< Amahubo 94 >
1 Oh Thixo, uNkulunkulu ophindiselayo, Oh Nkulunkulu ophindiselayo, khanya uvele.
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Phakama, awu Mahluli womhlaba; baphindisele abazigqajayo ngokubafaneleyo.
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 Koze kube nini ababi, Oh Thixo, koze kube nini ababi beklamasa na?
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 Bathulula amazwi okukloloda; zonke izigangi zifuthelene ngokuzikhukhumeza.
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 Ziyabanyathezela abantu bakho, Oh Thixo; zincindezela ilifa lakho.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 Zibulala umfelokazi kanye lowezizweni; zibulala intandane.
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 Zithi, “UThixo kaboni; uNkulunkulu kaJakhobe kananzi.”
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Limukani, lina elingelangqondo phakathi kwabantu; lina ziphukuphuku, lizahlakanipha nini?
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 Yena lowo owayigxumekayo indlebe kezwa yini? Yena lowo owabumba ilihlo kaboni na?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 Yena lowo oqondisa izizwe kajezisi yini? Yena lowo ofundisa umuntu kalalwazi na?
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 UThixo uyayazi imicabango yomuntu; uyayazi ukuthi iyize nje.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Ubusisiwe umuntu omqondisayo, Oh Thixo, umuntu omfundisa okomthetho wakho;
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 uyamphumuza ensukwini zokuhlupheka, kuze kuthi ababi bembelwe igodi.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 Ngoba uThixo kazukwala abantu bakhe; kasoze lanini afulathele ilifa lakhe.
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 Ukwahlulela kuzaphinda njalo kumiswe ngokulunga, kuthi bonke abaqotho ngenhliziyo bakulandele.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Ngubani ozangimela ekulweni lababi na? Ngubani ozangelekelela ekulweni lezigangi na?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 Aluba uThixo wayengangelulekanga, ngabe ngahle ngahlala ngathula zwi ekufeni.
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 Lapho ngasengisithi, “Unyawo lwami selutshelela,” uthando lwakho, Oh Thixo, lwangisekela.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 Nxa ukunqineka kwase kungikhulela, induduzo yakho yaletha intokozo emphefumulweni wami.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Kambe isihlalo sobukhosi esixhwalileyo singema lawe yini leso esiletha inhlupheko ngezimemezelo zaso?
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 Bayahlangana ukumelana labalungileyo ongelacala agwetshelwe ukufa.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 Kodwa uThixo useyinqaba yami, loNkulunkulu wami ulidwala engiphephela kulo.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 Uzabaphindisela ngenxa yezono zabo ababhubhise ngenxa yobubi babo; uThixo uNkulunkulu wethu uzababhubhisa.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.