< Ingoma Yezingoma 8 >

1 Aluba nje unjengomfowethu kimi, owondliwa emunya emabeleni kamama! Lapho-ke, nxa ngikufica phandle, ngithi loba ngikwanga, angabikhona ongisolayo.
Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga, amene anayamwa mawere a amayi anga! Ndikanakumana nawe pa njira, ndikanakupsompsona, ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.
2 Ngabe ngiyakudonsa ngikuse endlini kamama yena owangikhulisayo. Ngabe ngikupha iwayini elixutshiweyo unathe, uluju lwamaphomegranathi ami.
Ndikanakutenga ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, amayi amene anandiphunzitsa, ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe, zotsekemera za makangadza.
3 Ingalo yakhe yobunxele ngiyiqamele kuthi ingalo yakhe yokunene ingigonile.
Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.
4 Madodakazi aseJerusalema, ngiyaliqonqosela: Lingalunyakazisi loba liluvuse uthando luze luzifunele lona.
Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani: musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
5 Ngubani lo oqhamukayo evela enkangala na, eyeme isithandwa sakhe? Umlobokazi Ngikuvusile ngaphansi kwesihlahla se-aphula; kulapho unyoko akumithela khona, kulapho ahelelwa wakuzalela khona.
Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo, atatsamira wokondedwa wakeyo? Mkazi Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi, pamenepo ndi pamene amayi anachirira, pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.
6 Ngibeka ngibe njengesidindo enhliziyweni yakho, njengesidindo engalweni yakho; ngoba uthando lulamandla njengokufa, ubukhwele balo kabuyekethisi njengengcwaba. Luyatshisa njengomlilo obhebha kakhulu, njengelangabi elivuthayo. (Sheol h7585)
Undiyike pamtima pako ngati chidindo, ngati chidindo cha pa dzanja lako; pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa, nsanje ndiyaliwuma ngati manda. Chikondi chimachita kuti lawilawi ngati malawi a moto wamphamvu. (Sheol h7585)
7 Impophoma zamanzi ngeke zilucime uthando; imifula ngeke ilukhukhule. Nxa umuntu enganika yonke inotho yomuzi wakhe ngenxa yothando kungaba yinhlekisa.
Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi, mitsinje singachikokolole chikondicho. Ngati wina apereka chuma chonse cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi, adzangonyozeka nazo kotheratu.
8 Silentombazana engumnawethu, njalo kayikaphuhli. Sizamenzelani kambe umnawethu mhla sekuthiwa uyacelwa?
Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono, koma alibe mawere, kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu pa tsiku limene adzamufunsire?
9 Uba engumduli, sizakwakha imiphotshongo yesiliva phezu kwakhe. Uba engumnyango, sizamvala ngamapulanka esihlahla somsedari.
Ngati iye ndi khoma, tidzamumangira nsanja ya siliva. Ngati iye ndi chitseko, tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.
10 Ngingumduli, lamabele ami anjengemiphotshongo. Yikho-nje emehlweni akhe sengifana lalowo olethe ukusuthiseka.
Ine ndili ngati khoma, ndipo mawere anga ndi nsanja zake. Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa ndine wobweretsa mtendere.
11 USolomoni wayelesivini eBhali Hamoni; wasiqhatshisela ebalimini isivini sakhe. Munye ngamunye kwakumele athele umthelo wezithelo zawo ongamashekeli esiliva ayinkulungwane.
Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni; iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi, aliyense mwa iwo ankayenera kupereka ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.
12 Kodwa esami isivini ngesami ukupha santando; amashekeli lawo ayinkulungwane ngawakho, bakithi Solomoni, lamakhulu amabili amashekeli ngawalabo abalondoloza izithelo zawo.
Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha. Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000 ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.
13 Wena ohlala ezivandeni labangane bekususa isizungu, ake ngilizwe ilizwi lakho!
Iwe amene umakhala mʼminda uli pamodzi ndi anzako, ndilole kuti ndimve liwu lako!
14 Masihambe, sithandwa sami, woba njengembabala kumbe njengejongosana lomziki ezintabeni ezigcwele amakha.
Fulumira wokondedwa wanga, ndipo ukhale ngati gwape kapena mwana wa mbawala wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.

< Ingoma Yezingoma 8 >