< 1 Amakhosi 15 >
1 Ngomnyaka wetshumi lesificaminwembili wenkosi uJerobhowamu indodana kaNebati uAbhiyamu wasesiba yinkosi phezu kukaJuda.
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
2 Wabusa iminyaka emithathu eJerusalema. Lebizo likanina lalinguMahaka indodakazi kaAbishalomu.
ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
3 Wasehamba ezonweni zonke zikayise ayezenze phambi kwakhe, lenhliziyo yakhe yayingaphelelanga kuJehova uNkulunkulu wakhe, njengenhliziyo kaDavida uyise.
Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
4 Kodwa ngenxa kaDavida iNkosi uNkulunkulu wakhe yamnika isibane eJerusalema, ngokubeka indodana yakhe emva kwakhe, langokuqinisa iJerusalema.
Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
5 Ngoba uDavida wenza okulungileyo emehlweni eNkosi, kaphambukanga kukho konke eyamlaya khona insuku zonke zempilo yakhe, ngaphandle kwedabeni lukaUriya umHethi.
pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
6 Kwakukhona-ke impi phakathi kukaRehobhowamu loJerobhowamu zonke izinsuku zempilo yakhe.
Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
7 Ezinye-ke zezindaba zikaAbhiyamu, lakho konke akwenzayo, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoJuda? Njalo kwaba lempi phakathi kukaAbhiyamu loJerobhowamu.
Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
8 UAbhiyamu waselala laboyise, bamngcwabela emzini kaDavida. UAsa indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 Ngomnyaka wamatshumi amabili kaJerobhowamu inkosi yakoIsrayeli uAsa wasesiba yinkosi yakoJuda.
Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
10 Wasebusa iminyaka engamatshumi amane lanye eJerusalema. Lebizo likanina lalinguMahaka indodakazi kaAbishalomu.
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
11 UAsa wasesenza okulungileyo emehlweni eNkosi njengoDavida uyise.
Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
12 Wasusa izinkotshana elizweni, wasusa zonke izithombe oyise ababezenzile.
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
13 Laye-ke uMahaka unina wamsusa ekubeni yindlovukazi, ngoba wayenze into enengekayo ibe yiAshera; uAsa waseyigamula into yakhe enengekayo, wayitshisela esifuleni iKidroni.
Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
14 Kanti indawo eziphakemeyo kazisuswanga; lanxa kunjalo inhliziyo kaAsa yayiphelele kuJehova insuku zakhe zonke.
Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
15 Wasengenisa izinto ezehlukanisiweyo zikayise kanye lezakhe izinto ezehlukanisiweyo endlini yeNkosi, isiliva legolide lezitsha.
Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
16 Kwakukhona-ke impi phakathi kukaAsa loBahasha inkosi yakoIsrayeli zonke izinsuku zabo.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
17 UBahasha inkosi yakoIsrayeli wasesenyuka wamelana loJuda, wakha iRama, ukuze angavumeli muntu ukuphuma lokungena kuAsa inkosi yakoJuda.
Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
18 UAsa wasethatha sonke isiliva legolide okwakusele emagugwini endlu kaJehova lamagugu endlu yenkosi, wakunikela esandleni senceku zakhe; inkosi uAsa yakuthumela kuBenihadadi indodana kaTabirimoni indodana kaHeziyoni, inkosi yeSiriya, owayehlala eDamaseko, esithi:
Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
19 Kulesivumelwano phakathi kwami lawe, phakathi kukababa loyihlo; khangela, ngikuthumezela isipho, isiliva legolide. Hamba, yephula isivumelwano sakho loBahasha inkosi yakoIsrayeli, ukuze enyuke asuke kimi.
“Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
20 UBenihadadi waseyilalela inkosi uAsa, wathuma induna zamabutho ayelawo emelene lemizi yakoIsrayeli, watshaya iIjoni leDani leAbeli-Beti-Mahaka layo yonke iKinerothi lelizwe lonke lakoNafithali.
Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
21 Kwasekusithi uBahasha ekuzwa wayekela ukwakha iRama, wahlala eTiriza.
Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
22 Inkosi uAsa yasisenza isimemezelo kuyo yonke iJuda; kakho owayetshiywe ngaphandle; ukuze basuse amatshe eRama lezigodo zayo, uBahasha ayesakha ngakho. Inkosi uAsa wasesakha ngakho iGeba yakoBhenjamini leMizipa.
Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
23 Ezinye-ke zazo zonke indaba zikaAsa, lawo wonke amandla akhe, lakho konke akwenzayo, lemizi ayakhayo, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoJuda? Kodwa esikhathini sobudala bakhe wayelomkhuhlane ezinyaweni.
Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
24 UAsa waselala laboyise, wangcwatshelwa kuboyise emzini kaDavida uyise. UJehoshafathi indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 UNadabi indodana kaJerobhowamu wasesiba yinkosi phezu kukaIsrayeli ngomnyaka wesibili kaAsa inkosi yakoJuda; wabusa phezu kukaIsrayeli iminyaka emibili.
Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
26 Wasesenza okubi emehlweni eNkosi, wahamba ngendlela kayise, lesonweni sakhe, enza uIsrayeli one ngaso.
Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
27 UBahasha indodana kaAhiya, owendlu kaIsakari, wasemenzela ugobe; uBahasha wamtshaya eGibethoni engeyamaFilisti, lapho uNadabi loIsrayeli wonke bevimbezele iGibethoni.
Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
28 UBahasha wambulala-ke ngomnyaka wesithathu kaAsa inkosi yakoJuda, wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Kwasekusithi ekubuseni kwakhe watshaya yonke indlu kaJerobhowamu, katshiyanga loyedwa ophefumulayo kuJerobhowamu, waze wamqeda, njengelizwi leNkosi eyalikhuluma ngesandla senceku yayo uAhiya umShilo.
Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
30 Ngenxa yezono zikaJerobhowamu azonayo, lowenza uIsrayeli azone, ngentukuthelo yakhe athukuthelisa ngayo iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli.
chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
31 Ezinye-ke zezindaba zikaNadabi, lakho konke akwenzayo, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoIsrayeli?
Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 Njalo kwakulempi phakathi kukaAsa loBahasha inkosi yakoIsrayeli insuku zabo zonke.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
33 Ngomnyaka wesithathu kaAsa inkosi yakoJuda uBahasha indodana kaAhiya waba yinkosi phezu kukaIsrayeli wonke eTiriza; iminyaka engamatshumi amabili lane.
Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
34 Wasesenza okubi emehlweni eNkosi, wahamba ngendlela kaJerobhowamu, lesonweni sakhe, enza uIsrayeli one ngaso.
Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.