse, koma kaufa pangʼono mʼmbiya ndi mafuta pangʼono mʼbotolo. Ine ndikutola tinkhuni tochepa kuti ndipite nato ku nyumba ndi kukaphika chakudya changa ndi cha mwana wanga, kuti tikadye kenaka tife.”
13 UElija wasesithi kuye: Ungesabi; hamba wenze njengokwelizwi lakho, kodwa ngenzela kuqala iqebelengwana elincinyane ngakho, ulilethe lapha kimi, ngemva kwalokho-ke wenzele wena lendodana yakho.
Eliya anati kwa iye, “Musachite mantha. Pitani mukachite monga mwaneneramo. Koma poyamba mundipangire kachakudya pangʼono kuchokera pa ufa umene muli nawo ndi kubwera nako kwa ine, ndipo kenaka mukaphike choti mudye inuyo ndi mwana wanuyo.
14 Ngoba itsho njalo iNkosi uNkulunkulu wakoIsrayeli: Imbiza yempuphu kayiyikuphela, lesiphiso samafutha kasiyikuswela, kuze kube lusuku iNkosi ezanisa ngalo izulu ebusweni bomhlaba.
Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ufa umene uli mʼmbiyamo sudzatha ndipo mafuta amene ali mʼbotolomo sadzathanso mpaka tsiku limene Yehova adzagwetse mvula pa dziko lapansi.’”
15 Wasehamba wenza njengokwelizwi likaElija. Njalo yena kanye laye lendlu yakhe badla okwensuku ezinengi.
Mayi wamasiyeyo anapita nakachita zimene Eliya anamuwuza. Choncho panali chakudya cha Eliya, mayiyo pamodzi ndi banja lake lonse chimene anadya masiku ambiri.
16 Imbiza yempuphu kayiphelanga lesiphiso samafutha kasiswelanga, njengokwelizwi leNkosi eyalikhuluma ngesandla sikaElija.
Pakuti ufa umene unali mʼmbiya sunathe ndiponso mafuta amene anali mʼbotolo sanathe, monga momwe ananenera Yehova kudzera mwa Eliya.
17 Kwasekusithi emva kwalezizinto, indodana yowesifazana, inkosikazi yendlu, yagula; lomkhuhlane wayo wawulamandla kangangokuthi akwaze kwasala umphefumulo kuyo.
Tsiku lina mwana wake wa mkazi wamasiye uja, mwini nyumbayo, anadwala. Matenda ananka nakulirakulirabe, ndipo kenaka analeka kupuma.
18 Wasesithi kuElija: Ngilani lawe, muntu kaNkulunkulu? Uze kimi ukuze kukhumbuleke isono sami lokubulala indodana yami na?
Mayiyo anati kwa Eliya, “Kodi ndakulakwirani chiyani, inu munthu wa Mulungu? Kodi munabwera kuno kudzandikumbutsa tchimo langa ndi kudzandiphera mwana wanga?”
19 Wasesithi kuye: Nginika indodana yakho. Waseyithatha esifubeni sakhe, wayenyusela endlini ephezulu lapho ayehlala khona, wayilalisa embhedeni wakhe.
Eliya anayankha kuti, “Patseni mwana wanuyo.” Iye anatenga mwanayo mʼmanja mwa mayiyo napita naye mʼchipinda chapamwamba, kumene Eliyayo amagona, namugoneka pa bedi lake.
20 Wasekhala eNkosini wathi: Nkosi Nkulunkulu wami, umehlisele ububi lalo umfelokazi engingenise kwakhe ngokubulala indodana yakhe na?
Kenaka Eliya anafuwula kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wanga, kodi mwabweretsanso choyipa chotere pa mkazi wamasiye amene ine ndikukhala naye, pakuchititsa kuti mwana wake afe?”
21 Wasezelulela phezu komntwana kathathu, wakhala eNkosini wathi: Nkosi Nkulunkulu wami, ake ubuyele umphefumulo walumntwana phakathi kwakhe.
Pamenepo Eliya anakumbatira mwanayo katatu ndi kufuwula kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Mulungu wanga, mubwezereni mwanayu moyo wake!”
22 INkosi yasilizwa ilizwi likaElija, umphefumulo womntwana wasubuyela phakathi kwakhe, wasebuya ephila.
Yehova anamva kufuwula kwa Eliya, ndipo moyo wa mwanayo unabwerera mwa iye ndipo anatsitsimuka.
23 UElija wasemthatha umntwana, wamehlisa esuka endlini ephezulu waya endlini, wamnika unina; uElija wasesithi: Bona, indodana yakho iyaphila.
Eliya ananyamula mwanayo natsika naye kuchoka mʼchipinda chapamwamba chija nalowa naye mʼnyumba. Anamupereka kwa amayi ake ndipo anati, “Taonani, mwana wanu ali ndi moyo!”
24 Owesifazana wasesithi kuElija: Khathesi sengisazi lokhu, ukuthi ungumuntu kaNkulunkulu, ukuthi ilizwi leNkosi elisemlonyeni wakho liliqiniso.
Pamenepo mayiyo anati kwa Eliya, “Tsopano ndadziwa kuti ndinu munthu wa Mulungu ndipo mawu a Yehova amene mumayankhula ndi owona.”