< 1 Imilando 29 >
1 UDavida inkosi wasesithi ebandleni lonke: USolomoni indodana yami, yena yedwa uNkulunkulu amkhethileyo, usengumfana ubuthakathaka, lomsebenzi mkhulu; ngoba isigodlo kayisiso somuntu, kodwa ngeseNkosi uNkulunkulu.
Kenaka, mfumu Davide inati kwa gulu lonse: “Mwana wanga Solomoni amene Mulungu wamusankha ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Ntchitoyi ndi yayikulu chifukwa nyumba yaufumuyi si ya munthu, koma ndi ya Yehova Mulungu.
2 Ngakho ngiyilungisele indlu kaNkulunkulu wami ngamandla ami wonke, igolide lokwegolide, lesiliva lokwesiliva, lethusi lokwethusi, insimbi lokwensimbi, lezigodo lokwezigodo, amatshe e-onikse lawokubekwa, amatshe akhazimulayo lalemibala, lenhlobo zonke zamatshe aligugu, lamatshe e-alibasta ngobunengi.
Ine ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu zinthu zanga zonse, golide wopangira zinthu zagolide, siliva wopangira zinthu zasiliva ndi zitsulo zopangira zinthu zazitsulo, mkuwa wopangira zinthu zamkuwa ndi matabwa opangira zinthu zamatabwa komanso miyala yokongola ya onikisi yokongoletsera, miyala ya maonekedwe osiyanasiyana, ndi miyala yonse yosalala ndi miyala ya marabulo, zonsezi ndapereka zochuluka.
3 Laphezu kwakho, ngenxa yokuthanda kwami indlu kaNkulunkulu wami, nganikela indlu kaNkulunkulu wami inotho yegolide leyesiliva, engilakho, phezu kwakho konke engikulungisele indlu yendawo engcwele,
Kupatulapo izi, ine modzipereka ku Nyumba ya Mulungu wanga, tsopano ndikupereka chuma changachanga cha golide ndi siliva ku Nyumba ya Mulungu wanga, kuwonjezera pa zimene ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu woyerayu:
4 amathalenta egolide azinkulungwane ezintathu egolideni leOfiri, lamathalenta esiliva elicwengekileyo azinkulungwane eziyisikhombisa, ukuhuqa imiduli yezindlu.
Matani 100 agolide (golide wa ku Ofiri) ndi matani 240 a siliva woyengeka bwino wokutira makoma a nyumba,
5 Igolide kusenzelwa okwegolide, lesiliva kusenzelwa okwesiliva, langawo wonke umsebenzi ngesandla sezingcitshi. Ngubani-ke ovumayo ukuzehlukanisela iNkosi lamuhla?
zinthu zagolide ndi zinthu zasiliva, ndiponso zinthu zonse zimene anthu aluso adzagwiritse ntchito. Tsopano ndani amene akufuna kudzipatulira yekha kwa Yehova lero?”
6 Inhloko zaboyise zasezinikela ngesihle, lezinduna zezizwe zakoIsrayeli, labaphathi bezinkulungwane labamakhulu, labaphathi bomsebenzi wenkosi.
Tsono atsogoleri a mabanja, akuluakulu a mafuko a Israeli, olamulira asilikali 1,000, ndi olamulira asilikali 100, ndiponso akuluakulu onse amene amayangʼanira ntchito ya mfumu anapereka mwaufulu.
7 Basebenikela emsebenzini wendlu kaNkulunkulu amathalenta azinkulungwane ezinhlanu egolide, lenhlamvu ezizinkulungwane ezilitshumi, lamathalenta esiliva azinkulungwane ezilitshumi, lamathalenta ethusi azinkulungwane ezilitshumi lesificaminwembili, lamathalenta ensimbi azinkulungwane ezilikhulu.
Iwo anapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu matani 170 a golide, matani 340 a siliva, matani 620 a mkuwa ndi matani 3,400 a chitsulo.
8 Lalabo okwatholwa kibo amatshe aligugu bawanika indlu yokuligugu yendlu yeNkosi ngaphansi kwesandla sikaJehiyeli umGerishoni.
Aliyense amene anali ndi miyala yokongola anayipereka ku nyumba yosungiramo chuma cha Nyumba ya Yehova ndipo amene ankayangʼanira anali Yehieli Mgeresoni.
9 Basebethokoza abantu ngokunikela kwabo ngesihle, ngoba ngenhliziyo epheleleyo babenikele ngothando kuNkulunkulu; loDavida inkosi laye wathokoza ngentokozo enkulu.
Anthu anakondwa chifukwa cha kupereka mwaufulu kwa atsogoleri awo, pakuti anapereka kwa Yehova mwaufulu ndiponso ndi mtima wonse. Nayenso mfumu Davide anakondwera kwambiri.
