< Amahubo 98 >

1 Ihubo Hlabelelani uThixo ingoma entsha, ngoba wenzile izinto ezimangalisayo; isandla sakhe sokunene lengalo yakhe engcwele sekumenzele insindiso.
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
2 UThixo useyenze yaziwa insindiso yakhe waveza ukulunga kwakhe ezizweni.
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
3 Uselukhumbule uthando lwakhe lokuthembeka Kwakhe endlini ka-Israyeli; yonke imikhawulo yomhlaba iyibonile insindiso kaNkulunkulu wethu.
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
4 Hlokomani ngentokozo kuThixo, mhlaba wonke, hlabelani ingoma ngokujabula okukhulu, litshaya amachacho;
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
5 yenzani umsindo kuThixo ngomhubhe, ngomhubhe langomsindo wokuhlabela,
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
6 ngamacilongo langomsindo wophondo lwenqama hlokomani ngentokozo phambi kukaThixo, iNkosi.
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
7 Akuthi ulwandle luhlokome, lakho konke okuphakathi kwalo, umhlaba labo bonke abahlala kuwo.
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
8 Akuthi imifula iqakeze izandla zayo, akuthi izintaba zihlabele kanyekanye ngentokozo;
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
9 kazihlabele phambi kukaThixo, ngoba Uyeza ukuzakwahlulela umhlaba. Uzakwahlulela umhlaba ngokulunga labantu bonke ngokufaneleyo.
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.

< Amahubo 98 >