< Amahubo 95 >

1 Wozani sihlabelele ngentokozo kuThixo; kasihlokomeni kamnandi kulo iDwala lokusindiswa kwethu.
Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe, tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
2 Kasizeni phambi kwakhe ngokubonga simdumise ngamachacho langengoma.
Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
3 Ngoba uThixo unguNkulunkulu omkhulu, iNkosi enkulu ngaphezu kwabonkulunkulu bonke.
Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu, mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
4 Inziki zomhlaba zisezandleni zakhe, leziqongo zezintaba ngezakhe.
Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi, ndipo msonga za mapiri ndi zake.
5 Ngolwakhe ulwandle ngoba walwenza, lezandla zakhe zawenza umhlaba owomileyo.
Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye, ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
6 Wozani, kasikhothame simkhonze, kasiguqe phambi kukaThixo uMenzi wethu;
Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira, tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
7 ngoba unguNkulunkulu wethu, thina singabantu bedlelo lakhe, umhlambi awunakekelayo. Lamhla, nxa lisizwa ilizwi lakhe,
pakuti Iye ndiye Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za mʼdzanja lake. Lero ngati inu mumva mawu ake,
8 lingazenzi lukhuni inhliziyo zenu njengoba lenzenjalo eMeribha, njengelakwenza ngaleliyana ilanga eMasa enkangala,
musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba, monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
9 lapho okhokho benu abangilinga khona bengizama, lanxa babekubonile engakwenzayo.
Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa, ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
10 Okweminyaka engamatshumi amane ngangisizondele lesosizukulwane; ngathi, “Bangabantu onhliziyo zabo ziyahlanhlatha, njalo kabazazanga izindlela zami.”
Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo; ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera ndipo sanadziwe njira zanga.”
11 Ngakho ngamemezela ngesifungo ekuthukutheleni kwami ngathi, “Kabayikungena ekuphumuleni kwami.”
Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti, “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”

< Amahubo 95 >