10 UDavida waseyibusisa iNkosi phambi kwamehlo ebandla lonke; uDavida wathi: Kawubusiswe wena Nkosi Nkulunkulu kaIsrayeli ubaba, kusukela ephakadeni kuze kube sephakadeni.
Davide anatamanda Yehova pamaso pa gulu lonse, ponena kuti, “Mutamandidwe Inu Yehova Mulungu wa kholo lathu Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya.
11 Kungokwakho, Nkosi, ubukhulu lamandla lodumo lokunqoba lobukhosi; ngoba konke okusemazulwini lokusemhlabeni kungokwakho; umbuso ungowakho, Nkosi; wena uziphakamisile waba yinhloko phezu kwakho konke.
Wanu, Inu Yehova ndi ukulu ndi mphamvu, ulemerero ndiponso ufumu ndi kukongola. Pakuti zinthu zonse zakumwamba ndi pa dziko lapansi ndi zanu. Wanu, Inu Yehova ndi ufumu; Inu ndinu wokwezeka ndipo ndinu mtsogoleri wa zonse.
12 Lenotho lodumo kuvela phambi kwakho, wena-ke ubusa phezu kwakho konke; lesandleni sakho kukhona ukuqina lamandla, lesandleni sakho kukhona ukukhulisa lokupha amandla kubo bonke.
Chuma ndi ulemu zimachokera kwa Inu; Inu ndinu wolamulira zinthu zonse. Mʼdzanja lanu muli nyonga ndi mphamvu, kukweza ndi kupereka nyonga kwa onse.
13 Ngakho-ke Nkulunkulu wethu, siyakubonga, silidumise ibizo lakho elilodumo.
Tsopano Mulungu wathu, ife tikukuthokozani ndi kutamanda dzina lanu laulemerero.
14 Ngoba mina-ke ngingubani, labantu bami bangobani, ukuthi sithole amandla okunika ngothando ngokunje? Ngoba konke kuvela kuwe, sinikele kuwe okuvela esandleni sakho.
“Koma ine ndine yani, ndipo anthu anga ndani, kuti tikupatsani mowolowamanja motere? Zinthu zonse zimachokera kwa Inu, ndipo ife takupatsani zomwe zimachokera mʼdzanja lanu.
15 Ngoba singabemzini phambi kwakho labahlala njengabezizwe njengabo bonke obaba; insuku zethu emhlabeni zinjengesithunzi, njalo kalikho ithemba.
Ife ndife anthu osadziwika ndiponso alendo pamaso panu, monga analili makolo athu. Masiku anthu pa dziko lapansi ali ngati chithunzithunzi, wopanda chiyembekezo.
16 Nkosi Nkulunkulu wethu, konke lokhu okunengi, esikulungisele ukwakhela wena indlu, kusenzelwa ibizo lakho elingcwele, kuvela esandleni sakho, njalo konke kungokwakho.
Inu Yehova Mulungu wathu, zinthu zonse zimene tapereka kumangira Nyumba yanu zachokera mʼdzanja lanu ndipo zonsezi ndi zanu.
17 Ngiyazi-ke, Nkulunkulu wami, ukuthi wena uhlola inhliziyo, uyabuthanda ubuqotho. Mina, ebuqothweni benhliziyo yami nginikele ngesihle zonke lezizinto; khathesi sengibonile ngentokozo abantu bakho abatholakala lapha ukuthi banikela kuwe ngesihle.
Mulungu wanga, ine ndikudziwa kuti mumayesa mtima ndipo mumakondwera ndi anthu angwiro. Zinthu zonsezi ndapereka mwaufulu ndi cholinga chabwino. Ndipo tsopano ndaona ndi chimwemwe momwe anthu anu amene ali pano akuperekera mwaufulu kwa Inu.
18 Nkosi, Nkulunkulu kaAbrahama, uIsaka, loIsrayeli, obaba, gcina lokho laphakade ekuzindleni kweminakano yenhliziyo yabantu bakho, ulungise inhliziyo yabo kuwe.
Inu Yehova Mulungu wa makolo athu Abrahamu, Isake ndi Israeli, mukhazikitse chofuna ichi mʼmitima ya anthu anu kwamuyaya, ndipo mukhazikitse mtima wokhulupirika kwa Inu.
19 Njalo unike uSolomoni indodana yami inhliziyo epheleleyo ukugcina imilayo yakho, ubufakazi bakho, lezimiso zakho, lokwenza konke, lokwakha isigodlo engisilungiseleleyo.
Ndipo mumupatse mwana wanga Solomoni mtima wodzipereka kwathunthu kwa Inu kuti asunge malamulo anu, zofuna ndi malangizo anu. Achite chilichonse pomanga nyumba yaufumu imene ine ndayipezera zofunika zonse.”
