< 1 Imilando 26 >

1 Ngezigaba zabalindi bamasango. KwabakoKora kwakunguMeshelemiya indodana kaKore wamadodana kaAsafi.
Magulu a alonda a pa zipata: Kuchokera ku banja la Kora: Meselemiya mwana wa Kore, mmodzi mwa ana a Asafu.
2 LoMeshelemiya wayelamadodana, uZekhariya izibulo, uJediyayeli owesibili, uZebhadiya owesithathu, uJathiniyeli owesine,
Meselemiya anali ndi ana awa: woyamba Zekariya, wachiwiri Yediaeli, wachitatu Zebadiya, wachinayi Yatinieli,
3 uElamu owesihlanu, uJehohanani owesithupha, uEliyohenayi owesikhombisa.
wachisanu Elamu, wachisanu ndi chimodzi Yehohanani, ndipo wachisanu ndi chiwiri Elihunai.
4 UObedi-Edoma laye wayelamadodana, uShemaya izibulo, uJehozabadi owesibili, uJowa owesithathu, uSakari owesine, loNethaneli owesihlanu,
Obedi-Edomu analinso ndi ana awa: woyamba Semaya, wachiwiri Yehozabadi, wachitatu Yowa, wachinayi Sakara, wachisanu Netaneli,
5 uAmiyeli owesithupha, uIsakari owesikhombisa, uPhewulethayi owesificaminwembili; ngoba uNkulunkulu wayembusisile.
wachisanu ndi chimodzi Amieli, wachisanu ndi chiwiri Isakara ndipo wachisanu ndi chitatu Peuletayi. (Pakuti Mulungu anadalitsa Obedi-Edomu).
6 LakuShemaya indodana yakhe kwazalwa amadodana abusa jikelele endlini kayise, ngoba ayengamaqhawe alamandla.
Mwana wake Semaya analinso ndi ana amene anali atsogoleri mʼbanja la abambo awo chifukwa anali anthu amphamvu.
7 Amadodana kaShemaya: O-Othini, loRefayeli, loObedi, uElizabadi, abafowabo, amadodana alamandla, oElihu loSemakhiya.
Ana a Semaya anali: Otini, Refaeli, Obedi ndi Elizabadi; abale ake, Elihu ndi Semakiya, analinso anthu amphamvu.
8 Bonke laba babengabamadodana kaObedi-Edoma, bona lamadodana abo labafowabo, amadoda enelisayo ngamandla omsebenzi, bengamatshumi ayisithupha lambili bakoObedi-Edoma.
Onsewa anali adzukulu a Obedi-Edomu. Iwo ndi ana awo ndiponso abale awo anali anthu aluso ndi amphamvu pogwira ntchito. Zidzukulu zonse za Obedi-Edomu zinalipo 62.
9 Njalo uMeshelemiya wayelamadodana labafowabo, amadodana alamandla, elitshumi lesificaminwembili.
Meselemiya anali ndi ana ndi abale ake amene anali aluso ndipo onse analipo 18.
10 UHosha laye emadodaneni kaMerari wayelamadodana, uShimiri inhloko (lanxa wayengeyisilo izibulo, kodwa uyise wamenza waba yinhloko);
Hosa Mmerari anali ndi ana awa: woyamba anali Simiri (ngakhale kuti iye sanali woyamba kubadwa, abambo ake anamusankha kuti akhale mtsogoleri),
11 uHilikhiya owesibili, uTebaliya owesithathu, uZekhariya owesine; wonke amadodana labafowabo bakaHosa babelitshumi lantathu.
wachiwiri Hilikiya, wachitatu Tebaliya ndipo wachinayi Zekariya. Ana ndi abale onse a Hosa analipo 13.
12 Phakathi kwalabo kwakulezigaba zabalindi bamasango; izinhloko zamadoda zilemilandu njengabafowabo, ukukhonza endlini yeNkosi.
Magulu amenewa a alonda a pa zipata, motsogozedwa ndi atsogoleri awo, anali ndi ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova, monga momwe amachitira abale awo.
13 Basebesenza inkatho yokuphosa, omncinyane laye njengomkhulu, ngokwendlu yaboyise, besenzela isango lesango.
Iwo anachita maere mwa mabanja awo aangʼono ndi aakulu omwe kuti apeze mlonda pa chipata chilichonse.
14 Inkatho yempumalanga yawela-ke phezu kukaShelemiya; basebesenza inkatho yokuphosa ngoZekhariya indodana yakhe, umeluleki ohlakaniphileyo; inkatho yakhe yasiphuma ngenyakatho.
Maere a chipata chakummwa anagwera Selemiya. Maere anachitikanso chifukwa cha mwana wake Zekariya, phungu wanzeru ndipo maere a chipata chakumpoto anagwera iye.
15 KuObedi-Edoma ngeningizimu; lakumadodana akhe, indlu yokulondoloza.
Maere a chipata chakummwera anagwera Obedi-Edomu, ndipo maere a nyumba yosungiramo katundu anagwera ana ake.
16 KuShupimi lakuHosa ngentshonalanga, lesango iShalekethi elisemgwaqweni omkhulu oya phezulu, umlindi ngomlindi.
Maere a chipata chakumadzulo ndi chipata cha Saleketi ku msewu wa ku mtunda anagwera Supimu ndi Hosa. Mlonda ankayangʼanana ndi mlonda mnzake:
17 Ngempumalanga kwakulamaLevi ayisithupha, ngenyakatho abane ngosuku, ngeningizimu abane ngosuku, leziphaleni ababili ngababili;
Mbali ya kummawa kunkakhala Alevi 6 pa tsiku, kumpoto anayi pa tsiku, kummwera anayi pa tsiku ndipo awiri ankakhala pa nyumba yosungiramo katundu.
