< 1 Amakhosi 14 >
1 Ngalesosikhathi uAbhiya indodana kaJerobhowamu wagula.
Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
2 UJerobhowamu wasesithi kumkakhe: Akusuke uzifihle isimo ukuze bangakwazi ukuthi ungumkaJerobhowamu, uye eShilo; khangela, kukhona lapho uAhiya umprofethi owangitshela ukuthi ngizakuba yinkosi phezu kwalababantu.
ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
3 Uthathe izinkwa ezilitshumi esandleni sakho lamaqebelengwana alukhuni lodiwo loluju, uye kuye, yena uzakutshela okuzakwenzeka kulumntwana.
Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
4 UmkaJerobhowamu wasesenza njalo, wasuka waya eShilo, wafika emzini kaAhiya. Kodwa uAhiya wayengelakubona ngoba amehlo akhe ayesenqundekile ngenxa yobudala bakhe.
Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
5 INkosi yasisithi kuAhiya: Khangela, umkaJerobhowamu uyeza ukubuza ulutho kuwe ngendodana yakhe, ngoba iyagula. Uzamtshela ukuthi lokuthi. Ngoba kuzakuthi ekungeneni kwakhe, uzazitshaya omunye.
Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
6 Kwasekusithi uAhiya esizwa izisinde zenyawo zakhe lapho engena emnyango wathi: Ngena mkaJerobhowamu; uzitshayelani omunye? Ngoba ngithunywe kuwe ngento enzima.
Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
7 Hamba uthi kuJerobhowamu: Itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli, ithi: Njengoba ngakuphakamisa uphakathi kwabantu, ngakwenza umbusi phezu kwabantu bami uIsrayeli,
Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
8 ngadabula umbuso ngawususa endlini kaDavida, ngawunika wena; kodwa kawubanga njengenceku yami uDavida, owagcina imilayo yami, lowangilandela ngenhliziyo yakhe yonke, ukwenza okuhle kuphela emehlweni ami;
Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
9 kodwa wenzile ububi okwedlula bonke ababekhona phambi kwakho, kodwa uhambe wazenzela abanye onkulunkulu lezithombe ezibunjwe ngokuncibilikisa, ukuze ungithukuthelise, wangilahla emva komhlana wakho.
Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
10 Ngakho, khangela, ngizakwehlisela ububi endlini kaJerobhowamu, ngiqume asuke kuJerobhowamu ochamela emdulini, ovalelweyo lokhululekileyo koIsrayeli, ngihugule okulandelayo kwendlu kaJerobhowamu, njengomuntu ehugula umquba uze uphele.
“‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
11 OkaJerobhowamu ofela phakathi komuzi zizamudla izinja, lofela egangeni zizamudla inyoni zamazulu; ngoba iNkosi ikhulumile.
Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
12 Ngakho wena suka, uye endlini yakho; ekungeneni kwenyawo zakho emzini umntwana uzakufa.
“Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
13 Njalo uIsrayeli wonke uzamlilela amngcwabe; ngoba nguye kuphela koJerobhowamu ozakuza engcwabeni, ngoba kutholakala kuye into elungileyo ngaseNkosini uNkulunkulu kaIsrayeli endlini kaJerobhowamu.
Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
14 Futhi uJehova uzazivusela inkosi phezu kukaIsrayeli, ezaquma indlu kaJerobhowamu ngalolosuku. Kodwa kuyini? Lakhathesi.
“Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
15 Njalo iNkosi izamtshaya uIsrayeli njengomhlanga uzunguzeka emanzini, iquphule uIsrayeli elizweni leli elihle, eyalinika oyise, ibachithachithe ngaphetsheya komfula, ngenxa yokuthi bazenzela izixuku, bayithukuthelisa iNkosi.
Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
16 Njalo izanikela uIsrayeli ngenxa yezono zikaJerobhowamu, owonayo, wenza uIsrayeli one.
Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
17 UmkaJerobhowamu wasesuka wahamba, wafika eTiriza. Lapho efika embundwini wendlu, umfana wafa.
Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
18 Basebemngcwaba; loIsrayeli wonke wamlilela, njengokwelizwi leNkosi eyalikhuluma ngesandla senceku yayo uAhiya umprofethi.
Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
19 Ezinye-ke zezindaba zikaJerobhowamu, ukuthi walwa njani, lokuthi wabusa njani, khangela, zibhaliwe egwalweni lwemilando yamakhosi akoIsrayeli.
Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
20 Lensuku uJerobhowamu abusa ngazo zaziyiminyaka engamatshumi amabili lambili, walala laboyise, njalo uNadabi indodana yakhe waba yinkosi esikhundleni sakhe.
Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
21 URehobhowamu indodana kaSolomoni wabusa-ke koJuda. URehobhowamu wayeleminyaka engamatshumi amane lanye lapho esiba yinkosi, wabusa iminyaka elitshumi lesikhombisa eJerusalema, umuzi iNkosi eyayiwukhethile kuzo zonke izizwe zakoIsrayeli, ukubeka khona ibizo layo. Lebizo likanina lalinguNahama umAmonikazi.
Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
22 UJuda wasesenza okubi emehlweni eNkosi; bayivusa ubukhwele, ngezono zabo abazonayo, okwedlula konke oyise ababekwenzile, ngezono zabo abazonayo.
Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
23 Ngoba labo bazakhela izindawo eziphakemeyo, lezinsika eziyizithombe, lezixuku, phezu kwalo lonke uqaqa oluphakemeyo, langaphansi kwaso sonke isihlahla esiluhlaza.
Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
24 Kwakukhona-ke elizweni lezinkotshana. Benza njengokwezinengiso zezizwe iNkosi eyayizixotshile elifeni phambi kwabantwana bakoIsrayeli.
Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
25 Kwasekusithi ngomnyaka wesihlanu wenkosi uRehobhowamu uShishaki inkosi yeGibhithe wenyuka wamelana leJerusalema.
Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
26 Wathatha amagugu endlu kaJehova lamagugu endlu yenkosi, yebo wakuthatha konke, wathatha zonke izihlangu zegolide uSolomoni ayezenzile.
Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
27 Inkosi uRehobhowamu yasisenza endaweni yazo izihlangu zethusi, yazinikela esandleni senduna yabalindi ababegcina umnyango wendlu yenkosi.
Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
28 Njalo kwakusithi lapho inkosi ingena endlini kaJehova abalindi babezithwala, bazibuyisele endlini yabalindi.
Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
29 Ezinye-ke zezindaba zikaRehobhowamu, lakho konke akwenzayo, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoJuda?
Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
30 Kwakukhona-ke impi phakathi kukaRehobhowamu loJerobhowamu zonke izinsuku.
Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
31 URehobhowamu waselala laboyise, wangcwatshelwa kuboyise emzini kaDavida. Lebizo likanina lalinguNahama umAmonikazi. UAbhiyamu indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.
Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.