20 UDavida wasesithi kulo lonke ibandla: Khathesi busisani iNkosi uNkulunkulu wenu. Ibandla lonke laselibusisa iNkosi, uNkulunkulu waboyise; bakhothama bamkhonza uJehova, lenkosi.
Kenaka mfumu Davide inati kwa gulu lonse, “Tamandani Yehova Mulungu wanu.” Kotero onse anatamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anawerama pansi ndi kugona chafufumimba pamaso pa Yehova ndi mfumu.
21 Basebehlabela imihlatshelo eNkosini, banikela iminikelo yokutshiswa eNkosini, ngokusa kwalolosuku, amajongosi azinkulungwane, izinqama eziyinkulungwane, amawundlu ayinkulungwane, kanye leminikelo yabo yokunathwayo, lemihlatshelo ngobunengi kusenzelwa uIsrayeli wonke.
Mmawa mwake anthu anapereka nsembe zosiyanasiyana ndi nsembe zopsereza kwa Yehova; ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa zamphongo 1,000 ndi ana ankhosa 1,000, pamodzi ndi nsembe yachakumwa ndi nsembe zina zambiri zoperekera Aisraeli onse.
22 Basebesidla banatha phambi kweNkosi ngalolosuku ngentokozo enkulu. Basebembeka okwesibili uSolomoni indodana kaDavida ukuthi abe yinkosi, bamgcobela iNkosi waba ngumkhokheli, loZadoki waba ngumpristi.
Tsiku limeneli, iwo anadya ndi kumwa mosangalala pamaso pa Yehova ndipo anavomereza Solomoni mwana wa Davide kukhala mfumu yawo kachiwiri. Anamudzoza pamaso pa Yehova kukhala wolamulira wawo ndipo Zadoki anadzozedwa kukhala wansembe.
23 USolomoni wasehlala esihlalweni sobukhosi sikaJehova njengenkosi esikhundleni sikaDavida uyise, waphumelela; loIsrayeli wonke wamlalela.
Ndipo Solomoni ankakhala pa mpando waufumu wa Yehova monga mfumu mʼmalo mwa Davide abambo ake. Iye analemera ndipo Aisraeli onse ankamumvera.
24 Lazo zonke izinduna lamaqhawe kanye lawo wonke amadodana enkosi uDavida bazehlisela ngaphansi kukaSolomoni inkosi.
Akuluakulu onse a ankhondo ndi anthu amphamvu, pamodzinso ndi ana onse aamuna a mfumu Davide, analonjeza kumvera mfumu Solomoni.
25 INkosi yasimphakamisa uSolomoni kakhulu phambi kwamehlo kaIsrayeli wonke, yamnika ubukhosi bombuso obungazanga bube khona lakuyiphi inkosi ngaphambi kwakhe koIsrayeli.
Yehova anamukweza kwambiri Solomoni pamaso pa Aisraeli onse ndi kumupatsa ulemerero waufumu umene sunapatsidwepo kwa mfumu ina iliyonse ya Israeli.
26 Ngokunjalo uDavida indodana kaJese wayebuse phezu kukaIsrayeli wonke.
Davide mwana wa Yese anali mfumu ya Aisraeli onse.
27 Njalo insuku abusa ngazo phezu kukaIsrayeli zaziyiminyaka engamatshumi amane; eHebroni wabusa iminyaka eyisikhombisa, leJerusalema wabusa iminyaka engamatshumi amathathu lantathu.
Iye analamulira Israeli kwa zaka makumi anayi; zaka zisanu ndi ziwiri ali ku Hebroni ndi zaka 33 ali ku Yerusalemu.
28 Wasesifa eseluphele kuhle, enele ngezinsuku, inotho lodumo; uSolomoni indodana yakhe wasebusa esikhundleni sakhe.
Iye anamwalira atakalamba kwambiri, atakhala ndi moyo wautali, chuma ndi ulemu. Solomoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Njalo izindaba zikaDavida inkosi, ezokuqala lezokucina, khangela, zibhaliwe egwalweni lwezindaba zikaSamuweli umboni legwalweni lwezindaba zikaNathani umprofethi legwalweni lwezindaba zikaGadi umboni,
Tsono zonse zimene mfumu Davide anachita, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mneneri Samueli, mʼbuku la mneneri Natani ndi mʼbuku la mneneri Gadi,
30 kanye lakho konke ukubusa kwakhe lamandla akhe, lezikhathi ezedlula phezu kwakhe laphezu kukaIsrayeli laphezu kwayo yonke imibuso yamazwe.
pamodzi ndi tsatanetsatane wa mbiri ya ulamuliro wake ndi mphamvu zake, ndi zonse zomwe zinamuzungulira iye ndi Israeli ndiponso mafumu a mayiko ena onse.