18 eParibari ngentshonalanga, abane emgwaqweni omkhulu, ababili eParibari.
Ndipo ku bwalo cha kumadzulo, anayi amakhala mu msewu ndi awiri pabwalo penipeni.
19 Lezi yizigaba zabalindi bamasango bamadodana amaKora labamadodana kaMerari.
Awa anali magulu a alonda a pa zipata amene anali zidzukulu za Kora ndi Merari.
20 LakumaLevi, uAhiya wayephethe izinto eziligugu zendlu kaNkulunkulu, njalo wayephethe izinto eziligugu zezinto ezingcwele.
Abale awo Alevi, motsogozedwa ndi Ahiya, anali oyangʼanira chuma cha nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Mulungu.
21 Amadodana kaLadani, abantwana bomGerishoni uLadani, kaLadani umGerishoni, inhloko zaboyise zazingoJehiyeli.
Adzukulu a Ladani, mmodzi mwa ana a Geresoni, amene anali atsogoleri a mabanja a Ageresoni, anali awa: Yehieli,
22 Amadodana kaJehiyeli: UZethamu, loJoweli umfowabo, babephethe izinto eziligugu zendlu yeNkosi.
ana a Yehieli, Zetamu ndi mʼbale wake Yoweli. Iwo amayangʼanira chuma cha ku Nyumba ya Mulungu wa Yehova.
23 KumaAmramu, kumaIzihari, kumaHebroni, kumaUziyeli.
Kuchokera ku banja la Amramu, banja la Aizihara, banja la Ahebroni ndi banja la Auzieli:
24 LoShebuweli indodana kaGereshoma indodana kaMozisi wayeyisiphathamandla phezu kwezinto eziligugu.
Subaeli, chidzukulu cha Geresomu, mwana wa Mose, anali mkulu woyangʼanira chuma.
25 Labafowabo abakaEliyezeri: ORehabhiya indodana yakhe, loJeshaya indodana yakhe, loJoramu indodana yakhe, loZikiri indodana yakhe, loShelomithi indodana yakhe.
Abale ake obadwa mwa Eliezara, anali Rekabiya mwana wake, Yesaya mwana wake, Yoramu mwana wake, Zikiri mwana wake ndi Selomiti mwana wake.
26 UShelomithi lo labafowabo babephethe zonke izinto eziligugu zezinto ezingcwele uDavida inkosi ayezingcwelisile, lenhloko zaboyise, lenduna zezinkulungwane lezamakhulu, labalawulimabutho.
Selomiti ndi abale ake amayangʼanira zinthu zonse zoperekedwa kwa Mulungu ndi mfumu Davide, atsogoleri a mabanja amene anali olamulira ankhondo 1,000, olamulira ankhondo 100, ndi olamulira ankhondo ena.
27 Kokwempi lokwempangweni bakungcwelisela ukulungisa indlu yeNkosi.
Zina zofunkha ku nkhondo anazipereka kuti zikhale zokonzera Nyumba ya Yehova.
28 Lakho konke uSamuweli umboni ayekungcwelisile, loSawuli indodana kaKishi loAbhineri indodana kaNeri loJowabi indodana kaZeruya; konke okwakungcwelisiwe kwakungaphansi kwesandla sikaShelomithi labafowabo.
Ndipo zonse zimene zinaperekedwa ndi Mlosi Samueli, Sauli mwana wa Kisi, Abineri mwana wa Neri ndiponso Yowabu mwana wa Zeruya ndi zinthu zonse zimene zinkaperekedwa zimasungidwa ndi Selomiti ndi abale ake.
29 KumaIzihari uKenaniya lamadodana akhe babengabomsebenzi wangaphandle phezu kukaIsrayeli, beyizinduna bengabahluleli.
Kuchokera ku banja la Izihari: Kenaniya ndi ana ake anapatsidwa ntchito kutali ndi Nyumba ya Mulungu ngati akuluakulu ndi oweruza Israeli.
30 KumaHebroni uHashabhiya labafowabo, amadoda alamandla, ayinkulungwane lamakhulu ayisikhombisa, babephethe iziphathamandla zakoIsrayeli nganeno kweJordani ngentshonalanga, emsebenzini wonke kaJehova lenkonzweni yenkosi.
Kuchokera ku banja la Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake, anthu anzeru 1,700. Iwo ankayangʼanira ntchito zonse za Yehova ndi ntchito yonse ya mfumu cha kumadzulo kwa Yorodani.
31 KumaHebroni uJeriya wayeyinhloko, kumaHebroni, ngokwezizukulwana zaboyise. Ngomnyaka wamatshumi amane wokubusa kukaDavida adingwa, kwasekutholwa phakathi kwawo amaqhawe alamandla eJazere yeGileyadi.
Pa banja la Ahebroni, Yeriya anali mtsogoleri monga mwa mbiri ya mibado ya mabanja awo. Mʼchaka cha 40 cha ufumu wa Davide, panachitika kafukufuku ndipo ena mwa anthu aluso a banja la Hebroni anapezeka kuti anali ku Yazeri ku Giliyadi.
32 Labafowabo amadoda alamandla ayezinkulungwane ezimbili lamakhulu ayisikhombisa, inhloko zezindlu. UDavida inkosi wasebenza abaphathi phezu kwabakoRubeni labakoGadi lengxenye yesizwe sakoManase ezintweni zonke zikaNkulunkulu lezinto zenkosi.
Yeriya anali ndi abale 2,700 amene anali aluso ndiponso atsogoleri a mabanja. Mfumu Davide anawayika iwowa kuti aziyangʼanira fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase pa zinthu zonse za Mulungu ndi za mfumu.

< 1 Imilando 26 >