< UZefaniya 3 >

1 Maye kulo idolobho labancindezeli, elihlamukayo lelingcolileyo!
Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
2 Kalilaleli muntu, kalivumi kukhuzwa. Kalithembeli kuThixo, kalisondeli kuNkulunkulu walo.
Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
3 Izikhulu zalo ziyizilwane ezibhongayo, ababusi balo bazimpisi zakusihlwa, ezingatshiyi lutho lwekuseni.
Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
4 Abaphrofethi balo bayazazisa; bangabantu bamacebo amabi. Abaphristi balo bangcolisa indawo engcwele bephule lomthetho.
Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
5 UThixo phakathi kwalo ulungile; kenzi okubi, nsuku zonke ekuseni wenza ukulunga kwakhe njalo kaphambanisi ukusa kwamalanga wonke, ikanti abangalunganga kabalanhloni.
Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
6 “Ngizichithile izizwe; izinqaba zazo zidiliziwe. Ngitshiye imigwaqo yazo ideliwe kungekho odlula khona. Amadolobho azo adiliziwe; kakho ozasala kakho lamunye.
“Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
7 Ngathi kulo idolobho, ‘Impela uzangesaba uvume ukukhuzwa!’ Lapho-ke indlu yalo yokuhlala yayingayikudilizwa loba isijeziso sami sehlele phezu kwalo. Kodwa babelokhu betshisekela izenzo zokuxhwala kukho konke abakwenzayo.
Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
8 Ngakho ngilindela,” kutsho uThixo, “lolusuku engizasukuma ngalo ngifakaze. Sengimise ukubuthanisa izizwe, ngiqoqe imibuso, ngehlisele ulaka lwami phezu kwabo konke ukuthukuthela kwami okukhulu. Umhlaba wonke uzaqothulwa ngomlilo womona wentukuthelo yami.”
Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
9 “Lapho-ke ngizahlambulula izindebe zezizwe, ukuze zonke zikhuleke ebizweni likaThixo zimkhonze zimanyane.
“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
10 Kusukela ngaphetsheya kwemifula yaseKhushi abakhonzi bami, abantu bami abahlakazekileyo, bazangilethela iminikelo.
Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
11 Ngalolosuku kaliyikuyangiswa ngobubi bonke elabenza kimi, ngoba ngizabasusa kulelidolobho abathokoziswa yikuzigqaja kwabo. Kaliyikuzikhukhumeza futhi entabeni yami engcwele.
Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
12 Kodwa ngizatshiya phakathi kwenu abathambileyo labathobekileyo, abathembele ebizweni likaThixo.
Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
13 Kabayikwenza okubi; kabayikuqamba amanga, loba kube lenkohliso emilonyeni yabo. Bazakudla balale phansi, kakho ozabenza besabe.”
Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
14 Hlabela wena Ndodakazi yeZiyoni, klabalala kakhulu, wena Israyeli! Thaba uthokoze ngenhliziyo yakho yonke wena ndodakazi yaseJerusalema!
Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 UThixo usesisusile isijeziso sakho, usesixotshile isitha sakho. UThixo, iNkosi ka-Israyeli, ulawe; akulangozi ozaphinda uyesabe futhi.
Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
16 Ngalolosuku bazakuthi kulo iJerusalema, “Ungesabi, wena Ziyoni; ungavumeli ukuba izandla zakho zibe buthakathaka.
Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
17 UThixo uNkulunkulu wakho ulawe, ulamandla okusindisa. Uzathokoza kakhulu ngawe, uzakududuza ngothando lwakhe, uzakuthokozela ngokuhlabelela.”
Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
18 “Insizi zemikhosi emisiweyo ngizazisusa kuwe; zingumthwalo lehlazo kuwe.
“Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Ngalesosikhathi ngizababona bonke abalincindezelayo; ngizahlenga abaqhulayo ngibuthe lalabo abahlakazwayo, ngizabapha udumo lenhlonipho kuwo wonke amazwe lapho abahlaziswa khona.
Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 Ngalesosikhathi ngizalibutha; ngalesosikhathi ngizalisa ekhaya. Ngizalipha inhlonipho lodumo phakathi kwezizwe zonke zasemhlabeni lapho sengiliphumelelisa futhi phambi kwamehlo enu uqobo,” kutsho uThixo.
Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.

< UZefaniya 3 >